edaiofficial's picture
initial commits
78aa4ee
© 2017 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
Zopeleka zaufulu n’zimene zimathandiza kupititsa patsogolo nchito imeneyi .
Kuti mupeleke copeleka canu , yendani pa webusaiti ya www.jw.org .
Baibo imene taseŵenzetsa ni Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika kusiyapo ngati taonetsa ina .
© 2018 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
Yehova ndi dzina la Mulungu monga mmene lalembedwela m’Baibo .
Cifunilo canu cicitike , monga kumwamba , cimodzi - modzinso pansi pano , ” silinayankhidwe kothelatu . ( Mat .
( Ŵelengani Luka 21 : 1 - 4 . )
Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 8 m’buku ili Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova
( b ) Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
( b ) Ndi mafunso ati amene tidzakambitsilana m’nkhani yotsatila ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 10 : 13 . )
Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 3 m’buku ili , Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova
( Ŵelengani 1 Akorinto 6 : 9 - 11 . )
Pamenepo amene ali mu Yudeya adzayambe kuthaŵila kumapili , ndipo amene ali mkati mwa mzindawo adzatulukemo .
Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Ineyo Yehova ndidzafulumizitsa zimenezi pa nthawi yake . ”
( b ) Kodi tidzakambitsilana mafunso ati ?
( Ŵelengani Luka 10 : 29 - 37 . )
Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ?
Koma usadye zipatso za mtengo wodziŵitsa cabwino ndi coipa . Cifukwa tsiku limene udzadya , udzafa ndithu . ”
Ndimupangila womuthandiza , monga mnzake womuyenelela . ”
( b ) Tikambilana mafunso ati ?
“ Mau a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu . ” — AHEB .
( Ŵelengani Chivumbulutso 14 : 6 , 7 . )
( Ŵelengani 1 Atesalonika 2 : 13 . )
Adzaweluza mwacilungamo anthu onyozeka ndipo adzadzudzula anthu moongoka mtima , pothandiza ofatsa pa dziko lapansi . ”
“ Cikhulupililo ndico ciyembekezo cotsimikizilika ca zinthu zoyembekezeledwa . ” — AHEB .
( Ŵelengani Aheberi 13 : 7 , 17 . )
( b ) Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ?
Yesu anati : “ Kumene kuli cuma cako , mtima wako umakhalanso komweko . ”
( Ŵelengani Aroma 7 : 21 - 25 . )
Ngati n’conco , tikuyamikilani kwambili .
( Ŵelengani Aheberi 11 : 24 - 27 . )
“ Odala ndi anthu amene Mulungu wao ndi Yehova . ” — SAL .
Maakaunti Akubanki : Mukhoza kupeleka zinthu monga maakaunti anu akubanki , zikalata zosungitsila ndalama , kapena maakaunti a ndalama zimene mukusunga kuti mudzagwilitse nchito mukadzapuma pa nchito .
Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Kodi mwaŵelenga mosamala magazini aposacedwapa a Nsanja ya Mlonda ?
Yesani kuyankha mafunso otsatilawa :
Lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova koma tsopano anasiya kulisindikiza .
Maina ena asinthidwa .
( Ŵelengani Yakobo 5 : 14 - 16 . )
( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Iye anati : “ Ine ndine wakuthupi , wogulitsidwa ku ucimo .
Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
( b ) Tikambilana ciani m’nkhani ino ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 58 . )
Simungathe kutumikila Mulungu ndi Cuma nthawi imodzi . ”
( Ŵelengani Aheberi 10 : 24 , 25 . )
( Ŵelengani 2 Akorinto 8 : 13 - 15 . )
( Ŵelengani Mateyu 24 : 37 - 39 . )
Nowa anayenda ndi Mulungu woona . ” — Gen .
© 2016 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
MAGAZINI ya Nsanja ya Mlonda , imalemekeza Yehova Mulungu , amene ndi Wolamulila wa cilengedwe conse .
Imalimbikitsa anthu ndi uthenga wabwino wakuti Ufumu wa Mulungu posacedwapa udzacotsa zoipa zonse ndi kusintha dziko lapansi kukhala paladaiso .
Imalimbikitsa anthu kukhulupilila Yesu Kristu amene anatifela kuti tidzapeze moyo wosatha , ndipo panthawi ino iye akulamulila monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu .
Magaziniyi yakhala ikufalitsidwa kuyambila mu 1879 ndipo si yandale .
Mfundo zake zonse n’zocokela m’Baibulo .
Bebe anali kukonda kwambili atate ake .
Bwenzi la banja lao ndilo linakamba mau amene ali pamwambapa , koma mauwo sanamutonthoze .
Iye mobwelezabweleza anali kudziuza kuti : “ Atate anafa imfa yoipa . ”
Patapita zaka , Bebe analemba za imfa ya atate ake m’buku . Izi zinaonetsa kuti anali akali ndi cisoni .
Malinga ndi zimene zinacitikila Bebe , zimatenga nthawi yaitali kuti munthu apilile cisoni makamaka ngati munthu amene anamwalila anali kum’konda kwambili .
M’pomveka kuti Baibulo limacha imfa kuti “ mdani womalizila . ”
( 1 Akorinto 15 : 26 ) Imfa imasokoneza kwambili umoyo wathu , ndipo mwadzidzidzi imatenga anthu amene timakonda kwambili .
Palibe amene angapewe zotsatilapo za imfa .
Conco , n’zosadabwitsa kuti zimativuta kupilila imfa ndi zotsatilapo zake .
Mwina mumadzifunsa kuti : ‘ Kodi cisoni cimatenga nthawi yaitali bwanji kuti cithe ?
Ndingatonthoze bwanji anthu amene okondedwa ao anamwalila ?
Kodi pali ciyembekezo ciliconse kaamba ka okondedwa athu amene anamwalila ? ’
Kodi munadwalapo ?
Mwacitsanzo , ganizilani mmene Abulahamu anamvelela pamene mkazi wake anamwalila .
Baibulo limati : “ Abulahamu analoŵa muhema kukamulila Sara . ”
Mau akuti “ kukamulila ” aonetsa kuti cinamutengela nthawi yaitali kuti apilile imfa ya mkazi wake .
Yakobo analila mwana wake kwa “ masiku ambili , ” ndipo anali kukana kutonthozedwa ndi anthu a m’banja lake .
Ngakhale panali patapita zaka zambili , iye anali kukumbukilabe imfa ya Yosefe . — Genesis 23 : 2 ; 37 : 34 , 35 ; 42 : 36 ; 45 : 28 .
“ Mwamuna wanga Robert anamwalila pa July 9 , 2008 .
Ngakhale papita zaka 6 , ndimamvabe cisoni mumtima mwanga .
Sindidziŵa ngati imfa ya Rob ndidzaiiŵala . ” — Gail , wazaka 60 .
Papita zaka 18 kucokela pamene mkazi wanga anamwalila , koma ndimamuyewabe ndipo ndimamvabe cisoni .
Ndikaona cinthu cocititsa cidwi m’cilengedwe , ndimakumbukila mkazi wanga ndipo ndimaganizila mmene iye akanasangalalila kuona zinthu zimene ineyo ndikuona . ” — Etienne , wazaka 84 .
Kukamba zoona , n’kwacibadwa kumva ululu ndi cisoni .
Aliyense amalila m’njila zosiyanasiyana , ndipo kungakhale kupanda nzelu kuweluza munthu kaamba ka mmene akulilila cifukwa ca mavuto .
Komanso panthawi imodzimodzi , tisamadziimbe mlandu tikakhala ndi cisoni cimene sicikutha .
Malinga ndi zimene zili m’nkhani yakuti “ Tengelani Cikhulupililo Cao ” imene ili mu Nsanja ya Mlonda ino , Isaki analila amai ake kwa zaka zitatu . — Genesis 24 : 67 .
Mwacitsanzo , ena angakuuzeni kuti musalile kapena kuonetsa cisoni .
Ena angakuuzeni kuti muonetse cisoni canu conse .
Malangizo ake ndi ogwilizana kwambili ndi zimene ofufuza apeza masiku ano .
M’zikhalidwe zina , anthu amakamba kuti mwamuna weniweni salila .
Koma kodi tifunika kucita manyazi kulila tikakhala pagulu la anthu ?
Akatswili oona za matenda a m’maganizo anati , kulila ndi njila yabwino yoonetsela cisoni .
M’kupita kwa nthawi , kulila kungakuthandizeni kupilila imfa ya wokondedwa wanu .
Koma kubisa cisoni canu kungabweletse mavuto ambili .
Baibulo silicilikiza mfundo yakuti mwamuna weniweni salila .
Iye analila pamaso pa anthu pamene Lazaro bwenzi lake anamwalila , ngakhale kuti anali ndi mphamvu zoukitsa anthu . — Yohane 11 : 33 - 35 .
Kukhala wokwiya ndi njila inanso yoonetsela cisoni , makamaka pa imfa ya mwadzidzidzi .
Munthu wofeledwa amakhala wokwiya pa zifukwa zosiyanasiyana . Cifukwa cimodzi cingakhale cakuti , munthu amene amamulemekeza angakambe mau osathandiza kwenikweni .
Mwamuna wina dzina lake Mike , amene akhala ku South Africa , anakamba kuti : “ Atate anamwalila ndili ndi zaka 14 .
Tili pamalilo , m’busa wa chalichi ca Anglican anakamba kuti Mulungu amafuna anthu abwino ndipo amawatenga .
* Zimenezi zinandikhumudwitsa cifukwa atate ndinali kuŵakonda kwambili .
Pakacitika imfa ya mwadzidzidzi , wofeledwa angakhale ndi maganizo akuti , ‘ Ndikanacita zakutizakuti , munthuyo sakanamwalila . ’
Ngati mukudziimba mlandu kapena ndinu wokwiya cifukwa ca imfa ya wokondedwa wanu , musabise mmene mukumvelela .
Fotokozelani mnzanu wapamtima amene angakumvetseleni ndi kukutsimikizilani kuti maganizo otelo amavutitsa ofeledwa ambili .
Baibulo limati : “ Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse , ndipo ilo ndi m’bale amene anabadwila kuti akuthandize pakagwa mavuto . ” — Miyambo 17 : 17 .
Bwenzi la pamtima limene anthu ofeledwa angakhale nalo ndi Mlengi wathu , Yehova Mulungu .
Muuzeni zakukhosi kwanu m’pemphelo cifukwa iye “ amakudelani nkhawa . ”
( 1 Petulo 5 : 7 ) Kuonjezela apo , iye walonjeza onse amene amatelo kuti adzatsitsimula mtima ndi maganizo ao , cifukwa “ mtendele wa Mulungu umaposa kuganiza mozama kulikonse . ”
( Afilipi 4 : 6 , 7 ) Cinanso , lolani Mulungu kuti akuthandizeni kupilila cisoni kupitila m’Mau ake , Baibulo .
Kuganizila malembawa mozama kungakuthandizeni kwambili makamaka usiku mukakhala nokha , ndiponso ngati mukulephela kugona . — Yesaya 57 : 15 .
Mwamuna wina wa zaka 40 amene tam’patsa dzina lakuti Jack , mkazi wake anamwalila ndi matenda a kansa .
Iye anati : “ Kupemphela kwa Yehova kumandithandiza kuona kuti sindili ndekha .
Kaŵilikaŵili , ndimauka pakati pa usiku ndipo ndimalephela kugonanso .
Ndikaŵelenga ndi kuganizila mozama Malemba otonthoza , ndimauza Mulungu zakukhosi kwanga m’pemphelo . Ndikatelo , mtima wanga umakhala m’malo ndipo ndimakhala ndi mtendele wa m’maganizo . Izi zimandithandiza kupeza tulo . ”
Mai a mtsikana wina dzina lake Vanessa , anamwalila atadwala kwambili .
Iyenso waona kuti pemphelo limathandiza kwambili .
Iye anati : “ Panthawi yovutayi , ndinali kupemphela kwa Mulungu uku ndikulila .
Yehova anamvetsela mapemphelo anga ndipo anandipatsa mphamvu zakuti ndipilile . ”
Alangizi ena a anthu ofedwa amauza amene akuvutika ndi cisoni kuti azigwila nchito zothandiza ena .
Kugwila nchito zotelo kumabweletsa cimwemwe ndipo kumacepetsa cisoni ca munthu .
( Machitidwe 20 : 35 ) Ofedwa ambili amene ndi Akristu , aona kuti kugwila nchito zimenezi n’kotonthoza kwambili . — 2 Akorinto 1 : 3 , 4 .
Mulungu amamvetsa mmene mukumvelela . — Salimo 55 : 22 ; 1 Petulo 5 : 7 .
Mulungu amamvela mapemphelo a atumiki ake . — Salimo 86 : 5 ; 1 Atesalonika 5 : 17 .
Mulungu amakumbukila anthu amene anamwalila . — Yobu 14 : 13 - 15 .
Mulungu analonjeza kuti adzaukitsa akufa . — Yesaya 26 : 19 ; Yohane 5 : 28 , 29 .
Kodi munasoŵapo cocita pamene mnzanu anali ndi cisoni cifukwa ca wokondedwa wake amene anamwalila ?
Izi zikacitika , nthawi zina timasoŵa cokamba kapena cocita , cakuti timangokhala cete .
Komabe , pali zinthu zina zimene tingacite kuti tithandize olila .
Cofunika kwambili ndi kupita kunyumba ya malilo ndi kunena mau monga akuti , “ Pepani ndi zimene zacitika . ”
M’zikhalidwe zambili , anthu amaona kuti kukumbatila munthu ndi kulila naye ndi njila yabwino yoonetsela kuti mumasamala za ena .
Ngati wofeledwa akukuuzani zinazake , mvetselani bwinobwino .
Koposa zonse , mungacitile banja limene lili ndi cisoni zinthu zina , makamaka zimene silingakwanitse kucita . Zinthu monga kuphika cakudya , kusamalila ana , kapena kukonza pulogalamu yamalilo ngati n’zotheka .
M’kupita kwa nthawi , mungayambe kukamba za womwalilayo .
Mwacitsanzo , mungakambe za makhalidwe ake abwino , kapena zocitika zina zosangalatsa zokhudza iye .
Makambilano a conco , angathandize munthu wofeledwa kukhala wosangalala .
Mwacitsanzo , Pam , amene mwamuna wake anamwalila zaka 6 zapitazo anati : “ Nthawi zina , anthu amandiuza zinthu zabwino zimene mwamuna wanga Ian anali kucita , zimene sindinali kuzidziŵa .
Zimenezo zimandipangitsa kumva bwino . ” Ofufuza ena apeza kuti ofeledwa ambili amangolandila thandizo panthawi ya malilo yokha , koma m’kupita kwa nthawi amanyalanyazidwa , cifukwa anzao amakhala otangwanika ndi zocitika zina .
Conco , muziyesetsa kukamba ndi wofeledwa nthawi zonse kucokela pamene wokondedwa wao anamwalila .
* Ofeledwa ambili amayamikila mocokela pansi pamtima ngati mwakamba nao . Zimenezi zimacepetsa cisoni cao .
Ganizilani za Kaori , mtsikana wa Cijapanizi amene anakhumudwa kwambili amai ake atamwalila .
Patapita caka ndi miyezi itatu , mkulu wake nayenso anamwalila .
Koma zosangalatsa n’zakuti anzake okhulupilika anali kum’thandiza panthawi yovutayo .
Mai wina wacikulile dzina lake Ritsuko , anakhala mnzake wa pamtima wa Kaori .
Kaori anati : “ Kukamba zoona , sindinali wokondwa ndipo sindinali kufuna aliyense kuti akhale amai anga .
Koma cifukwa ca mmene a Ritsuko anali kucitila nane zinthu , ndinayamba kuwakonda kwambili .
Mlungu uliwonse , tinali kupitila limodzi mu ulaliki ndi ku misonkhano yacikristu .
Nthawi zambili anali kundiitana kuti tidzamwele tiyi pamodzi , kundibweletsela zakudya , ndiponso kundilembela makalata ndi makadi .
Cikondi cimene a Ritsuko anandionetsa cinandilimbikitsa kwambili . ”
Papita zaka 12 kucokela pamene amake Kaori anamwalila . Tsopano , iye ndi mwamuna wake ndi alaliki a nthawi zonse a Mau Mulungu .
Kaori anati : “ A Ritsuko amandikondabe mpaka pano .
Ndikabwelela kwathu , nthawi zonse ndimapita kukawaona , ndipo amandilimbikitsa kwambili . ”
Citsanzo cina ndi Poli , wa Mboni za Yehova wa m’dziko la Cyprus , amene anapindula ndi thandizo limene anali kulandila .
Mwamuna wa Poli dzina lake Sozos anali m’busa wacikristu wacitsanzo cabwino komanso wokoma mtima . Iye anali kuitana ana ndi akazi amasiye kunyumba kwao kuti adzaceze nao ndi kudya nao pamodzi .
( Yakobo 1 : 27 ) Zacisoni n’zakuti Sozos anapezeka ndi cotupa mu ubongo , ndipo anamwalila ali ndi zaka 53 .
Kumeneko , iye anapitiliza kusonkhana ndi mpingo wina wa Mboni za Yehova .
Poli anati : “ Mabwenzi a mumpingo watsopanowo sanali kudziŵa mavuto amene tinali kukumana nao .
Ngakhale n’conco , io sanaleke kutitonthoza ndi mau ao abwino komanso kutithandiza mwakuthupi .
Thandizo limenelo linali la mtengo wapatali makamaka pa nthawi imene mwana wanga anali kuyewa atate ake .
Anthu amene anali kutsogolela mumpingo anali kum’konda kwambili Daniel .
Mkulu wina mumpingowo , anali kuitana Daniel kuti adzaceze naye pamodzi ndi mabwenzi ena kapena kukachaya bola . ”
Masiku ano , Poli ndi mwana wake akusangalala .
Kukamba zoona , pali njila zambili za mmene tingatonthozele ndi kuthandizila anthu olila .
Baibulo nalonso limatitonthoza mwa kutipatsa ciyembekezo cabwino kwambili ca mtsogolo .
Ena amalemba pa kalenda tsiku limene munthuyo anamwalila , n’colinga cakuti azikumbukila kutonthoza ofeledwa pamene akufunikila citonthozo .
Kumbukilani kuti Gail amene tamuchula m’nkhani zapita zija , anakaikila ngati adzakwanitsa kupilila imfa ya mwamuna wake Rob .
Komabe , iye ali ndi ciyembekezo cakuti adzaonananso naye m’dziko latsopano la Mulungu .
Ndimacitila cifundo anthu amene okondedwa ao anamwalila , amenenso sadziŵa za ciyembekezo cakuti akufa adzaukitsidwa . ”
Posacedwapa , Mulungu adzaukitsa Yobu limodzi ndi ena ambili , dzikoli likadzakhala paladaiso .
( Luka 23 : 42 , 43 ) Lemba la Machitidwe 24 : 15 limatitsimikizila kuti : “ Kudzakhala kuuka . ”
Yesu nayenso akutitsimikizila kuti : “ Musadabwe nazo zimenezi , cifukwa idzafika nthawi pamene onse ali m’manda acikumbutso adzamva mau ake ndipo adzatuluka . ”
Iye adzakhalanso ndi ‘ mphamvu monga mmene analili pa unyamata wake , ’ ndipo ‘ mnofu wake udzasalala kuposa wa mwana . ’
( Yobu 33 : 24 , 25 ) Izi n’zimene zidzacitikila anthu amene amayamikila makonzedwe acikondi a Mulungu , akuti akufa adzakhalanso ndi moyo padziko lapansi .
Ngati munthu amene mumakonda anamwalila , mwina mukuona kuti mfundo zimene takambilanazi sizingathetseletu cisoni canu .
Koma kuganizila mozama malonjezo a Mulungu opezeka m’Baibulo , kudzakuthandizani kukhala ndi ciyembekezo komanso mphamvu zakuti mupilile cisoni . — 1 Atesalonika 4 : 13 .
Kodi mufuna kudziŵa zambili zokhudza zimene mungacite kuti mupilile cisoni canu ?
Kapena kodi mufuna kupeza mayankho a mafunso monga lakuti “ N’cifukwa ciani Mulungu amalolela kuti anthu azivutika ? ”
Pitani pa webusaiti yathu ya jw.org kuti mupeze mayankho otonthoza ndi othandiza a m’Baibulo .
ZINA ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA
“ Mulungu . . . adzapukuta misozi yonse m’maso mwao , ndipo imfa sidzakhalaponso . ” — Chivumbulutso 21 : 3 , 4 .
Nsanja ya Mlonda iyi ifotokoza mmene Mulungu adzakwanilitsila lonjezo limeneli ndi mmene mudzapindulila .
NKHANI YA PACIKUTO | N’CIFUKWA CIANI YESU ANAVUTIKA NDI KUTIFELA ?
Mu 33 C.E . , Yesu wa ku Nazareti anaphedwa .
Iye anapatsidwa mlandu wabodza woukila boma , anamenyedwa mwankhanza , ndipo anakhomeledwa pamtengo .
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa , ndipo patapita masiku 40 Yesu anabwelela kumwamba .
Zocitika zapadela zimenezi zinalembedwa m’mabuku anai a Uthenga Wabwino a m’Malemba Acigiliki Acikristu , amene amadziŵika kuti Cipangano Catsopano .
( 1 Akorinto 15 : 14 ) Komabe , ngati zinthuzo zinacitikadi , ndiye kuti anthu ali ndi tsogolo labwino kwambili , limene inu mungauzeko ena .
Koma kodi nkhani za m’Mauthenga Abwino zinacitika kapena sizinacitike ?
Mosiyana ndi nthano zabodza , nkhani za m’Mauthenga Abwino zinafufuzidwa mosamala ndi kulembedwa molondola .
Mwacitsanzo , zimachula maina a malo enieni , ndipo ambili mwa malo amenewa anthu angapite kukawaona masiku ano .
Cina , zimafotokoza anthu enieni , ndipo akatswili olemba mbili yakale amacitila umboni kuti anthuwo analikodi . — Luka 3 : 1 , 2 , 23 .
Olemba ena a m’nthawi ya atumwi komanso a m’zaka za m’ma 100 C.E . , anachulapo za Yesu .
Kuonjezela apo , zocitika zimene analemba ndi zofanana m’njila yakuti zinalembedwa molondola ndiponso mosapita m’mbali .
Iwo analembanso ngakhale zolakwa za ophunzila ena a Yesu .
( Mateyu 26 : 56 ; Luka 22 : 24 - 26 ; Yohane 18 : 10 , 11 ) Maumboni onsewa akuonetsa kuti olemba Mauthenga Abwino anali oona mtima , ndipo analemba zinthu zokhudza Yesu molondola kwambili .
Ngakhale kuti ambili amakhulupilila kuti Yesu anabweladi padziko lapansi kenako anaphedwa , ena amakaikila zakuti iye anaukitsidwa .
Atumwi ake naonso sanakhulupilile pamene anamva lipoti lakuti iye waukitsidwa .
( Luka 24 : 11 ) Komabe , pamene io ndi ophunzila ena anamuona Yesu woukitsidwayo panthawi zosiyanasiyana , m’pamene anakhulupilila .
Ndipo panthawi ina , Yesu anaonekela kwa anthu oposa 500 . — 1 Akorinto 15 : 6 .
Molimba mtima , ophunzila a Yesu analengeza za kuukitsidwa kwake kwa anthu ambili kuphatikizapo amene anamupha , ngakhale kuti kucita zimenezo kunaika moyo wao pangozi .
( Machitidwe 4 : 1 - 3 , 10 , 19 , 20 ; 5 : 27 - 32 ) Kodi ophunzila ambili akanalimba mtima conco zikanakhala kuti sanali otsimikiza mtima kuti Yesu anaukitsidwadi ?
Kukamba zoona , mfundo yakuti Yesu anaukitsidwadi ndi imene inacititsa kuti Cikristu cifalikile kwambili m’nthawi zakale ngakhale masiku ano .
Nkhani zokhudza imfa ya Yesu ndi kuukitsidwa kwake zolembedwa m’Mauthenga Abwino , ndi umboni wakuti nkhani zonse zofotokoza mbili yakale n’zoona .
Kuŵelenga nkhani zimenezi bwinobwino , kudzakuthandizani kukhulupilila kuti zinacitikadi .
Ndipo cikhulupililo canu cidzalimbanso mukamvetsetsa cifukwa cake zinthuzo zinacitika .
Ena mwa anthu amenewa ndi Tacitus , amene anabadwa mu 55 C.E . Iye analemba kuti Akristu anatengela dzinali kwa “ Kristu ” amene Pontiyo Pilato , mmodzi mwa olamulila athu , anamulamula kuti azunzidwe ndi kuphedwa mu ulamulilo wa mfumu Tiberiyo . ”
Enanso amene analemba za Yesu anali Suetonius , ( wa m’nthawi ya atumwi ) , wolemba mbili yakale waciyuda Josephus ( wa m’nthawi ya atumwi ) , ndi Pliny Wamng’ono amene anali bwanamkubwa wa ku Bituniya ( wa kumayambililo kwa zaka za m’ma 100 C.E ) .
( 1 Petulo 1 : 24 , 25 ) Ndiyeno , anthu ambili amene anali kutsutsa Yesu sakanalemba zinthu zimene zikanapangitsa anthu kukhulupilila Yesu .
Pankhani ya kuukitsidwa kwa Yesu , Petulo , amene anali mmodzi wa atumwi ake , anafotokoza kuti : “ Ameneyu Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu ndi kumulola kuonekela , osati kwa anthu onse , koma kwa mboni zoikidwilatu ndi Mulungu , zomwe ndi ife amene tinadya ndi kumwa naye limodzi atauka kwa akufa . ”
Uthenga Wabwino wa Mateyu umatiuza kuti pamene atsogoleli acipembedzo amene anali adani a Yesu anamva kuti iye waukitsidwa , io anapeza njila yothetsela kufalitsidwa kwa nkhani yakuti Yesu wauka . — Mateyu 28 : 11 - 15 .
Kodi izi zitanthauza kuti Yesu anali kufuna kuti nkhani yakuti iye anaukitsidwa isafalikile ?
Iyai . Petulo anapitiliza kufotokoza kuti : “ Anatilamula kuti tilalikile kwa anthu ndi kupeleka umboni wokwanila wakuti iyeyu ndi amene Mulungu anamuika kukhala woweluza anthu amoyo ndi akufa . ”
Akristu oona akhala akucita zimenezi kuyambila kale . — Machitidwe 10 : 42 .
‘ Ucimo unaloŵa m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi [ Adamu ] , ndi imfa kudzela mwa ucimo . ’ — Aroma 5 : 12
Mungayankhe bwanji mutafunsidwa kuti , “ Kodi mungakonde kukhala ndi moyo kwamuyaya ? ”
Anthu ambili angakambe kuti inde , koma amaona kuti zimenezo sizingacitike .
Iwo amakamba kuti anthufe tinalengedwa kuti tizifa .
Koma bwanji ngati akufunsani kuti , “ Kodi mwakonzekela kufa ? ”
Anthu ambili angakambe kuti iyai .
Baibulo limakamba kuti Mulungu analenga anthu ndi cifuno cokhala ndi moyo kwamuyaya .
Limakamba kuti “ [ iye ] anapatsa anthu mtima wofuna kukhala ndi moyo mpaka kalekale . ” — Mlaliki 3 : 11 .
Koma zoona zake n’zakuti anthu sakhala ndi moyo kwamuyaya .
Kodi Mulungu anacitapo ciliconse kuti akonze zinthu ?
Mayankho a m’Baibulo ndi okhazika mtima pansi , ndipo amaonetsa cifukwa cake Yesu anavutika ndi kufa .
Macaputala atatu oyambilila a buku la Genesis m’Baibulo , amatiuza kuti Mulungu anapatsa anthu oyambilila Adamu ndi Hava mwai wakuti akhale ndi moyo kwamuyaya .
Iye anawauza zimene anayenela kucita kuti akhale kwamuyaya .
Macaputala amenewa afotokoza kuti iwo sanamvele Mulungu ndipo anataya mwai umenewo . Anthu ambili amaona kuti nkhani imeneyo ndi nthano cabe .
Koma mofanana ndi mabuku a Uthenga Wabwino , zimene zinalembedwa m’buku la Genesis ponena za mbili yakale n’zoona .
Kodi n’ciani cinacitika pambuyo pakuti Adamu sanamvele Mulungu ?
Baibulo limayankha kuti : “ Monga mmene ucimo unaloŵela m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi [ Adamu ] ndi imfa kudzela mwa ucimo , imfayo n’kufalikila kwa anthu onse cifukwa onse anacimwa . ”
Zimenezi zinacititsa kuti ataye mwai wokhala ndi moyo kwamuyaya .
Patapita nthawi , iye anafa . Popeza ndife mbadwa zake , tinatengela ucimo kwa iye .
Kodi Mulungu anacitapo ciliconse kuti akonze zinthu ?
Mulungu anapanga makonzedwe akuti abwezeletse mwai wokhala ndi moyo kwamuyaya umene Adamu anataya kwa mbadwa zake .
M’Baibulo , pa Aroma 6 : 23 pamati : “ Malipilo a ucimo ndi imfa . ”
Zimenezi zitanthauza kuti ucimo umabweletsa imfa .
Mofananamo , ifenso ndife ocimwa ndipo timalandila malipilo a ucimo amene ndi imfa .
Conco , timabadwa ndi ucimo ngakhale kuti si mwakufuna kwathu .
Mwacikondi , Mulungu anatuma Mwana wake , Yesu , kudzatilipilila “ malipilo a ucimo . ”
Imfa ya Yesu inatsegula njila yodzakhala ndi moyo wacimwemwe komanso wamuyaya
Popeza munthu mmodzi wangwilo , Adamu , anabweletsa ucimo ndi imfa mwa kusamvela Mulungu , panafunikanso munthu wangwilo womvela mpaka imfa n’colinga cakuti atimasule ku ucimo .
Baibulo limafotokoza kuti : “ Monga mwa kusamvela kwa munthu mmodziyo , ambili anakhala ocimwa , momwemonso kudzela mwa kumvela kwa munthu mmodziyu , ambili adzakhala olungama . ”
Iye anacoka kumwamba , ndi kukhala munthu wangwilo * , kenako anatifela .
Pa cifukwa cimeneci , zinakhala zotheka kwa ife kuyesedwa olungama ndi kuima pamaso pa Mulungu , komanso kukhala ndi mwai wodzakhala ndi moyo kwamuyaya .
Nanga n’cifukwa ciani Yesu anafunika kufa ?
Kodi Mulungu Wamphamvuyonse sakanangopeleka lamulo lakuti mbadwa za Adamu zikhale kwamuyaya ?
Ngati kuti Mulungu sanaonetse cilungamo pankhaniyi , anthu akanaganiza kuti Mulungu sangacite zinthu mwacilungamo pankhani zinanso .
Mwacitsanzo , kodi cikanakhala cilungamo ngati akanasankha mbadwa zina za Adamu kuti zikhale kwamuyaya ?
Kodi anthu akanam’khulupilila kuti amasunga malonjezo ake ?
Cilungamo cimene Mulungu anatsatila kuti atipulumutse , cimatitsimikizila kuti iye amacita zinthu mwacilungamo nthawi zonse .
Cifukwa ca nsembe ya Yesu , Mulungu anatsegula mwai wodzakhala ndi moyo wosatha m’Paladaiso padziko lapansi .
Pa Yohane 3 : 16 Yesu anati : “ Mulungu anakonda kwambili dziko mwakuti anapeleka Mwana wake wobadwa yekha , kuti aliyense wokhulupilila iye asaonongeke , koma akhale ndi moyo wosatha . ”
Imfa ya Yesu simangoonetsa cilungamo ca Mulungu , koma imaonetsanso cikondi cacikulu cimene Mulungu ali naco pa anthu .
Nanga n’cifukwa ciani Yesu anavutika ndi kufa imfa yoŵaŵa monga mmene zinalembedwela m’Mauthenga Abwino ?
Mwa kukhalabe wokhulupilika pokumana ndi mavuto aakulu , Yesu anaonetselatu kuti zimene Mdyelekezi anakamba zakuti anthu sangakhale okhulupilika kwa Mulungu akakumana ndi , n’zabodza .
( Yobu 2 : 4 , 5 ) Zimene Satana anakamba zinaoneka monga n’zoona cifukwa poyamba anacititsa Adamu munthu wangwilo kucimwa .
Koma Yesu , amene anali wangwilo monga Adamu , anakhalabe womvela ngakhale kuti anavutika kwambili .
( 1 Akorinto 15 : 45 ) Motelo , iye anaonetsa kuti zinali zotheka kwa Adamu kusankha kumvela Mulungu .
Mwa kupilila pamene anali kuvutitsidwa , Yesu anatisiila citsanzo cakuti titsatile . (
1 Petulo 2 : 21 ) Mulungu anadalitsa Mwana wake cifukwa ca kumvela mwa kumuukitsila kumoyo wosafa , kumwamba .
Yesu anafotokoza zimene tifunika kucita pamene anati : “ Pakuti moyo wosatha adzaupeza akamaphunzila ndi kudziŵa za inu , Mulungu yekhayo amene ali woona , ndi za Yesu Kristu , amene inu munamutuma . ” — Yohane 17 : 3 .
Amene amafalitsa magazini ino akukupemphani kuti muphunzile zambili za Yehova , Mulungu woona , ndi za Mwana wake Yesu Kristu .
A Mboni za Yehova amene ali m’dela lanu ndi okonzeka kukuthandizani .
Mudzaphunzilanso zambili mukapita pa webusaiti yathu ya www.jw.org .
Onani nkhani yakuti “ The Historical Character of Genesis , ” m’buku lacingelezi la Insight on the Scriptures , pa tsamba 922 , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova .
Mulungu anasamutsa moyo wa mwana wake ndi kuuika m’mimba mwa Mariya , ndipo iye anakhala ndi pakati . Mzimu woyela wa Mulungu unateteza Yesu kuti asatengele kupanda ungwilo kwa Mariya . — Luka 1 : 31 , 35 .
Usiku wakuti aphedwa maŵa , Yesu anasonkhana pamodzi ndi atumwi ake okhulupilika , kenako anayambitsa Cikumbutso ca imfa yake .
Iye anawauza kuti : “ Muzicita zimenezi pondikumbukila . ”
( Luka 22 : 19 ) Pomvela lamulo limeneli , Mboni za Yehova padziko lonse zimasonkhana kamodzi pa caka kuti zikumbukile imfa ya Yesu .
Caka cino , Cikumbutso ca imfa ya Yesu cidzakhalako pa Citatu , March 23 , dzuŵa litaloŵa .
Simudzalipila ndalama iliyonse , ndipo sipadzayendetsedwa mbale ya ndalama .
Funsani a Mboni za Yehova a m’dela lanu kuti akuuzeni nthawi ndi malo kumene kudzakhalila cocitikaco .
Kapena pitani pa webusaiti yathu ya www.jw.org .
KODI MUMAONA KUTI Mdyelekezi ndi . . .
Maganizo oipa a munthu ?
Mdyelekezi anakamba ndi Yesu , ndi ‘ kumuyesa . ’
Poyamba , Satana anali mngelo wabwino , koma iye “ sanakhazikike m’coonadi . ”
( Yohane 8 : 44 ) Iye anakhala wabodza ndipo anapandukila Mulungu .
Angelo enanso anapanduka ndi kugwilizana ndi Satana . — Chivumbulutso 12 : 9 .
Mdyelekezi amacititsa anthu kuganiza kuti iye kulibe . ​ — 2 Akorinto 4 : 4 .
ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI zoti Mdyelekezi amalamulila anthu ndi nthano cabe , koma ena amaopa kugwidwa ndi ziŵanda .
“ Dziko lonse lili m’manja mwa woipayo . ”
( 1 Yohane 5 : 19 ) Mdyelekezi akusonkhezela anthu ambili kucita zoipa , koma sakulamulila anthu onse .
Mdyelekezi amagwilitsila nchito cinyengo kuti asokoneze anthu ambili . ​ — 2 Akorinto 11 : 14 .
Nthawi zina ziŵanda zimavutitsa anthu . ​ — Mateyu 12 : 22 .
Mothandizidwa ndi Yehova , mungathe ‘ kutsutsa Mdyelekezi . ’ ​ — Yakobo 4 : 7 .
Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 10 m’buku ili , Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova
1 : 16 .
Kodi njila yaikulu koposa imene Yehova waonetsela kukoma mtima kwakukulu kwa anthu ni iti ?
Tingaonetse bwanji kuti tsopano tikulamulidwa ndi kukoma mtima kwakukulu osati ucimo ?
Ni madalitso a bwanji amene timapeza cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova ?
1 , 2 . ( a ) Fotokozani fanizo la Yesu la mwini munda wa mpesa . ( b ) Kodi fanizoli liwonenetsa bwanji khalidwe la kuwolowa manja ndi kukoma mtima kwakukulu ?
Kodi n’kosaloleka kupatsa anchito anga onse malipilo amene nifuna ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 6 : 1 . )
N’cifukwa ciani Yehova anaonetsa anthu onse kukoma mtima kwakukulu ? Nanga anacita bwanji zimenezo ?
Kodi Malemba atanthauza ciani pamene akamba kuti Yehova wasonyeza kukoma mtima kwake kwakukulu “ m’njila zosiyanasiyana ? ”
Mtumwi Petulo analemba kuti : “ Molingana ndi mphatso imene aliyense walandila , igwilitseni nchito potumikilana monga oyang’anila abwino amene alandila kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu , kumene wakusonyeza m’njila zosiyanasiyana . ” ( 1 Pet .
Mtumwi Yohane analemba kuti : “ Tonsefe tinalandila zinthu kucokela pa zoculuka zimene ali nazo . Tinalandila kukoma mtima kwakukulu kosefukila . ” ( Yoh .
Timapindula bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova ? Nanga tingaonetse bwanji kuti timayamikila ?
( Ŵelengani 1 Yohane 1 : 8 , 9 . )
Ni mwayi wabwanji umene tili nawo cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
Mmene Mulungu waonetsela kukoma mtima kwake kwakukulu : Mwayi womvela uthenga wabwino ( Onani ndime 11 )
Kodi odzozedwa amathandiza bwanji a “ nkhosa zina ” kukhala olungama ?
Mphatso ya pemphelo ( Onani ndime 12 )
Kodi pemphelo ligwilizana bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
Tingapindule bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu “ pa nthawi imene tikufunika thandizo ” ?
Kodi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova kumatithandiza bwanji ?
Ni ciyembekezo ca bwanji cimene tili naco cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
( Ŵelengani Salimo 49 : 7 , 8 . )
Kodi Akhiristu ena akale ananyoza bwanji kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
Ni udindo wa bwanji umene tili nawo cifukwa ca kukoma mtima kwa Yehova ?
Kodi m’nkhani yotsatila tidzakambilana za udindo uti ?
[ 1 ] ( ndime 2 ) Onani mau akuti “ Kukoma mtima kwakukulu ” pa cigawo cakuti “ Matanthauzo a Mau Ena ” mu Baibulo la Dziko Latsopano .
20 : 24 .
Kodi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova kuyenela kutilimbikitsa kucita ciani ?
Kodi “ uthenga wabwino wa Ufumu ” umaonetsa bwanji kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
Kodi Yehova adzaonetsa bwanji kukoma mtima kwake kwakukulu m’dziko latsopano ?
Kodi mtumwi Paulo anaonetsa bwanji kuti anali kuyamikila kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
MOONA mtima , mtumwi Paulo anakamba kuti : “ Kukoma mtima kwake kwakukulu kumene [ Mulungu ] anandisonyeza sikunapite pacabe . ”
( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 9 , 10 . )
( Ŵelengani Aefeso 3 : 5 - 8 . )
N’cifukwa ciani tikamba kuti “ uthenga wabwino wa Ufumu ” n’cimodzi - modzi ndi uthenga wabwino wa “ kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ” ?
N’cifukwa ciani tingakambe kuti pamene tifotokozela anthu za dipo , ndiye kuti tilalikila uthenga wabwino wa kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ?
N’cifukwa ciani anthu ocimwa ayenela kugwilizana ndi Mulungu ?
Yohane anati : “ Iye wokhulupilila mwa Mwanayo ali nawo moyo wosatha . Wosamvela Mwanayo sadzauona moyowu , koma mkwiyo wa Mulungu ukhalabe pa iye . ” ( Yoh .
9 , 10 . ( a ) Ni udindo wa bwanji umene Khiristu anapatsa abale ake odzozedwa ?
Cotelo ndife akazembe m’malo mwa Khristu , ngati kuti Mulungu akucondelela anthu kudzela mwa ife .
N’cifukwa ciani anthu amakondwela akadziŵa kuti angapemphele kwa Yehova ?
Anthu ambili amapemphela kuti amveleko cabe bwino , koma sakhulupilila kuti Mulungu amayankha mapemphelo awo .
Iwo afunika kudziŵa kuti Yehova ni “ Wakumva pemphelo . ”
Wamasalimo Davide analemba kuti : “ Inu Wakumva pemphelo , anthu a mitundu yonse adzabwela kwa inu .
Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Ngati mutapempha ciliconse m’dzina langa , ine ndidzacicita . ” ( Yoh .
13 , 14 . ( a ) Ni udindo wapadela uti umene odzozedwa adzakhala nawo kutsogolo ?
( b ) Ni zinthu zabwino ziti zimene odzozedwa adzacitila anthu ?
Kodi Yehova adzaonetsa bwanji kukoma mtima kwake kwakukulu kwa “ nkhosa zina ” m’dziko latsopano ?
Anthu mamiliyoni ambili amene anamwalila akalibe kudziŵa Mulungu nawonso adzaukitsidwa .
Yohane analemba kuti : “ Ndinaona akufa , olemekezeka ndi onyozeka , ataimilila pamaso pa mpando wacifumuwo , ndipo mipukutu inafunyululidwa .
Koma mpukutu wina unafunyululidwa , ndiwo mpukutu wa moyo .
Ndipo akufa anaweluzidwa malinga ndi zolembedwa m’mipukutuyo , mogwilizana ndi nchito zawo .
Nyanja inapeleka akufa amene anali mmenemo . Nayonso imfa ndi Manda zinapeleka akufa amene anali mmenemo . Aliyense wa iwo anaweluzidwa malinga ndi nchito zake . ”
Kodi tiyenela kukumbukila ciani pamene tilalikila uthenga wabwino ?
Baibulo imati : “ Cilengedweco cidzamasulidwa ku ukapolo wa kuvunda n’kukhala ndi ufulu waulemelelo wa ana a Mulungu . ”
Anakambanso kuti : “ Lemba , pakuti mawu awa ndi odalilika ndi oona . ”
Kukamba zoona , pamene tilalikila uthenga wabwino umenewu kwa ena , timalemekeza Yehova cifukwa ca kukoma mtima kwake kwakukulu .
“ Pitilizani kufunafuna ufumu [ wa Mulungu ] , ndipo zinthu zimenezi zidzawonjezedwa kwa inu . ” — LUKA 12 : 31 .
Kodi zimene timafunikila mu umoyo zimasiyana bwanji ndi zimene timalakalaka ?
N’cifukwa ciani sitiyenela kufuna zinthu zambili zakuthupi ?
N’cifukwa ciani mumakhulupilila kuti Yehova adzakupatsani zinthu zofunikila mu umoyo ?
Kodi Satana amaseŵenzetsa bwanji “ cilakolako ca maso ” ?
Musaiŵale kuti mtumwi Yohane anapeleka cenjezo lakuti : “ Dziko likupita limodzi ndi cilakolako cake . ”
Kodi anthu amene amacita khama kuti akhale ndi zinthu zambili amakumana ndi mavuto ya bwanji ?
Nanga n’cifukwa ciani ?
8 , 9 . ( a ) N’cifukwa ciani sitiyenela kudela nkhawa kwambili zinthu zofunikila mu umoyo ?
( b ) N’ciani cimene Yesu anali kudziŵa ponena za anthu ndi zinthu zimene amafunikila ?
Pophunzitsa ophunzila ake kupemphela , kodi Yesu anakamba kuti n’ciani ciyenela kukhala cofunika kwambili ?
Tiphunzila ciani tikaganizila mmene Yehova amasamalila mbalame ?
‘ Tizionetsetsa mbalame zam’mlengalenga . ’
( Sal . 147 : 9 ) Sikuti amacita kutenga zakudya ndi kuziika mkamwa mwa mbalame iyayi .
N’ciani cionetsa kuti ndife ofunika kwambili kuposa mbalame ?
( Yelekezelani ndi Luka 12 : 6 , 7 . )
15 , 16 . ( a ) Tiphunzilapo ciani tikaganizila mmene Yehova amasamalila maluwa ?
( Onani cithunzi kuciyambi kwa nkhani ino . ) ( b ) Ni funso liti limene tingadzifunse ? Cifukwa ?
N’ciani cimene Yehova amadziŵa cokhudza aliyense wa ife ? Nanga adzaticitila ciani ?
N’cifukwa ciani sitiyenela kudela nkhawa za kutsogolo ?
Mungacite ciani kuti mukhale na umoyo wosafuna zambili kuti muike patsogolo zinthu za Ufumu ?
( a ) Ni zolinga za bwanji zimene mungasankhe potumikila Yehova ?
( b ) Mungacite ciani kuti mucepetseko zocita mu umoyo wanu ?
N’ciani cingatithandize kuti Yehova akhale bwenzi lathu ?
Fotokozani citsanzo cimene cionetsa kufunika kodziŵa nthawi imene tikukhalamo ndi zimene zikucitika .
N’cifukwa ciani Yesu anauza ophunzila ake kuti ‘ akhalebe maso ’ ?
( Mat . 24 : 3 ; ŵelengani Maliko 13 : 32 - 37 . )
( a ) N’cifukwa ciani tikhulupilila kuti Yesu adziŵa tsiku la Aramagedo ?
( b ) Ngakhale kuti sitidziŵa tsiku limene cisautso cacikulu cidzayamba , kodi tiyenela kutsimikiza za ciani ?
Pamene Yesu anali pa dziko lapansi , anati : “ Kunena za tsikulo ndi ola lake , palibe amene akudziŵa , ngakhale angelo akumwamba kapenanso Mwana , koma Atate yekha . ” ( Mat .
( Ŵelengani Habakuku 2 : 1 - 3 . )
Fotokozani citsanzo coonetsa kuti maulosi a Yehova amakwanilitsika panthawi yake .
Maulosi a Yehova amakwanilitsika panthawi yake .
( Agal . 3 : 17 , 18 ) Patapita nthawi , Yehova anauza Abulahamu kuti : “ Udziŵe ndithu kuti mbewu yako idzakhala mlendo m’dziko la eni , ndipo idzatumikila eni dzikolo . Iwo adzasautsa mbewu yako kwa zaka 400 . ” ( Gen .
Patapita zaka zambili anakumbutsa anthu zimene zinacitika .
7 , 8 . ( a ) Kodi kale alonda anali ndi nchito yanji ? Nanga tiphunzilapo ciani ?
( b ) Fotokozani citsanzo ca zimene zingacitike ngati mlonda wagona pa nchito .
Kodi anthu ambili masiku ano sadziŵa ciani ?
10 , 11 . ( a ) N’ciani cimene tiyenela kusamala naco ?
Cifukwa ? ( b ) N’ciani cimakucititsani kutsimikiza kuti Mdyelekezi wacititsa anthu kunyalanyaza ulosi wa m’Baibulo ?
N’cifukwa ciani sitiyenela kulola kuti Mdyelekezi atinamize ?
( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 1 - 6 . )
Yesu anaticenjezanso kuti : “ Khalani okonzeka , cifukwa pa ola limene simukuliganizila , Mwana wa munthu adzafika . ”
Kodi mzimu wa dziko umawakhudza bwanji anthu ?
Ni cenjezo ya bwanji imene ili pa Luka 21 : 34 , 35 ?
( Ŵelengani Luka 21 : 34 , 35 . )
N’ciani cinacitikila Petulo , Yakobo , ndi Yohane ? Nanga zimenezo zingaticitikile bwanji ?
Mogwilizana ndi lemba la Luka 21 : 36 , kodi Yesu anatilangiza kucitanji ?
Tingacite ciani kuti tikhale okonzekela zimene zidzacitika posacedwapa ?
[ 1 ] ( ndime 14 ) Onani Nkhani 21 m’buku lakuti Ufumu wa Mulungu Ukulamulila .
Ndikulimbitsa . Ndithu ndikuthandiza .
Pa msonkhano wadela , m’bale wina ananifunsa ngati ningakonde kulalikila .
Titapita m’gawo , ananipatsa tumabuku tokamba za Ufumu wa Mulungu .
Pamene n’nayendako , mlongo wina anayamba kuphunzitsa ife ana nkhani za m’Baibulo poseŵezetsa buku lakuti Zeze wa Mulungu .
Kucokela nili mwana , napeza cimwemwe cifukwa copatsa mwa kuuzako ena ciyembekezo copezeka m’Mau a Mulungu .
N’nauza m’baleyo kuti , “ Mbuzi iyo . ” M’baleyo anaimitsa njinga yake ndi kunipempha kuti tikhale pansi pamalo ena ake .
Iye ananifunsa kuti : “ Ndani anakupatsa mphamvu zoweluza anthu kuti ni mbuzi ?
Udziŵa , nchito yathu n’kuuza anthu uthenga wabwino koma kuweluza n’kwa Yehova . ”
M’bale wina wacikulile ananiphunzitsa kuti nthawi zina kupeza cimwemwe kumafuna kupilila .
N’zoonekelatu kuti apa Mulungu anadalitsa m’baleyo cifukwa cokhala woleza mtima .
Pambuyo pa nkhondo , n’napita kukacita upainiya kum’mwela kwa dziko la Ireland kwa zaka ziŵili .
Iwo anacititsanso kuti ticotsedwe m’nyumba zimene tinali kukhala .
Popeza n’nali n’kalibe kukwelapo boti n’nakondwela kwambili .
Kwa zaka 5 tinalalikila kwambili pa zisumbu za kutali kumene kunalibe Mboni .
Anzanga amene n’nali kucita nawo umishonale titakwela boti ( kucokela kumanzele kupita kulamanja ) Ron Parkin , Dick Ryde , Gust Maki , ndi Stanley Carter
Nthawi zambili anali kutipatsa nsomba , makotapela , na nshawa .
Zinali zokondweletsa kuona kuti anthuwo abwela kudzamvela nkhani .
Zinali zosangalatsa kwambili kuona mmene ena anakwanilitsila bwino udindo wawo .
Titafika kumeneko n’nakumana ndi Maxine Boyd , mlongo wokongola amene anali m’mishonale .
Motelo , n’naziuza kuti : ‘ Ronald , ngati umufunadi mtsikanayu , ufunika kucitapo kanthu mwamsanga . ’
Pambuyo pa milungu itatu ninam’funa , ndipo patapita milungu 6 tinamanga banja .
Ndiyeno anatituma kukacita umishonale ku Puerto Rico . Conco , sin’nabwelele nawo anzangawo ndi boti yatsopano .
Mwacitsanzo , m’mudzi wina wa Potela Pastillo munali mabanja aŵili a Mboni amene anali ndi ana ambili ndipo n’nali kukonda kuwalizila citolilo .
N’nafunsa kamtsikana kena , dzina lake Hilda , ngati kangakonde kukalalikila nafe .
Tinakagulila nsapato ndipo kanapita nafe mu ulaliki .
Mlongoyo anali pafupi kupita ku Ecuador kukatumikila monga m’mishonale . Anatifunsa kuti : “ Kodi mwanikumbukila ?
Ndine uja mtsikana wa ku mudzi wa Pastillo amene munagulila nsapato . ”
Johnson ndi mkazi wake ndiwo anali Mboni zoyamba m’dziko la Dominican Republic .
M’bale Nathan Knorr , amene anali kutsogolela gulu la Yehova panthawiyo , anabwela ku Puerto Rico .
Ngakhale conco , anakhumudwa ndi kunipatsa uphungu wamphamvu . Anakamba kuti sinicita zinthu mwadongosolo .
Pamene ine ndi Amayi tinali kuphunzila coonadi , atate anali kukana .
Mu 2011 , wokondedwa wanga Maxine anamwalila .
Nikuyembekezela mwacidwi kudzamuonanso akadzaukitsidwa .
Zaka 60 zimene n’nakhala pa cisumbu , n’nayamba kudziona kuti ndine wa ku Puerto Rico monga kacule ka kumeneko kamene kamakhala m’mitengo kochedwa coqui .
Ena amene amanifikila amafuna kuti niwathandize pamavuto aumwini kapena a m’banja .
Koma cofunika ni kuganizila cifukwa cake zimene ucita n’zofunika kwambili .
24 : 45 ) Tili ndi mwayi wotamanda Yehova kulikonse kumene tingakhale .
Mbili ya m’bale Leonard Smith ili mu Nsanja ya Olonda ya April 15 , 2012 .
N’cifukwa ciani tinganene kuti cikwati ni mphatso yocokela kwa Mulungu ?
Kodi vikwati vinali bwanji kucokela pa Adamu kudzafika m’nthawi ya Yesu ?
N’ciani cingathandize Mkhiristu kusankha kukwatila kapena kusakwatila ?
1 , 2 . ( a ) Kodi cikwati cinayamba kwanji ?
( b ) N’ciani cimene mwamuna ndi mkazi oyamba anazindikila ponena za cikwati ?
( Ŵelengani Genesis 2 : 20 - 24 . )
2 : 18 ) Cifuno cina cacikulu ca cikwati cinali kubala ana kuti padziko lapansi pakhale anthu .
Malinga ndi mmene Adamu na Hava anayankhila kwa Yehova , kodi tiphunzilapo ciani ?
Kodi mungalifotokoze bwanji lemba la Genesis 3 : 15 ?
( a ) Kodi nkhani ya cikwati yakhala ikuyenda bwanji kuyambila pa cipanduko ca Adamu na Hava ?
( b ) Nanga Baibulo imawalangizanji amuna ndi akazi ali pabanja ?
Kodi vikwati vinali bwanji kucokela pa Adamu kudzafika pa Cigumula ca Nowa ?
Kodi Yehova anacita nawo bwanji anthu oipa m’masiku a Nowa ? Ndipo titengapo punzilo lanji pa zimene zinacitikazo ?
( a ) Ni makhalidwe oipa ati amene anafala kwa anthu ambili ?
( b ) Nanga Abulahamu na Sara anapeleka bwanji citsanzo cabwino m’cikwati cawo ?
( Ŵelengani 1 Petulo 3 : 3 - 6 . )
Kodi Cilamulo ca Mose cinawateteza bwanji Aisiraeli ?
( Ŵelengani Deuteronomo 7 : 3 , 4 . )
12 , 13 . ( a ) M’masiku a Malaki , kodi azimuna ena anali kuwacitila motani akazi awo ?
( b ) Ngati masiku ano munthu wobatizika athaŵitsana ndi mkazi kapena mwamuna wa mwiniwake , kodi pamakhala zotsatilapo zanji ?
( a ) Kodi lamulo lokhudza cikwati mu mpingo wacikhiristu n’lakuti ciani ?
Ndiyeno anawonjezela kuti : “ Koma ngati sangathe kudziletsa , akwatile , pakuti ndi bwino kukwatila kusiyana ndi kuvutika ndi chilakolako . ”
18 , 19 . ( a ) Kodi cikwati cacikhiristu ciyenela kuyamba bwanji ?
( b ) Nanga tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Kodi Mulungu anapeleka maudindo anji kwa mwamuna ndi m’kazi m’banja ?
N’cifukwa ninji cikondi komanso tumacitidwe tokopana n’tofunika m’cikwati ?
Pakaoneka mavuto m’cikwati , kodi Baibulo ingathandize bwanji ?
Ngakale kuti cikwati cimayamba ndi cisangalalo , kodi omanga banja ayenela kuyembekezela ciani ?
Baibulo imagogomeza kufunika kwa cikondi .
Kodi cikondi m’cikwati ciyenela kukhala camphamvu bwanji ?
Paulo analemba kuti : “ Amuna inu , pitilizani kukonda akazi anu monga mmene Khiristu anakondela mpingo n’kudzipeleka yekha cifukwa ca mpingowo . ” ( Aef .
Ŵelengani Yohane 13 : 34 , 35 ; 15 : 12 , 13 . )
4 , 5 . ( a ) Monga mutu , kodi mwamuna afunika kucita mbali yanji m’banja ?
( b ) Nanga mkazi ayenela kukaona bwanji kakonzedwe ka umutu ?
( c ) Kodi a m’cikwati ena anapanga masinthidwe otani ?
Koma kukwatiwa kunanisintha , cifukwa n’nafunika kuzoloŵela kudalila mwamuna wanga .
Cinali cotivuta poyamba , koma tsopano cikondi cathu catiphunzitsa kucita zinthu m’njila ya Yehova . ”
Ndiye kukhala aŵili kunangowonjezela vutolo .
Koma kupempha citsogozo kwa Yehova , ndi kumvetsela maganizo a mkazi wanga , kwathandiza kucepetsa vutolo .
Nimamva kuti mkazi wanga alidi mcilikizi wanga ! ”
Kodi cikondi cimakhala bwanji ‘ cogwilizanitsa camphamvu ’ mukabuka mavuto m’banja ?
7 , 8 . ( a ) Kodi Baibulo imalangiza ciani pa nkhani ya kucipinda ?
( b ) N’cifukwa ninji a m’cikwati afunika kumaonetsana cikondano cawo ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 3 - 5 . )
Ifunika izicitika mwacibadwa . N’zoona kuti kaŵili - kaŵili thupi la mwamuna ndilo limatsogola .
N’cifukwa ciani tifunika kupewa kaleya koceza mokopana ndi munthu amene sitili naye pabanja ?
10 , 11 . ( a ) Kodi kusudzulana n’kofala bwanji ?
( b ) Nanga Baibulo imati ciani za kupatukana ?
( c ) N’ciani cingathandize wa m’cikwati kusaganiza msanga zopatukana ?
N’ciani cingapangitse wa m’cikwati kuganiza zopatukana ?
Kodi Baibulo imati ciani kwa Akhiristu amene anzawo a m’cikwati satumikila Yehova ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 12 - 14 . )
Kapena mwamunawe , udziŵa bwanji , mwina ungapulumutse mkazi wako ? ”
15 , 16 . ( a ) Kodi Baibulo imapeleka uphungu wanji kwa akazi acikhiristu amene amuna awo si Mboni ?
( b ) Nanga Mkhiristu angacite bwanji ‘ ngati wosakhulupililayo asankha kucoka ’ ?
Mtumwi Petulo analangiza akazi acikhiristu kugonjela amuna awo . Anati “ ngati ali osamvela mawu akopeke , osati ndi mawu , koma ndi khalidwe lanu , poona okha ndi maso awo khalidwe lanu loyela ndi ulemu wanu waukulu . ”
Koma bwanji ngati wosakhulupilila asankha kupatukana ?
Baibulo imati : “ Ngati wosakhulupililayo wacoka , acoke . M’bale kapena mlongo sakhala womangika zinthu zikatelo , koma Mulungu anakuitanani kuti mukhale mu mtendele . ” ( 1 Akor .
N’ciani cimene Akhiristu ali pabanja ayenela kuika patsogolo ?
N’cifukwa ciani n’zotheka Akhiristu kukhala ndi cikwati cacimwemwe ndi copambana ?
[ 1 ] ( ndime 5 ) Maina asinthidwa .
[ 2 ] ( ndime 13 ) Onani kamutu kakuti “ Zimene Baibo Imanena pa Kulekana ndi Kupatukana , ” m’buku yakuti “ Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu , ” masa . 219 - 221 .
Kukamba zoona , kulalikila m’maŵa m’mbali mwa mtsinje wa Danube kumakondweletsa kwambili !
Ofalitsa akulalikila mokondwela uthenga wa Ufumu kwa munthu wacidwi m’tawuni ya Vigadó mu Budapest ku Hungary
Mungacite ciani kuti mupite patsogolo kuuzimu ?
Mungacite ciani kuti musafooke pamene muyesetsa kupita patsogolo ?
Mungacite ciani kuti muzilalikila mwaluso ?
1 , 2 . ( a ) Kodi lemba la Yesaya 60 : 22 lakwanilitsika bwanji masiku ano ?
( b ) Kodi m’gulu la Yehova la padziko lapansi mufunika ciani ?
“ WAMNG’ONO adzasanduka anthu 1000 , ndipo ocepa adzasanduka mtundu wamphamvu . ”
Kupita patsogolo kuuzimu kumatanthauza ciani ?
Ni zinthu ziti zimene acicepele angacite kuti acilikize nchito ya Ufumu ?
6 - 8 . ( a ) Kodi wacicepele wina anacita ciani kuti ayambe kuona zinthu zakuuzimu moyenelela ?
( b ) Tingacite ciani kuti ‘ tilawe ndi kuona kuti Yehova ni wabwino ?
Nikayang’ana madalitso amene napeza , nimayamikila kwambili Mulungu cakuti nimapitiliza kucita zambili mu utumiki wake .
( Ŵelengani Salimo 34 : 8 - 10 . )
N’cifukwa ciani mufunika ‘ kuyembekezela moleza mtima ’ ?
Ni makhalidwe abwino ati amene tifunika kukhala nawo ? Nanga n’cifukwa ciani ni ofunika ?
Kodi anthu mumpingo angaonetse bwanji kuti ni okhulupilika ?
Mungatsatile bwanji citsanzo ca Yosefe ngati ena akucitilani zoipa ?
Mumacita ciani ngati anthu ena akucitilani zinthu zoipa ?
14 , 15 . ( a ) N’cifukwa ciani tifunika ‘ kusamala nthawi zonse ’ ndi kalalikidwe kathu ?
( b ) N’cifukwa ciani nthawi zina mungafunikile kusintha njila yolalikilila ?
( Onani cithunzi kuciyambi kwa nkhani ino , ndi bokosi yakuti “ Kodi Mumayesako Kulalikila M’njila Zina ? ” )
Kodi tingalalikile bwanji mwaluso mu ulaliki wapoyela ?
17 , 18 . ( a ) N’ciani cingakuthandizeni kukhala ndi cidalilo mu ulaliki wapoyela ?
( b ) N’cifukwa ciani mzimu wa Davide wotamanda Yehova ni wothandiza pamene tili mu ulaliki ?
Iye anati : “ Pakulambila kwa pabanja , ndinali kufufuza ndi mkazi wanga m’zofalitsa zathu kuti tipeze mfundo zoyankhila anthu pa zimene amakhulupilila kapena amene amatsutsa .
Timapemphanso malingalilo kwa Mboni zinzathu . ”
( Ŵelengani 1 Timoteyo 4 : 15 . )
Iwo adzanena za ulemelelo wa ufumu wanu . Ndi kulankhula za mphamvu zanu , Kuti ana a anthu adziŵe za nchito zanu zamphamvu Ndi kukula kwa ulemelelo wa ufumu wanu . ” ( Sal .
Kodi anthu ena angapindule bwanji ngati mwapita patsogolo m’gulu la Yehova ?
Lomba Venecia amati : “ Ulaliki wa pa foni ni wothandiza . ”
Mkazi wanga anamwalila zaka zitatu zapita , ndipo mwana wanga anafa pangozi caka catha . ”
Papita zaka ziŵili tsopano , ndipo nalemba kalata ino kuti nikuuzeni kuti ndine mlongo wanu wakuuzimu . ”
N’cifukwa ciani tiyenela kuthandiza anthu amene timaphunzila nawo Baibulo kuti azikonda kucita phunzilo laumwini ?
Tingathandize bwanji acatsopano kuti azimasuka kukambilana ndi anthu mu ulaliki ?
N’cifukwa ciani tiyenela kuyesetsa kuphunzitsa ena kuti ayenelele kuŵeta gulu la nkhosa za Mulungu ?
N’cifukwa ciani tifunika kuphunzitsa ena kuti akwanilitse utumiki wawo ?
3 , 4 . ( a ) Kodi Paulo anagwilizanitsa bwanji kuphunzila Baibulo ndi kubala zipatso mu ulaliki ?
( b ) Tiyenela kucita ciani coyamba tikalibe kulimbikitsa ophunzila Baibulo kuti azicita phunzilo laumwini ?
Pelekani malingalilo a mmene mungathandizile acatsopano kukhala na cizoloŵezi cocita phunzilo laumwini .
Dzifunseni kuti , ‘ Ningaphunzitse bwanji wophunzila Baibulo kuti azicita phunzilo laumwini nthawi zonse ? ’
Mungamulimbikitse kuti aziŵelenga magazini iliyonse yatsopano ya Nsanja ya Mlonda ndi Galamukani !
( a ) Mungathandize bwanji wophunzila wanu kuti azikonda kuŵelenga Baibulo ?
( b ) Kodi wophunzila Baibulo adzapindula bwanji ngati wayamba kukonda kuŵelenga Baibulo ?
Kodi Yesu anaphunzitsa bwanji atumwi ake kulalikila ?
8 , 9 . ( a ) Kodi Yesu anali kukambilana nawo bwanji anthu mu ulaliki ?
( b ) Tingathandize bwanji acatsopano kuti azikambilana ndi anthu mu ulaliki monga mmene Yesu anacitila ?
10 - 12 . ( a ) Kodi Yesu anakulitsa bwanji cidwi ca anthu mu ulaliki ?
( b ) Tingathandize bwanji ofalitsa atsopano kuwonjezela luso lawo ?
13 , 14 . ( a ) Muphunzilapo ciani mukaganizila zitsanzo za m’Baibulo za anthu amene anadzipeleka kuti athandize ena ?
( b ) Mungathandize bwanji ofalitsa atsopano komanso acicepele kuti adzikonda abale ndi alongo ?
( Mat . 20 : 28 ) Dorika “ anali kucita nchito zabwino zambili , ndi kupeleka mphatso zacifundo zoculuka . ” ( Mac .
N’cifukwa ciani akulu ayenela kuyesetsa kuthandiza abale kupita patsogolo mumpingo ?
16 , 17 . ( a ) N’ciani cimene Paulo anacita kuti athandize Timoteyo kupita patsogolo ?
( b ) Kodi akulu angaphunzitse bwanji abale kuti ayenelele kukhala akulu mumpingo ?
N’cifukwa ciani kuphunzitsa ena n’kofunika kwambili ?
N’cifukwa ciani tingakhale otsimikiza mtima kuti khama lathu pophunzitsa ena mu utumiki wa Yehova silizapita pacabe ?
Amandipembedza pacabe , cifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati ziphunzitso za Mulungu . ’
Mumanyalanyaza malamulo a Mulungu , ndi kuumilila mwambo wa anthu . ” — Maliko 7 : 6 - 8 .
3 “ Manja Anu Asakhale Olefuka ”
Kodi Mulungu amatiphunzitsa bwanji kulimbana ndi adani athu ?
Amatiphunzitsanso mwa zofalitsa zophunzilila Baibulo , misonkhano ya mpingo , ya dela , ndi ya cigawo .
Tiyenela kucita ciani kuti tisagonje ku coipa ?
( b ) Tidzakambilana za anthu ati ochulidwa m’Baibulo ?
N’ciani cinathandiza Yakobo kucilimika ?
( Ŵelengani Genesis 32 : 24 - 28 . )
N’ciani cinathandiza wacicepele ndi mlongo wina kugonjetsa zilakolako zoipa ?
Wacicepeleyo anati : “ Pa cifukwa cimeneci , niona kuti n’zotheka kukhala wokhulupilika tsiku lililonse .
Niyamikila Yehova kwambili cifukwa coseŵenzetsa gulu lake kutipatsa malangizo othandiza kuti tikhale osiyana ndi dziko loipali . ”
Ganizilani citsanzo cina ca mlongo wa ku America .
Iye analemba kuti : “ Nikuyamikilani cifukwa copitiliza kutipatsa malangizo amene tifunikila panthawi yake .
Nthawi zambili , nimaona kuti nkhani ngati zimenezi amalembela ine .
Kwa zaka zambili , nakhala nikulimbana ndi cizoloŵezi coipa cimene Yehova amadana naco .
Nthawi zina , nimangofuna kuleka kumenya nkhondoyo .
Nidziŵa kuti Yehova ni wacifundo ndipo amakhululukila . Koma cifukwa cakuti nikulimbanabe na cizoloŵezi coipa cimeneci ndipo sinisintha , nimaona kuti siningalandile thandizo lake .
Vuto limeneli lakhudza kwambili umoyo wanga . . .
Pambuyo poŵelenga nkhani yakuti ‘ Kodi Muli Ndi “ Mtima Wodziŵa ” Yehova ? ’
mu Nsanja ya Olonda ya March 15 , 2013 , n’naonadi kuti Yehova afuna kunithandiza . ”
( a ) Kodi Paulo anamvela bwanji polimbana ndi zilakolako zoipa ?
Tiphunzilapo ciani pa malamulo amene Mulungu anapatsa Aisiraeli pa nkhani ya mavalidwe ?
N’ciani cimene cingathandize Akhiristu kusankha bwino zovala ?
Ni pa nthawi iti maka - maka pamene tifunika kuvala moyenelela ?
( 1 Tim . 2 : 10 ) Komabe , mavalidwe amene angakhale oyenela kwina angakhale osayenela kumalo ena .
( Ŵelengani 1 Akorinto 10 : 32 , 33 . )
N’ciani cingathandize m’bale kudziŵa ngati n’koyenela kuti azisunga ndevu kapena ayi ?
Cilamulo ca Mose cinalamula amuna kusunga ndevu .
Komanso , sikulepheletsa anthu kumvela uthenga wa Ufumu .
Ndipo abale ena a maudindo amasunga ndevu .
Kodi mavalidwe athu na mmene timadzikonzela afunika kupangitsa anthu kutiona bwanji ?
M’bale wacicepele ku Germany analemba kuti : “ Matica kusukulu kwathu amaona kuti nkhani za m’Baibulo ni nthano cabe .
Ndipo amangoona ngati ana a sukulu onse amakhulupilila za cisanduliko . ”
Mlongo wacicepele ku France anati : “ Matica kusukulu kwathu amadabwa ngako akamvela kuti pakali ana a sukulu amene amakhulupilila Baibulo . ”
na kakuti The Origin of Life — Five Questions Worth Asking , na buku yakuti Is There a Creator Who Cares About You ?
Natuŵelenga nthawi zambili . ”
Zimaonetsa kuti , ngakhale kuti akatswili opanga zinthu ali na luso lapatali , safikako olo pang’ono kwa amene anapanga zacilengedwe . ”
N’cifukwa ciani Mulungu amafuna kuti acicepele aziseŵenzetsa luso la kuganiza ?
( Ŵelengani Aroma 12 : 1 , 2 ; 1 Timoteyo 2 : 4 . )
Ambili a iwo anakhalako pa nthawi zosiyana - siyana ndipo sanali kudziŵana . ”
N’naganizilapo kwambili za cakudya ca Pasika cokambidwa m’maulosi . ”
( 2 Sam . 12 : 1 - 14 ; Maliko 14 : 50 ) M’bale wacicepele ku Britain anati : “ Kuona mtima kwa conco n’kosoŵa kwambili .
Ni umboni wakuti Baibulo inacokeladi kwa Yehova . ”
( Ŵelengani Salimo 19 : 7 - 11 . )
Wacicepele wina ku Japan analemba kuti : “ Pamene tinayamba kutsatila mfundo za m’Baibulo m’banja mwathu , timakhala acimwemwe kwambili .
Timakhala amtendele , ogwilizana , ndi okondana . ”
Palinso amene amaleka kukhulupilila Mulungu cifukwa cokhumudwa na zocitika za cipembedzo .
Ngakhale kamoyo kakang’ono - ng’ono , moyo wake ni wocolowana modabwitsa kwambili . ”
Iye anati : “ Nyumba iliyonse inamangidwa ndi winawake , koma amene anapanga zinthu zonse ndi Mulungu . ” ( Aheb .
N’cifukwa ninji mufunika kuwadziŵa bwino ana anu ?
Ana athu afunika kucikulitsa pang’ono - pang’ono . ”
Amanifunsa kuti : ‘ Baibulo imati ciani ? ’
‘ Kodi ukhulupilila zimene ikamba ? ’
Amafuna kuti n’ziyankha m’mau anga - anga , osati kungotengela iwo kapena amayi .
Popeza tsopano nikukula , nimayankha mofikapo . ”
Anayankha mafunso anga onse kucokela m’Baibulo . ”
( Ŵelengani Deuteronomo 6 : 5 - 8 ; Luka 6 : 45 . )
Conco , ngati amati moyo unasandulika kucokela ku twamoyo tung’ono - ng’ono tosacolowana kufika ku zamoyo zikulu - zikulu zocolowana , n’cifukwa ciani twamoyo twamakedzanato tunali tocolowana kale kwambili ?
Mfundoyi inanigwila mtima cakuti n’nauzako mwana wanga . ”
Ndiyeno anapempha kuti mwana aliyense am’pangile khofi .
“ Aliyense anacita khama kwambili , ” anatelo mayiyo .
“ N’tawafunsa kuti n’cifukwa ciani anacita mosamala conco , aliyense anati anafuna kuti anipangile khofi yabwino mmene nimaikondela .
Ndiyeno n’nawauza kuti ni mmenenso Mulungu naye anacitila khama posakaniza bwino mipweya yopanga cifungadziko ( atmosphere ) kuti tikhalepo na moyo pa dziko lapansi . ”
Ndipo n’ciani cimacita congo pouluka , mbalame kapena ndeke ?
Conco , uganiza wanzelu kwambili n’ndani , wopanga ndeke olo amene anapanga mbalame ? ”
( Ŵelengani Salimo 1 : 1 - 3 . )
Tate wina anati : “ Osalema kuyesa njila zatsopano pokambilana nkhani za m’Baibulo . ”
Anawonjezela kuti : “ Kuyambila ali ana , n’nali kuphunzila nawo kwa mphindi 15 cabe tsiku lililonse , kupatulapo masiku osonkhana .
Koma m’kupita kwa nthawi , mafunso anga ambili anayankhidwa pa misonkhano , pa kulambila kwa pabanja kapena pocita phunzilo laumwini .
Ndiye cifukwa cake makolo safunika kuleka kuphunzitsa ana awo . ”
Ana anu aziona kuti Yehova ni weni - weni kwa inu .
Amalimbikitsanso ana awo kumapemphela pawokha .
Anati : “ Timauzanso mtsikana wathu wamkulu kuti ‘ Uzidalila Yehova , osada nkhawa kwambili , uziika patsogolo zinthu za Ufumu . ’
Akaona kuti zimenezi zamuthandiza , amadziŵa kuti Yehova ali nafe .
Nkhani yoyamba ionetsa mmene cikhulupililo cingakulile na kukhalabe colimba .
Lekani nifotokoze cimene cinayambitsa makambilano amenewa .
N’NABADWA pa 10 December mu 1936 , ku Wichita ku Kansas mu America . Ndine woyamba pa ana 4 .
Ndiyeno panafika msilikali , ndipo dokota ameneyo anakuwa kuuza msilikali kuti , “ Cigwile ici cimunthu ca mantha ! ”
Msilikaliyo anazindikila kuti dokotayo anali woledzela , conco anamuuza kuti “ Yenda kunyumba ukhale bwino coyamba ! ”
Iwo anali ndi ma babashopu aŵili m’tauni ya Wichita ndipo dokota ameneyo anali kasitoma wawo .
Pamene n’nali na zaka 8 , makolo anga anagulitsa nyumba na mashopu awo , n’kupanga nyumba yamawilo ( kalavani ) imene tinali kuyenda nayo .
Ndi dalitso la Yehova pamodzi na khama lawo panchito yolalikila , anakhazikitsa mpingo .
M’baleyo ananigulitsilanso motoka ija pamtengo wa madola 25 .
Tinatumidwa kukacita upainiya wapadela ku tauni ya Walnut Ridge ku Arkansas .
Mu 1962 , tinakondwela kwambili titaitanidwa ku sukulu ya Giliyadi ya namba 37 .
Tili mu ulaliki na Mary ndi Chris Kanaiya
Ndiyeno , mwana wathu woyamba wamkazi Kimberly anabadwa . Patapita miyezi 17 , Stephany anabadwa .
Tinalinso kuyenda nawo kumalo okaceza ndi kukagona m’matenti , tikumaceza pootha moto .
Tinapanga makonzedwe akuti atumiki ena a nthawi zonse tiziwalandilako kunyumba kwathu .
Anawo anadabwa kwambili ndipo anayamba kulila na kukamba kuti afuna tiphunzile .
Kukamba zoona , tinakondwela maningi onse aŵili atayamba upainiya pambuyo potsiliza sukulu .
Paulendo wina , Kimberly anakumana ndi mnzake wa Paul dzina lake Brian Llewellyn .
Conco , anakhaladi mbeta mpaka atakwanitsa zaka 23 .
Panthawi imodzi - modzi , Brian na Kimberly anaitanidwa kukatumikila pa Beteli ya ku London .
Tsiku lotsatila , pambuyo popita ku Likulu la Maphunzilo la Watchtower ku Patterson , Linda anatuma foni kutiuza kuti Amayi amwalila .
Ndiyeno , tinayenda kuphunzitsa ku Zimbabwe ndi ku Zambia .
Ndiyeno mu 2006 , Brian na Kimberly anabwela kuno kudzalela ana awo akazi aŵili , Mackenzie na Elizabeth .
Koma Paul na Stephany akali ku Malawi kumene Paul akutumikila mu Komiti ya Nthambi .
N’cifukwa ciani tingafunike kusintha mmene timaonela alendo ?
N’tacoka ku eyapoti , n’namvela kuzizila kumene sin’nakumvelepo cibadwile cakuti ninayamba kulila . ”
6 : 1 ) Pofuna kuthetsa vuto limeneli , atumwi anasankha amuna 7 okatsimikizila kuti aliyense asanyalanyazidwe .
1 : 22 ) Kaya tidziŵa kapena ayi , kaonedwe kathu ka zinthu kamasonkhezeledwa ndi cikhalidwe ca kwathu .
( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 22 . )
7 : 12 ) Muzicita zinthu moleza mtima ndi anthu amene akuyesetsa kuzoloŵela dziko lacilendo .
Poyamba , sitingamvetsetse mmene amaganizila ndi mmene amacitila zinthu .
N’citsanzo citi cimene alendo angatengele poonetsa ulemu ndi kuyamikila ?
Coyamba , iye analemekeza miyambo ya m’dziko lacilendo , mwa kupempha cilolezo kuti akunkhe tiligu .
[ 1 ] ( ndime 1 ) Dzina talisintha .
14 : 6 ) Kodi ndinu mmodzi wa anthu amene akuphunzila cinenelo cina ?
( Ŵelengani Nehemiya 13 : 23 , 24 . )
( b ) Zimenezi zingatheke bwanji ?
1 : 9 , 10 ) Kumbukilani kuti nthawi zambili pokonzekela ulaliki , misonkhano kapena nkhani , sitingaganizile mmene mfundozo zikhudzila umoyo wathu .
Popeza nimaika maganizo pa kudziŵa cinenelo , zimene nimaŵelenga sizinifika pamtima .
Ndiye cifukwa cake nimapatula nthawi yophunzila Baibo ndi zofalitsa zina m’cinenelo ca kwathu . ”
“ Sanali kukondwela kulalikila m’cinenelo cina , koma kale anali kukondwela kulalikila m’cinenelo cathu Cifulenci , ” anatelo Muriel .
“ Titaona kuti zimenezi zikupangitsa mwana wathu kusapita patsogolo kuuzimu , tinaganiza zobwelela kumpingo wakale , ” anafotokoza conco Serge .
Muzionetsetsa kuti coonadi cikufika pamtima pa ana anu ( Onani ndime 14 , 15 )
Koma timakonzekela ulaliki ndi kucita maseŵela ena m’Cilingala kuti ana athu aziphunzila cinenelo uku akusangalala . ”
Yesetsani kudziŵa cinenelo ca kumaloko ndi kuyankhapo pamisonkhano ( Onani ndime 16 , 17 )
Tinapanganso zoti tizipezeka pa misonkhano ya Cifulenci kamodzi pa mwezi . Tikakhala pa holide timapezelapo mwayi wopita kumisonkhano yacigawo ya m’cinenelo cathu . ”
( Ŵelengani Aroma 15 : 1 , 2 . )
Tingaonetse bwanji kuti timakonda Mau a Mulungu ?
Abale ali m’gawo la malonda , ndipo alalikila makanika pamalo okonzela mamotoka .
( Ŵelengani Chivumbulutso 21 : 3 - 6 . )
N’ciani cinathandiza Abulahamu na banja lake kukhalabe na cikhulupililo colimba ?
( Ŵelengani 1 Yohane 5 : 14 , 15 . )
Ni mayeselo ati amene aneneli ena anapilila cifukwa ca cikhulupililo cawo ?
Enanso monga Eliya , “ anayenda uku ndi uku m’zipululu , m’mapili , m’mapanga , ndi m’maenje a dziko lapansi . ”
Kodi citsanzo ca Nowa citithandiza bwanji kumvetsa zimene kukhala na cikhulupililo kumatanthauza ?
Tingaonetse bwanji kuti tili na cikhulupililo ?
Kodi Aheberi 11 : 1 imafotokoza cikhulupililo m’njila ziŵili ziti ?
Waonatu kuti cikhulupililo cake cinayendela limodzi ndi nchito zake , ndipo mwa nchito zakezo cikhulupililo cakeco cinakhala cangwilo . ”
Mwacitsanzo , Yohane anati : “ Iye wokhulupilila mwa Mwanayo ali nawo moyo wosatha . Wosamvela Mwanayo sadzauona moyowu , koma mkwiyo wa Mulungu ukhalabe pa iye . ” ( Yoh .
Cofunika kwambili n’citi pakati pa cikondi na cikhulupililo ?
( 1 Pet . 1 : 8 ) Ngakhale Yakobo anafunsa abale ake odzozedwa kuti : “ Mulungu anasankha anthu amene ali osauka m’dzikoli kuti akhale olemela m’cikhulupililo ndi olandila colowa ca ufumu umene anaulonjeza kwa omukonda , sanatelo kodi ? ” ( Yak .
Aroma anali kulanga aliyense amene waphwanya malamulo na kubweletsa msokonezo .
Aroma anapatsa mphamvu atsogoleli a ndale kuti aziyang’anila zocitika mumzinda wawo .
Tumizani ndalamazo pamodzi na kalata yokamba kuti n’zobweleketsa .
N’lonjezo liti limene Yehova anapatsa anthu ake ?
Nanga n’cifukwa ciani lonjezoli linali locititsa cidwi ?
Conco , zioneka kuti anthu a Yehova sanaloŵe mu ukapolo kwa Babulo Wamkulu mu 1918 .
( Ŵelengani 1 Petulo 2 : 9 , 10 . )
( Ŵelengani Mateyu 13 : 24 , 25 , 37 - 39 . )
Kodi zinali zotheka kuti Akhiristu oona akamasuke ndi kulambila Mulungu mwaufulu ?
Kodi odzozedwa anamasulidwa liti kucoka m’Babulo wamkulu ?
Ndiyeno , M’bale Rutherford anatipempha kulinganiza misonkhano m’mizinda ingapo ya kumadzulo kwa America ndi kutumiza alankhuli kuti akalimbikitse abale athu .
13 : 15 .
Nimalila nthawi zambili , ndipo nimangoleka kukamba nawo .
Pamene n’namuuza mmene n’nali kumvelela anamvetsela mwacifundo .
Ndiyeno ananikumbutsa zinthu zabwino zimene n’nali kucita .
Ananikumbutsanso mau a Yesu akuti , aliyense wa ife ni wofunika kuposa mbalame zambili zampheta .
Nthawi zonse nikakumbukila lembali , nimalimbikitsika kwambili .
Tingaphunzilenji tikaona mmene Yehova , Yesu na Paulo anali kulimbikitsila ena ?
( Ŵelengani Mlaliki 4 : 9 , 10 . )
Tiphunzilapo ciani tikaona mmene Yesu anacitila ndi atumwi ake ?
Iye anayenda - yenda m’madela akumeneko ndi kulimbikitsa ophunzila ndi mawu ambili , kenako anafika ku Girisi . ’
( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 12 , 13 . )
Tikafunika cilimbikitso , timawatenga n’kumaŵelenga .
7 : 8 - 11 ) Andreas amene alela ana aŵili anati : “ Kulimbikitsa ana kumawathandiza kukula kuuzimu na m’nzelu .
Koma cimene cimawathandiza kucita cabwino nthawi zonse ni cilimbikitso cathu cosalekeza . ”
( Ŵelengani Luka 21 : 1 - 4 ; 2 Akorinto 8 : 12 . )
( Ŵelengani Chivumbulutso 2 : 18 , 19 . )
Dziŵani kuti pamene munali kukamba mokoma mtima pa pulatifomu , ndi pokamba na ine mwacindunji , n’naona kuti ni mphatso yocokela kwa Yehova . ”
[ 1 ] ( palagilafu 1 ) Maina ena tawasintha .
( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani ino ?
15 : 6 ) Amuna a m’bungwe lolamulila ndi owathandiza anali kupeleka uphungu na malangizo kwa Akhiristu kupitila m’makalata ouzilidwa .
( Ŵelengani 3 Yohane 9 , 10 . )
( Ŵelengani Mateyu 5 : 23 , 24 ; 18 : 15 - 17 . )
3 : 8 ) Izi zinathandiza abale ndi alongo amenewo kucita zambili m’nchito yolalikila .
Baibo imatilangiza kuti tizipezeka ku misonkhano nthawi zonse .
Kodi mumaiseŵenzetsa webusaiti yathu mu ulaliki ndi pa kulambila kwanu kwa pabanja ?
kapena kukambilana naye bulosha yakuti Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano ?
Tili na zifukwa ziti zoyamikilila Yehova ?
Ha , tili na zifukwa zambili cotani nanga zoyamikilila Yehova !
Idzaonetsanso mmene tingapindulile na ciyembekezo codzalandila mphoto .
Panthawiyo n’nali na zaka 8 cabe .
Atate anali kuletsa amayi kuniuzako zimene anali kuphunzila .
Koma popeza n’nali na cidwi , n’nali kufunsa mafunso . Conco anali kuphunzila nane atate akacokapo .
Pa cifukwa cimeneci , inenso n’nafuna kudzipeleka kwa Yehova .
Ndiye amayi ananiuza kuti nikakambe na mtumiki woyendela ( amene lomba timati woyang’anila dela ) .
Ananiuza kuti , “ Kulekelanji ! ”
Patapita miyezi inayi , n’nasankha m’bale wina kukhala mnzanga wocita naye upainiya .
Amayi nawo ndi mlongo wina anakacitila upainiya ku mpingo wina .
Mu 1951 , n’nalemba fomu yofunsila Sukulu ya Giliyadi .
Nili m’ndendemo , n’nalandila ciitano ca sukulu ya Giliyadi ya namba 22 .
Ndiyeno n’nakwela sitima yopita ku South Lansing ku New York , kumene kunali sukuluyo .
Nili na Janet pa cisumbu cina ku Philippines
Tikali kutumikila pa ofesi ya nthambi ku Quezon City
Kodi mungapeze bwanji “ mtendele wa Mulungu ” ?
Nanga mpingo ungakuthandizeni bwanji kucepetsa nkhawa zanu ?
( Onani pikica pamwambapa . ) ( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani ino ?
5 : 7 ) Koma kodi tingacite bwanji zimenezi ?
Wamasalimo anacondelela Yehova kuti : “ Inu Mulungu , mvetselani pemphelo langa . ”
N’cifukwa ciani pemphelo n’lofunika tikakhala na nkhawa ?
( Ŵelengani Mateyu 11 : 28 - 30 . )
Kodi Yesu anatanthauza ciani pamene anati : “ Musamade nkhawa ” ?
Tsiku lililonse limakhala kale na mavuto ake .
Kodi mufunika kucita ciani na nkhawa zakumbuyo ?
55 : 2 - 5 ) Koma sanalole nkhawa kumutayitsa cidalilo cake mwa Yehova .
Baibo imati : “ Nkhawa mumtima mwa munthu ndi imene imauwelamitsa , koma mau abwino ndi amene amausangalatsa . ”
10 : 24 , 25 ) ‘ Kulimbikitsana ’ kumeneku kudzakupatsani mphamvu mwauzimu , ndipo mudzakwanitsa kulimbana na nkhawa iliyonse . — Aroma 1 : 12 .
( a ) Tingam’tulile bwanji nkhawa zathu Mulungu ?
Tingatsimikize bwanji kuti Yehova amapeleka mphoto kwa atumiki ake ?
Kodi Yehova anadalitsa bwanji atumiki ake kumbuyoku ?
1 , 2 . ( a ) Kodi cikondi na cikhulupililo n’zogwilizana bwanji ? (
Kodi ciyembekezo codzalandila mphoto cimatithandiza bwanji ?
Yesu anati ophunzila ake adzafupidwa pa kudzimana kwawo ( Onani palagilafu 5 )
Mtumwi Petulo anafunsa Yesu kuti : “ Ife tasiya zinthu zonse ndi kukutsatilani , kodi tidzapeza ciani ? ”
Pa Ulaliki wa pa Phili , Yesu anati : “ Kondwelani , dumphani ndi cimwemwe , cifukwa mphoto yanu ndi yaikulu kumwamba , pakuti umu ndi mmenenso anazunzila aneneli amene analipo inu musanakhaleko . ”
Mose anauza mtundu wa Isiraeli kuti : “ Yehova adzakudalitsa ndithu m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa kuti likhale colowa cako . Adzakudalitsa ngati udzamveladi mau a Yehova Mulungu wako ndi kutsatiladi malamulo onsewa amene ndikukupatsa lelo .
Yehova Mulungu wako adzakudalitsa ndithu monga mmene anakulonjezela . ”
Waciŵiliyo anamucha Efuraimu , cifukwa anati , ‘ Mulungu wandipatsa ana m’dziko la masautso anga . ’ ”
Mau a Mulungu amati : “ Cifukwa ca cimwemwe cimene anamuikila patsogolo pake , anapilila mtengo wozunzikilapo .
Komanso , Atate wake anamuyanja na kumuonjezela maudindo osililika .
Kodi Yehova amamvela bwanji pa zimene timacita kaamba ka iye ?
“ Wokomela mtima munthu wonyozeka akukongoza Yehova , ndipo adzam’bwezela zimene anacitazo . ”
Kodi timapeza citonthozo canji pa 1 Yohane 3 : 19 , 20 ?
( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 19 , 20 . )
Ni madalitso ena ati amene tili nawo kale ?
Kodi atumiki a Yehova amamvela bwanji na madalitso amene amalandila ?
Mwacitsanzo , Bianca wa ku Germany anati : “ Nicita kusoŵa mau oyamikilila Yehova ponithandiza pa nkhawa zanga , na kunicilikiza tsiku ndi tsiku .
Kunja kuli msokonezeko wokha - wokha m’dziko .
Koma potumikila moyandikana na Yehova , nimamva kukhala wotetezeka m’manja mwake .
Pamene nidzimana zinthu pom’tumikila , m’pamenenso iye amaniwonjezela madalitso . ”
Kuti nizikumbukila mfundo zonilimbikitsa , nimalemba m’kabuku malemba na mfundo za m’zofalitsa zathu kuti niziyang’anamo .
Nimakaitana kuti ‘ Cithandizo ca Panthawi Yake . ’
Tikasumika maganizo pa malonjezo a Yehova , mavuto amaoneka kuti ni a kanthawi cabe .
Yehova ni wokonzeka kutithandiza nthawi zonse , olo tikumane na mavuto abwanji . ”
Komabe , mukhoza kuganizila njila zimene Yehova wakudalitsilani imwe na anthu ena .
Kodi Paulo na anthu ena anamasulidwa bwanji ku ucimo ndi imfa ?
( Ŵelengani Aroma 6 : 1 , 2 . )
N’cosankha canji cimene aliyense wa ife afunika kupanga ?
( Ŵelengani Aroma 7 : 21 - 23 . )
( Ŵelengani Miyambo 14 : 5 ; Aefeso 4 : 25 . )
Iwo amalandila “ mzimu ” monga amene ‘ akudikila . . . kuti atengedwe kukhala ana a Mulungu , . . . kuti atuluke m’matupi [ awo a nyama ] . ’
( Ŵelengani Aroma 4 : 20 - 22 . )
( Ŵelengani Machitidwe 18 : 2 - 4 ; 20 : 20 , 21 , 34 , 35 . )
Anthu ambili okaona malo amapita ku mzinda wa Aveiro , kumpoto kwa dziko la Portugal , kukaona maiŵe a mcele .
Mboni za kumaloko zimatengela mwayi kulalikila uthenga wabwino kwa anthu ogulitsa mcele kumeneko
Mfundo zina zimene Baibo imakamba
“ Olungama adzalandila dziko lapansi , ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya . ” — Salimo 37 : 29 .
M’nkhani iyi , tidzaona mmene tingagwilitsile nchito mphatso yathu ya ufulu wosankha m’njila yokondweletsa Mulungu .
Nkhani yoyamba , idzafotokoza tanthauza la kudzicipetsa ndi zimene sikutanthauza .
Kodi Yehova amafuna kuti tiziseŵenzetsa bwanji maluso athu ?
4 : 10 ) N’zoonekelatu kuti Yehova amafuna tizicita zinthu zopindulitsa ife ndi anthu ena .
Nowa anali kukhala m’dziko ‘ lodzala ndi ciwawa ’ ndi zaciwelewele .
Kuletsa nchito yathu ( Onani palagilafu 6 mpaka 9 )
6 , 7 . ( a ) N’ciani cimene Nowa sakanakwanitsa kucita ?
( b ) Nanga n’zofanana bwanji kwa ifenso ?
Ifenso tikukhala m’dziko lodzala ndi zoipa , ndipo tidziŵa kuti Yehova adzaliwononga .
( 1 Yoh . 2 : 17 ) Sitingakakamize anthu kulandila “ uthenga wabwino wa Ufumu . ”
Zimene Nowa anakwanitsa kucita : M’malo molefuka ndi zimene sakanakwanitsa kucita , Nowa anasumika maganizo pa zimene anakwanitsa kucita .
( Maliko 4 : 22 ) Koma pamene linaululika , kodi Davide anacita ciani ?
Macimo akale ( Onani palagilafu 11 mpaka 14 )
11 , 12 . ( a ) Sakanakwanitsa kucita ciani Davide ?
Zimene Davide sakanakwanitsa kucita : Kwa Davide , inali nkhani ya madzi akatayika sayoleka , sakanatha kuzibwezela m’mbuyo .
12 : 10 - 12 , 14 ) Conco , anafunika kukhulupilila kuti ngati alapa , Yehova adzam’khululukila , ndi kum’thandiza kupilila zotulukapo zimenezo .
8 : 1 - 3 ) Anafunikila kusiya nkhaniyo m’manja mwa Yehova .
Citsanzo ni m’bale Malcolm , amene anakhalabe wokhulupilika mpaka imfa yake mu 2015 .
Sumika maganizo pa zimene ungakwanitse , osati zimene sungakwanitse . ”
( b ) Nanga imwe pa canu , lidzakuthandizani bwanji lembali mu umoyo wanu ?
Lemba lathu la caka ca 2017 : “ Khulupilila Yehova ndipo cita zabwino . ”
Nanga tingalemekeze bwanji ufulu wa ena pa zimene amasankha ?
Ndidzawakonda mwa kufuna kwanga . ”
4 , 5 . ( a ) Ndani anali woyamba kupatsidwako mphatso ya ufulu wosankha zocita ?
( b ) Aliyense afunika kudzifunsa funso liti ?
Yankho la funso limeneli lingakhudze tsogolo lathu lonse .
Mulungu “ anayamba kuzibweletsa kwa munthuyo , kuti ciliconse aciche dzina . ”
Tipeweletu kucita ciani ndi mphatso yathu yosankha zocita ?
Yelekezani kuti munapatsa mnzanu mphatso yodula kwambili .
Monga Akhiristu , tingapewe bwanji kuseŵenzetsa molakwa ufulu wathu ?
( Ŵelengani 1 Petulo 2 : 16 . )
Munthu amene akuyenda alibe ulamulilo wowongolela mapazi ake . ”
Tiphunzilanji pa mfundo ya pa Agalatiya 6 : 5 ?
Kumbukani mfundo ya pa Agalatiya 6 : 5 .
Mudzacita ciani poonetsa kuti mumayamikila mphatso ya ufulu wosankha zocita ?
( a ) Kodi anthu ambili amakuona bwanji kudzicepetsa ?
Ndipo kudzicepetsa n’ciani maka - maka ?
N’cifukwa ciani tiyenela kupewa kuganizila molakwa zolinga za ena ?
Tingaphunzilenji kwa Yesu utumiki wathu ukasintha ?
( Ŵelengani Agalatiya 6 : 4 , 5 . )
( Ŵelengani Miyambo 3 : 5 , 6 . )
( Ŵelengani Mlaliki 11 : 4 - 6 . )
N’ciani cidzatithandiza kukhalabe wodzicepetsa kwamuyaya ?
N’cifukwa ciani cimakhala covuta kwa ena kugaŵilako ena maudindo ?
Anauza Natani kuuza Davide kuti : “ Si iwe amene udzandimangila nyumba yokhalamo . ”
( Ŵelengani Numeri 11 : 24 - 29 . )
Ayi usatelo . Ndikanakonda anthu onse a Yehova akanakhala aneneli , cifukwa Yehova akanaika mzimu wake pa iwo ! ”
( Ŵelengani Afilipi 2 : 20 - 22 . )
Ofesi ya nthambi inatitumizila magazini ogaŵila mu ulaliki okwana 800 .
N’nali kuphunzitsa m’mizinda ya Manaus , Belém , Fortaleza , Recife , ndi Salvador .
Mu August 1964 , tinafika mumzinda wa Lisbon , ku Portugal .
Ndilo gulu lokha limene likugwila nchito imene Yesu analamula ophunzila ake kucita — yolalikila uthenga wabwino wokamba za Ufumu wa Mulungu . ”
Pamene nkhani ino inali kulembedwa kuti ifalitsidwe , m’bale Douglas Guest anamwalila pa 25 October , 2015 ali wokhulupilika kwa Yehova .
( Ŵelengani Yesaya 63 : 11 - 14 . )
( Ower . 6 : 34 ) Ndipo “ mzimu wa Yehova unayamba kugwila nchito pa Davide . ”
N’cifukwa ciani Mulungu anafuna kuti anthu ake azilemekeza atsogoleli mu Isiraeli ?
( Ŵelengani Aheberi 1 : 7 , 14 . )
Baibo imachula Cilamulo cimene cinapatsidwa kwa Aisiraeli kuti “ Cilamulo ca Mose . ”
11 , 12 . ( a ) Kodi Yoswa ndi mafumu olamulila anthu a Mulungu anafunika kucita ciani ?
“ Mfumuyo itangomva mau a m’buku la cilamulolo , nthawi yomweyo inang’amba zovala zake . ”
N’cifukwa ciani Yehova anali kulanga atsogoleli ena a anthu ake ?
Nthawi zina , Yehova anali kuwalanga kapena kusankha wina kuti atsogolele .
N’ciani cionetsa kuti mzimu woyela unalimbitsa Yesu ?
Patangopita nthawi yocepa Yesu atabatizika , “ kunabwela angelo ndi kuyamba kum’tumikila . ”
( Mat . 4 : 11 ) Kutatsala maola ocepa kuti Yesu aphedwe , “ mngelo wocokela kumwamba anaonekela kwa iye ndi kumulimbikitsa . ”
Kodi Mau a Mulungu anatsogolela bwanji umoyo wa Yesu ndi ziphunzitso zake ?
Amandipembedza pacabe , cifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati ziphunzitso za Mulungu . ” ( Mat .
Palibe wabwino , koma Mulungu yekha . ”
“ Nthawi yomweyo mngelo wa Yehova anamukantha , cifukwa sanapeleke ulemelelo kwa Mulungu . Ndipo anadyedwa ndi mphutsi n’kumwalila . ” ( Mac .
Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
M’nkhani yotsatila tidzakambilana mayankho a mafunso amenewa .
Umenewu uyenela kuti unali mpukutu woyambilila wolembedwa ndi Mose .
1 : 15 - 26 ) N’cifukwa ciani cosankha cimeneci cinali cofunika kwambili kwa iwo ndi kwa Yehova ?
Pokhala bungwe lolamulila , anali kupeleka malangizo ku mipingo yonse . — Mac . 15 : 2 .
5 , 6 . ( a ) Kodi mzimu woyela unali kugwila bwanji nchito pa bungwe lolamulila ?
( c ) Kodi Mau a Mulungu anatsogolela bwanji bungwe lolamulila ?
Cifukwa coyamba n’cakuti mzimu woyela unali kugwila nchito pa bungwe lolamulila .
5 : 19 , 20 ) Cacitatu , Mau a Mulungu anatsogolela bungwe lolamulila .
N’cifukwa ciani tingati Yesu anali kutsogolela Akhiristu oyambilila ?
( a ) Ni liti pamene Yesu anasankha “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ” ?
Mu 1919 , apo n’kuti papita zaka zitatu pamene m’bale Russell anamwalila , Yesu anasankha “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu . ”
6 : 4 ) Nsanja ya Mlonda ya July 1 , 2013 inafotokoza kuti “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ” ni kagulu kocepa ka abale odzozedwa amene amapanga Bungwe Lolamulila .
Conco , kodi tingaliyankhe bwanji funso la Yesu lakuti : “ Ndani kweni - kweni amene ali kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ? ” ( Mat .
Kodi mzimu woyela wathandiza bwanji Bungwe Lolamulila ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 10 . )
Ni njila imodzi iti imene tingakumbukile Bungwe Lolamulila ?
N’cifukwa ciani ndimwe ofunitsitsa kutsatila Mtsogoleli wathu , Yesu ?
Pamene Yesu anabwelela kumwamba , sanaiŵale otsatila ake . ( Mat .
Posacedwa , adzatitsogolela ku moyo wamuyaya .
Kuyambila mu 1955 , bungwe limenelo lakhala likuchedwa kuti Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania .
Yehova “ amatitonthoza m’masautso athu onse ”
“ Ineyo ndalankhula ndipo ndidzazicita .
1 , 2 . ( a ) Kodi Yehova anatidziŵitsa ciani ?
MAU oyamba m’Baibo ali ndi mfundo yosavuta kumvetsa koma yofunika yakuti : “ Pa ciyambi , Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi . ”
( c ) Nanga tidzakambilana mafunso ati ?
N’cifukwa ciani nsembe ya dipo la Yesu ndiye inatsegula khomo kuti colinga ca Mulungu cikwanilitsike ?
Ni mphatso zina ziti zimene Yehova anapatsa Adamu ndi Hava ?
Zinali ngati kuti iye akukamba kuti : ‘ Kodi simungacite zimene mufuna ? ’
Koma Yehova ni wokhulupilika ku malamulo ake , ndipo sawaphwanya olo pang’ono .
( Ŵelengani Deuteronomo 32 : 4 , 5 . )
N’cifukwa ciani dipo ni mphatso ya mtengo wapatali ?
Yehova anapeleka dipo ya mtengo wapatali . ( 1 Pet .
Ni liti pamene Yehova adzakhala “ zinthu zonse kwa aliyense ” ?
( Ŵelengani Salimo 40 : 8 - 10 . )
Nanga ise tingaonetse bwanji kuti timaikonda dzina la Yehova ?
( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 15 , 16 . )
N’cifukwa ciani Yehova angatione olungama ngakhale kuti ndise ocimwa ?
Iye amalandila anthu amene adzipeleka kwa iye kukhala alambili ake .
Kodi Yesu anatanthauza ciani pamene anapempha kuti : “ Cifunilo canu cicitike ” ?
Kodi dipo limapindulitsa bwanji anthu amene anafa ?
Kodi Mulungu ali nalo colinga canji “ khamu lalikulu ” ?
( a ) Ni madalitso anji amene timalandila kwa Yehova ?
( Ŵelengani Machitidwe 3 : 19 - 21 . )
( Mal . 3 : 6 ) Yehova anatipatsa zinthu zambili osati cabe mphatso ya moyo .
Baibo imati : “ Tikudziŵa ndipo tikukhulupilila za cikondi cimene Mulungu ali naco kwa ife . ”
Kodi m’poyenela nthawi zina kusintha zosankha zimene tinapanga kale ?
M’nkhani imeneyi tidzapeza mayankho a mafunso amenewa .
Ngakhale n’conco , Yehova anaona kuti mafumuwo anali na mtima wathunthu .
Nanga bwanji ife ? Kodi Mulungu adzaona kuti tili na mtima wathunthu ngakhale kuti nthawi zina timalakwa ?
Tinali kukhala pa famu yaing’ono kum’maŵa kwa South Dakota .
Nchito yaikulu imene tinali kugwila pa banja lathu ni yaulimi , koma sikuti ndiyo inali nchito yofunika kwambili pa umoyo wathu .
Makolo anga anabatizika n’kukhala Mboni za Yehova mu 1934 .
Atate , dzina lawo a Clarence , ndi akulu awo , a Alfred , onse anatumikilapo monga mtumiki wa mpingo ( tsopano mgwilizanitsi wa bungwe la akulu ) mu mpingo wathu waung’ono ku Conde , m’dela la South Dakota .
Ine ndi mlongo wanga , Dorothy , tinakhala ofalitsa uthenga wa Ufumu pamene tinali na zaka 6 .
Tinali kukondanso kupezeka pa misonkhano yadela ndi yacigawo .
Baibo imati : “ Munthu woyenda ndi anthu anzelu adzakhala wanzelu . ”
Nthawi zina akamatumikila mipingo ya pafupi ndi kwathu , anali kunipempha kuti nipite nawo mu ulaliki .
Naimilila pa galimoto ya pa famu , nitangofika kumene ku Beteli
Pa famu ya ku Staten Island panali nyumba ya wailesi ya Mboni yochedwa WBBR .
Pa famuyo panali kuseŵenzela atumiki a pa Beteli okwana cabe 15 mpaka 20 .
Ambili amene tinali kumeneko tinali acicepele ndi osadziŵa zambili .
M’baleyu anali kugwila mokhulupilika nchito yake pa Beteli , koma sanali kunyalanyaza nchito yolalikila .
Nili na Angela mu 1975 , kuyembekezela kuti atifunse mafunso pa TV
Patapita zaka zitatu , tinaitanidwa kuti tikatumikile ku Beteli .
N’cifukwa ciani Yehova ndi Khristu ayenela kulemekezedwa ?
Anthu analengedwa “ m’cifanizilo ca Mulungu . ”
8 , 9 . ( a ) Kodi Mboni za Yehova zimawaona bwanji olamulila a boma ?
( Aef .
Komanso musamachule aliyense kuti atate wanu padziko lapansi pano , pakuti Atate wanu ndi mmodzi , wakumwamba Yekhayo .
Musamachedwe ‘ atsogoleli , ’ pakuti Mtsogoleli wanu ndi mmodzi , Khristu .
Koma wamkulu kwambili pakati panu akhale mtumiki wanu .
Aliyense wodzikweza adzatsitsidwa , koma aliyense wodzicepetsa adzakwezedwa . ” ( Mat .
N’cifukwa ciani anthu ena safunika kutipangila zosankha ?
( a ) Kuti tipange zosankha mwanzelu , kodi tifunika kukhulupilila ciani ?
N’ciani cingatithandize kupanga zosankha mwanzelu ?
( Ŵelengani Yakobo 1 : 5 - 8 . )
( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 24 ) Masiku ano , akulu ayenela kutsatila citsanzo ca Paulo pamene apeleka uphungu kwa ena pa nkhani zaumwini .
Akulu acikondi amathandiza ena kudziŵa mmene angapangile zosankha paokha ( Onani palagilafu 11 )
21 : 9 - 12 ) Nawonso akulu afunika kupeza nthawi yofufuza asanapange zosankha .
Kodi cidzathandiza banja langa kukhala lacimwemwe ndi lamtendele ?
Nanga kodi cidzaonetsa kuti ndine woleza mtima ndi wokoma mtima ? ’
N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizidzipangila tokha zosankha ?
Kodi kutumikila Yehova ndi mtima wathunthu kumatanthauzanji ?
Pa mafumu anayi amenewa , kodi inu mungafune kutengela iti ?
( Ŵelengani 2 Mbiri 14 : 11 . )
Kodi mtima wanu ungakusonkhezeleni kucita ciani ?
Yehosafati mwana wa Asa “ anapitiliza kuyenda m’njila za Asa bambo ake . ”
( Ŵelengani 2 Mbiri 20 : 2 - 4 . )
( Ŵelengani Yesaya 37 : 15 - 20 . )
( Ŵelengani 2 Mafumu 20 : 1 - 3 . )
( Ŵelengani 2 Mbiri 34 : 1 - 3 . )
( Ŵelengani 2 Mbiri 34 : 18 , 19 . )
N’cifukwa ciani tidzakambilana zitsanzo za mafumu anayi aciyuda ?
( Ŵelengani 2 Mbiri 16 : 7 - 9 . )
( Ŵelengani 2 Mbiri 32 : 31 . )
Ndipo abale ndi alongo ambili angayambe kumutamanda .
( Ŵelengani 2 Mbiri 35 : 20 - 22 . )
Baibo imakamba kuti mau a Neko anali “ ocokela pakamwa pa Mulungu . ”
Tiyeni tipitilize kuganizila nkhani za m’Baibo zimenezi , ndipo tiziyamikila kuti Yehova watipatsa zitsanzo zimenezi kuti zitilangize .
Kodi munapangapo malonjezo angati kwa Yehova ?
Nanga bwanji ponena za lonjezo lanu la kudzipeleka kapena la cikwati ?
Tikaona kuti ife kapena munthu wina wacitilidwa zinthu zopanda cilungamo , cikhulupililo , kudzicepetsa , ndi kukhulupilika kwathu zingayesedwe .
“ Dziko likupita limodzi ndi cilakolako cake , koma wocita cifunilo ca Mulungu adzakhala kosatha . ” — 1 YOH .
Kodi Yehova adzacita ciani kwa anthu oipa ndi mabungwe acinyengo ?
Baibo imati : “ Dziko likupita . ” ( 1 Yoh .
Kulibe mdima wandiweyani woti amene akucita zopweteka ena abisaleko . ”
Vesi ina mu salimo imeneyi imati : “ Olungama adzalandila dziko lapansi , ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya . ” ( Sal .
37 : 11 , 29 ) Kodi “ ofatsa ” ndi “ olungama ” amenewa n’ndani ?
Tingatsimikize bwanji kuti anthu okhala m’dziko latsopano azidzacita zinthu mwadongosolo ?
Kodi padziko padzakhala dongosolo lililonse pambuyo pa Aramagedo ?
14 : 33 ) Conco , “ dziko lapansi latsopano ” lidzakhala ladongosolo .
Ni makhalidwe oipa ati amene ni ofala m’dela lanu ? Nanga inu ndi a m’banja lanu amakukhudzani bwanji ?
Tiphunzilapo ciani pa ciŵeluzo cimene Yehova anapeleka ku mizinda ya Sodomu ndi Gomora ?
( Ŵelengani 2 Petulo 2 : 6 - 8 . )
( Ŵelengani Salimo 46 : 8 , 9 . )
N’zinthu ziti zimene sizidzakhalakonso pambuyo pa Aramagedo ?
Fotokozani citsanzo . ( b ) Tifunika kucita ciani kuti tidzapulumuke pamene dziko loipali liwonongedwa ?
“ KODI Woweluza wa dziko lonse lapansi sadzacita colungama ? ”
Akhristu amadziŵa kuti angacitilidwe zinthu zopanda cilungamo ndi munthu amene sali mumpingo wacikhristu .
Mu 1946 , analoŵa kalasi ya namba 8 ya Sukulu ya Giliyadi , ku New York , m’dziko la United States .
Atatsiliza maphunzilo , anam’tumiza ku Switzerland kukatumikila monga woyang’anila dela .
Kodi tidzakambilana zocitika ziti m’nkhani ino ndi yotsatila ?
M’nkhani ino , tidzakambilana za Yosefe mdzukulu wa Abulahamu , ndi zimene abale ake anamucitila .
10 , 11 . ( a ) N’zinthu zopanda cilungamo ziti zimene zinacitikila Yosefe ?
( Ŵelegani Mateyu 5 : 23 , 24 ; 18 : 15 . )
Kukhala wokhulupilika kwa Yehova ndi kwa abale athu kudzatithandiza kupewa mijedo .
Cacikulu , iye sanalole kuti kupanda ungwilo ndi zolakwa za ena zisokoneze ubale wake na Yehova .
N’cifukwa ciani tifunika kuyandikila kwambili Yehova ngati wina mumpingo watilakwila ?
Tingaonetse bwanji kuti timakhulupilila “ Woweluza wa dziko lonse lapansi ” ?
Onani nkhani yofotokoza mbili ya moyo wa m’bale Willi Diehl , yamutu wakuti “ Yehova Ndiye Mulungu Wanga , Amene Ndimkhulupirira , ” mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 1991 .
( Onani mapikica pamwambapa . ) ( b ) Ni mafunso ati amene adzayankhidwa m’nkhani ino ?
Iwo n’zitsanzo zabwino ngako kwa amuna ndi akazi amakono , amene amacita malonjezo kwa Yehova .
N’cifukwa ciani malonjezo amene timapanga kwa Mulungu ni nkhani yaikulu ?
Nanga tingaphunzile ciani kwa Yefita ndi Hana pa nkhaniyi ?
2 , 3 . ( a ) Kodi lonjezo n’ciani ?
( b ) Kodi Malemba amati ciani pa nkhani yopanga malonjezo kwa Mulungu ?
Acite malinga ndi mau onse otuluka pakamwa pake . ”
( a ) Kodi kupanga lonjezo kwa Mulungu ni nkhani yaikulu bwanji ?
( b ) Tidzaphunzila zotani zokhudza Yefita ndi Hana ?
( a ) Kodi cinali copepuka kwa Yefita na mwana wake kukwanilitsa zimene analonjeza kwa Mulungu ?
Iye anati : “ Ndatsegula pakamwa panga pamaso pa Yehova , ndipo sindingathe kubweza mau anga . ”
( b ) Kodi lonjezo la Hana linatanthauza ciani kwa Samueli ?
Ndipo Hana anauza Eli kuti : “ Ndinali kupemphela kuti Yehova andipatse mwana uyu , kuti andipatse cimene ndinam’pempha .
Lonjezo lina lofunika kwambili limene munthu angapange , ni lonjezo la cikwati .
Kodi Baibo imakamba zotani pa pankhani yothetsa cikwati ndi kupatukana ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 10 , 11 . )
Banja lina linati : “ Kucokela pamene tinayamba kuphunzila kabuku kameneka , banja lathu lakhala lacimwemwe ngako . ”
Lomba banja lathu likuyenda bwino . ”
18 , 19 . ( a ) Kodi makolo ambili Acikhristu acita ciani ?
( b ) Fotokozani zokhudza atumiki a nthawi zonse apadela .
Lonjezo la utumiki wanthawi zonse wapadela ( Onani palagilafu 19 )
Amavomelezanso kuti adzakhala na umoyo wosalila zambili , ndi kuti sadzaloŵa nchito kwina kulikonse popanda cilolezo .
Onani buku lakuti “ Khalanibe M’cikondi ca Mulungu , ” mapeji . 219 - 221 .
Kodi Wamphamvuyonse amasangalala kuti ndiwe wolungama ? Kapena amapindula ciliconse cifukwa cakuti sucita colakwa ? ”
( b ) Kodi Aisiraeli anagonjetsa bwanji asilikali a Yabini ?
( Ŵelengani Oweruza 4 : 14 - 16 . )
Mtsinje wa Kisoni unawakokolola . ”
Onani nkhani yakuti “ Nkhawa Zokhudza Ndalama , ” mu Nsanja ya Mlonda ya September 1 , 2015 .
1 , 2 . ( a ) Kodi Naboti ndi ana ake anacitilidwa zinthu zopanda cilungamo ziti ?
( b ) Ni makhalidwe aŵili ati amene tidzakambilana m’nkhani ino ?
Nanga n’cifukwa ciani anakana kugulitsa munda wake wa mpesa kwa Mfumu Ahabu ?
Naboti anakhalabe wokhulupilika kwa Yehova pa nthawi imene Aisiraeli ambili anali kutsatila citsanzo coipa ca Mfumu Ahabu ndi mkazi wake , Yezebeli .
Ŵelengani 1 Mafumu 21 : 1 - 3 .
Mwaulemu , iye anafotokoza kuti : “ Sindingacite zimenezo pamaso pa Yehova , kupeleka colowa ca makolo anga kwa inuyo . ”
Kodi kudzicepetsa kuyenela kuti kunawateteza bwanji acibale a Naboti ndi mabwenzi ake ?
( Ŵelengani Deuteronomo 32 : 3 , 4 . )
( b ) Kodi kudzicepetsa kumatiteteza bwanji ?
Mungacite bwanji ngati akulu apeleka cilengezo cimene inu simunagwilizane naco ?
Kodi tidzakambilana ciani tsopano ? Nanga n’cifukwa ciani ?
Kodi Petulo anawongoleledwa bwanji ? Nanga pakubuka mafunso otani ?
Ndipo pambuyo pa izi , iye anauzilidwa kulemba makalata aŵili amene anakhala mbali ya Baibo .
3 Kuthandiza Alendo Ocokela ku Mayiko Ena “ Kutumikila Yehova Mokondwela ”
Nkhani yaciŵili idzafotokoza mmene mfundo za m’Baibo zingathandizile makolo amene akukhala m’dziko lina kupanga zosankha zimene zingapindulitse ana awo .
Tinaona anthu akuthaŵa , ndipo ena anali kuombela mfuti anzawo .
Makolo anga na ise ana 11 tinathaŵa kuti tipulumutse miyoyo yathu , ndipo tinangothaŵa na zovala za m’thupi .
N’cifukwa ciani Yesu ndi ophunzila ake ambili anathaŵa kwawo ?
Iye anati : “ Akakuzunzani mumzinda wina , muthaŵile mumzinda wina . ”
( b ) pamene akhala m’kampu ?
Mendo yanga yanatupa ngako cakuti n’nauza abale anga kuti anisiye cabe .
Koma atate ananinyamula . Sanafune kuti asilikali oukilawo anipeze n’kunipha .
Anali kungokhalila kujeda anzawo , kuledzela , kuchova njuga , kuba , ndipo anali kucita ciwelewele . ”
( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 17 , 18 . )
( b ) N’cifukwa ciani tifunika kuwathandiza moleza mtima ?
Iwo afunika kuona kuti timawakonda .
( b ) Nanga angaonetse bwanji kuyamikila ?
Kodi tingawathandize bwanji abale na alongo athu othaŵa kwawo ?
( a ) Ni ciyeso citi cimene othaŵa kwawo afunika kupewa ?
Ndiyeno , ananyamula cola copanda katundu cija n’kukamba kuti : ‘ Mwaona ka ?
Zonse zimene zinali m’colamu sizofunika kweni - kweni pa moyo ! ’ ” — Ŵelengani 1 Timoteyo 6 : 8 .
Conco , akafika m’dela lathu afunika kuona kuti Yehova na ise Akhristu anzawo timawakonda .
Masiku ano , anthu ambili othaŵa kwawo amacokela m’mayiko amene nchito yolalikila si yovomelezeka mwalamulo .
( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Mlongoyu anati : “ Abale kumeneko anatilandila monga acibale awo .
Anatipatsa zakudya , zovala , pogona ndi ndalama zoyendela .
Ni Mboni za Yehova zokha ! ” — Ŵelengani Yohane 13 : 35 .
Abale othaŵa kwawo akangofika , akulu ayenela kutsatila malangizo a m’buku la Gulu Lochita Chifunilo ca Yehova mutu 8 , palagilafu 30 .
Poyembekezela , iwo mosamala angafunse abale othaŵa kwawo za mipingo imene anali kusonkhanako , ndi zokhudza utumiki kuti adziŵe umoyo wawo wauzimu .
“ Palibe cimene cimandisangalatsa kwambili kuposa kumva kuti ana anga akuyendabe m’coonadi . ” — 3 YOH . 4 .
Kodi makolo angapeleke bwanji citsanzo cabwino kwa ana awo ?
Pofuna kusankha kuti banja lizisonkhana mpingo wa citundu citi , kodi mutu wa banja angacite ciani ?
Kodi ena angathandize bwanji makolo amene anasamukila m’dziko lina pamodzi na ana awo ?
1 , 2 . ( a ) Ni vuto liti limene makolo ambili osamukila m’dziko lina amakumana nalo ?
( b ) Tidzakambilana mafunso ati m’nkhani ino ?
Iye anapitiliza kuti : “ Koma n’tayamba kupita kusukulu , n’nayamba kukonda citundu ca m’dziko limene tinasamukila .
Patapita zaka zocepa cabe , zinthu zinasinthilatu .
Sin’nali kumvetsetsa zimene zinali kukambidwa pa misonkhano , ndipo sin’nali kudziŵa bwino cikhalidwe ca makolo anga . ”
3 , 4 . ( a ) Kodi makolo angapeleke bwanji citsanzo cabwino kwa ana awo ?
( b ) Kodi makolo sayenela kuyembekezela ciani kwa ana awo ?
Ana anu akaona kuti ‘ mukufuna - funa ufumu coyamba , ’ amaphunzila kudalila Yehova kuti adzawapatsa zofunika pa umoyo .
Musamakhale bize kwambili mpaka kusoŵa nthawi yoceza ndi ana anu .
Kodi ana anu angapindule bwanji ngati aphunzila citundu canu ?
Mukacita zimenezi , mudzakwanitsa kuphunzitsa ana anu coonadi mosavuta .
Kodi mungacite ciani ? Kodi simungaphunzile cinenelo camanja kuti muzikwanitsa kukamba naye ?
3 : 15 ) Ngati m’banja lanu muli vuto laconco , n’zotheka ndithu kuthandiza ana anu kudziŵa Yehova ndi kum’konda .
Koma tinali kuwaona akucita phunzilo laumwini , kupemphela , ndi kucititsa kulambila kwa pabanja wiki iliyonse . Zimenezi zinatithandiza kuona kuti kudziŵa Yehova n’kofunika ngako . ”
N’cifukwa ciani ana ena amafunika kuphunzila za Yehova m’zitundu ziŵili ?
( a ) N’ndani afunika kusankha mpingo umene banja lizisonkhanako ?
Koma ngati citundu sacimvetsetsa , sangapindule mokwanila .
( Ŵelengani 1 Akorinto 14 : 9 , 11 . )
Tinalinso kupempha nzelu kwa Mulungu . Zimene tinapeza sizinali zotikomela .
Koma titaona kuti anawo sapindula mokwanila na misonkhano ya m’citundu cathu , tinaganiza zosamukila mumpingo wa citundu ca m’dzikolo .
Nthawi zonse , tinali kusonkhana ndi kuyenda muulaliki pamodzi .
Tinalinso kuitana abale na alongo a kumaloko , kuti tidzadye nawo cakudya kapena kupita nawo kokaona malo .
Zimenezi zinathandiza ana athu kudziŵana ndi abale . Zinawathandizanso kudziŵa Yehova Mulungu ndi kuyamba kumuona monga Tate ndi Bwenzi lawo .
Tinaona kuti zimenezi ndizo zinali zofunika ngako kwa anawo kupambana kuti aphunzile citundu cathu . ”
M’bale Samuel anakambanso kuti : “ Pofuna kuti tikhalebe olimba mwauzimu , ine na mkazi wanga tinali kusonkhananso na mpingo wa citundu cathu .
Umoyo unali wa bize kwambili , ndipo tinali kukhala otopa .
Koma Yehova anatidalitsa cifukwa ca khama lathu ndi kudzipeleka kwathu , ndipo timamuyamikila kwambili .
Tsopano , ana athu onse atatu akutumikila Yehova mu utumiki wanthawi zonse . ”
Kristina anati : “ N’nali kudziŵako ndithu citundu ca makolo anga , koma zimene zinali kukambidwa kumisonkhano sin’nali kuzimvetsetsa .
Pamene n’nafika zaka 12 , n’napezeka pa msonkhano wacigawo wa m’citundu cimene n’naphunzila kusukulu .
Kwa nthawi yoyamba , n’nadziŵa kuti zimene n’nali kumva ni coonadi .
Zinthu zinasinthanso kwambili n’tayamba kupemphela m’citundu cimene n’naphunzila kusukulu .
N’nayamba kupemphela kwa Yehova mocokela pansi pa mtima . ”
Inu acicepele , kodi muona kuti mufunika kusamukila mumpingo wa citundu ca m’dela limene mukhala ?
Nadia , amene lomba atumikila pa Beteli , anati : “ Pamene ine na abale anga tinafika zaka za pakati pa 13 ndi 19 , tinafuna kusamukila mumpingo wacinenelo ca m’dela limene tikhala . ”
Nadia anati : “ Tsopano timayamikila kuti makolo athu anayesetsa kutiphunzitsa citundu cawo , ndipo tinapitiliza kukhala mumpingo wa citundu ca m’dziko limene tinacokela .
Zimenezi zatithandiza kukhala na umoyo watanthauzo , ndiponso zatipatsa mwayi waukulu wothandiza anthu kudziŵa Yehova . ”
( b ) Nanga makolo angapeze kuti thandizo pophunzitsa ana awo coonadi ?
( Ŵelengani Miyambo 1 : 8 ; 31 : 10 , 27 , 28 . )
Komabe , makolo amene sadziŵa bwino cinenelo ca ana awo , afunika thandizo kuti aphunzitse ana awo mowafika pamtima .
Ana ndi makolo awo , onse amapindula akamagwilizana ndi mpingo ( Onani mapalagilafu 18 ndi 19 )
( b ) Kodi makolo afunika kupitiliza kucita ciani ?
Akanithandiza kukonzekela nkhani za m’sukulu , n’nali kuphunzilapo zambili .
Komanso n’nali kukondwela na zosangulutsa zimene tinali kucita . ”
Makolo , muzipemphela kwa Yehova kuti akuthandizeni , ndipo muzicita zimene mungathe kuti muphunzitse ana anu .
( Ŵelengani 2 Mbiri 15 : 7 . )
Muziona ubwenzi wa anawo ndi Yehova kuti ni wofunika kwambili kuposa zofuna zanu .
Koma mu 1946 m’pamene n’namvetsetsa coonadi ca m’Baibo .
M’kupita kwa nthawi , n’naphunzila cinenelo camanja , ndipo n’nayamba kusangalala nikamaseŵela na anzanga .
Iye analembetsa kuti azilandila magazini , ndipo ananipempha kuti nikalalikilekonso mwamuna wake , Gary .
Posapita nthawi , atsikanawo anayamba kuuzako anzawo a m’kilasi zimene anali kuphunzila .
Panthawiyo , ananipatsa switi n’kunipempha kuti nikhale mnzake .
Atasankha kuti abatizike , makolo ake anamuuza kuti , “ Ukakhala wa Mboni za Yehova , udzacoka pano panyumba . ”
Iye anapitilizabe kuphunzila Baibo ndipo anabatizika .
Pamene tinakwatilana mu 1960 , makolo ake sanabwele ku cikwati cathu .
Mwana wanga , Nicholas na mkazi wake , Deborah , atumikila pa Beteli ku London
Faye na James , Jerry na Evelyn , Shannan na Steven
Lomba , tisonkhana mumpingo wa cinenelo camanja wa Calgary , ndipo nikali kutumikila monga mkulu .
Tingacite ciani kuti tipitilize kum’konda kwambili Yehova ?
Tingacite ciani kuti tizikonda kwambili coonadi ca m’Baibo ?
N’cifukwa ciani tifunika kukonda abale athu ?
N’ciani cimene ciyenela kuti cinacititsa cikondi ca Akhristu ena kuzilala ?
Anthu mamiliyoni ambili aleka kudalila Mulungu .
Limeneli ndilo lamulo lalikulu kwambili komanso loyamba . ”
Muzionetsa kuti mumakonda Yehova ( Onani palagilafu 10 )
( Ŵelengani Salimo 119 : 97 - 100 . )
Muzionetsa kuti mumakonda coonadi ca m’Baibo ( Onani palagilafu 14 )
Usiku wakuti mawa aphedwa , Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Ndikukupatsani lamulo latsopano , kuti muzikondana . Mmene ine ndakukondelani , inunso muzikondana .
Mwakutelo , onse adzadziŵa kuti ndinu ophunzila anga , ngati mukukondana . ” — Yoh . 13 : 34 , 35 .
( 1 Yoh .
Muzionetsa kuti mumakonda abale na alongo ( Onani palagilafu 17 )
Ni zinthu ziti zimene tingacite zoonetsa kuti timakonda abale na alongo athu ?
Ŵelengani 1 Atesalonika 4 : 9 , 10 .
21 : 15 .
Ndiyeno , anati : “ ‘ Ponyani ukonde kumbali ya kudzanja lamanja kwa ngalawayo ndipo mupeza kenakake . ’
Pamenepo anaponyadi ukondewo , koma sanathenso kuukoka cifukwa ca kuculuka kwa nsomba . ” — Yoh . 21 : 1 - 6 .
( b ) Ni mfundo yofunika kwambili iti imene m’bale wina ku Thailand anaphunzila pankhani yokhudza nchito ?
Zimenezi zinapangitsa kuti nizisoŵa nthawi yocita zinthu zauzimu .
Patapita nthawi , n’nazindikila kuti nifunika kupeza nchito ina kuti nizikwanitsa kuika zinthu za Ufumu patsogolo . ”
M’baleyu anati : “ N’takonzekela pafupi - fupi kwa caka cathunthu , n’naleka kugwila nchitoyo n’kuyamba kugulitsa aisikilimu m’misewu .
Poyamba , n’nali kusoŵa ndalama , ndipo n’nanganiza zongoleka .
Nikakumana na anzanga amene n’nali kugwila nawo nchito yokonza makompyuta , anali kuniseka ndi kunifunsa cifukwa cake n’naleka nchito yokonza makompyuta pa malo abwino n’kuyamba kugulitsa aisikilimu .
N’napemphela kwa Yehova kuti anithandize kupilila ndi kukwanilitsa colinga canga cofuna kukhala na nthawi yokwanila yocita zinthu zauzimu .
N’nafika podziŵa bwino zimene makasitomala anga anali kukonda , ndipo n’naidziŵa bwino nchito yopanga aisikilimu .
N’nayamba kugulitsa aisikilimu yonse imene napanga patsiku .
Kunena zoona , n’nali kupeza ndalama zambili kusiyana ndi pamene n’nali kugwila ntchito yokonza makompyuta .
Ndine wosangalala kwambili cifukwa nilibenso nkhawa ngati imene n’nali nayo pa nchito yakale ija .
Ndipo cokondweletsa ngako n’cakuti lomba nili pa ubale wolimba na Yehova . ” — Ŵelengani Mateyu 5 : 3 , 6 .
Atabatizika , anati : “ Nimaona kuti n’nachedwa kuyamba kutumikila Mulungu . Kutumikila Yehova kumabweletsa cimwemwe coculuka kuposa kucita zosangulutsa za m’dzikoli . ”
Yesu anakamba kuti “ kapolo sangatumikile ambuye aŵili . ”
Anakambanso kuti : “ Simungathe kutumikila Mulungu ndi Cuma nthawi imodzi . ”
( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 14 . )
Onani nkhani yakuti “ Kodi Zimene Mumachita pa Nthawi Yosangalala Zimakhala Zopindulitsa ? ”
Komanso , tinali kulalikila mokhazikika . ”
Tinali kukwinyilila tikaganizila kuti tidzasiya maphunzilo athu a Baibo . ”
Koma patangopita mwezi umodzi , iwo analandila uthenga wokondweletsa .
Miriam anati : “ Tinauzidwa kuti tiyambe kutumikila monga apainiya apadela .
Tinakondwela ngako kudziŵa kuti tidzapitiliza utumiki wathu . ”
Anakhulupilila lonjezo la pa Salimo 37 : 5 , pamene pamati : “ Lola kuti Yehova akutsogolele panjila yako , umudalile ndipo iye adzacitapo kanthu . ”
Koma lomba timakwanitsa . Sitisoŵa ciliconse cofunika paumoyo . ”
N’cifukwa ciani tingayembekezele kuti munthu akaloŵa m’banja adzakumana ndi mavuto ?
Tingakhale otsimikiza kuti iye amatifunila zabwino , monga mmene anacitila na atumiki ake akale . — Ŵelengani Yeremiya 29 : 11 , 12 .
( Ŵelengani 1 Samueli 1 : 4 - 7 . )
Paula anati : “ Ngakhale kuti Ann sanali m’bululu wanga , cikondi cimene ananionetsa cinanithandiza kwambili .
Cinanithandiza kuti nipitilize kutumikila Yehova . ”
( Ŵelengani Salimo 145 : 18 , 19 . )
“ Kumene kuli cuma canu , mitima yanunso idzakhala komweko . ” — LUKA 12 : 34 .
Pamene tikambilana , ganizilani zimene inu pamwekha mungacite kuti muzikonda kwambili cuma cauzimu cimeneci .
Mosakayikila , ngaleyo inalidi yamtengo wapatali kwa iye .
( Ŵelengani Maliko 10 : 28 - 30 . )
( a ) N’cifukwa ciani mtumwi Paulo anakamba kuti utumiki wathu ni “ cuma m’zonyamulila zoumbidwa ndi dothi ? ”
( Ŵelengani Aroma 1 : 14 , 15 ; 2 Timoteyo 4 : 2 . )
Ena mwa iwo ni atumiki a pa Beteli , ena ni apainiya , ndipo ena ni akulu .
Irene anati : “ Niona kuti palibe colinga cina cimene cikananibweletsela cimwemwe coculuka kuposa zimene n’nasankha kucita . ”
Kodi “ mosungilamo cuma , ” kapena kuti nkhokwe , imene Yesu anachula pa Mateyu 13 : 52 n’ciani ?
( Welengani Miyambo 2 : 4 - 7 . )
Ganizilani zimene zinacitikila m’bale wina , dzina lake Peter .
M’rabiyo pofuna kuyesa Peter anamufunsa kuti : “ Mnyamata iwe , buku la Danieli linalembedwa m’citundu canji ? ”
Pamene n’nabwelela kunyumba ndi kufufuza m’magazini a Nsanja ndi Galamukani !
a miyezi yapambuyo , n’napeza nkhani imene inafotokoza kuti buku la Danieli linalembedwa m’Ciaramu . ”
Pamene mucita zimenezi , mudzaunjika “ cuma cosatha kumwamba , kumene mbala singafikeko , ndipo njenjete singawononge .
Pakuti kumene kuli cuma canu , mitima yanunso idzakhala komweko . ” — Luka 12 : 33 , 34 .
“ Ine n’nali na vuto lokonda kukangana ndi m’bale amene nimaseŵenza naye .
Tsiku lina pamene tinali kukangana , anthu aŵili anabwela kuti amvele zimene tinali kukangana . ” — CHRIS .
“ Mlongo wina amene kaŵili - kaŵili n’nali kugwila naye nchito yolalikila , mwadzidzidzi analeka kulalikila na ine .
Ine sin’nadziŵe cifukwa cimene anacitila zimenezo . ” — JANET .
“ Tsiku lina n’nalumikizana ndi anzanga aŵili n’kumaceza pafoni .
Mmodzi wa iwo anakamba kuti bayi , kuonetsa kuti walaila . Ndipo ine n’naganiza kuti wadula foni .
Conco , n’nayamba kukamba mau oipa okhudza mnzangayo , osadziŵa kuti iye sanadule foniyo . ” — MICHAEL .
“ Mumpingo mwathu , apaniya aŵili anayamba kukangana .
Kukangana kwawo kunali kukhumudwitsa ena mumpingo . ” — GARY .
“ Musakanganetu m’njila . ” ( Gen .
“ Zolingalila sizikwanilitsidwa ngati anthu sakambilana moona mtima . ” ( Miy .
Michael anati : “ M’baleyo ananikhululukila ndi mtima wonse . ”
“ Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana ndi mtima wonse , ngati wina ali ndi cifukwa codandaulila za mnzake . ” ( Akol .
Tsopano amalalikila uthenga wabwino pamodzi mwamtendele .
Kusiyana kumeneku kungaoneke ngati nkhani yaing’ono , koma kungabweletse mavuto aakulu . ”
Mkwiyo utakula , n’nayamba kum’citila zinthu mwamwano .
Mumtima n’nati : ‘ Iye sanipatsa ulemu , na ine n’dzaleka kum’patsa ulemu . ’ ”
Iye anati : “ N’nazindikila kuti zimene n’nali kucita si zabwino , ndipo n’nayamba kudziimba mlandu .
N’naona kuti nifunika kusintha .
N’tapemphela kwa Yehova za nkhaniyi , n’nagulila mlongoyo kamphatso , kumulembela kakalata , na kupita kukam’pepesa .
Tinakumbatilana ndi kugwilizana zoiŵalako nkhaniyo .
Apa lomba , ndise ogwilizana . ”
ANTHU ambili masiku ano amaona kuti ndalama ndiye nkhani yaikulu .
N’cifukwa ciani nkhani yokhudza ulamulilo wa Mulungu iyenela kuthetsedwa ?
Kodi kucilikiza ulamulilo wa Yehova n’kofunika bwanji ?
Taonani , kucokela tsiku limene makolo athu anamwalila , zinthu zonse zikupitililabe cimodzimodzi ngati mmene zakhalila kuyambila pa ciyambi ca cilengedwe . ”
( Ŵelengani Yesaya 55 : 10 , 11 . )
( Ŵelengani Yobu 1 : 7 - 12 . )
( Ŵelengani Yobu 38 : 18 - 21 . )
( Ŵelengani Aroma 5 : 3 - 5 . )
Cimodzi n’cakuti iye amalamulila mwacikondi .
Amatisamalila kuposa mmene ise tingadzisamalile .
Kodi akulu na mitu ya mabanja angatengele bwanji citsanzo ca Yehova ?
Salimo 147 imalimbikitsa anthu a Mulungu mobweleza - bweleza kuti afunika kutamanda Yehova .
N’zinthu ziti zokhudza Yehova zimene zinapangitsa wolemba salimoyi kuona kuti Mulungu ni wofunika kutamandidwa ?
Abale na alongo ambili acicepele ayamba utumiki wa nthawi zonse .
“ Dzipezeleni mabwenzi ndi cuma cosalungama . ” — LUKA 16 : 9 .
Tingapewe bwanji kukhala akapolo kwa anthu amalonda a m’dzikoli masiku ano ?
N’cifukwa ciani nthawi zonse m’dziko la Satanali mudzakhala anthu osauka ?
Tingaphunzilepo ciani pa malangizo a Yesu amenewa ?
Tidziŵa bwanji kuti kucita malonda siinali mbali ya colinga ca Mulungu ?
Fotokozani zitsanzo za mmene ena aonetsela kukhulupilika poseŵenzetsa cuma cawo .
Nakhala munthu wokonzeka kukhululukila ena , woleza mtima , wopilila , ndi wokonzeka kulandila uphungu . ”
Kodi Abulahamu anaonetsa bwanji kuti anali kudalila Mulungu ?
( b ) Nanga tingaonetse bwanji kuti timamvela malangizo a Paulo ?
Paulo anachula Timoteyo kuti ndi “ msilikali wabwino wa Khristu Yesu . ” Pambuyo pake anamuuza kuti : “ Msilikali amene ali pa nkhondo sacita nawo zamalonda zimene anthu wamba amacita , pofuna kukondweletsa amene anamulemba usilikali . ” ( 2 Tim .
Yehova amadalitsa anthu amene ni “ olemela pa nchito zabwino . ”
( Ŵelengani 1 Timoteyo 6 : 17 - 19 . )
Golide , siliva , ndi miyala ina yamtengo wapatali zidzakhala zinthu zokongoletsela , osati zogulitsa kapena zosunga monga cuma .
Kuti mupeleke ndalama kupitila pa intaneti , yendani pa jw.org ndi kutinika pa mau akuti , “ Citani Copeleka ku Nchito Yathu ya Padziko Lonse . ”
“ MWANA wathu wamwamuna atamwalila , tinavutika na cisoni pafupi - fupi kwa caka cathunthu , ” anatelo Susi .
( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 3 , 4 . )
Nthawi zonse tikacita zimenezi , mtendele wa Mulungu unali kuteteza mitima yathu na maganizo athu . ” — Ŵelengani Afilipi 4 : 6 , 7 .
Pamene Lazaro anafa , kodi Yesu anaonetsa bwanji kuti anali ndi cisoni ?
( Aroma 15 : 4 ) Ngati munafedwa , mungapeze citonthozo pa malemba monga awa :
( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 11 . )
N’ciani cimene tifunika kukumbukila pankhani ya kumva cisoni ?
( Miy . 14 : 10 ) Ngakhale munthu atafotokoza mmene amvelela , nthawi zina zimakhalabe zovuta kumumvetsetsa .
Panthawiyi , nimatonthozedwa poona kuti anzanga nawonso ali na cisoni . ”
Junia anati : “ Nikalandila meseji yonilimbikitsa kapena ngati Mkhristu waniitana kuti nikaceze kwawo , nimalimbikitsidwa ngako .
Zimenezi zimanicititsa kuona kuti ena amanikonda ndi kuniganizila . ”
Dalene anati : “ Nthawi zina alongo akabwela kudzaniona , nimawapempha kuti anipemphelele .
Poyamba kupemphela , nthawi zambili amakamba movutikila , koma posakhalitsa mau awo amayamba kumveka amphamvu ndi acidalilo , ndipo pemphelo limene amapeleka limakhala locokela pansi pamtima .
Cikhulupililo canga cimalimba kwambili nikaganizila cikondi cawo , nkhawa imene amanionetsa , ndi cikhulupililo cawo . ”
Baibo imati : “ Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse , ndipo ilo ndi m’bale amene anabadwila kuti akuthandize pakagwa mavuto . ”
M’bale wina anati : “ Mkazi wanga atamwalila , n’nadziŵa kuti tsiku lokumbukila cikwati cathu likadzafika nidzavutika kwambili ndi cisoni , ndipo zinalidi zovuta .
Koma abale na alongo ena , amene nanzanga anakonza zakuti tidzakhale na maceza n’colinga cakuti patsikulo nisadzakhale nekha . ”
Junia anati : “ Nthawi zambili , kukhala na maceza ndi kupeleka thandizo kwa munthu pamene kulibe zocitika zapadela kumakhala kothandiza kwambili .
Kucita zinthu mwanjila imeneyi n’kopindulitsa ndiponso kumatonthoza kwambili . ”
Ananicititsa kuona kuti Yehova amanikonda . ”
Kodi malonjezo a Yehova amatitonthoza bwanji ?
Adzacita zimenezi pamene “ onse ali m’manda acikumbutso adzamva mau ake [ a Yesu ] ndipo adzatuluka . ” ( Yoh .
Malemba ena amene amatonthoza anthu ambili ndi Salimo 20 : 1 , 2 ; 31 : 7 ; 38 : 8 , 9 , 15 ; 55 : 22 ; 121 : 1 , 2 ; Yesaya 57 : 15 ; 66 : 13 ; Afilipi 4 : 13 ; na 1 Petulo 5 : 7 .
Onani nkhani yakuti “ Muzitonthoza Anthu Amene Aferedwa , Ngati Mmene Yesu Anachitira , ” mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 2010 .
“ Sitidziŵa cimene tingakambe , koma timakukondani kwambili .
Ife sitingadziŵe bwino - bwino mmene mumvelela , koma Yehova adziŵa ndipo adzapitiliza kukulimbikitsani .
Tidzapitiliza kukupemphelelani . ”
“ Yehova akulimbitseni panthawi yovuta kwambili imeneyi . ”
“ Dziŵani kuti Mulungu akum’kumbukila wokondedwa wanu . Iye sadzamuiŵala ngakhale pang’ono ndipo adzamuukitsa . ”
“ Mulungu sanaiŵale nchito za cikhulupililo za wokondedwa wanu , ndipo adzamuukitsa m’Paradaiso .
Akadzaukitsidwa , sadzakumananso na mdani wotsiliza , imfa . ”
“ Sitingakwanitse kufotokoza mmene cimaŵaŵila ngati munthu amene tinali kum’konda wamwalila . Koma tiyembekezela mwacidwi nthawi pamene Atate wathu wakumwamba adzaukitsa wokondedwa wanu .
Pa cisautso cacikulu , Akhristu adzadalila Yehova , osati kudziteteza okha
Wofalitsa akulalikila mmodzi mwa oseŵenza m’munda wa maapozi ku Grójec .
( b ) Nanga kuphunzila za lemba limeneli kungatithandize bwanji ?
Ndipo cioneka kuti mumlengalenga muli milalang’amba mathililiyoni ambili .
Nifuna kuti uzisangalala pa umoyo wako cifukwa ndiwe Mboni yanga . ”
( Ŵelengani Salimo 147 : 8 , 9 . )
Mutsuo anati : “ N’naona kuti Yehova anali pafupi na aliyense wa ife ndi kuti anali kutisamalila .
12 , 13 . ( a ) Kodi tifunika kupewa ciani kuti Mulungu azitithandiza ?
Mosiyana ndi ofatsa , “ anthu oipa [ Mulungu ] amawagwetsela pansi . ”
Malemba amati : “ Yehova amasangalala ndi anthu amene amamuopa , amene amayembekezela kukoma mtima kwake kosatha . ”
15 - 17 . ( a ) Kodi nthawi zina tingamvele bwanji cifukwa ca mavuto amene timakumana nawo ?
Masiku ano , Yehova amatitsogolela kupitila m’Mau ake , Baibo .
( Ŵelengani Salimo 147 : 19 , 20 . )
Kodi wacicepele angaphunzile ciani pamene acita utumiki wa nthawi zonse ?
Kodi acicepele afunika kusankha ciani cokhudza tsogolo lawo ?
IMWE acicepele mungavomeleze kuti ni cinthu canzelu kudziŵa kumene mufuna kupita mukalibe kuyamba ulendo .
Moyo nawonso uli ngati ulendo , ndipo nthawi yabwino yosankha zimene mudzayamba kucita pa umoyo wanu , ndi pamene muli wacicepele .
Mudziŵa bwanji kuti Yehova amafuna kuti muzipanga zosankha mwanzelu n’colinga cakuti mudzakhale na tsogolo labwino ?
Mlengi wathu ndi “ Mulungu wacikondi ” ndi “ wacimwemwe , ” ndipo analenga anthu “ m’cifanizilo cake . ” ( 2 Akor . 13 : 11 ; 1 Tim . 1 : 11 ; Gen .
1 : 27 ) Ngati mutengela citsanzo ca Mulungu wathu , amene ni wacikondi , mudzakhala na umoyo wacimwemwe .
Yesu Khristu anapeleka citsanzo cabwino kwambili kwa inu acicepele .
3 : 4 ) Yesu analinso kuphunzila Malemba kuti alimbitse ubwenzi wake na Yehova .
Baibo imati : “ Zolingalila sizikwanilitsidwa ngati anthu sakambilana moona mtima , koma aphungu akaculuka zimakwanilitsidwa . ”
Mofanana ndi nchito ina iliyonse , pafunika nthawi kuti mukhale na luso pa nchito imeneyi .
Poyamba n’nalibe phunzilo , koma pamene n’nasamukila m’gawo lina , n’napeza maphunzilo ambili m’mwezi umodzi cabe .
Mmodzi wa ophunzilawo anayamba kupezeka pamisonkhano .
Mwacitsanzo , Jacob wa ku North America , analemba kuti : “ Pamene n’nali na zaka 7 , anzanga ambili m’kilasi anali ocokela ku Vietnam .
N’nali kufuna kuwauza za Yehova . Conco , patapita nthawi yocepa n’naganiza zoyamba kuphunzila citundu cawo .
Cacikulu cimene cinanithandiza ni kulinganiza nkhani za m’magazini a Nsanja ya Mlonda yacizungu ndi ya Civietinamu .
Cinanso , n’napeza anzanga mumpingo wa Civietinamu umene unali pafupi na kwathu .
N’takwanitsa zaka 18 , n’nayamba kucita upainiya .
Pambuyo pake , n’naloŵa Sukulu Yophunzitsa Baibo ya Abale Osakwatila .
Tsopano nitumikila m’kagulu ka Civietinamu , ndipo ndine nekha amene nikutumikila monga mkulu .
Anthu ambili ocokela ku Vietnam amadabwa kwambili kuti n’naphunzila citundu cawo .
Iwo amanilandila ku nyumba zawo , ndipo ambili amavomela kuti niziphunzila nawo Baibo .
Ena apita patsogolo mpaka kufika pa kubatizika . ” — Yelekezelani na Machitidwe 2 : 7 , 8 .
Nimakonda kulimbikitsa abale acicepele mumpingo mwathu ndipo nimasangalala kuona mmene akupitila patsogolo mwauzimu .
N’tatsiliza maphunzilo a Sukulu Yophunzitsa Baibo ya Abale Osakwatila , ananitumiza ku gawo lina latsopano kumene n’napitiliza kucita upainiya .
N’zoona kuti pa anthu amene n’nali kuphunzila nawo Baibo m’gawolo , palibe amene anapita patsogolo kufika pobatizika .
Kodi kucita upainiya kungakupatseni bwanji mwayi wocitako mautumiki ena ?
M’bale wina dzina lake Kevin anati : “ Kuyambila nili mwana , n’nali na colinga cakuti nikadzakula nidzatumikile Yehova mu utumiki wanthawi zonse .
N’takwanitsa zaka 19 , n’nayamba kucita upainiya .
Kuti nizipeza zofunika pa umoyo , n’nali kuseŵenza kwa maola ocepa kwa m’bale amene anali kugwila nchito yomanga .
N’naphunzila kukhoma mtenje , kuika mawindo ndi zitseko .
Pambuyo pake , kwa zaka ziŵili n’natumikila m’gulu la abale amene anali kupeleka thandizo kwa okhudzidwa ndi cimphepo coopsa ca mkuntho .
N’tamvela kuti ku South Africa kufunikila anchito omanga , n’nafunsila utumiki umenewu ndipo ananiitana .
Kuno ku Africa , timamanga Nyumba ya Ufumu kwa mawiki angapo cabe , ndipo tikatsiliza timapita pa ina .
Timakhala pamodzi , kuphunzila Baibo pamodzi , na kuseŵenzela pamodzi .
Nimasangalalanso kugwila nchito yolalikila wiki iliyonse pamodzi na abale a pampingo umene tili .
Zolinga zimene n’napanga nili mwana zanicititsa kukhala na cimwemwe coculuka kuposa cimene n’nali kuyembekezela . ”
Kucita utumiki wa pa Beteli kumabweletsa cimwemwe cifukwa zilizonse zimene munthu ungacite , umacitila Yehova .
Kumeneko , n’naphunzila kuseŵenzetsa mashini opulintila , ndipo pambuyo pake n’naphunzila kukonza mapulogilamu a pa kompyuta .
Kuno ku Beteli , nimadzionela nekha mmene nchito yopanga ophunzila ikupitila patsogolo padziko lonse .
Nimakondwela kutumikila kuno cifukwa zimene timacita zimathandiza anthu kukhala pa ubwenzi na Yehova . ”
Yehova amafuna kuti ‘ mugwile mwamphamvu ’ tsogolo lacimwemwe .
Ndiyeno , dziikileni zolinga zimene zingam’kondweletse .
Iye wakhala akuphunzila zocita za anthu kucokela pamene munthu woyamba analengedwa .
Mufunika kucitapo kanthu kuti mucipeze . ”
Yesu anati : “ Musamaope amene amapha thupi lokha , amene sangathe kucita zoposa pamenepa . ”
Usacite mantha kapena kuopa , pakuti Yehova Mulungu wako ali nawe kulikonse kumene upiteko . ” ( Yos .
( Miy . 26 : 24 , 25 ) Muzimvetsela kwa Yehova na kum’dalila m’zocita zanu zonse .
Nkhani yaciŵili idzaonetsa mmene Yehova nthawi zina amacitila zinthu m’njila imene sitinali kuyembekezela .
1 : 7 ) Molingana ndi mlimi , ifenso tifunika kuyembekezela moleza mtima .
Tingaphunzile ciani pa citsanzo ca mneneli Mika ?
( Ŵelengani Mika 7 : 1 - 3 . )
Ngati tili na cikhulupililo monga ca Mika , tidzayembekezela Yehova na mtima wonse .
Conco , ‘ timapilila zinthu zonse ndi kukhala oleza mtima ndiponso acimwemwe . ’
Abulahamu anafunika kuyembekezela kwa zaka zambili kuti adzukulu ake , Esau na Yakobo abadwe ( Onani palagilafu 9 , 10 )
( Ŵelengani Aheberi 11 : 8 - 12 . )
Koma ganizilani cabe cimwemwe cimene iye adzakhala naco akadzaukitsidwa m’paradaiso padziko lapansi .
Koma Mulungu anali ndi colinga cabwino , kuti apulumutse miyoyo ya anthu ambili ngati mmene akucitila panomu . ” ( Gen .
( b ) Nanga n’ciani cinam’thandiza kuyembekezela moleza mtima ?
Mtima wanga ukondwele cifukwa ca cipulumutso canu .
( Ŵelengani 2 Petulo 3 : 9 . )
N’ciani cidzatithandiza kukhala okonzeka kuyembekezela moleza mtima ?
Tiphunzilapo ciani pa zimene zinacitikila mtumwi Paulo ku Filipi ?
( Ŵelengani Machitidwe 16 : 8 - 10 . )
Atangofika ku Makedoniya , anaikidwa m’ndende .
Mosakayikila , Paulo anadzifunsa kuti : ‘ N’cifukwa ciani Yehova walola zimenezi kunicitikila ?
M’malomwake , onse aŵili Paulo na Sila , anayamba “ kupemphela ndi kutamanda Mulungu poimba nyimbo . ” ( Mac .
4 , 5 . ( a ) Kodi zimene zimaticitikila zingalingane bwanji na zimene zinacitikila Paulo ?
( b ) Kodi zinthu zinasintha bwanji pamene Paulo anali m’ndende ?
Kodi lomba tidzakambilana ciani ?
( Ŵelengani 1 Petulo 5 : 6 , 7 . )
Timafunika kucita zinthu mogwilizana ndi mapemphelo athu .
Anatumiza mngelo amene anapha asilikali 185,000 a Senakeribu pa usiku umodzi cabe .
( a ) Tiphunzilapo ciani pa zimene zinacitikila Yosefe ?
40 : 15 ; 41 : 39 - 43 ; 50 : 20 ) Mosakayikila , Yosefe sanayembekezele kuti Yehova angamuthandize mwanjila imeneyi .
Ganizilaninso za Sara , ambuye ake a Yosefe .
( Ŵelengani Yesaya 43 : 10 - 13 . )
Timadziŵa kuti Yehova amatikonda ndipo amafuna kuti zinthu zizitiyendela bwino .
N’ciani cingatithandize kuvula umunthu wakale ndi kusauvalanso ?
Podzafika mu 1939 , [ m’ndende zozunzilako anthu ] za Nazi munali Mboni za Yehova zokwana 6,000 . ”
Ndiponso anthu inu mwayeletsa bwino kwambili sitediyamuyi .
Koma koposa zonse , ndinudi gulu locokela m’mitundu yosiyana - siyana . ”
Kodi tidzaphunzila ciani m’nkhani ino ?
Koma pamene n’napitiliza kucita zaciwelewele , vuto langa lodziona kuti ndine wosafunika linakulila - kulila . ”
Sakura anapitiliza khalidwe loipali mpaka pamene anakwanitsa zaka 23 .
Iye anati : “ Pang’ono ndi pang’ono , n’nakhala na cizoloŵezi cotamba zamalisece .
N’ciani cinathandiza Stephen kuleka kupsa mtima ndi kukamba mau acipongwe ?
Iye anati : “ Zinthu zinayamba kuyenda bwino m’banja lathu .
Pali pano , Stephen ni mtumiki wothandiza , ndipo mkazi wake wakhala akucita upainiya wa nthawi zonse kwa zaka zambili .
Koma malemba amene ananilimbikitsa kusintha ndi Yesaya 55 : 7 , imene imati : ‘ Munthu woipa asiye njila yake , ’ ndi 1 Akorinto 6 : 11 , imene imakamba za anthu amene analeka makhalidwe oipa . Lembali limati : ‘ Ndipo ena mwa inu munali otelo . ’
Kwa zaka zambili , Yehova ananithandiza moleza mtima pogwilitsila nchito mzimu wake woyela kuti nivale umunthu watsopano . ”
Tifunikanso kupempha Mulungu kuti atipatse nzelu ndi mphamvu n’colinga cakuti tikwanitse kuseŵenzetsa mfundo za m’Baibo . ( Yos . 1 : 8 ; Sal . 119 : 97 ; 1 Ates .
M’nkhani ino , maina ena asinthidwa .
Onani mutu 25 m’buku lakuti Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa , Buku Loyamba .
( Ŵelengani Akolose 3 : 10 - 14 . )
Iye anakamba kuti palibe “ Mgiriki kapena Myuda , kudulidwa kapena kusadulidwa , mlendo , Msukuti , kapolo , kapena mfulu . ”
( a ) Kodi atumiki a Yehova afunika kuwaona bwanji anthu ena ?
( Onani pikica kuciyambi . ) ( b ) Nanga pakhala zotulukapo zanji ?
Ndiyeno , tsiku lina iye anapezeka pa msonkhano wa Mboni za Yehova .
Umadzionela wekha ubale wa padziko lonse ndi mgwilizano wapadela umene tili nawo . ”
Tikawaonetsa malemba monga Chivumbulutso 21 : 3 , 4 kapena Salimo 37 : 10 , 11 , 29 m’Baibo yawo ya Cipwitikizi , anali kucita cidwi ndipo nthawi zina anali kucita kugwetsa misozi ya cisangalalo . ”
Timamuyamikila ngako Yehova . ” — Ŵelengani Machitidwe 10 : 34 , 35 .
Kodi Yesu anapeleka citsanzo canji pankhani yokhala wofatsa ndi woleza mtima ?
Monga Yehova anakukhululukilani ndi mtima wonse , inunso teloni . ”
Ndiyeno , anawonjezela kuti : “ Mukapitiliza kukhala okondela , mukucita chimo . ”
N’cifukwa ciani tifunika kuvala cikondi ?
Kuwonjezela apo , cikondi “ n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima ” ndipo “ sicidzikuza . ”
Poonetsa kufunika kwa khalidweli , Paulo anakamba kuti popanda cikondi , sembe iye ‘ sali kanthu . ’
Cikondi cimeneci cikutanthauza kuti ife sitinakonde Mulungu , koma iye ndi amene anatikonda ndi kutumiza Mwana wake monga nsembe yophimba macimo athu . ” ( 1 Yoh .
Yesu anati : “ Palibe amene ali ndi cikondi cacikulu kuposa ca munthu amene wapeleka moyo wake cifukwa ca mabwenzi ake . ” ( Yoh .
Tiyeni tione mmene tingacitile zimenezo .
Mtumwi Yohane analemba kuti : “ Ana anga okondedwa , tisamakondane ndi mau okha kapena ndi pakamwa pokha , koma tizisonyezana cikondi ceniceni m’zocita zathu . ” ( 1 Yoh .
Koma n’nadzifunsa kuti , ‘ Ningatengele bwanji Yesu pocita zinthu na munthu ameneyu ? ’
Pambuyo poganizila zimene Yesu akanacita , n’nasankha kungoiŵalako nkhaniyo , osalimbana naye .
Patapita nthawi , n’namva kuti mnzangayo ali na matenda aakulu , ndipo amavutika kwambili na nkhawa .
Conco , n’naona kuti mwina analemba mesejiyo cifukwa covutika maganizo .
Kuganizila mmene Yesu anaonetsela cikondi ngakhale pamene anali kunyozedwa , kunanithandiza kunyalanyaza colakwa ca mnzanga wakunchito . ”
Pamene iye anacoka kumwamba , “ anasiya zonse zimene anali nazo ” ‘ mpaka kufa ’ cifukwa ca ise .
MTENDELE : ‘ Kulolelana m’cikondi ’ kumatithandiza kukhala pa mtendele , umene uli “ monga comangila cotigwilizanitsa . ” ( Aef .
Kodi si zoona kuti mtendele umenewu ni wapadela kwambili m’dzikoli , limene ni logaŵikana ? ( Sal .
Paulo analemba kuti : “ Cikondi cimamangilila . ” ( 1 Akor .
Tsiku lotsatila , anthu anaculuka kwambili pamsonkhanowo cakuti malo anacepa . ”
Pa cithunzico panali mau akuti : “ Anakhamukila m’miseu . ”
Conco , iwo anali kukwela mahosi kapena kuyenda na mendo masiku angapo kuti akafike kokwelela sitima , imene ikanawanyamula kupita kumene kukucitikila msonkhano .
Ku Mexico , anthu amene anapezeka pa Cikumbutso mu 2016 anali 2,262,646 .
Buku la Mateyu limafotokoza kwambili zocitika zokhudza Yosefe .
1 , 2 . ( a ) Ni mavuto ati amene amabwela cifukwa ca kusadziletsa ?
Tiyenelanso kupempha nzelu kwa Mulungu kuti tikambe na kucita zinthu mwanzelu .
Mungakonzekele bwanji kukaniza ziyeso ?
N’ciani cinacitikila m’bale wina ?
Kodi makolo angathandize bwanji ana awo kukhala odziletsa ?
Kodi mungathandize bwanji ana anu kukhala odziletsa ?
( Ŵelengani Ekisodo 34 : 5 - 7 . )
( b ) N’cifukwa ciani kuphunzila zimene Baibo imakamba ponena za khalidwe la cifundo n’kofunika ?
( a ) N’cifukwa ciani Yehova anatumiza angelo ku Sodomu ?
( Ŵelengani Ekisodo 22 : 26 , 27 . )
Baibo imati : “ Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiliza kuwatumizila macenjezo kudzela mwa amithenga ake . Anawatumiza mobwelezabweleza cifukwa ankamvela cisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala . ”
“ Anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambili . ”
Koma nchito yathu ni kuyesetsa kuthandiza anthu mmene tingathele .
3 : 8 ) Tanthauzo limodzi la liu lakuti cifundo ni “ kuvutikila pamodzi . ”
“ Limba mtima , ugwile nchitoyi mwamphamvu .
Kodi acicepele na makolo awo angaonetse bwanji kulimba mtima ?
1 , 2 . ( a ) Kodi Solomo anapatsidwa nchito iti yofunika kwambili ?
Kuti akwanitse nchitoyo , Solomo anafunika kukhala wolimba mtima ndi kugwila nchito mwamphamvu .
Kodi Solomo ayenela kuti anaphunzila ciani kwa atate wake pankhani ya kulimba mtima ?
( Ŵelengani 1 Mbiri 28 : 20 . ) .
Kodi kulimba mtima kwa Yesu kunawathandiza bwanji atumwi ?
( Ŵelengani 2 Timoteyo 1 : 7 . )
Tsopano tiyeni tikambilane mmene tingaonetsele kulimba mtima m’banja ndi mumpingo .
( b ) Kodi acicepele angatengele bwanji citsanzo ca Mose ?
M’zaka 100 zoyambilila , wacicepele Timoteyo anayesetsa kukwanilitsa zolinga zake zauzimu .
Iye analemba kuti : “ Pamene n’nali wamng’ono , n’nali wamanyazi kwambili .
Maka - maka kugogoda pa makomo a anthu osawadziŵa mu ulaliki , zinali kunivuta kwambili . ”
Mothandizidwa na makolo ake ndi ena mumpingo , mlongo wacicepeleyu anakwanilitsa colinga cake cokhala mpainiya wanthawi zonse .
Kodi malemba awa : Salimo 37 : 25 ndi Aheberi 13 : 5 , angathandize bwanji makolo ?
( Ŵelengani Salimo 37 : 25 ; Aheberi 13 : 5 . )
M’bale wina amene ali ndi ana aŵili anati : “ Makolo ambili amacita khama ndi kuwononga cuma cawo pothandiza ana awo kuti akhale akatswili a zamaseŵela ndi zosangalatsa zina , ndiponso kuti akhale ophunzila kwambili .
Niona kuti ni cinthu canzelu kwambili kucita khama ndi kugwilitsila nchito cuma cathu pothandiza ana kukwanilitsa zolinga zimene zidzawathandiza kukhalabe pa ubwenzi wabwino na Yehova .
Timasangalala kwambili kuona ana athu akukwanilitsa zolinga zawo zauzimu , ndipo zimakhala ngati kuti nafenso tikulandila nawo madalitso . ”
Fotokozani njila zina zimene tingaonetsele kulimba mtima mumpingo .
( Ŵelengani Tito 2 : 3 - 5 . )
( a ) Kodi abale obatizika angaonetse bwanji kulimba mtima ?
( Ŵelengani Afilipi 2 : 13 ; 4 : 13 . )
Tikukulimbikitsani abale nonse obatizika kuti mukhale olimba mtima , ndipo mugwile nchito mwamphamvu pothandiza mpingo .
Conco , ‘ limbani mtima , ndipo mugwile nchito mwamphamvu . ’
1 , 2 . ( a ) Kodi umoyo ukanakhala bwanji kukanakhala kuti kulibe Baibo ?
Mtumwi Petulo anagwila mau a pa Yesaya 40 : 8 .
( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 24 , 25 . )
( Ŵelengani Chivumbulutso 14 : 6 . )
M’mabaibo amene anapulintiwa pambuyo pake , dzina lakuti “ AMBUYE , ” lolembedwa m’zilembo zazikulu , limapezekanso m’mavesi ena a Malemba Acigiriki Acikhristu .
N’cifukwa ciani timayamikila kuti tili na Baibulo la Dziko Latsopano ?
( b ) Kodi Septuagint ya Cigiriki n’ciani ?
( Ŵelengani Salimo 119 : 162 - 165 . )
( Ŵelengani Yesaya 48 : 17 , 18 . )
Onani nkhani yakuti “ Kodi Muyenera Kuphunzira Chiheberi ndi Chigiriki ? ”
mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 2009 .
Pa April 3 , 2017 , nyumba yosungilamo Mabaibo akale na zinthu zina zakale zokhudzana ndi Baibo , inatsegulidwa ku likulu lathu ku Warwick , mumzinda wa New York , m’dziko la United States .
M’nyumba imeneyi , muli malo oonetselapo zinthu zakale zacikhalile . Pamalowo m’polemba kuti , “ Baibo na Dzina la Mulungu . ”
Tikuitanani kuti mukabwele kukaona nyumba yosungilamo zinthu zakale imeneyi , ndi malo ena osungilako zinthu zakale zokhudzana ndi Baibo , amene ali ku likulu lathu .
Pitani pa www.jw.org ndi kutumiza pempho lanu lodzaona malo .
Yendani pa ZOKHUDZA IFE > MAOFESI NDI KUONA MALO .
( Ŵelengani Aefeso 5 : 15 , 16 . )
Anaŵelenga 2 Akorinto 1 : 3 , 4 , imene imati : “ Tate wacifundo cacikulu ndi Mulungu amene amatitonthoza m’njila iliyonse , . . . amatitonthoza m’masautso athu onse . ”
Kodi abale amene amaphunzitsa papulatifomu ali na udindo wanji ?
Ndithudi , timamuyamikila kwambili Yehova cifukwa cotipatsa Mau ake , Baibo !
Onani bokosi yakuti “ Mmene Anasinthila . ”
Fotokozani lemba , pelekani fanizo , ndi kumveketsa bwino mmene tingaseŵenzetsele mfundo yake
“ Zinthu zinasintha pambuyo pa zaka 15 kucokela pamene n’nabatizika .
Tsiku lina , m’bale pokamba nkhani m’Nyumba ya Ufumu . . . , anaŵelenga lemba la Yakobo 1 : 23 , 24 .
Mavesi amenewa amayelekezela Mau a Mulungu na gilasi . Mau a Mulungu angatithandize kuti tizidziona monga mmene Yehova amationela .
N’nayamba kuzindikila kuti mmene nimadzionela si mmene Yehova amandionela .
Koma poyamba sin’nakhutile na mfundo imeneyi .
N’nali kuonabe kuti n’zosatheka Yehova kunikonda .
“ Patapita masiku ocepa , n’naŵelenga lemba limene linasinthalatu umoyo wanga .
Linali lemba la Yesaya 1 : 18 , pamene pali mau a Yehova akuti : ‘ Bwelani tsopano anthu inu .
Tiyeni tikambilane . . . Ngakhale macimo anu atakhala ofiila kwambili , adzayela kwambili . ’
N’namvela monga kuti Yehova akamba na ine kuti : ‘ Bwela Victoria , tiye tikambilane .
Nimakudziŵa , nimadziŵanso zolakwa zako , na mtima wako , ndipo nimakukonda . ”
“ Tsiku limenelo sin’nagone .
N’nali kukaikilabe kuti Yehova anganikonde . Kenako , n’nayamba kuganizila za nsembe ya dipo la Yesu .
Nthawi imeneyo , n’nazindikila kuti Yehova wakhala akunilezela mtima kwa nthawi yaitali . Anali kunicitila zinthu zambili zoonetsa kuti amanikonda .
Koma , zinali monga kuti ine nikumuuza kuti : ‘ Cikondi canu n’cosakwanila kwa ine .
Nsembe ya Mwana wanu siingakwanitse kuphimba macimo anga . ’
Zinali ngati kuti nikukana nsembe imene Yehova anapeleka na kuibweza kwa iye .
Koma cifukwa cosinkha - sinkha za mphatso ya dipo imeneyi , n’nayamba kuona kuti Yehova amanikondadi . ”
Nkhani izi zidzafotokoza masomphenya a Zekariya a namba 6 , 7 , na 8 .
Coyamba , lekani n’kuuzeni mmene umoyo wanga unalili poyamba .
N’NABADWILA m’tauni ya Hemsworth mu 1923 , ku Yorkshire , m’dziko la England .
Caka cotsatila , ine na mlongo Mary Henshall tinaikiwa kukhala apainiya apadela .
Tinatumiziwa ku gawo limene kunalibe ofalitsa , m’dela lochedwa Cheshire .
M’maŵa , tinali kudya cakudya cogwila pamimba .
Mlongosi wanga na mkazi wake , Lottie , anali kale ku Northern Ireland , kumene anali kutumikila monga apainiya apadela . Mu 1952 , tonse anayi tinacitila pamodzi msonkhano wacigawo ku Belfast .
Conco , tinafunafuna nyumba yokhalamo koma sitinaipeze cakuti usikuwo tonse tinagona m’motoka .
Cokondweletsa n’cakuti alimi anali kutikomela mtima potilola kuika kalavani yathu pafamu pawo .
Kukamba zoona , tinali kukondwela maningi m’nchito yadela .
Mu 1965 , m’dziko la Ireland munacitika msonkhano woyamba wa maiko .
Panapezeka anthu 3,948 , ndipo okwana 65 anabatizika .
Arthur akupeleka moni kwa M’bale Nathan Knorr atangofika pamsonkhano wacigawo wa mu 1965
Mu 1983 , Arthur atulutsa buku lakuti Buku Langa la Nkhani za M’baibo la Cigaeliki
Mu 2011 , zinthu zinasintha kwambili mu umoyo wathu pamene ofesi ya nthambi ya Britain ndi ya Ireland zinaphatikiziwa pamodzi .
M’zaka zapitazi , nakhala nikupsinjika maganizo ndi kuvutika na cisoni .
Arthur anali kunilimbikitsa nthawi zonse .
Koma mavuto onse amene napitamo , anicititsa kuyandikila kwambili kwa Yehova .
“ Tisamakondane ndi mau okha kapena ndi pakamwa pokha , koma tizisonyezana cikondi ceni - ceni m’zocita zathu . ” — 1 YOH . 3 : 18 .
Kodi “ cikondi copanda cinyengo ” cimatanthauza ciani ?
Kodi Yehova waonetsa bwanji cikondi copanda dyela kwa anthu ?
Iye analenga dziko kuti tikhalepo kwamuyaya .
( Yak . 2 : 21 ) Molingana ndi amuna okhulupilika amenewa , na ise tifunika kuonetsa cikondi , ngakhale kuti nthawi zina zingakhale zovuta .
6 , 7 . ( a ) Kodi “ cikondi copanda cinyengo ” cimatanthauza ciani ?
( Ŵelengani Mateyu 6 : 1 - 4 . )
Kodi cikondi ceni - ceni tingacionetse bwanji poceleza ena ?
( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 17 . )
( Ŵelengani Aroma 12 : 17 , 18 . )
Tingaonetse bwanji kuti takhululuka na mtima wonse ?
Kodi “ lupanga ” limene Yesu anakamba kuti adzabweletsa n’ciani ?
N’ciani cingakuthandizeni kukhalabe wokhulupilika kwa Yehova ngati abululu anu sagwilizana ndi kulambila koona ?
3 , 4 . ( a ) Kodi ziphunzitso za Yesu zimawakhudza bwanji anthu ?
Yesu anati : “ Musaganize kuti ndinabweletsa mtendele padziko lapansi , sindinabweletse mtendele koma lupanga .
Ndinabwela kudzacititsa munthu kutsutsana ndi bambo ake , mwana wamkazi kutsutsana ndi mayi ake , ndiponso mtsikana wokwatiwa kutsutsana ndi apongozi ake aakazi .
Kodi Akhristu angaphunzitse bwanji ana awo kuti azilemekeza kholo losakhulupilila ?
M’malomwake , afotokozeleni kuti munthu aliyense ali na ufulu wosankha kutumikila Yehova kapena ayi .
Baibo imakamba kuti : “ Nthawi zonse mau anu azikhala acisomo . ”
( Ŵelengani 1 Petulo .
Mungacite ciani ngati mumadela nkhawa kuti zocita zanu zidzakhumudwitsa abululu anu ?
Amodzi mwa malo ocitilapo ulaliki wapoyela ku Lagos , mzinda wokhala na anthu ambili mu Africa .
Kodi zinthu panthawiyo zinali bwanji pakati pa Aisiraeli ?
( Ŵelengani Zekariya 1 : 3 , 4 . )
Caputa 5 ya buku la Zekariya imayamba na masomphenya ocititsa cidwi kwambili .
( Ŵelengani Zekariya 5 : 1 , 2 . )
8 - 10 . ( a ) Kodi lumbilo n’ciani ?
Tiphunzilapo ciani pa masomphenya a namba 6 a Zekariya ?
( Ŵelengani Zekariya 5 : 5 - 8 . )
( Ŵelengani Zekariya 5 : 9 - 11 . )
Kodi mumamvela bwanji mukaganizila za nchito yaikulu kwambili yomanga imene icitika masiku ano ?
( Ŵelengani Zekariya 6 : 1 - 3 . )
Yehova akali kuseŵenzetsa angelo poteteza na kulimbikitsa anthu ake
7 , 8 . ( a ) Kodi mapili aŵili amkuwa aimila ciani ?
( b ) N’cifukwa ciani ni amkuwa ?
M’Baibo , mapili nthawi zina amaimila maufumu , kapena maboma .
Kodi okwela pa magaleta n’ndani ? Nanga anapatsiwa nchito yanji ?
( Ŵelengani Zekariya 6 : 5 - 8 . )
( Ŵelengani Zekariya 6 : 9 - 12 . )
Kodi Yehova anawatsimikizila za ciani Ayuda ?
Yehova sadzaiŵala ngakhale pang’ono cikondi cimene timamuonetsa !
ATATE ake John anabatizika n’kukhala Mboni ya Yehova cakumapeto kwa zaka za m’ma 1950 , m’tauni yaing’ono ku Gujarat , m’dziko la India .
Mlongoyo anaona kuti John anali atadziceka pacala .
Iye anapita kwa wansembe wa ku chechi kwawo kukam’funsa mafunso amodzi - modzi amene anakambilana ndi mlongo uja .
Ni pati m’Baibo pamene pamakamba kuti Yesu si Mulungu ?
Nanga ni pati pamene pamakamba kuti sitifunika kulambila Mariya ?
Tingaphunzilepo zambili pa makonzedwe a mizinda yothaŵilako ya ku Isiraeli wakale .
Kodi kuimba n’kofunika bwanji pa kulambila koona ?
Koma mau a m’nyimbo zoimba pakamwa amacititsa munthu kumvela bwino . ”
( b ) Kodi tiyenela kuimba bwanji nyimbo zotamanda Yehova ?
Ŵelengani mau a m’nyimboyo mokweza ndi mwamphamvu .
( a ) N’ciani cina cimene tingacite kuti tiziimba mwamphamvu na mokweza ?
( a ) Kodi pamsonkhano wa pacaka wa mu 2016 panalengezedwa ciani ?
Nyimbo zimenezi muziziphunzila pa kulambila kwanu kwa pabanja ( Onani palagilafu 18 )
( Ŵelengani Numeri 35 : 24 , 25 . )
Pokumbukila zimene zinacitikazo , iye anati : “ Kukamba zoona , n’nali kucita mantha kuulula chimo langa kwa akulu .
Iye analemba kuti : “ Taonani zimene cisoni cogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu cimeneci cakucitilani . Cakucititsani kukhala akhama kwambili , cakucititsani kudziyeletsa , kuipidwa , mantha , kufunitsitsa kulapa , kudzipeleka , ndiponso kukonza colakwaco . ” ( 2 Akor .
Nkhani yanga itasamalidwa , n’naleka kudziimba mlandu .
Ngati Mulungu wakukhululukila chimo , ndiye kuti latha .
Monga mmene Yehova anakambila , amacotsa zolakwa zathu na kuziika kutali kwambili na ise cakuti sitingakwanitse kuzionanso . ”
N’cifukwa ciani muyenela kuthaŵila kwa Yehova ?
Tingatengele bwanji cifundo ca Yehova ngati ena atilakwila ?
1 , 2 . ( a ) Kodi Yesu anali kuciona bwanji Cilamulo ca Mulungu ?
( b ) Kodi zimenezi zitiphunzitsa ciani za Yehova ?
( Ŵelengani Machitidwe 20 : 26 , 27 . )
( Ŵelengani Numeri 35 : 20 - 24 . )
Conco pitani mukaphunzile tanthauzo la mau akuti , ‘ Ndikufuna cifundo , osati nsembe . ’
Cifukwa ine sindinabwele kudzaitana anthu olungama , koma ocimwa . ” ( Mat .
Iwo sanabwele kunyumba kwa Mateyu kudzadya cakudya cabe .
Pa zimene taphunzila zokhudza mizinda yothaŵilako , ni mfundo ziti zimene mufuna kuseŵenzetsa mu umoyo wanu ?
Alongo aŵili akulalikila uthenga wa m’Baibo kwa munthu wamalonda m’tauni ya Tipitapa
Ni malangizo anji amene mtumwi Paulo anapeleka ponena za maganizo a anthu a m’dzikoli ?
Chulani citsanzo ca maganizo a dziko na kufotokoza mmene tingapewele kutengela maganizo aconco .
Samalani : mwina wina angakugwileni ngati nyama , mwa nzelu za anthu ndi cinyengo copanda pake , malinga ndi miyambo ya anthu , malinganso ndi mfundo zimene zili maziko a moyo wa m’dzikoli , osati malinga ndi Khristu . ”
“ Ningakhalebe munthu wabwino popanda kukhulupilila Mulungu . ”
“ Munthu angakhale wacimwemwe olo kuti sali m’cipembedzo . ”
Lamulo la Mulungu n’lakuti mwamuna na mkazi okwatilana ndiwo okha ayenela kugonana .
Tsopano ngati diso lako lakumanja limakucimwitsa , ulikolowole ndi kulitaya . ” ( Mat .
Paja Yesu anati : “ Kapolo sangatumikile ambuye aŵili , pakuti adzadana ndi mmodzi ndi kukonda winayo , kapena adzakhulupilika kwa mmodzi ndi kunyoza winayo .
( Ŵelengani 1 Atesalonika 2 : 13 , 19 , 20 . )
“ Anthu angakwanitse kuthetsa mavuto awo . ”
Mungacite ciani kuti nonse m’banja lanu mukapeze mphoto ?
( b ) N’ciani cimatithandiza kuyang’anabe pa mphoto ?
Kodi tingadziteteze bwanji pa zocitika zimene zingatiike pa ciyeso ?
Kuti tithetse zilakolako zoipa , tifunika kupewa zosangalatsa zoipa .
Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana ndi mtima wonse , ngati wina ali ndi cifukwa codandaulila za mnzake .
Monga Yehova anakukhululukilani ndi mtima wonse , inunso teloni .
( Ŵelengani Mlaliki 7 : 21 , 22 . )
10 , 11 . ( a ) N’cifukwa ciani nsanje ni yoopsa ?
Mau a Mulungu amati : “ Cikondi n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima .
23 : 16 - 18 ) Na ise tiyenela kukhala okoma mtima ndi acikondi ngati Yonatani .
Inu amuna , musaleke kukonda akazi anu ndipo musamawapsele mtima kwambili .
Ananu , muzimvela makolo anu pa zinthu zonse , pakuti kucita zimenezi kumakondweletsa Ambuye .
Inu abambo , musamakwiyitse ana anu , kuti angakhale okhumudwa . ” ( Akol .
Kodi mwamuna wacikhristu ayenela kucita ciani ngati mkazi wake amene si Mboni samulemekeza ?
Mau a Mulungu amati : “ Aliyense wosalankhulapo mau ake ndi wodziŵa zinthu , ndipo munthu wozindikila amakhala wofatsa . ”
Nkhani zimenezi zidzalimbitsa cikhulupililo canu cakuti akufa adzauka .
11 : 11 .
Ni nkhani za m’Baibo ziti zimene zinacititsa Marita kukhulupilila kuti akufa adzauka ?
Mofanana na Marita , kodi imwe muyembekezela cocitika cokondweletsa citi cam’tsogolo ?
Koma anakamba kuti , “ Ndikudziŵa kuti adzauka . ”
17 : 8 - 16 ) Patapita nthawi , mwana wake anadwala mpaka kufa .
Mulungu anamvela pemphelo la Eliya , ndipo mwanayo anakhalanso na moyo .
( Ŵelengani 1 Mafumu 17 : 17 - 24 . )
( Ŵelengani 2 Mafumu 4 : 32 - 37 ) Mzimayiyo ayenela kuti anakumbukila pemphelo la Hana , mkazi amene poyamba anali wosabeleka .
Kodi Petulo anam’thandiza bwanji mlongo wacikhristu amene panthawiyo anali atamwalila ?
Tsiku lina , mtumwi Paulo anali pa msonkhano m’cipinda capamwamba ku Torowa , kumene manje ni kumpoto ca kum’madzulo kwa dziko la Turkey .
Mnyamata wina dzina lake Utiko anali kumvetsela atakhala pawindo .
13 : 14 - 16 ; 18 : 18 ; Aroma 4 : 17 , 18 ) Komanso , Yehova anakamba kuti mbeuyo ‘ idzacokela mwa Isaki . ’ ( Gen .
( Ŵelengani Aheberi 11 : 17 - 19 . )
89 : 48 ) Koma izi sizitanthauza kuti Mulungu angalephele kuukitsa munthu wakufa .
( Ŵelengani Yobu 14 : 13 - 15 . )
( b ) N’cifukwa ciani cikhulupililo cakuti akufa adzauka n’cofunika kwambili ?
Koma kodi mungachule ciyembekezo ca kuuka kwa akufa monga cimodzi mwa zikhulupililo zanu zofunika ngako ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 12 - 19 . )
Komabe , tidziŵa kuti Yesu anaukitsidwa .
Kodi ulosi wa mu Salimo 118 unakwanilitsika bwanji pa Yesu ?
‘ Omanga nyumba anam’kana ’ Mesiya ( Onani palagilafu 7 )
Kodi Yesu anakhala bwanji “ mwala wofunika kwambili wapakona ” ?
Popeza kuti Yesu anakaniwa ndipo anaphedwa , kodi zikanatheka bwanji kuti iye akhale “ mwala wofunika kwambili wapakona ” ?
( a ) Kodi lemba la Salimo 16 : 10 linalosela ciani ?
Simudzalola kuti wokhulupilika wanu aone dzenje . ”
( Ŵelengani Machitidwe 2 : 29 - 32 . )
( Ŵelengani Machitidwe 2 : 33 - 36 . )
( Ŵelengani Machitidwe 13 : 32 - 37 , 42 . )
Inde , pali zinthu zina zokhudza “ nthawi kapena nyengo zimene Atate waziika pansi pa ulamulilo wake . ” ( Mac . 1 : 6 , 7 ; Yoh .
Paulo analemba kuti , “ Khristu anaukitsidwa kwa akufa , n’kukhala cipatso coyambilila ca amene akugona mu imfa . ”
N’ciani cidzacitikila ena mwa odzozedwa pa nthawi ya kukhalapo kwa Khristu ?
Pakuti ngati timakhulupilila kuti Yesu anafa ndi kuukanso , ndiye kuti amenenso agona mu imfa . . .
Mulungu adzawasonkhanitsa kuti akhale naye limodzi . . . Ife amoyofe amene tidzakhalapo pa nthawi ya kukhalapo kwa Ambuye , sitidzakhala patsogolo pa amene agona mu imfa . Cifukwa Ambuye mwini adzatsika kumwamba , ndi mfuu yolamula . . . Ndipo amene anafa mwa Khristu adzauka coyamba .
Odzozedwa amene adzakhala na moyo pa nthawi ya cisautso cacikulu ‘ adzatengedwa m’mitambo . ’
Ukabwelanso , nidzakuthyola miyendo . ”
N’nabadwa pa July 29 , 1929 , ndipo n’nakulila m’mudzi wina umene uli m’cigawo ca Bulacan , ku Philippines .
N’nali kukonda kuŵelenga Baibo , maka - maka mabuku anayi a Uthenga Wabwino .
Kucita izi kunanisonkhezela kutsatila citsanzo ca Yesu . — Yoh . 10 : 27 .
Ca panthawi imeneyo , makolo anga ananiuza kuti nibwelele ku nyumba .
Wacikulile wina wa Mboni anafika pa nyumba pathu , ndipo anatifotokozela zimene Baibo imakamba ponena za “ masiku otsiliza . ” ( 2 Tim .
3 : 1 - 5 ) Iye anatipempha kuti tikapezekepo pa phunzilo la Baibo m’mudzi wina wapafupi .
Madzulo a tsikulo , tinakambilana kwambili nkhani zokhudza Baibo .
Ine n’nayankha kuti , “ Inde , nifuna . ”
N’nali kufuna ‘ kutumikila Ambuye wathu , Khristu , monga kapolo . ’
( Akol . 3 : 24 ) Conco , pa February 15 , 1946 , ine na mnzanga wina tinabatizika mu mtsinje wina wapafupi .
Ndiyeno , banja la m’bale Cruz linanipempha kuti nikakhale nawo ku Angat .
Nkhaniyo anaikamba m’Cizungu .
M’mamaŵa , n’nali kuthandizila nchito yophika cakudya .
Pamene tinatsiliza maphunzilo a Giliyadi , n’natumiziwa ku Bronx , mu mzinda wa New York , kukatumikila monga mpainiya wapadela wogwilizila .
Wiki yotsatila , tinapita kukacezela mpingo wa pa cisumbu ca Rapu Rapu .
Tinafika mpaka pogula malo a munthu uja amene anakamba kuti , “ Ise Machainizi sitigulitsa malo . ”
Zikakhala conco , dzilalo lingayambe kukulila m’cubu yopita ku cibalilo , ( monga mimba yokhala pa malo olakwika ) , kapena lingayende n’kukaloŵa m’cibalilo .
Komabe , akatswili amakamba kuti zaconco sizicitika - citika .
Buku lofalitsidwa na bungwe lina la zaumoyo ku Britain linati : “ Ma IUD okhala na kopa yambili ni odalilika ngako cakuti ciŵelengelo ca azimayi amene satenga mimba ngati amaseŵenzetsa njilayi cimapitilila 99 pelesenti .
Izi zitanthauza kuti ciŵelengelo ca azimayi amene angatenge mimba pa caka ngati aseŵenzetsa ma IUD aconco sicifika ngakhale 1 pelesenti .
Koma ma IUD okhala na kopa yocepa , amakhalanso ocepelako mphamvu . ” — England’s National Health Service .
( a ) Kodi ‘ kukhulupilila pambuyo pokhutila nazo ’ kumatanthauzanji ?
( b ) Tidziŵa bwanji kuti Timoteyo anakhutila na uthenga wabwino wokamba za Yesu ?
Kukamba zoona , timakhalako na nkhawa ngati iye avomeleza zilizonse popanda kufunsa mafunso . ”
Kodi zimene Baibo imakamba pankhaniyi amazikhulupilila ?
N’ciani cina cofunika pophunzitsa ana anu ?
Stephanie , amene ni kholo la ana atatu , anati : “ Kucokela pamene ana anga anali aang’ono , nakhala nikudzifunsa kuti , ‘ Kodi nimawauza ana anga cifukwa cake ine nimakhulupilila kuti Yehova aliko , amatikonda komanso kuti mfundo zake n’zabwino ?
Kodi ana anga amaona kuti ine nimam’kondadi Yehova ? ’
Siningayembekezele ana anga kukhulupilila zinthu zimene ine sinizikhulupilila . ”
Baibo imakamba kuti “ ucitsilu umakhazikika mumtima mwa mwana . ” ( Miy .
2 : 12 ) Kucita zinthu mwanjila imeneyi kumaonetsa kuti ali na nzelu zimene n’zofunika kuti akapulumuke .
Kodi makolo angathandize bwanji ana awo kukhala na ‘ nzelu zowathandiza kuti akapulumuke ’ ?
Pitani pa peji ya Chichewa ya jw.org , na kuona pa ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > ZOKUTHANDIZANI POPHUNZIRA BAIBULO .
Kodi mungakonze bwanji cipulumutso canu ?
Ena mwa iwo analeledwa na makolo amene ni Mboni .
Koma pambuyo pa zaka zingapo , pamene cilakolako cake cakugonana cikhala camphamvu kwambili , angayambe kukayikila ngati kumvela malamulo a Yehova n’kwabwino nthawi zonse . ”
( b ) Kodi tiphunzilapo ciani pa lemba la Afilipi 4 : 11 - 13 ?
Kodi kukonza cipulumutso canu “ mwamantha ndi kunjenjemela ” kutanthauza ciani ?
Ni zida ziti zimene zimakuthandizani pa phunzilo lanu laumwini ?
Yesu anati : “ Palibe munthu angabwele kwa ine akapanda kukokedwa ndi Atate amene anandituma ine . ” ( Yoh .
Nimaona kuti na ine nifunika kukamba momasuka nanzanga .
Conco , mkati mokambilana nkhani inayake , nimakambako tumau monga twakuti , ‘ Tsiku lina pamene n’nali kuphunzitsa anthu Baibo , . . .
’ Kenako , nimapitiliza na nkhaniyo .
Olo kuti nkhani imene tinali kukambilana siinali yokhudzana na Baibo , nthawi zambili anzanga amacita cidwi ndipo amafuna kudziŵa zimene nimacita pophunzitsa anthu Baibo .
Pamene niseŵenzetsa njila imeneyi kaŵili - kaŵili , m’pamenenso zimakhala zosavuta kulalikila .
Ndipo nikatelo , nimamvela bwino ngako ! ”
M’malomwake , anayamba kuganizila kuti : “ Acicepele ambili sadziŵa zambili zokhudza Mboni za Yehova .
Conco , zimene timacita zingapangitse kuti amvetsele uthenga wathu kapena ayi .
Bwanji ngati timacita manyazi na mantha , kapena ngati sitimasuka pofotokoza zimene timakhulupilila ?
Ndiye kuti iwo angayambe kuona kuti sitinyadila kukhala a Mboni za Yehova .
Mwina angafike mpaka potinyoza cifukwa coona kuti timacita zinthu modzikayikila .
Koma ngati tikamba momasuka na molimba mtima pofotokozela anzathu zimene timakhulupilila , monga kuti tikuceza nawo cabe , iwo angayambe kutilemekeza . ”
Yesu anati : “ Ngati munthu akufuna kunditsatila , adzikane yekha ndi kunyamula mtengo wake wozunzikilapo ndipo anditsatile mosalekeza . ” ( Mat .
Ni mfundo yanji imene tingaphunzilepo pa Yesaya 40 : 26 ?
Palibe munthu amene angakwanitse kuŵelenga nyenyezi zonse kumwamba .
Tidziŵa bwanji kuti Yehova angakwanitse kutipatsa mphamvu zotithandiza kupilila mavuto ?
Ndipo anapitiliza kuti : “ Mudzatsitsimulidwa , pakuti goli langa ndi lofewa ndipo katundu wanga ndi wopepuka . ”
( Mat .
Koma kodi timamvela bwanji tikabwelako ?
Nkhaniyo inakambiwa mogwila mtima na mwaubwenzi cakuti n’nakhudzidwa kwambili mpaka kugwetsa misozi .
N’nakumbutsidwa kuti kupezeka pa misonkhano n’kofunika ngako . ”
Kodi mtumwi Paulo anatanthauzanji pamene analemba kuti : “ Pamene ndili wofooka , m’pamene ndimakhala wamphamvu ” ?
Iye anaimba kuti : “ Ndi thandizo lanu , ndingathamangitse gulu la acifwamba . Ndi thandizo la Mulungu wanga ndingakwele khoma . ”
Kapena tidzatsatila malangizo anzelu a m’Baibo akuti tiyenela kuthetsa nkhani mwamsanga ?
” Ngati zokambilana zanu sizinayende bwino kweni - kweni , yesani kusakila mpata wina wabwino wokakamba naye kuti mukhazikitse mtendele .
Pakuti dzanja lanu linali kundilemela usana ndi usiku . ”
Ndipo inu munandikhululukila zolakwa zanga ndi macimo anga . ” ( Sal .
( 4 ) Kodi kudzakhala Cikumbutso cothela ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 13 : 5 . )
( Ŵelengani Yohane 3 : 16 ; 17 : 3 . )
( a ) Kodi Yesu anapemphelela ciani pa tsiku limene anayambitsa Mgonelo wa Ambuye ?
( b ) N’ciani cimaonetsa kuti Yehova anayankha pemphelo la Yesu ?
( Ŵelengani Yohane 17 : 20 , 21 . )
( Ŵelengani Ezekieli 37 : 15 - 17 . )
Kodi tingalimbitse bwanji mgwilizano pakati pa anthu a Mulungu ?
Tingaonetse bwanji kuti ‘ timalolelana m’cikondi ’ ?
Tidziŵa bwanji kuti kudzakhala Cikumbutso cothela ?
Abale aŵili na azikazi awo akupakila mabuku m’ndeke ku Riberalta , m’cigawo ca Beni .
N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizim’patsako cuma cathu olo kuti zonse ni zake ?
Kodi gulu la Mulungu limaseŵenzetsa bwanji zopeleka masiku ano ?
N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizim’patsako cuma cathu olo kuti zonse ni zake ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 8 : 18 - 21 . )
Zopeleka zanu zimathandiza pa nchito ya padziko lonse ( Onani palagilafu 14 - 16 )
Mwa ici , nthawi zina timadziona monga tili kwa tekha , ndipo timaiwala zinthu zambili zimene Yehova akucita m’gulu lake .
Koma tikaonelela mapulogilamu a JW Broadcasting , timakumbukila kuti tili m’gulu la abale a pa dziko lonse .
Abale na alongo athu okondedwa amakondwela ngako na JW Broadcasting .
Nthawi zambili amakamba kuti akaonelela mapulogilamu apamwezi , amamvela kuti ali pafupi na abale a m’Bungwe Lolamulila .
Tsopano amanyadila kwambili kukhala m’gulu la Mulungu . ”
( Ŵelengani Miyambo 11 : 24 , 25 . )
Yesu anati : “ Uzikonda mnzako mmene umadzikondela wekha . ”
Amene amakonda mkazi wake amadzikonda yekha , pakuti palibe munthu anadapo thupi lake , koma amalidyetsa ndi kulikonda . ” ( Aef .
Tingapewe bwanji kukhala odzikonda ?
Paulo analemba kuti anthu adzakhala “ okonda ndalama . ”
Munthuyo anatenga kacikwama kake , na kutulutsamo ndalama .
Kodi Aguri analemba ciani ponena za cuma na umphawi ?
Iye anafotokoza kuti : “ Kuti ndisakhute kwambili n’kukukanani kuti : ‘ Kodi Yehova ndani ? ’ ”
Anali kukonda kukamba kuti : ‘ Ine nimaseŵenzela bwana wabwino ngako ! ’
Koma popeza tonse lomba ndise apainiya , timaseŵenzela Bwana mmodzi , Yehova . ”
Tingapewe bwanji kukhala okonda ndalama ?
Koma imatanthauza kuti sam’konda ngakhale pang’ono . ”
Tingapewe bwanji kukhala okonda zosangalatsa ?
( Ŵelengani 2 Timoteyo 3 : 1 - 5 , 13 . )
3 : 12 ) Komanso , timadziŵa kuti cikondi “ sicidzitama , sicidzikuza . ”
N’nali kuona kuti amanikonda , ndipo zimenezo zinanilimbikitsa kuti nizicita zinthu zowakondweletsa . ”
( Ŵelengani Yohane 13 : 34 , 35 . )
Anali kucilitsa akhungu , olumala , akhate , na ogontha .
( Ŵelengani Yesaya 11 : 6 , 7 . )
Mungaŵelenge za ena mwa anthu amenewa , m’nkhani za pa jw.org , za mutu wakuti “ Baibo Imasintha Anthu . ”
Sitiyenela kudzibisa kuti ndise a Mboni za Yehova .
3 Tengelani Cikhulupililo ndi Kumvela kwa Nowa , Danieli , na Yobu
28 Cimwemwe — Khalidwe Locokela kwa Mulungu
9 , 10 . ( a ) Kodi tingatengele bwanji cikhulupililo ndi kumvela kwa Nowa ?
( Ŵelengani Malaki 3 : 17 , 18 . )
( b ) Kodi Yehova anali kumuona bwanji Danieli ?
( b ) Kodi makolo masiku ano angatengele bwanji citsanzo ca makolo a Danieli ?
( Ŵelengani Yobu 1 : 9 , 10 . )
19 , 20 . ( a ) Tingatengele bwanji cikhulupililo ndi kumvela kwa Yobu ?
1 - 3 . ( a ) N’ciani cingatithandize kukhalabe okhulupilika kwa Mulungu m’masiku otsiliza ano ?
( Ŵelengani Danieli 6 : 7 - 10 . )
( Ŵelengani Salimo 11 : 5 ; 26 : 4 . )
( Sal . 1 : 1 - 3 ) Cotelo , dzifunseni kuti , ‘ Kodi nimam’dziŵa Yehova monga mmene Nowa , Danieli , na Yobu anali kum’dziŵila ? ’
Nayenso Inoki , ambuye awo a atate ake a Nowa , “ anayenda ndi Mulungu woona . ”
( Gen . 22 : 15 - 18 ; Aheb .
Siningakwanitse kufotokoza cimwemwe cimene tili naco . ”
Pakuti mwa mzimu wake , Mulungu anaululila ifeyo zinthu zimenezi . ” ( 1 Akor .
Yesu anati : “ Ndalankhula zinthu izi kwa inu , kuti cimwemwe canga cikhale mwa inu , ndi kuti cimwemwe canu cisefukile . ” ( Yoh .
( 3 ) Kodi kuyetsetsa kukhala na “ maganizo a Khristu ” kungatithandize bwanji kukhala anthu auzimu ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 14 - 16 mau amunsi . )
Kodi Baibo imakamba ciani ponena za anthu okonda zinthu zauzimu ?
Kodi tingaphunzile ciani pa citsanzo ca Yakobo ?
Kodi tingaphunzile ciani pa citsanzo ca Mariya ?
( Ŵelengani Luka 1 : 46 - 55 . )
( Ŵelengani Yesaya 63 : 9 ; Maliko 6 : 34 . )
Koma kuphunzila coonadi kunanilimbikitsa kusintha na kukhala munthu wauzimu .
Kusintha sikunali kopepuka , koma n’tasintha n’napeza cimwemwe ndipo lomba nimaona kuti moyo wanga uli na colinga . ”
Motelo , kutsatila citsanzo Yesu kumatithandiza kumuyandikila kwambili Yehova .
Ophunzilawo anati : “ Ife ndife mboni za zinthu zonse zimene anacita . ” ( Mac .
Kodi kukhala na maganizo ofanana ndi a Khristu kungakhudze bwanji umoyo wathu wa tsiku na tsiku ?
Iye anati : “ Sin’nacite colakwa ciliconse , koma n’nali kucita zinthu zauzimu mwamwambo cabe .
N’nali kupezeka pa misonkhano yonse , ndipo n’nali kucitako upainiya wothandiza kangapo pa caka .
Iye anati : “ Zinali monga kuti sin’nali kudziŵa ciliconse .
N’nayamba kuganiza kuti , ‘ Monga mutu wa mkazi wanga , nifunika kuwongolela . ’ ”
Iye anakamba kuti : “ N’nayamba kuŵelenga kwambili Baibo , ndipo m’kupita kwa nthawi n’namvetsetsa mfundo za coonadi .
N’nakhala na cidziŵitso , ndipo koposa zonse , ubwenzi wanga na Yehova unalimba . ”
( 3 ) Kodi kukhala munthu wolimba mwauzimu kungatithandize bwanji mu umoyo wathu wa tsiku na tsiku ?
( b ) Tiyenela kukhala na colinga canji tikamaphunzila na kusinkha - sinkha Mau a Mulungu ?
( b ) Nanga ni citsanzo citi ca m’Baibo cimene tingatengele ?
12 , 13 . ( a ) N’ciani cingatithandize “ kukhala ndi maganizo amene Khristu Yesu anali nawo ” ?
( Ŵelengani 2 Petulo 1 : 5 - 8 . )
Kodi kukhala munthu wauzimu kumakhudza bwanji umoyo wathu ?
Kodi ni “ nchito zakufa ” ziti zimene tifunika kupewa ?
Kodi zosankha zanga zidzanithandiza kukhala na zolinga zauzimu ?
N’cifukwa ciani ndimwe ofunitsitsa kupita patsogolo mwauzimu ?
Mtumwi Petulo anauza Akhristu a m’nthawi yake kuti : “ Muzicelezana popanda kudandaula . ” ( 1 Pet .
Nyamuka , ubatizidwe . ” — MAC . 22 : 16 .
Kodi makolo acikhristu amafuna kutsimikizila ciani ana awo asanabatizike ?
POFOTOKOZA zimene zinacitika atapanga cosankha cobatizika , mlongo Blossom Brandt anati : “ Kwa miyezi ingapo n’nali kuuza atate na amayi kuti nifuna kubatizika , ndipo iwo nthawi zambili anali kukamba nane za nkhaniyi .
Iwo anali kufuna kutsimikizila ngati n’nali kudziŵadi kuti kubatizika ni nkhani yaikulu .
Tsiku la cocitika capadela cimeneci mu umoyo wanga , linafika pa December 31 , 1934 . ”
5 , 6 . ( a ) Kodi zimene Baibo imakamba zokhudza Timoteyo zitiphunzitsa ciani pa nkhani ya ubatizo ?
( Ŵelengani Akolose 1 : 9 , 10 . )
Iwo anauza Yehova kuti akondwela ngako kuti ine mwana wawo wamng’ono nasankha kupeleka moyo wanga kwa iye . ”
( Ŵelengani 1 Petulo 3 : 20 , 21 . )
N’cifukwa ciani sitifunika kukakamiza aliyense kuti abatizike ?
Tidzakambilana mafunso ati m’nkhani yotsatila ?
Ngati ndimwe kholo , mwina munadzifunsapo kuti : ‘ Kodi mwana wanga ni wokonzekadi kubatizika ?
Funso loyamba limakhala lakuti , “ Pamaziko a nsembe ya Yesu Khristu , kodi munalapa macimo anu na kudzipeleka kwa Yehova kuti mucite cifunilo cake ? ”
Pa misonkhano yathu , tingaonetse bwanji kuti ndise oceleza ?
( Ŵelengani 3 Yohane 5 - 8 . )
Iye analemba kuti : “ Poyamba n’nali kuyopa kulandila alendo cifukwa tinali titangokwatilana kumene , ndipo tinali kukhala m’nyumba yaing’ono .
Koma tinakondwela ngako kukhala na abale na alongo amenewo .
Monga okwatilana kumene , tinaona cimwemwe cimene anthu amakhala naco ngati akutumikila Yehova mogwilizana na kuyesetsa kukwanilitsa zolinga zawo zauzimu pamodzi . ”
N’cifukwa ciani tifunika kuceleza ofalitsa amene akukila mu mpingo mwathu ?
( Ŵelengani Luka 10 : 41 , 42 . )
Tsiku lina , mkazi wanga anayewa kwambili ku nyumba .
N’nayesetsa kumulimbikitsa , koma sizinathandize .
Ndiyeno , ca m’ma 19 : 30hrs tinamva kugogoda pakhomo .
Iye anabwela kudzationa .
Tinamuuza kuti aloŵe , ndipo tinamupatsa madzi akumwa .
Ngati mumaopa kuceleza alendo , dziŵani kuti si ndinu nokha .
Mkulu wina wa ku Britain anati : “ Nthawi zina , munthu angakhale na nkhawa pamene akukonzekela kulandila alendo .
Koma molingana na zinthu zina zimene timacita potumikila Yehova , kuceleza ena kumatibweletsela mapindu na cimwemwe coculuka .
Ine nthawi zina nimamwa cabe khofi na alendo , kwinaku tikuceza . ”
Mkulu winanso analemba kuti : “ Kuceza na abale a mu mpingo mwathu ku nyumba kwanga kumanipatsa mwayi wowadziŵa bwino , maka - maka kudziŵa mmene anaphunzilila coonadi . ”
Koma mkazi wa mmodzi wa alangizi a sukuluzi ananilimbikitsa ngako .
Anakamba kuti pamene iye na mwamuna wake akutumikila m’dela , amakondwela kwambili akapita kukaceza kwa munthu wauzimu , olo wosauka , amene ali na umoyo wosalila zambili , ndipo amaika mtima wake wonse pa kutumikila Yehova .
Izi zinanikumbutsa zimene amayi anali kutiuza pamene tinali ana . Anali kukamba kuti ‘ Ni bwino kudya zamasamba pamene pali cikondi . ’ ” ( Miy .
( Ŵelengani Miyambo 25 : 21 , 22 . )
Nthawi zambili , anthu amene aitana alendo amakonzekela bwino ( Onani palagilafu 20 )
Wamasalimo Davide anafunsa kuti : “ Inu Yehova , ndani amene angakhale mlendo m’cihema canu ? ”
Cinanso , ni bwino kulemekeza cikhalidwe ca kwanuko .
Koma m’zikhalidwe zina , kukana ciitano kumaoneka monga n’kusayamikila .
Abale aŵili akugaŵila kapepa kauthenga kwa munthu wogwila nchito yopenta , pa ulalo wa pafupi na malo a citetezo camphamvu ochedwa Kaštilac , amene anamangidwa m’zaka za m’ma 1500 C.E . Malowa ali pafupi na mzinda wa Split
( Ŵelengani Tito 2 : 11 - 14 . )
Mkuluyo anati : “ Graham anali na khalidwe lonyada .
Anali kupeza zifukwa akulu amene anasamalila mlandu wake umene unam’cotsetsa mu mpingo .
Conco , pa maulendo angapo otsatila , tinakambilana malemba ofotokoza za kunyada na zotulukapo za khalidweli .
Pamene tinali kukambilana , zinali monga kuti Graham akudziyang’ana pa gilasi ya Mau a Mulungu , ndipo sanakondwele na mmene anali kuonekela .
Graham anavomeleza kuti anacititsidwa khungu na mzimu wonyada , umene unali ngati “ mtanda wa denga ” m’diso lake . Anazindikila kuti iye ndiye anali na vuto . Anali kukonda kupeza zifukwa akulu . Conco , mwamsanga anayamba kusintha .
Iye anayamba kupezeka pa misonkhano ya mpingo nthawi zonse , kuphunzila Mau a Mulungu mwakhama , na kupemphela tsiku lililonse .
Anati , ‘ Nakhala m’coonadi kwa zaka zambili , ndipo natumikilapo monga mpainiya .
Mtumwi Petulo anati : “ Wetani gulu la nkhosa za Mulungu lomwe analisiya m’manja mwanu , osati mokakamizika , koma mofunitsitsa . Osatinso cifukwa cofuna kupindulapo kenakake , koma ndi mtima wonse . Osati mocita ufumu pa anthu amene ali coloŵa cocokela kwa Mulungu , koma mukhale zitsanzo kwa gulu la nkhosa . ” ( 1 Pet .
Kodi makolo angalele bwanji ana awo m’malangizo a Yehova ?
( Ŵelengani Aheberi 12 : 5 - 11 . )
Kodi mwana angaphunzile bwanji kudzilanga yekha ?
4 , 5 . ( a ) N’cifukwa ciani kudzilanga wekha ni mbali yofunika kwambili ya “ umunthu watsopano ” ?
Tingacite ciani kuti tizikonda kuŵelenga Mau a Mulungu ?
M’bale wina anati , “ Nimayamikila ngako kuti makolo anga ananilela bwino .
( b ) Kodi banja lina linapindula bwanji pamene makolo a m’banjalo anamvela Yehova ?
Patapita zaka , mwanayo anabwezeletsedwa .
( b ) N’ciani cimene tiyenela kucita kuti akulu azikondwela na utumiki wawo ?
Conco , n’naona kuti nifunika kuuzako akulu .
Iwo sananikalipile kapena kunidzudzula , koma ananilimbikitsa . Ndipo nthawi zonse pambuyo pa misonkhano , akulu anali kunifunsako za umoyo wanga olo pamene anali otangwanika kwambili .
Cifukwa ca zimene zinanicitikila m’mbuyomo , n’nali kuona kuti Mulungu sanganikonde .
Komabe , nthawi na nthawi , Yehova anali kuseŵenzetsa mpingo na akulu ponitsimikizila kuti amanikonda .
Nimapemphela kuti nisakamusiye . ”
Ukasintha n’kucita cabwino , sindikuyanja kodi ?
Koma ngati susintha kuti ucite cabwino , ucimo wamyata pakhomo kukudikilila , ndipo ukulakalaka kukudya . Kodi iweyo suugonjetsa ? ” ( Gen .
1 : 24 - 31 ) Conco , tifunika ‘ kumvela malangizo kuti tikhale anzelu . ’
Anthu pa dziko lonse amafunitsitsa kukhala na ufulu waukulu .
15 Tengelani Yehova — Mulungu Amene Amapeleka Cilimbikitso
8 : 36 .
( Ŵelengani 1 Mbiri 29 : 11 , 12 . )
Kuti anthu akhale na umoyo ‘ wabwino , ’ afunika kudalila Mulungu na kumumvela .
Apo ayi , adzafunika kudziŵa okha cabwino . . . na coipa . ”
Angacite ngozi yoopsa kwambili .
Anati : “ Mukamasunga mau anga nthawi zonse , ndiye kuti ndinudi ophunzila anga . Mudzadziŵa coonadi , ndipo coonadi cidzakumasulani . ”
N’cifukwa ciani tingakambe kuti ufulu umene Yesu anatilonjeza udzakhaladi weni - weni ?
( Ŵelengani Aroma 8 : 1 , 2 , 20 , 21 . )
( c ) Tidzakambilana mafunso ati ?
( Pitani pa ZOCITIKA NA KUFUNSA MAFUNSO > KUPILILA ZIYESO . )
Zinthu zonse ndi zololeka , koma si zonse zimene zili zolimbikitsa . ”
N’citsanzo canji cimene Nowa na banja lake anapeleka ?
Iwo anali kukhala m’dziko lokonda ciwawa na ciwelewele .
Baibo imati : “ Nowa anacita zonse motsatila zimene Mulungu anamulamula .
Nanga Yehova watipatsa nchito yanji masiku yano ?
( Ŵelengani Luka 4 : 18 , 19 . )
Apa m’pamene n’namvetsetsadi tanthauzo la Yakobo 4 : 8 , imene imati : ‘ Yandikilani Mulungu , ndipo iyenso adzakuyandikilani . ’
N’nadziŵa kuti napeza cimene n’nali kufuna , cimene ni umoyo waphindu . ”
M’bale na mkazi wake , amene na apainiya apadela akulalikila m’dela linalake lakutali ca kufupi na mzinda wa Balykchy
( b ) Kodi Yehova anamulimbikitsa bwanji Mwana wake ?
Ndikugwila mwamphamvu ndi dzanja langa lamanja lacilungamo . ” ( Yes . 41 : 10 ) Nawonso Akhristu oyambilila anali kudziŵa kuti Mulungu amatilimbikitsa .
Sangalala limodzi ndi ine mbuye wako . ”
Kodi Hezekiya anawalimbikitsa bwanji akulu - akulu a asilikali ndi anthu a mu Yerusalemu ?
Kodi Petulo anawalimbikitsa bwanji Akhristu anzake ?
Koma ine ndakupemphelela iwe kuti cikhulupililo cako cisathe . Cotelo iwenso , ukabwelela , ukalimbikitse abale ako . ” — Luka 22 : 31 , 32 .
Nanga n’cifukwa ciani ?
Kodi akulu angapeleke bwanji uphungu m’njila yolimbikitsa ?
Makolo , kodi mumaphunzitsa ana anu kuti azilimbikitsa ena ?
Mlongoyo ananiuza kuti nayenso anakumanapo na vuto monga limene ine n’nali nalo . Conco , n’nayamba kuona kuti si ine nekha amene n’nali na vutolo . ”
Mfumu Solomo inalemba kuti : “ Mawu onenedwa pa nthawi yoyenela ndi abwino kwambili .
Maso owala amapangitsa mtima kusangalala . Uthenga wabwino umanenepetsa mafupa . ”
Pakuti mwandicititsa kusangalala , inu Yehova , cifukwa ca zocita zanu . Ndimafuula mosangalala cifukwa ca nchito ya manja anu . ” ( Sal .
Mtumwi Paulo anati : “ Mulungu si wosalungama woti angaiŵale nchito yanu ndi cikondi cimene munacisonyeza pa dzina lake . ” ( Aheb .
6 : 10 ) Mukhoza kudziikila zolinga olo pamene muli wamng’ono .
Miyambo 21 : 5 imati : “ Zolinga za munthu wakhama zimam’pindulila . ”
Mukadziikila zolinga zabwino mukali aang’ono , kupanga zosankha kumakhala kosavuta .
N’zoona kuti nikanaphunzila ku univesiti na kutenga digili ya za malamulo , sembe nilandila ndalama zambili . Koma sembe nilibe mwayi wokwanila wopeza nchito ya uloya ya maola ocepa . ”
17 , 18 . ( a ) Kodi Yehova amawafunila zotani acicepele masiku ano ?
N’nabadwila m’nyumba yamitengo ya cipinda cimodzi m’tauni yaing’ono yochedwa Liberty , ku Indiana , m’dziko la United States .
M’kupita kwa nthawi , amayi anabeleka ang’ono anga aŵili na mlongosi wanga mmodzi .
PAMENE n’nali pa sukulu , zinthu zambili sizinasinthe .
Tauni ya Liberty inali yozungulilidwa na mafamu ang’ono - ang’ono , ndipo alimi ambili anali kulima milisi .
Anali kupita nase ku chechi ya Baptist pa Sondo paliponse .
Koma ine sin’naikonde nchitoyi .
Koma panthawiyi , ananiitanila ku Phunzilo la Buku la Mpingo , kumene anali kukambilana na kuphunzila zokhudza Baibo . Phunziloli linali kucitikila ku nyumba kwawo .
N’nawauza kuti nidzaganizilapo .
N’nadabwa poona kuculuka kwa zimene anali kudziŵa zokhudza Baibo .
Zaka zingapo m’mbuyomo , pamene n’nafunsa amayi za Mboni za Yehova , ananiuza kuti , “ Amalambila munthu winawake wakale wochedwa Yehova . ”
Koma n’tayamba kuphunzila , n’naona kuti maso anga ayamba kutseguka .
Caka cotsatila ca 1958 , n’nayamba upainiya .
Gloria anali ciphadzuwa , ndipo na manje ni ciphadzuwa .
Ine na Gloria tinakwatilana mu February , 1959 .
M’bale wokondedwa , dzina lake Simon Kraker anatifunsa mafunso kuti aone ngati tinali oyenelela .
Iye anatiuza kuti pa nthawiyo ku Beteli sanali kuitana anthu amene ali pabanja .
Mkazi wanga anali kugwila nchito pa nyumba zingapo .
Ine n’nali kugwila nchito za panja , kutsuka mawindo , na nchito zina .
Nikumbukila zimene zinacitika nthawi ina pamene tinaima pa filing’i sitesheni .
Mosiyana na zimenezi , tinali kukondwela ngako kukhala na abale , komanso ulaliki tinali kuukonda .
Inenso n’nayamba kuphunzila na mwana wawo wamkazi pamodzi na mwamuna wake .
Mwanayo na amayi ake , onse anasankha kutumikila Yehova ndipo anabatizika .
Tinalinso na anzathu mumpingo wa azungu .
Pa nthawiyo , gulu lolimbikitsa tsankho na ciwawa , lochedwa Ku Klux Klan ( KKK ) , linali lamphamvu maningi .
Mu 1962 , ananiitana ku Sukulu ya Utumiki wa Ufumu ku South Lansing , mu New York .
Ngakhale n’conco , kampani ina ya zamafoni ku Pine Bluff inali itanifunsa mafunso kuti inilembe nchito .
Nikanalembedwa nchitoyo , sembe n’nakhala munthu woyamba wakuda pa kampaniyo .
N’nalibe ndalama zoyendela ku New York .
Iye anati , “ Yendani ku sukulu mukaphunzile zambili , kuti mukadzabwela mudzatiphunzitse ! ”
Ndine wokondwa kuti sin’nayambe nchitoyo .
Lomba lekani Gloria afotokozeko mmene anali kumvelela pamene tinali kutumikila ku Pine Bluff : “ Gawo la kumeneko n’nalikonda ngako !
Conco , tinali kucita ulaliki wa ku nyumba ndi nyumba m’maŵa , ndipo m’madzulo tinali kucititsa maphunzilo a Baibo .
Pamene tinali kucita upainiya ku Pine Bluff , tinafunsila upainiya wapadela ku Beteli .
Pa nthawiyo , nayenso M’bale Leon Weaver , amene lomba ni mgwilizanitsi wa Komiti ya Nthambi ya ku United States anaikidwa kukhala woyang’anila dela .
N’nali kuyopa kukhala woyang’anila dela .
N’taikidwa pa udindowo , M’bale Thompson ndiye anali woyang’anila wacigawo woyamba kutumikila naye .
M’masiku amenewo , woyang’anila dela sanali kuphunzitsidwa kwa nthawi itali .
Nikumbukila n’nauza mkazi wanga kuti , “ Niona kuti acoka mwamsanga . ”
Tsiku lina , gulu la KKK linacita zionetselo m’tauni ya Tennessee , kumene tinali kucezetsa mpingo .
M’mwezi wokonkhapo , tinayamba utumiki wathu wa pa Beteli .
Mkazi wanga Gloria anali ciphadzuwa , ndipo na manje ni ciphadzuwa
Ndiyeno , mu 1999 , n’naikidwa kukhala mmodzi wa mamembala a m’Bungwe Lolamulila .
Lemba la Yesaya 32 : 17 limati : “ Nchito ya cilungamo ceniceni idzakhala mtendele , ndipo zocita za cilungamo ceniceni zidzakhala bata ndi mtendele mpaka kalekale . ”
Yaciŵili , tifunika kupempha mzimu woyela wa Mulungu .
Ngati nyumbayo ili yoyenela , mtendele umene mukuifunila ukhale panyumbayo , koma ngati si yoyenela , mtendele wanu ubwelele kwa inu . ”
Conco , n’namupatsa moni m’citundu cakeco .
Iye anadabwa , ndipo ananifunsa kuti : ‘ Tikuthandizeni ciani ? ’
Mwaulemu , n’namuuza kuti nifuna kuonana ndi Kazembe .
Iye anatumila foni Kazembeyo , ndipo anabwela na kunipatsa moni m’citundu ca kwawo .
Pambuyo pake , anamvetsela mwachelu pamene n’nali kumufotokozela za nchito ya mtendele ya Mboni za Yehova . ”
‘ Komano zogwela panthaka yabwino , ndi anthu amene . . . amabeleka zipatso mwa kupilila . ’ — LUKA 8 : 15 .
N’ciani cimene cingatithandize kupitiliza kubala zipatso mopilila ?
( Onani pikica pamwambapa . ) ( b ) Kodi Yesu anakamba ciani za kulalikila m’gawo la “ kwawo ” ?
Winanso anati : “ Kukhulupilika kwawo kumanilimbikitsa kupitiliza kulalikila mopilila ndi molimba mtima . ”
Kodi tidzakambilana mafunso atatu ati ? Cifukwa ciani ?
Koma palibe nchito ina imene ningakonde kugwila kuposa imeneyi . ” Ni mmene ise tonse timaonela .
Ŵelengani Yohane 15 : 1 - 5 , 8 .
Kutanthauza kulalikila uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu .
Ŵelengani Luka 8 : 5 - 8 , 11 - 15 .
Kodi timabala bwanji zipatso mwa kupilila ?
Pakuti ndikuwacitila umboni kuti ndi odzipeleka potumikila Mulungu , koma samudziŵa molondola . ”
Tsiku lina titapitanso pa malowo , munthu wina wopita na njila anatifunsa kuti , ‘ N’cifukwa ninji simunali kuoneka ?
Kodi mwatsimikiza mtima ‘ kubala zipatso mwa kupilila ’ ?
15 : 8
( Ŵelengani Yohane 15 : 1 , 8 . )
Kumbukilani kuti Yesu anauza atumwi kuti : “ Atate amalemekezeka mukapitiliza kubala zipatso zambili . ”
( b ) Kodi mumamvela bwanji mukaganizila mwayi umene muli nawo woyeletsa dzina la Mulungu ?
Zimenezi zimanilimbikitsa kupitiliza kulalikila . ”
( a ) Kodi lemba la Yohane 15 : 9 , 10 limachula cifukwa cina citi cogwilila nchito yolalikila ?
Kodi timaonetsa bwanji kuti tifuna kukhalabe m’cikondi ca Khristu ?
Baibo imakamba kuti Nowa anali “ mlaliki . ”
( Ŵelengani 2 Petulo 2 : 5 . )
( a ) Kodi pa Mateyu 22 : 39 pali cifukwa canji cimene tiyenela kugwilila nchito yolalikila ?
Iwo amafunikila kumva uthenga wabwino . ”
13 , 14 . ( a ) Ni mphatso yanji imene imachulidwa pa Yohane 15 : 11 ?
( a ) Ni mphatso yanji imene imachulidwa pa Yohane 14 : 27 ?
( a ) Ni mphatso iti imene yachulidwa pa Yohane 15 : 15 ?
( b ) Kodi atumwi anafunika kucita ciani kuti akhalebe mabwenzi a Yesu ?
( Ŵelengani Yohane 15 : 14 - 16 . )
Timakhulupilila kuti Yehova amayankha mapemphelo athu opempha thandizo ( Onani palagilafu 18 )
Mtumwi Petulo anachula Satana Mdyelekezi kuti “ mkango wobangula , ” ndipo Yohane anamuchula kuti “ njoka , ” komanso “ cinjoka . ” ( 1 Pet . 5 : 8 ; Chiv .
Mwa thandizo lawo , tingakwanitse kumutsutsa Satana .
18 : 11 ) Anthu amene amakhulupilila bodza limeneli amaseŵenzetsa moyo wawo wonse kutumikila “ Cuma ” m’malo motumikila Mulungu . ( Mat .
Tifunika kum’dziŵa bwino mdani wathu , koma sitifunika kumuyopa .
2 : 14 ) Ngati timutsutsa , iye adzatithaŵa . ( Yak .
Kodi zida zankhondo yathu yauzimu ni ziti ?
Ndipo makolo anga na anzanga amanidalila . ”
Kumatithandiza kukhala wolimba mtima na kuyandikila kwambili Yehova , ndipo anthu amene amatikonda amayamba kutilemekeza . ”
Lamba wa coonadi ( Onani palagilafu 3 - 5 )
Cifukwa ca zimenezi , n’nayamba kudzikayikila na kuvutika maganizo . ”
Anzanga ena anayamba kuseŵenzetsa amkolabongo , ndipo ena analeka sukulu .
Cinali comvetsa cisoni kuona mavuto amene anakumana nawo .
Iye anati : “ Nimayesetsa kukumbukila kuti ndine Mboni ya Yehova na kuti ciyeso ni njila imene Satana amaseŵenzetsa pofuna kunigonjetsa .
Nikapambana ciyeso , nimamvela bwino ngako . ”
Codzitetezela pacifuwa cacilungamo ( Onani palagilafu 6 - 8 )
Lomba , nimakondwela kulalikila anzanga . ”
Mwa ici , nimakwanitsa kudziŵa zimene zingawathandize .
Nikakhala wokonzeka , nimakwanitsa kukamba nawo mfundo zimene zingawapindulitse . ”
Ine nimaonetsetsa kuti naŵelenga nkhani na zofalitsa zonse zokhudza acicepele .
Mwa ici , nimatha kuwaonetsa mfundo za m’Baibo kapena zofalitsa za pa jw.org zimene zingawathandize . ”
Mapazi ovekedwa nsapato zokonzekela uthenga wabwino ( Onani palagilafu 9 - 11 )
Kodi ina mwa “ mivi yoyaka moto ” ya Satana ni iti ?
Koma lomba nimakonzekela misonkhano na kuyesetsa kuyankhapo , kaŵili kapena katatu .
Zimanivuta , koma nimamvela bwino kwambili nikayankhapo .
Komanso , abale na alongo amanilimbikitsa maningi .
Conco , nthawi zonse pamene nicoka ku misonkhano , nimakhala wotsimikiza kuti Yehova amanikonda . ”
Cishango cacikulu cacikhulupililo ( Onani palagilafu 12 - 14 )
Cisoti colimba cacipulumutso ( Onani palagilafu 15 - 18 )
Naona kuti anthu amamvetsela kwambili akazindikila kuti umaikonda Baibo komanso umayesetsa kuwathandiza . ”
Lupanga la mzimu ( Onani palagilafu 19 - 20 )
20 : 1 - 3 , 7 - 10 ) Mdani wathu timam’dziŵa bwino .
Lemba la Miyambo 14 : 15 limati : “ Munthu amene sadziŵa zinthu amakhulupilila mau alionse , koma wocenjela amaganizila za mmene akuyendela . ”
N’cifukwa ciani kukonda abale n’kofunika kwambili ?
N’cifukwa ciani Paulo analembela kalata Akristu aciheberi ?
( Ŵelengani Aheberi 10 : 36 - 39 ) Ndiye cifukwa cake , mouzilidwa ndi Yehova , Paulo anawalembela kalata abale ndi alongo okondedwa amenewo .
N’cifukwa ciani buku la Aheberi n’lothandiza kwa ife ?
Kodi lemba la caka ca 2016 ndi liti ?
Vesi limeneli ndi limene lasankhidwa kukhala lemba la caka ca 2016 .
Lemba la caka ca 2016 : “ Mupitilize kukonda abale . ” ​ — Aheberi 13 : 1
Kodi Akristu oona amaona kuti ‘ m’bale ’ wao ndani ?
( a ) Kodi cifukwa cacikulu cimene tiyenela kuonetsela cikondi kwa abale athu n’citi ?
( b ) Ndi cifukwa cina citi cimene tiyenela kulimbitsila cikondi pakati pathu ?
Yesu anali atafotokozelatu kuti nthawi imeneyo idzakhala yovuta kwambili .
N’ciani cimene tiyenela kucita tsopano cisautso cacikulu cisanayambe ?
( a ) Ndi mipata iti imene tingaonetsele kuti timakonda abale athu ?
( b ) Fotokozani zitsanzo za mmene anthu a Yehova anaonetsela cikondi kwa abale ao .
Kodi tingawakumbukile bwanji “ amene ali m’ndende ” ?
“ Kumbukilani amene ali m’ndende . ”
“ Ukwati ukhale wolemekezeka kwa onse . ”
Kodi kukhala okhutila kumatithandiza bwanji kukonda abale athu ?
“ Mukhale okhutila ndi zimene muli nazo pa nthawiyo . ”
Kodi kukhala “ olimba mtima ” kumatithandiza bwanji kukonda abale athu ?
N’ciani cingatilimbikitse kukonda kwambili akulu ?
“ Kumbukilani amene akutsogolela . ”
Tingacite ciani kuti tiziwakonda kwambili abale ?
Kodi cikondi ca Kristu cimatilimbikitsa kucita ciani ?
Kodi cikondi ca Mulungu cimatilimbikitsa bwanji kukonda abale athu ?
Kodi kudziŵa kuti Mulungu ndi wokhululukila kungatilimbikitse bwanji kukhululukila abale athu ?
1 , 2 . ( a ) Kodi mphatso ya Mulungu ‘ imene sitingathe kuifotokoza ’ imaphatikizapo ciani ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 20 . )
3 , 4 . ( a ) Mumamva bwanji munthu wina akakupatsani mphatso ?
( b ) Kodi mphatso yapadela ingasinthe bwanji umoyo wanu ?
Kodi mphatso ya dipo imaposa bwanji mphatso zina zonse ?
( a ) Ndi madalitso ati amene tidzalandila cifukwa ca mphatso imene Yehova anapeleka ?
( b ) Chulani zinthu zitatu zimene cikondi ca Mulungu cimatilimbikitsa kucita .
Kodi tiyenela kumva bwanji tikaganizila cikondi cimene Kristu anatisonyeza ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 5 : 14 , 15 . )
Komanso wondikonda ine , Atate wanga adzamukondanso . Inenso ndidzamukonda ndipo ndidzadzionetsela bwinobwino kwa iye . ” — Yohane 14 : 21 ; 1 Yohane 5 : 3 .
Pa nyengo ino ya Cikumbutso , ndi mafunso ati amene tiyenela kudzifunsa ? Nanga mayankho ake angatilimbikitse kucita ciani ?
( Ŵelengani 1 Timoteyo 2 : 9 , 10 . )
( a ) Kodi kukonda Yehova ndi Yesu kumatilimbikitsa kucita ciani pa nchito yathu yolalikila ?
( b ) Kodi kukonda Mulungu kudzatilimbikitsa kucitila ciani abale athu mumpingo ?
Kodi cikondi ca Mulungu cidzatilimbikitsanso kucita ciani ?
Kodi Yesu anapeleka citsanzo cotani pa nkhani yokonda anthu ena ?
Kodi mungathandizeko m’bale kapena mlongo wokalamba kulalikila ?
Tingaonetse bwanji kuti timakonda abale athu ?
( Ŵelengani Luka 14 : 12 - 14 . )
16 , 17 . ( a ) Tingaphunzile ciani pa fanizo la Yesu la mfumu ndi akapolo ?
( b ) Pambuyo poganizila fanizo la Yesu , kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ?
Kodi cikondi ca Mulungu cinalimbikitsa mlongo wina kucita ciani ?
Ndifuna kuti ndikam’dziwe bwino ali wangwilo . ”
Kodi mphatso yaulele ya Mulungu ‘ imene sitingathe kuifotokoza ’ imakulimbikitsani kucita ciani ?
[ 1 ] ( ndime 18 ) Maina ena m’nkhani ino asinthidwa .
Ndi zinthu ziti zimene zinapangitsa tsiku la Pentekosite mu 33 C.E . kukhala lapadela ? Nanga zimenezo zinakwanilitsa bwanji ulosi wa m’Malemba ?
( a ) Kodi zimene zinacitika pa Pentekosite zimatikhudza bwanji ?
( b ) Ndi cocitika citi cimene ciyenela kuti cinacitika zaka zambili m’mbuyomo pa tsiku lofanana ndi la Pentekosite ?
Timadziŵa bwanji kuti Akristu sadzozedwa m’njila yofanana ndendende ?
Kodi Akristu onse odzozedwa amalandila ciani ?
Kodi Mkristu aliyense wodzozedwa ayenela kucita ciani kuti adzalandile colowa cake ?
Petulo anafotokoza kuti : “ Pa cifukwa cimeneci abale , citani ciliconse cotheka kuti mukhalebe okhulupilika , n’colinga coti mupitilizebe kukhala pakati pa anthu amene Mulungu wawaitana ndi kuwasankha , pakuti mukapitiliza kucita zinthu zimenezi simudzalephela ngakhale pang’ono .
Ndipo mukatelo , adzakutsegulilani khomo kuti mulowe mwaulemelelo mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Kristu . ”
8 , 9 . ( a ) N’cifukwa ciani ambili amalephela kumvetsa zimene zimacitika munthu akadzozedwa ?
( b ) Kodi munthu amadziŵa bwanji kuti wasankhidwa kuti adzapita kumwamba ?
Iye anati : “ Simunalandile mzimu wa ukapolo woyambitsanso mantha , koma munalandila mzimu wakuti mukhale ana , umene timafuula nao kuti : ‘ Abba , Atate ! ’
Pakuti mzimuwo umacitila umboni limodzi ndi mzimu wathu kuti ndife ana a Mulungu . ”
Kodi lemba la 1 Yohane 2 : 27 limatanthauza ciani pamene limati Mkristu wodzozedwa sakufunikila wina aliyense kuti azimuphunzitsa ?
Kodi Mkristu wodzozedwa angakhale ndi maganizo otani ? Nanga n’ciani cimene sakaikila ?
Kodi kaganizidwe ka odzozedwa kamasintha bwanji akadzozedwa ? Nanga n’ciani cimacititsa zimenezi ?
Kodi odzozedwa amamva bwanji pamene ali ndi moyo pano padziko lapansi ?
Ndi zinthu ziti zimene sizipeleka umboni wakuti munthu anadzozedwa ndi mzimu woyela ?
Timadziŵa bwanji kuti ena amene analandila mzimu wa Mulungu sanapite kumwamba ?
17 , 18 . ( a ) Ndi ciyembekezo cotani cimene atumiki ambili a Mulungu ali naco ?
Kodi lemba la Zekariya 8 : 23 likukwanilitsidwa bwanji masiku ano ?
1 , 2 . ( a ) Kodi Yehova anakamba kuti n’ciani cidzacitika masiku ano ?
( b ) Ndi mafunso ati amene adzayankhidwa m’nkhani ino ?
N’cifukwa ciani n’zosatheka kwa ife kudziŵa amene adzakhaladi mbali ya a 144,000 ?
Ndi cenjezo liti limene odzozedwa ayenela kukumbukila ? Nanga n’cifukwa ciani ?
Kodi Akristu odzozedwa sayembekezela ciani ?
N’cifukwa ciani tiyenela kusamala ndi mmene timaonela Akristu amene amadya mkate ndi kumwa vinyo pa Cikumbutso ?
( Onani bokosi lakuti “ Cikondi ‘ Sicicita Zosayenela . ’ ” )
Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Nonsenu ndinu abale . ”
Mungaonetse bwanji kuti mumalemekeza Akristu odzozedwa ?
Kodi timadziteteza bwanji ngati tipewa ‘ kutamanda anthu ena ’ ?
N’cifukwa ciani sitiyenela kuda nkhawa ndi ciŵelengelo ca amene amadya mkate ndi kumwa vinyo pa Cikumbutso ?
“ Yehova amadziŵa anthu ake . ”
Kodi Baibulo limakamba ciani za ciŵelengelo ca odzozedwa amene adzakhala padziko lapansi pamene cisautso cacikulu cidzayamba ?
N’ciani cimene tiyenela kudziŵa pa nkhani ya a 144,000 osankhidwa ndi Yehova ?
M’nthawi ya atumwi , Mulungu anagwilitsila nchito Akristu odzozedwa ocepa kuti alembe Malemba Acigiliki Acikristu .
imalimbitsa ubwenzi wathu ndi Mulungu ndiponso anzathu ?
Ngakhale kuti Yehova ndi Mulungu Wamkulu Koposa , kodi wapatsa ena mwai wotani ?
Kodi Yehova anapatsa Yesu mwai wogwila naye nchito yotani ?
Nanga n’cifukwa ciani ?
Mwacitsanzo , anapatsa Adamu nchito yakuti ache nyama maina .
Kodi anthu ena anagwila nchito bwanji ndi Mulungu pokwanilitsa cifunilo cake ?
Kodi tili ndi mwai wogwila nao nchito iti ? Kodi Yehova amafunikadi thandizo lathu kuti akwanitse kugwila nchitoyi ?
( 1 Akorinto 3 : 9 ) Mtumwi Paulo analemba kuti : “ Pamene tikugwila naye nchito limodzi , tikukudandaulilaninso kuti musalandile kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu n’kuphonya colinga ca kukoma mtimako . ”
Kodi Mwana woyamba kubadwa wa Mulungu anali kumva bwanji pamene anali kugwila nchito ndi Atate wake ?
N’cifukwa ciani nchito yolalikila imatipatsa cimwemwe ?
Kodi anthu ena anakamba ciani za cimwemwe cimene amapeza cifukwa cogwila nchito ndi Yehova ?
Nayenso Franco amene akutumikila ku Italy anati : “ Kudzela m’Mau ake ndi zogaŵila zakuuzimu , nthawi zonse Yehova amatikumbutsa kuti amatikonda ndi kuti amayamikila zimene timacita pom’tumikila , ngakhale kuti nthawi zina tingaone ngati palibe zimene tikucita .
Kumandipangitsanso kuona moyo wanga kukhala wofunika . ”
Kodi Yehova ndi Yesu anali pa ubwenzi wotani ? Nanga n’cifukwa ciani ?
Kodi nchito yolalikila imalimbitsa bwanji ubwenzi wathu ndi Mulungu ndiponso anzathu ?
Iye anati : “ Kuti akhale amodzi mmene ife tilili . ”
Timadziŵa cifukwa cake tiyenela kum’dalila ndi kumvela malangizo ake .
N’ciani cidzalimbitsa kwambili ubwenzi wathu ndi Yehova ndiponso ndi anzathu m’dziko latsopano ?
Kodi m’bale wina wa ku Australia amaiona bwanji nchito yolalikila ?
Joel , amene amakhala ku Australia , anati : “ Kulalikila kumandithandiza kuti ndiziona zinthu moyenela .
Kumandikumbutsa za mavuto amene anthu akukumana nao ndiponso mapindu amene ndapeza cifukwa cotsatila mfundo za m’Baibulo pa umoyo wanga .
Nchito yolalikila imandithandiza kukhala wodzicepetsa . Imandipatsanso mwai wodalila Yehova ndi abale ndi alongo anga . ”
Kodi kupilila kwathu pa nchito yolalikila kumaonetsa bwanji kuti mzimu wa Mulungu ukutitsogolela ?
Kodi mungapitilize kugwila nchito yotelo ?
Kodi nchito yolalikila uthenga wabwino imagwilizana bwanji ndi colinga ca Mulungu cokhudza anthu ?
Kodi kulalikila kumagwilizana bwanji ndi malamulo aakulu a Mulungu ?
Laciŵili lofanana nalo ndi ili , ‘ Uzikonda mnzako mmene umadzikondela wekha . ’ ”
Kodi mumamva bwanji cifukwa ca mwai wolalikila uthenga wabwino ?
Ndakupatsa mphamvu , Mau anga Baibulo , thandizo la angelo , anzako padziko , maphunzilo , ndi malangizo a panthawi yake . ’
Ndithudi , ndi mwai waukulu kwambili kucita zimene Yehova watilamula ndi kugwila naye nchito . ”
Ndinauza wapolisi kuti ndinakhalapo kale m’ndende cifukwa cokana kumenya nkhondo .
NDINABADWA mu 1926 , mumzinda wa Crooksville ku Ohio , m’dziko la United States .
Amai ndi Atate sanali kupemphela , koma anali kulimbikitsa anafe kupita ku chalichi .
Margaret Walker ( mlongo waciŵili kucokela kumanzele ) anandithandiza kuphunzila coonadi
Panthawi imeneyo , mai wina wa Mboni za Yehova , amene tinali kukhala naye pafupi dzina lake Margaret Walker , anayamba kucezela amai ndi kuwauza uthenga wa m’Baibulo .
Koma ndinayesetsa kuti ndizimvetselako zimene anali kukambilana .
Atawacezela kwa maulendo angapo , a Margaret anandifunsa kuti , “ Kodi dzina la Mulungu umalidziŵa ? ”
Ndinayankha kuti , “ Aliyense amalidziŵa , ndi Mulungu . ”
Iwo anati , “ Tenga Baibulo lako ndipo uŵelenge Salimo 83 : 18 . ”
Nditaŵelenga lembalo , ndinadziŵa kuti dzina la Mulungu ndi Yehova .
Ndinathamangila panja ndi kuuza anzanga kuti , “ Mukafika ku nyumba , muŵelenge Salimo 83 : 18 m’Baibulo lanu , kuti mudziŵe dzina la Mulungu . ”
Mwina tinganene kuti apa m’pamene ndinayambila kulalikila .
Ndinayamba kuphunzila Baibulo , ndipo mu 1941 ndinabatizidwa .
Pambuyo pake , ndinapatsidwa udindo wocititsa phunzilo la buku la mpingo .
Ndinalimbikitsa amai ndi azilongosi anga onse kuti azipezekapo pa phunzilo limenelo , ndipo anayambadi kupezekapo .
Nthawi zina , amai akamapita kumisonkhano , io anali kuwathamangila ndi kuwakokela ku nyumba .
Koma amai anali kutulukila khomo lina ndi kupita kumisonkhano .
Koma ndinauza akuluakulu a boma kuti sindingakhale msilikali .
Woweluza wina anati : “ Nditapatsidwa mwai wokuweluza , ndikhoza kulamula kuti ukhale m’ndende kwa umoyo wako wonse .
Ndinayankha kuti : “ Wolemekezeka , ine ndine minisitala .
Nchito yanga ndi kulalikila Uthenga wabwino wa Ufumu khomo ndi khomo , ndipo ndalalikila anthu ambili . ”
Ndiyeno woweluzayo anauza oweluza anzake kuti : “ Simunabwele kuno kudzakambilana ngati mnyamatayu ndi minisitala kapena ai .
Mwabwela kudzakambilana ngati iye anavomela kuloŵa usilikali kapena ai . ”
Ndili mmenemo , ndinapemphela kwa Yehova kuti : “ Yehova sindingakwanitse kukhala muno zaka 5 .
Tsiku lotsatila , asilikali olondela ananditulutsa m’cipindaco .
Nditatuluka ndinapita pamene panali mkaidi wina wamtali ndi wojincha . Tinaimilila pa windo ndi kumayang’ana panja .
Iye anandifunsa kuti , “ Unalakwa ciani iwe ? ”
Ndinayankha kuti , “ Ndine Mboni ya Yehova . ”
Ndinati , “ Mboni za Yehova sizipita kunkhondo ndi kupha anthu . ”
Ndinati , “ Iyai , si cilungamo . ”
Kenako iye anati , “ Kwa zaka 15 ndinali m’ndende ina ndipo ndinali kuŵelengako mabuku anu . ”
Ndinali pakati pa Mboni zimene zinaikidwa m’ndende ku Ashland ku Kentucky cifukwa cokana kumenya nkhondo
Izi n’zimene tinali kucita kuti tizilalikila mwadongosolo .
Ndinali kudela nkhawa a m’banja langa cifukwa atate anandiuzapo kuti , “ Ndikathana ndi iwe , enawa sangandivute . ”
Pamenepo ndinati , “ Cabwino , ngakhale n’telo sindingaloŵe usilikali . ”
Ndinagwila mau lemba la 2 Timoteyo 2 : 3 ndi kukamba kuti , “ Ndine kale msilikali wa Kristu . ”
Iye anakhala cete kwa kanthawi , kenako anati , “ Ungapite kunyumba . ”
Patapita nthawi yocepa , ndinapezeka pa kukumana kwa ofuna kutumikila pa Beteli pa msonkhano umene unacitikila ku Cincinnati ku Ohio .
Ndinalinso kukonza makina oonongeka ndi maloko .
Ndapeza mabwenzi ambili pa Beteli ndiponso mumpingo .
Ndinaphunzilako Cicainizi Cacimandarini , ndipo ndimakonda kulalikila m’miseu kwa anthu okamba Cicainizi .
Nthawi zina m’maŵa ndimagaŵila magazini 30 kapena 40 kwa anthu a cidwi .
Kulalikila anthu a Cicainizi ku Brooklyn , New York
Panthawi ina , ndinacita ulendo wobweleza kwa munthu amene anali ku China .
Analandila ndipo anandiuza kuti dzina lake ndi Katie .
Kuyambila pamenepo , Katie akandiona , anali kubwela kudzandilankhula .
Ndinam’phunzitsa maina a Cingelezi a zipatso ndiponso a ndiwo za masamba , ndipo iye anali kubweleza zimene ndinali kukamba .
Ndinamuuzanso uthenga wa m’Baibulo ndi kum’gawila buku la Zimene Baibo Imaphunzitsa .
Koma patapita milungu yocepa , ndinaleka kumuona .
Mlungu wotsatila , mtsikanayo anandipatsa foni ndi kukamba kuti , “ Pali munthu wina wa ku China amene afuna kukamba nanu . ”
Ndinamuuza kuti , “ Sindidziŵa munthu aliyense ku China . ”
Koma mtsikanayo analimbikila , conco ndinatenga foni ndi kukamba kuti , “ Halo , ndine Robison . ”
Kenako ndinamva mau pa foniyo akuti , “ A Robby , ndine Katie .
Conde nayenso m’phunzitseni zimene munandiphunzitsa . ”
Ndinati , “ Ndidzacita zimene ndingathe Katie .
Zikomo kwambili pondidziŵitsa kumene uli . ”
Ndinapitiliza kukambilana ndi mkulu wakeyo kwa kanthawi , koma nayenso anasiya kuoneka .
Ndikhulupilila kuti anthu a m’banja langa ndi anzanga amene anamwalila adzakhalanso ndi moyo m’dziko latsopano .
Pamene nkhaniyi inali kukonzedwa , m’bale Corwin Robison anamwalila ali wokhulupilika kwa Yehova .
Kodi zimene Abulahamu anali kudziŵa zokhudza Mulungu , ndiponso zocitika pa umoyo wake zinalimbitsa bwanji cikhulupililo cake ?
Kodi Abulahamu anacita ciani kuti alimbitse ubwenzi wake ndi Mulungu ?
Kodi mungatengele bwanji citsanzo ca Abulahamu kuti mulimbitse ubwenzi wanu ndi Yehova ?
1 , 2 . ( a ) Timadziŵa bwanji kuti anthu angakhale mabwenzi a Mulungu ?
3 , 4 . ( a ) Ndi nthawi iti pamene cikhulupililo ca Abulahamu cinayesedwa kwambili ? ( b ) N’cifukwa ciani Abulahamu anali wokonzeka kupeleka Isaki nsembe ?
Kodi zioneka kuti Abulahamu anaphunzila bwanji za Yehova ? Nanga zimene anaphunzila zinam’thandiza bwanji ?
Kodi tiyenela kucita ciani kuti tim’dziŵe bwino Yehova ndi kum’mvela ?
9 , 10 . ( a ) Kodi cofunika n’ciani kuti ubwenzi ukhale wolimba ?
( b ) N’ciani cionetsa kuti Abulahamu analimbitsa ubwenzi wake ndi Yehova ndi kuuona kukhala wamtengo wapatali ?
Abulahamu anaona ubwenzi wake ndi Yehova kukhala cinthu camtengo wapatali ndipo anali kuuteteza .
N’cifukwa ciani Abulahamu anada nkhawa atamva kuti Sodomu ndi Gomora adzaonongedwa ?
12 , 13 . ( a ) Kodi zimene Abulahamu anaphunzila ndi zocitika pa umoyo wake zinamuthandiza bwanji panthawi ina ?
( b ) N’ciani cimene cionetsa kuti Abulahamu anali kukhulupilila Yehova ?
Ndi mavuto otani amene mumakumana nao potumikila Yehova ? Nanga citsanzo ca Abulahamu cingakuthandizeni bwanji ?
Abulahamu ndi Sara anadziŵa Yehova ndi kuyamba kumulambila
Abulahamu anamwalila “ ali wokalamba , atakhala ndi moyo wabwino , wautali ndi wokhutila ”
N’cifukwa ciani ndife otsimikiza kuti Abulahamu sanadziimbepo mlandu cifukwa cokhala wokhulupilika kwa Yehova ?
Kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ? Nanga tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ?
Motelo , tiyeni tonse tiziyesetsa kutengela cikhulupililo ca Abulahamu .
( Ŵelengani Aheberi 6 : 10 - 12 . )
M’nkhani yotsatila , tidzakambilana zitsanzo zitatu za anthu okhulupilika amene anakhala mabwenzi a Mulungu .
Kodi tingaphunzile ciani pa ubwenzi wa Rute ndi Mulungu ?
N’cifukwa ciani Mfumu Hezekiya anali bwenzi lapamtima la Yehova ?
Ndi makhalidwe otani amene Mariya , mai wa Yesu , anali nao omwe anam’pangitsa kukhala bwenzi la Yehova Mulungu ?
1 - 3 . ( a ) N’cifukwa ciani sitiyenela kukaikila zoti tingakhale mabwenzi a Mulungu ?
( b ) Tikambilana za ndani m’nkhani ino ?
Kodi Rute anafunika kupanga cosankha cotani ? Nanga n’cifukwa ciani kusankha zimenezo kunali kovuta ?
( a ) Ndi cosankha ca nzelu citi cimene Rute anapanga ?
( b ) N’cifukwa ciani Boazi anakamba kuti Rute anathaŵila m’mapiko mwa Yehova ndi kupezamo citetezo ?
N’ciani cingathandize anthu amene amawayawaya kudzipeleka kwa Yehova ?
9 , 10 . ( a ) N’cifukwa ciani cinali capafupi kuti Hezekiya akwiile Mulungu ?
( b ) N’cifukwa ciani sitiyenela kukwiila Mulungu ?
( c ) Nanga n’cifukwa ciani sitiyenela kuganiza kuti banja limene tinakulilamo likhoza kuticititsa kukhala munthu woipa kapena wabwino ?
Acicepele ambili aphunzila coonadi ngakhale kuti anakulila m’banja la citsanzo coipa ( Onani ndime 9 ndi 10 )
N’ciani cinacititsa kuti Hezekiya akhale mfumu yabwino ya Yuda ?
( Ŵelengani 2 Mafumu 18 : 5 , 6 . )
Mofanana ndi Hezekiya , kodi anthu ambili masiku ano aonetsa bwanji kuti ndi mabwenzi a Yehova ?
N’cifukwa ciani udindo umene Mariya anapatsidwa unaoneka wovuta kwambili ? Koma kodi Mariya anayankha ciani kwa Gabirieli ?
N’ciani cionetsa kuti Mariya anali mmvetseli wabwino ?
Pa zocitika zonsezi , Mariya anamvetsela ndi kusunga zimene anamva , kenako anayamba kuzisinkhasinkha . — Ŵelengani Luka 2 : 16 - 19 , 49 , 51 .
Tiphunzila ciani zokhudza Mariya tikaona zimene anali kukamba ?
Tingatengele bwanji cikhulupililo ca Mariya ?
Kodi tingayembekezele ciani ngati titengela zitsanzo za m’Baibulo za anthu a cikhulupililo ?
KUMBUKILANI tsiku limene munasangalala kwambili pa umoyo wanu .
Kodi ndi tsiku limene mwana wanu woyamba anabadwa ?
Mosakaikila , kucokela pamene munabatizidwa , mwapeza cimwemwe cacikulu potumikila Yehova .
Kodi ndi zinthu ziti zimene zimatilimbikitsa kupitiliza kutumikila Yehova mwacimwemwe ?
( 1 Yohane 5 : 3 ) Kumbukilani mau a Yesu akuti : “ Bwelani kwa ine nonsenu ogwila nchito yolemetsa ndi olemedwa , ndipo ndidzakutsitsimutsani .
Timatumikila Mulungu wacimwemwe , amene anatipatsa moyo .
Ganizilani za Héctor , amene anatumikila Yehova kwa zaka 40 monga woyang’anila dela .
Iye anati : “ Cimandiŵaŵa kuona mkazi wanga akudwaladwala , ndipo ndimavutika pom’samalila . Koma sindilola kuti zimenezi zindilande cimwemwe canga potumikila Mulungu woona .
Kudziŵa kuti ndili ndi moyo cifukwa ca Yehova , amene analenga munthu n’colinga , kumandicititsa kum’konda kwambili ndi kum’tumikila ndi mtima wonse .
Ndimayesetsa kukhala wacangu pa nchito yolalikila , ndiponso ndimaganizila za madalitso amene Ufumu wa Mulungu udzabweletsa .
Timatha kukhala acimwemwe cifukwa cakuti Yehova watipatsa nsembe ya dipo .
Zoonadi , “ Mulungu anakonda kwambili dziko mwakuti anapeleka Mwana wake wobadwa yekha , kuti aliyense wokhulupilila iye asaonongeke , koma akhale ndi moyo wosatha . ”
Jesús anasintha umoyo wake ndipo anatumikila Yehova mwacimwemwe kwa zaka zambili
Ndinali kucita zimenezi kuti ndipeze ndalama zambili .
Kenako , ndinaphunzila za Yehova ndi kuti anapeleka Mwana wake wokondedwa cifukwa ca anthu , ndipo ndinayamba kufuna kum’tumikila .
Conco , ndinadzipeleka kwa Yehova .
Pambuyo poseŵenza kwa zaka 28 pa kampani , ndinasankha zosiya nchito ndi kuyamba utumiki wa nthawi zonse . ”
Kodi mukumbukila mmene umoyo wanu unalili musanadziŵe Yehova ?
Mtumwi Paulo anakumbutsa Akristu a ku Roma kuti poyamba anali “ akapolo a ucimo , ” koma anakhala “ akapolo a cilungamo . ”
“ Ngati pali zaka zosangalatsa kwambili pa umoyo wanga , ndi zaka zimene ndakhala ndikutumikila Yehova . ” ​ — Jaime
Kuti asinthe umoyo wake wakale , Jaime anapempha Yehova kuti am’thandize kukhala ndi cikhulupililo mwa Iye .
Jaime anati : “ Pang’ono ndi pang’ono , ndinadziŵa kuti kuli Tate wacikondi ndiponso Mulungu wacifundo .
Zikanakhala kuti sindinasinthe umoyo wanga , ndikanaphedwa monga anzanga ena amene anali ankhonya .
Ngati pali zaka zosangalatsa kwambili pa umoyo wanga , ndi zaka zimene ndakhala ndikutumikila Yehova . ”
Kodi Yonatani mwana wa Mfumu Sauli anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Yehova ?
Tingaonetse bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Mulungu ngati munthu winawake waudindo sacita zinthu mwacilungamo ?
Tingaonetse bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Yehova ngati anthu ena sakutimvetsetsa kapena akuticitila zinthu mopanda cilungamo ?
N’cifukwa ciani ubwenzi wa Davide ndi Yonatani ndi citsanzo cabwino ca kukhulupilika ?
N’ciani cinali cofunika kwambili kwa Yonatani kuposa kukhala wokhulupilika kwa Davide ?
( a ) N’ciani cingatithandize kukhaladi osangalala komanso okhutila ?
N’cifukwa ciani cinali covuta kwa Aisiraeli kukhala okhulupilika kwa Mulungu pamene Sauli anali mfumu ?
N’ciani cionetsa kuti Yonatani anakhalabe wokhulupilika kwa Yehova ?
Kodi kulemekeza amene amatitsogolela kumaonetsa bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Mulungu ?
( Ŵelengani Aroma 13 : 1 , 2 . )
N’cifukwa ciani Yonatani anasankha kukhala wokhulupilika kwa Davide ?
Kodi kukonda Mulungu kumatithandiza bwanji kusankha kukhala wokhulupilika kwa iye ?
Kodi kukhala wokhulupilika kwa Mulungu kungatithandize bwanji kulimbana ndi mavuto m’banja ?
N’ciani cimene tiyenela kucita ngati m’bale waticitila zinthu mopanda cilungamo ?
Ndi pa zocitika ziti pamene tiyenela kukhala okhulupilika kwa Yehova ndi kupewa kudzikonda ?
[ 1 ] ( ndime 9 ) Maina ena asinthidwa .
N’cifukwa ciani Yonatani ndi Abineri anali kuona Davide mosiyana kwambili ?
Ndi makhalidwe ati amene angatithandize kukhala okhulupilika kwa Mulungu ?
Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ?
( a ) Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ?
( b ) Tikambilana zitsanzo zina ziti ?
Ndi mfundo yofunika iti imene tikuphunzila pa maganizo olakwika amene Abisai anali nao ?
Ngakhale kuti timafuna kukhala okhulupilika kwa acibale athu ndi anzathu , n’cifukwa ciani tiyenela kusamala ?
Kodi mlongo wina anaonetsa bwanji kukhulupilika kwa Mulungu ngakhale panthawi zovuta ?
Ndi makhalidwe ati amene angatithandize kukhala okhulupilika kwa Yehova ?
Kodi zitsanzo za m’Baibulo za Abineri , Abisalomu , ndi Baruki zingatipindulitse bwanji ?
Koma iwe , ukufunafunabe zinthu zazikulu .
Fotokozani citsanzo coonetsa kuti sitingakhale okhulupilika kwa Mulungu ngati ndife odzikonda ?
Pambuyo popeleka mapemphelo ambili uku ndikulila , ndinaleka kum’tumila mameseji .
Davide atacimwa , kodi Natani anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ndiponso kwa Davide ?
Mungaonetse bwanji kuti ndinu wokhulupilika kwa Yehova ndi kwa mnzanu kapena wacibale ?
N’cifukwa ciani Husai anafunika kulimba mtima kuti akhalebe wokhulupilika kwa Mulungu ?
N’cifukwa ciani tifunika kulimba mtima kuti tikhale okhulupilika ?
Ndinapempha Yehova kuti andithandize kukhala wolimba mtima kuti ndisasinthe maganizo anga .
Tsopano , io anasintha ndipo ndimapita kukawacezela nthawi zambili . ” — Ŵelengani Miyambo 29 : 25 .
[ 1 ] ( ndime 7 ) maina ena asinthidwa .
“ Ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja sayamba wakhala pansi ndi kuŵelengela ndalama zimene adzaononge , kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanila kumalizila nsanjayo ? ” — LUKA 14 : 28 .
Kodi kukhala wokhwima mwakuuzimu kumatanthauza ciani ?
Kodi mungadziŵe bwanji kuti mwasankha kucokela pansi pamtima kuti mubatizidwe ?
Kodi kudzipeleka n’kutani ? Nanga kumagwilizana bwanji ndi kubatizidwa ?
1 , 2 . ( a ) N’ciani cimasangalatsa anthu a Mulungu masiku ano ?
( b ) Kodi makolo acikristu ndi akulu angathandize bwanji acinyamata kumvetsa tanthauzo la ubatizo ?
Kenako anati : “ Koma n’cifukwa ciani ufuna kubatizidwa ? ”
( Ŵelengani Luka 14 : 27 - 30 . )
( a ) Kodi zimene Yesu ndi Petulo anakamba zimaonetsa bwanji kuti ubatizo ndi wofunika ?
( Mateyu 28 : 19 , 20 ; 1 Petulo 3 : 21 ) ( b ) Tikambilana mafunso ati ?
( 2 ) Kodi ndikufuna kubatizidwa mwa kufuna kwanga ?
( 3 ) Kodi ndimamvetsetsa tanthauzo la kudzipeleka kwa Yehova ?
4 , 5 . ( a ) N’cifukwa ciani ubatizo si wa anthu acikulile okha ?
( b ) Kodi kukhala Mkristu wokhwima kumatanthauza ciani ?
Pa Miyambo 20 : 11 timaŵelenga kuti : “ Ngakhale mnyamata amadziŵika ndi nchito zake , ngati zocita zake zili zoyela ndiponso zoongoka . ”
6 , 7 . ( a ) Fotokozani mavuto amene Danieli anakumana nao ku Babulo . ( b ) Kodi Danieli anaonetsa bwanji kuti anali wofikapo mwakuuzimu ?
Wacinyamata wofikapo mwakuuzimu sakhala bwenzi la Mulungu ku Nyumba ya Ufumu koma akapita kusukulu n’kukhala bwenzi la dziko ( Onani ndime 8 )
Wacinyamata wotelo sacita zinthu monga bwenzi la Mulungu ku Nyumba ya Ufumu koma akapita kusukulu n’kukhala bwenzi la dziko .
9 , 10 . ( a ) Kodi wacinyamata angapindule bwanji akaganizila zimene anacita atayesedwa ?
11 , 12 . ( a ) Kodi munthu amene afuna kubatizidwa ayenela kuonetsetsa kuti wacita ciani ?
( b ) N’ciani cidzakuthandizani kuona moyenelela makonzedwe a Yehova a ubatizo ?
Mungadziŵe bwanji ngati cosankha canu cofuna kubatizidwa ndi cocokeladi pansi pa mtima ?
Iye wakupatsani mapepala oonetsa kuti galimotoyo ndi yanu , ndipo akukuuzani kuti : “ Galimotoyi ndi yanu . ”
18 , 19 . ( a ) Kodi mau amene Rose ndi Christopher anakamba akuonetsa bwanji kuti ubatizo umabweletsa madalitso ?
( b ) Kodi mumamva bwanji mukaganizila za ubatizo ?
Ndimakhala ndi zocita zambili zosangalatsa potumikila Yehova ndi gulu lake . ”
Kodi ‘ kukhulupilila pambuyo pokhutila ’ kumatanthauza ciani ?
Kodi ‘ makhalidwe oyela ’ ndiponso ‘ nchito zosonyeza kudzipeleka kwa Mulungu ’ n’ciani ?
Kodi kusinkhasinkha za dipo kungakuthandizeni bwanji kuyamikila kwambili Yehova ?
1 , 2 . ( a ) N’cifukwa ciani ubatizo ndi cosankha cacikulu ?
Kodi acinyamata angaphunzile ciani pa citsanzo ca Timoteyo ?
Fotokozani mmene nkhani zakuti “ Kodi Baibulo Limaphunzitsa Ciani ? ” za pa webusaiti yathu zingakuthandizileni kulimbitsa cikhulupililo .
Mlongo wina wacitsikana anati : “ Ndikalibe kuganiza zobatizidwa , ndinaphunzila Baibulo ndipo ndinakhulupilila kuti ici ndiye cipembedzo coona .
Ndipo tsiku ndi tsiku , cikhulupililo canga cinali kulimbilalimbila . ”
N’cifukwa ciani Mkristu wobatizidwa ayenela kukhala ndi makhalidwe oonetsa kuti ali ndi cikhulupililo ?
Baibulo limati : “ Cikhulupililo pacokha , ngati cilibe nchito zake , ndi cakufa . ”
Kodi ‘ makhalidwe oyela ’ n’ciani ?
Mwacitsanzo , ganizilani za miyezi 6 yapitayi .
Kodi “ nchito zosonyeza kuti ndinu odzipeleka kwa Mulungu ” zimaphatikizapo ciani ? Ndipo inuyo mumaziona bwanji ?
N’ciani cingakuthandizeni kucita “ nchito zosonyeza kuti ndinu odzipeleka kwa Mulungu ” ? Nanga acinyamata ena apindula bwanji ndi mbali imeneyi ?
Nanga mapemphelo anuwo amasonyeza kuti mumakondadi Yehova ? ”
“ Kodi mumaloŵa mu utumiki ngakhale ngati makolo anu sanaloŵe ? ”
Mlongo wina wacitsikana , dzina lake Tilda anati : “ Ndinalemba zolinga zanga pa masamba amenewo .
Ndinayamba kukwanilitsa zolinga zimenezo cimodzi ndi cimodzi , ndipo patapita caka cimodzi ndinakhala woyenelela kubatizidwa . ”
Kodi mungapitilize kutumikila Yehova ngakhale makolo anu atasiya kum’tumikila ?
N’cifukwa ciani muyenela kudzipeleka mwa kufuna kwanu ?
16 , 17 . ( a ) N’ciani ciyenela kulimbikitsa munthu kukhala Mkristu ?
( b ) Ndi fanizo liti limene lionetsa kuti tifunika kuyamikila dipo ?
Yesu anamuyankha kuti : “ Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse , moyo wako wonse , ndi maganizo ako onse . ”
( Ŵelengani 2 Akorinto 5 : ​ 14 , 15 ; 1 Yohane 4 : ​ 9 , 19 . )
18 , 19 . ( a ) N’cifukwa ciani simuyenela kuopa kudzipeleka kwa Yehova ?
( b ) Kodi kutumikila Yehova kungakupindulitseni bwanji ?
Kodi wacinyamata angacite ciani kuti akhale wokonzeka kudzipeleka ndi kubatizidwa ?
“ Kodi Ndingatani Kuti Mapemphelo Anga Azikhala Abwino ? ” — November 2008
“ Kodi Ndingatani Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzindisangalatsa ? ” — April 2009
“ Kodi Ndimadziwa Mfundo Zimene Ndimayendera ? ” — October 2011
“ Kodi Ndingatani Kuti Ndizisangalala Ndikamawerenga Baibulo ? ” — February 2012
“ N’chifukwa Chiyani Ndiyenera Kumapita ku Misonkhano ya Mpingo ? ” — April 2012
Kodi kugwila nchito yolalikila kumatithandiza bwanji kukhala ogwilizana ?
Ndi zinthu zina ziti zimene tingacite kuti tilimbitse mgwilizano mumpingo ?
N’ciani cingathandize mwamuna ndi mkazi kukhala ogwilizana ?
Kuyambila paciyambi , kodi Mulungu wakhala akugwila bwanji nchito ndi ena ?
( a ) Kodi Akristu oyambilila anali kudziŵika ndi mzimu wotani ?
( b ) Kodi tikambilana mafunso ati ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 12 : 4 - 6 , 12 . )
N’ciani cimene timakwanitsa kucita tikamagwila nchito yolalikila mogwilizana ?
8 , 9 . ( a ) Ndi fanizo lotani limene Paulo anapeleka kuti athandize Akristu kukhala ogwilizana ?
( b ) Tingatani kuti tikhale ogwilizana mumpingo ?
( Welengani Aefeso 4 : 15 , 16 . )
N’ciani cingathandize kuti onse m’banja azigwilizana ?
Ngati mwamuna kapena mkazi wanu satumikila Yehova , kodi mungacite ciani kuti banja likhalebe lolimba ?
Kodi Akristu amene akhala m’banja kwa zaka zambili angathandize bwanji acinyamata amene ali pabanja ?
Ndi ciyembekezo cotani cimene atumiki a Mulungu ali naco ?
Kodi Yehova anapeleka malangizo otani m’nthawi ya Nowa ndi ya Mose ?
Ndi malangizo ena ati amene Mulungu anapeleka kwa Akristu ?
Tingaonetse bwanji kuti timafuna kutsogoleledwa ndi Mulungu ?
1 , 2 . ( a ) Ndi cenjezo lotani limene lateteza anthu ambili ?
N’ciani cinacititsa kuti anthu akhale pa njila yopita ku imfa ?
( a ) N’cifukwa ciani Mulungu anapeleka malangizo ena pambuyo pa Cigumula ?
( b ) Pamene zinthu zinasintha , kodi Mulungu anaonetsa bwanji maganizo ake ?
Nanga n’cifukwa ciani ?
N’cifukwa ciani anthu a Mulungu anafunika kumvela malamulo amene Mulungu anawapatsa kudzela mwa Mose ? Nanga anafunika kuwaona bwanji malamulowo ?
( a ) N’cifukwa ciani Yehova anapatsa malangizo anthu ake ? ( b ) Kodi Cilamulo cinakhala bwanji mtsogoleli kwa Aisiraeli ?
N’cifukwa ciani tiyenela kutsatila mfundo za m’Cilamulo ca Mose ?
Ndi kusintha kotani kumene kunacititsa kuti Mulungu apelekenso malangizo atsopano ?
N’cifukwa ciani mpingo wacikristu unapatsidwa malamulo atsopano ?
Ndithudi , “ Mulungu alibe tsankho .
Kodi “ cilamulo ca Kristu ” cinali kukhudza mbali ziŵili ziti za umoyo wa Mkristu ?
Zimenezi zinatanthauza kuti Akristu anayenela kulalikila munthu aliyense padziko lapansi . 13 , 14 .
( b ) Tikuphunzila ciani pa citsanzo cimene Yesu anapeleka ?
Kodi zinthu zasintha bwanji masiku ano ? Nanga Mulungu amatitsogolela bwanji ?
Kodi tiyenela kucita ciani ndi malangizo amene timalandila ?
Kodi mumaona kuti malangizo amenewa ndi ocokeladi kwa Mulungu ?
Ndi mipukutu yotani imene idzafunyululidwa mtsogolo ?
Ifotokozanso nchito imene khalidwe la kupilila liyenela kumaliza mwa aliyense wa ife .
Kodi citsanzo ca Yefita ndi mwana wake cingatithandize bwanji kupewa maganizo a dziko ?
Ndi mfundo za m’Baibulo ziti zimene zimakuthandizani kuthetsa mikangano ?
Kodi nkhani ino yakulimbikitsani bwanji kudzipeleka pocilikiza Ufumu wa Mulungu ?
Kodi Yefita ndi mwana wake anakumana ndi zocitika zotani ?
Kodi citsanzo ca Yefita ndi mwana wake cingatithandize bwanji masiku ano ?
4 , 5 . ( a ) Kodi Yehova anapeleka lamulo lotani kwa Aisiraeli pamene analoŵa m’Dziko Lolonjezedwa ?
( b ) Malinga ndi Masalimo 106 , kodi mtundu wa Aisiraeli unakumana ndi mavuto otani cifukwa ca kusamvela ?
Ndi zinthu ziti zimene anthu m’dzikoli amakonda ?
( a ) Ndi zinthu ziti zimene anthu a mtundu wa Yefita anam’citila ?
8 , 9 . ( a ) Ndi mfundo ziti za m’Cilamulo ca Mose zimene zinathandiza Yefita ?
( b ) N’ciani cimene cinali cofunika kwambili kwa Yefita ?
Kodi tingacite ciani kuti mfundo za m’Baibulo zitithandize kucita zinthu monga Mkristu ?
Kodi Yefita analonjeza ciani ? Nanga lonjezolo linali kutanthauza ciani ?
Kodi mau a Yefita a pa Oweruza 11 : 35 amaonetsa bwanji cikhulupililo cake ?
Kodi ndi lonjezo lotani limene ambili a ife tinapanga ?
Kodi mwana wa Yefita anacita ciani atamva za lonjezo la atate ake ?
( a ) Kodi tingatsanzile bwanji cikhulupililo ca Yefita ndi mwana wake ?
( b ) Kodi mau a pa Aheberi 6 : 10 - 12 amakulimbikitsani bwanji kukhala odzipeleka ?
Kodi taphunzila ciani pa nkhani ya Yefita ndi mwana wake ? Nanga tingawatsanzile bwanji ?
Kodi ‘ kulola kuti kupilila kumalize kugwila nchito yake ’ kumatanthauza ciani ?
1 , 2 . ( a ) Tingaphunzilepo ciani pa citsanzo ca kupilila kwa Gidiyoni ndi asilikali ake 300 ?
( Onani cithunzi pamwambapa . ) ( b ) Malinga ndi Luka 21 : 19 , n’cifukwa ciani kupilila n’kofunika ?
Adani athu ndi Satana , dziko lake , ndi kupanda ungwilo kwathu .
Kodi tingaphunzilepo ciani pa zitsanzo za anthu amene anapilila m’mbuyomu ?
N’cifukwa ciani tingakambe kuti cikondi n’cimene cimatilimbikitsa kupilila ?
( Ŵelengani 1 Akorinto 13 : 4 , 7 . )
( Luka 22 : 41 , 42 ) Kukonda abale athu kumatilimbikitsa kunyalanyaza zolakwa zao .
N’cifukwa ciani Yehova ndiye yekha amene angatithandize kwambili kupilila ?
Yehova ndi “ Mulungu amene amatipatsa mphamvu kuti tithe kupilila ndiponso amene amatitonthoza . ”
Mogwilizana ndi zimene Baibulo linalonjeza , kodi Yehova amapeleka bwanji “ njila yopulumukila ” ciyeso ?
Fotokozani citsanzo coonetsa kuti timafunika cakudya cakuuzimu kuti tithe kupilila .
8 , 9 . ( a ) Malinga ndi Yobu 2 : 4 , 5 , ndi nkhani iti imene imaloŵetsedwamo tikakumana ndi ziyeso ?
( b ) Mukakumana ndi mavuto , ndi zocitika zosaoneka ziti zimene muyenela kuganizila ?
( Yobu 2 : 4 , 5 ) Kodi tsopano Satana analeka kuneneza anthu a Mulungu ?
N’cifukwa ciani tiyenela kukambilana za “ anthu amene anapilila ” ?
Tikuphunzilapo ciani pa citsanzo ca akerubi amene anaikidwa mu Edeni ? Akerubi .
N’ciani cinathandiza Yobu kupilila ziyeso ?
Yobu anakhala ndi moyo wautali ndiponso wokhutilitsa . — Yobu 42 : 10 , 17 .
Malinga ndi 2 Akorinto 1 : 6 , kodi ena anapindula bwanji cifukwa ca kupilila kwa Paulo ?
( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 6 . )
15 , 16 . ( a ) Ndi “ nchito ” yotani imene kupilila kuyenela kumaliza ?
( b ) Pelekani zitsanzo zoonetsa zimene tingacite kuti ‘ tilole kupilila kumaliza kugwila nchito yake . ’
Kupilila mayeselo kumatithandiza kukonza umunthu wathu ( Onani ndime 15 ndi 16 )
17 , 18 . ( a ) Pelekani citsanzo coonetsa kuti tifunika kupilila mpaka mapeto . ( b ) Kodi sitiyenela kukaikila za ciani pamene mapeto akuyandikila ?
Pakuti ndatsimikiza mtima kuti imfa , moyo , angelo , maboma , zinthu zimene zilipo , zinthu zimene zikubwela m’tsogolo , mphamvu , msinkhu , kuzama , kapena colengedwa cina ciliconse , sicidzatha kutilekanitsa ndi cikondi ca Mulungu cimene cili mwa Kristu Yesu Ambuye wathu . ”
[ 1 ] ( ndime 11 ) Mungalimbikitsidwenso kwambili mukaŵelenga za kupilila kwa anthu a Mulungu amakono .
[ 2 ] ( ndime 12 ) Baibulo silikamba ciŵelengelo ca akerubi amene anapatsidwa udindo umenewu .
NWT ] — MACHITIDWE 2 : 42 .
mmene timalimbikitsila ena tikapezeka pa misonkhano .
1 - 3 . ( a ) Kodi Akristu amaonetsa bwanji kuti amafunitsitsa kupezeka pamisonkhano ?
( Onani cithunzi pamwambapa . ) ( b ) Tikambilana ciani m’nkhani ino ?
Panthawi imeneyi , tinalimbikitsidwa ndipo cikhulupililo cathu cinalimba kwambili . ”
Kodi misonkhano imatithandiza bwanji kuphunzila za Yehova ?
Nanga yakuthandizani bwanji kunola luso lanu mu ulaliki ?
Kodi misonkhano yathu imatithandiza bwanji kuti tikhalebe olimba ?
( Ŵelengani Machitidwe 15 : 30 - 32 . )
N’cifukwa ciani kupezeka pamisonkhano yathu n’kofunika ?
Kodi kupezeka pamisonkhano , kupeleka mayankho , ndi kuimba nyimbo zimathandiza bwanji Akristu anzathu ?
( Onaninso Bokosi lakuti “ Amamvelako Bwino Akapezeka Pamisonkhano . ” )
9 , 10 . ( a ) Fotokozani mmene mau a Yesu a pa Yohane 10 : 16 amatithandizila kumvetsa cifukwa cake kupezeka pamisonkhano n’kofunika kwambili . ( b ) Kodi kupezekapo kwathu pamisonkhano kungathandize bwanji anthu amene anakanidwa ndi mabanja ao ?
“ POSACEDWAPA , ndinayamba kudwala matenda amene amacititsa kuti ndizivutika kufika pamisonkhano .
Koma ndikakhala ndi mwai wopezekapo , ndimasangalala ndi cakudya cakuuzimu cimene Yehova amakonza .
Popita kumisonkhano ndimakhala kuti sindikumvela bwino cifukwa ca matenda a shuga , vuto la mtima , ndi kuŵaŵa kwa nkhongono . Koma pambuyo pamisonkhano , ndimamvelako bwino .
“ Tsiku loyamba kumva nyimbo nambala 68 , ya mutu wakuti ‘ Pemphero la Munthu Wovutika , ’ ikuimbidwa pamisonkhano , ndinakhudzika kwambili cakuti ndinagwetsa misozi .
Makina amene amandithandiza kuti ndizimvetsela bwino , anandithandiza kumva mau a anthu onse amene anali kuimba ndipo ndinaimba nao pamodzi .
Kodi pamisonkhano timakhala ndi mipata iti yolambila Yehova ?
Kodi Yehova amamva bwanji tikamvela lamulo lakuti tizipezeka pamisonkhano ?
Kodi kupezeka pamisonkhano kumatithandiza bwanji kuyandikila Yehova ndi Yesu ?
Ngati tipezeka pamisonkhano , kodi timaonetsa bwanji kuti tifuna kumvela Mulungu ?
16 , 17 . ( a ) Tidziŵa bwanji kuti Akristu oyambilila anali kuona misonkhano kukhala yofunika kwambili ?
( b ) Kodi m’bale George Gangas anali kuiona bwanji misonkhano yacikristu ?
Ndimakonda kufika mwamsanga pa Nyumba ya Ufumu , ndipo ndimakhala mmodzi wa anthu othela kucoka .
Ndimasangalala kuceza ndi anthu a Mulungu .
Ndikakhala pamodzi ndi abale ndi alongo , ndimamva ngati ndikuceza ndi banja langa , m’paladaiso wauzimu .
Kodi misonkhano mumaiona bwanji ? Nanga ndinu ofunitsitsa kucita ciani ?
[ 2 ] ( ndime 3 ) Onani bokosi lakuti “ Cifukwa Cake Tiyenela Kupezeka Pamisonkhano . ”
Kumeneko amamva uthenga wabwino kwa Mboni zimene zimacita ulaliki wa poyela
Malo okhala masisitele ku Zaragoza , ku Spain ( kumanzele ) Baibulo la Cináka - kolunga ( kulamanja )
Koma sindinali kudziŵa ngati ndinali kucita zinthu zoyenela .
Ndikumbukila tsiku lina ndinapemphela kuti , “ Yehova , ndiyamikila kwambili cifukwa simunandisiye , ndipo nthawi zambili munali kundipatsa mwai wopeza cidziŵitso colondola ca m’Baibulo cimene ndinali kufuna . ”
Nanga anthu a m’banja langa ndi mamembala a chalichi canga adzandiona bwanji ? ”
Ndinam’yankha kuti : “ Nanga muganiza kuti Mulungu adzamvela bwanji ? ”
Iwo anamwalila kutatsala miyezi iŵili kuti abatizidwe .
Kodi tiyenela kucita ciani ngati zavuta kuti tipewe kutenga mbali m’ndale ?
Tingaphunzile ciani kwa atumiki okhulupilika a Yehova amene sanatengemo mbali m’ndale ?
Tingacite ciani kuti tizimvela Mulungu ndi maboma a anthu ?
Kodi timaonetsa bwanji kuti sititenga mbali m’ndale za dzikoli ?
( a ) Tidziŵa bwanji kuti mtsogolomu zidzakhala zovuta kupewa kutenga mbali m’ndale ?
( b ) N’cifukwa ciani tifunika kukonzekela tsopano kuti tisadzatenge mbali m’ndale ?
Kodi akuluakulu a boma tiyenela kuwaona bwanji ?
Tingacite ciani kuti tikhale “ ocenjela ” koma “ oona mtima ” ngati tayesedwa kuti titenge mbali m’ndale ?
( Ŵelengani Mateyu 10 : 16 , 17 . )
Ndi zinthu ziti zimene tiyenela kusamala nazo pamene tikukambilana ndi anthu ?
Tingacite ciani kuti maganizo athu asasokonezeke ndi zimene ofalitsa nkhani amakamba ?
12 , 13 . ( a ) Kodi Yehova amawaona bwanji anthu ?
( b ) Tingadziŵe bwanji kuti tayamba kukonda kwambili dziko lathu ?
Nanga m’Baibulo muli citsanzo cotani coonetsa kuti zimenezi n’zoona ?
Kodi Baibulo lingatithandize bwanji kupewa kutenga mbali m’ndale ?
( Onaninso bokosi lakuti “ Mau a Mulungu Anawathandiza Kuti Asatenge Mbali m’Ndale . ” )
Tingaphunzile ciani kwa atumiki a Mulungu okhulupilika amene sanatenge mbali m’ndale ?
( Ŵelengani Danieli 3 : 16 - 18 . )
18 , 19 . ( a ) Kodi abale ndi alongo mumpingo wanu angakuthandizeni bwanji kuti musatenge mbali m’ndale ?
( b ) Kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ?
“ Kuganizila kwambili lemba la Miyambo 27 : 11 , Mateyu 26 : 52 , ndi la Yohane 13 : 35 kunandilimbikitsa kukana kuloŵa usilikali .
Malemba amenewa anandithandizanso kukhala wodekha pamene anali kundiimba mlandu . ” — Andriy , wa ku Ukraine .
“ Lemba la Yesaya 2 : 4 linandithandiza kusatenga mbali m’ndale pamene ndinali kuyesedwa .
Ndinali kuganizila za umoyo wamtendele umene tidzakhala nao m’paladaiso , pamene anthu sadzanyamulanso zida kuti aphe anzao . ” — Wilmer , wa ku Colombia .
“ Sungani mtendele pakati panu . ” — MALIKO 9 : 50 .
Kodi Yesu anapeleka malangizo otani otithandiza kuthetsa mikangano mwamtendele ?
Ndi mafunso ati amene Mkristu ayenela kudzifunsa akamasankha mmene ayenela kuthetsela mikangano ?
Kodi tingagwilitsile nchito bwanji malangizo a pa Mateyu 18 : 15 - 17 kuti tithetse mikangano ?
Ndi mikangano yotani imene inalembedwa m’buku la Genesis ?
Ndi mzimu wotani umene wafala padziko lonse ? Nanga pakhala zotsatilapo zotani ?
Kodi Yesu anauza ophunzila ake kuti ayenela kucita ciani pakabuka mikangano ?
6 , 7 . ( a ) N’cifukwa ciani kuthetsa mikangano mwamsanga n’kofunika ?
( b ) Ndi mafunso otani amene anthu onse a Yehova ayenela kudzifunsa ?
Atate wathu wakumwamba adzayankha mapemphelo ocokela pansi pamtima amenewo . — 1 Yohane 5 : 14 , 15 .
Tiyenela kucita ciani munthu wina akatikhumudwitsa ?
( Ŵelengani Miyambo 10 : 12 ; 1 Petulo 4 : 8 . )
( a ) Kodi mlongo wina anacita ciani anthu ena atamunena ?
( b ) Ndi lemba liti limene linathandiza mlongoyo kukhalabe wosangalala ?
11 , 12 . ( a ) Kodi Mkristu ayenela kucita ciani akaona kuti Mkristu mnzake ‘ ali naye cifukwa ’ ?
Kodi woyang’anila wina anacita ciani atauzidwa mau oipa ? Nanga mwaphunzilapo ciani pa citsanzo cake ?
14 , 15 . ( a ) Ndi pa zocitika ziti pamene tingagwilitsile nchito malangizo amene ali pa Mateyu 18 : 15 - 17 ?
( b ) Ndi masitepe atatu ati amene Yesu anakamba ?
N’ciani cionetsa kuti kutsatila malangizo a Yesu ndi njila yacikondi yothetsela mikangano ndiponso yothandiza ?
Kodi tidzalandila madalitso otani tikamayesetsa kukhala mwamtendele ndi ena ?
uthenga umene timalalikila ndiponso cifukwa cimene timalalikilila ?
Kodi mau a Yesu a pa Mateyu 24 : 14 amayambitsa mafunso otani ?
Mogwilizana ndi lemba la Mateyu 28 : 19 , 20 , kodi otsatila a Yesu ayenela kucita zinthu zinai ziti ?
Kodi kukhala “ asodzi a anthu ” kumafuna ciani ?
( Ŵelengani Mateyu 4 : 18 - 22 . )
Ndi mafunso anai ati amene tifunika kuyankha ? Nanga n’cifukwa ciani ?
N’cifukwa ciani tingakambe kuti Mboni za Yehova zimalalikila uthenga woyenela ?
Tidziŵa bwanji kuti atsogoleli a machalichi acikristu salalikila uthenga woyenela ?
Ndi colinga coipa citi cimene anthu ena amakhala naco pogwila nchito yolalikila ?
( Ŵelengani Machitidwe 20 : 33 - 35 . )
Kodi Mboni za Yehova zaonetsa bwanji kuti zimagwila nchito yolalikila ndi colinga cabwino ?
Kodi Yesu ndi ophunzila ake anali kulalikila bwanji ?
Kodi Mboni za Yehova zimasiyana bwanji ndi Machalichi Acikhristu pankhani yolalikila uthenga wabwino ?
Ndiwo okha amene amalalikila kuti Yesu wakhala akulamulila monga Mfumu kuyambila mu 1914 .
Kodi nchito yolalikila iyenela kugwilidwa pa mlingo wotani ?
N’ciani cikuonetsa kuti Mboni za Yehova zikukwanilitsa ulosi wa Yesu malinga ndi mmene zimagwilila nchito yao ?
Komanso webusaiti yathu ikupezeka m’zinenelo zoposa 750 .
Tidziŵa bwanji kuti Mboni za Yehova zili ndi mzimu woyela wa Mulungu ?
17 , 18 . ( a ) N’cifukwa ciani tingakambe kuti ndi Mboni za Yehova zokha zimene zikulalikila uthenga wabwino wa Ufumu masiku ano ?
( b ) N’ciani cimatithandiza kupitiliza kugwila nchito imeneyi ?
N’ciani cingatilepheletse kupindula ndi zinthu zina zakuuzimu ?
Ndi malangizo ati amene angatithandize kupindula ndi mbali zonse za m’Baibulo ?
Mungapindule bwanji mwa kuŵelenga zofalitsa zogaŵila ndiponso zimene amalembela acinyamata ?
1 , 2 . ( a ) Kodi Mboni za Yehova zimaliona bwanji Baibulo ?
( b ) Ndi mbali iti ya m’Baibulo imene mumakonda kwambili ?
3 , 4 . ( a ) Kodi zofalitsa zathu timaziona bwanji ?
( b ) Chulani zofalitsa zimene zimalembedwela anthu osiyanasiyana .
Kodi Yehova amakondwela ndi ciani ?
N’cifukwa ciani tiyenela kuŵelenga Baibulo tili ndi maganizo oyenela ?
8 , 9 . ( a ) Ndi mafunso ati amene tiyenela kudzifunsa tikamaŵelenga Baibulo ?
( b ) Kodi ziyeneletso zimene akulu Acikristu ayenela kukwanilitsa zimatiuza ciani ponena za Yehova ?
Nanga ndingazigwilitsile nchito bwanji pothandiza anthu ena ? ’
( Ŵelengani 1 Timoteyo 3 : 2 - 7 . )
10 , 11 . ( a ) Pamene tiŵelenga ziyeneletso za akulu , kodi tingazigwilitsile nchito bwanji pa umoyo wathu ?
( b ) Nanga ndingazigwilitsile nchito bwanji pothandiza anthu ena ?
12 , 13 . ( a ) Ndi kufufuza kotani kumene tingacite pogwilitsila nchito zofufuzila zimene tili nazo ?
( b ) Kambani citsanzo coonetsa mmene kufufuza kungatithandizile kudziŵa mfundo zobisika .
Kodi zofalitsa zimene zimalembedwela acinyamata zingawathandize bwanji ? Nanga ena zingawathandize bwanji ?
N’cifukwa ciani Akristu acikulile ayenela kuŵelenga zofalitsa zimene zimalembedwela acinyamata ?
Kodi zofalitsa zathu zimawathandiza bwanji acinyamata ?
( Ŵelengani Mlaliki 12 : 1 , 13 . )
Kodi Ndingatani Kuti Kuŵelenga Baibulo Kuzindisangalatsa ? ”
Tingapindule bwanji ndi zofalitsa zogaŵila ?
Tingaonetse bwanji kuti timayamikila Yehova cifukwa ca zofalitsa zimene amatipatsa ?
Kodi zosankha zathu zingakhudze bwanji ifeyo ndiponso anthu ena ?
Ngati Baibulo silinapeleke lamulo pankhani ina yake , kodi tingadziŵe bwanji zimene zingakondweletse Yehova ?
Tingacite ciani kuti tiziona zinthu mmene Yehova amazionela ?
Ndi malamulo ena ati amene amapezeka m’Baibulo ? Nanga kuwamvela kumatipindulitsa bwanji ?
2 , 3 . ( a ) N’cifukwa ciani Baibulo silipeleka malamulo pankhani zina ?
( b ) Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ?
Nanga zingakhudze bwanji anthu ena ?
Ngati m’Baibulo mulibe lamulo lacindunji pankhani ina yake , kodi tingadziŵe bwanji zimene Yehova afuna kuti ticite ?
Kodi Yesu anazindikila bwanji zimene Yehova anali kufuna kuti iye acite ?
( Ŵelengani Mateyu 4 : 2 - 4 . )
Uzim’kumbukila m’njila zako zonse , ndipo iye adzawongola njila zako .
Ndi mafunso ati amene tingadzifunse pamene tiŵelenga Baibulo kapena kucita phunzilo laumwini ?
Kodi zofalitsa zathu ndi misonkhano zingatithandize bwanji kudziŵa mmene Yehova amaonela zinthu ?
Pelekani citsanzo coonetsa kuti kudziŵa mmene Yehova amaonela zinthu kungatithandize kupanga zosankha mwanzelu .
( Ŵelengani Luka 18 : 29 , 30 . )
Kodi mungadziŵe bwanji ngati sitayilo inayake ya zovala ndi yovomelezeka kwa Yehova ?
( c ) Kodi tiyenela kucita bwanji tikafuna kupanga zosankha zazikulu ?
Kodi timapindula bwanji tikapanga zosankha zimene zimakondweletsa Yehova ?
N’zoona kuti sitingadziŵe zonse zokhudza Yehova .
N’cifukwa ciani tiyenela kupitiliza kusintha zinthu zina pambuyo pobatizidwa ?
N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tiziyesetsa kulimbana ndi zizoloŵezi zoipa ?
Tingacite ciani kuti Mau a Mulungu apitilize kutisintha ?
1 - 3 . ( a ) Ndi zinthu ziti zimene zingativute kusintha pambuyo pa ubatizo ?
( b ) Ndi mafunso ati amene tingadzifunse ngati tikulephela kusintha zinthu zina zimene siticita bwino ?
N’cifukwa ciani nthawi zina timalephela kukondweletsa Yehova ?
Ndi zinthu ziti zimene tinasintha tikalibe kubatizika ? Nanga ndi zofooka ziti zimene tingakhale tikulimbana nazo mpaka pano ?
6 , 7 . ( a ) N’ciani cimacititsa kuti tikhale paubwenzi wabwino ndi Yehova ngakhale kuti ndife opanda ungwilo ?
( b ) N’cifukwa ciani sitiyenela kuopa kupempha Yehova kuti atikhululukile ?
Tidziŵa bwanji kuti kuvala umunthu watsopano ndi cinthu cimene tifunika kucita nthawi zonse ?
Kodi tifunika kucita ciani kuti Baibulo litithandize kusintha umunthu wathu ? Nanga tingadzifunse mafunso ati ?
N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tiziyesetsa kulimbana ndi zofooka zathu ?
Kodi tingacite ciani kuti tikhale ndi makhalidwe amene Mulungu amakondwela nawo ?
( Onani bokosi lakuti “ Baibulo ndi Pemphelo Zinasintha Umoyo Wao . ” )
N’cifukwa ciani sitiyenela kutaya mtima ngati sitikusintha mwamsanga ?
Kodi tidzapeza madalitso otani ngati tikhalabe okhulupilika kwa Yehova ?
Tidziŵa bwanji kuti Baibulo lili ndi mphamvu zotithandiza kusintha umunthu wathu ?
[ 1 ] ( ndime 1 ) Dzina lasinthidwa .
Russell : “ Kupeleka mapemphelo opembedzela kwa Yehova ndi kuŵelenga Baibulo tsiku lililonse kwandithandiza .
Cinanso cimene candithandiza ndi kuganizila lemba la 2 Petulo 2 : 11 ndiponso uphungu umene akulu anandipatsa . ”
Maria Victoria : “ Ndinacondelela Yehova m’pemphelo kuti andithandize kulamulila lilime langa .
Ndinaona kuti ndifunika kuleka kuceza ndi anthu amene amakonda kunena anzao .
Pamene ndinaŵelenga lemba la Salimo 64 : 1 - 4 , ndinaona kuti ndifunika kusintha kuti anthu ena asamandiope .
Ndinadziŵanso kuti ndikapitiliza kunena anthu ena ndidzakhala citsanzo coipa ndipo ndidzanyozetsa dzina la Yehova . ”
Linda : “ Ndinayesetsa kutudziŵa bwino tumapepala tonse twa uthenga n’colinga cakuti ndizikhala okonzeka kugaŵila anthu ena .
Kulalikila ndi anthu amene amagwilitsila njila zosiyanasiyana mu utumiki , kwandithandiza kwambili .
Komanso ndimadalila Yehova kudzela m’pemphelo . ”
Ife tonse timacita zinthu zimene zingakhumudwitse anthu ena .
mmene Yehova amasankhila anthu amene afuna kuwaumba ?
mmene Mulungu amaumbila anthu amene amamumvela ?
Kodi tingatengele bwanji citsanzo ca Aisiraeli olapa ?
Kodi Yehova amasankha bwanji anthu amene amawakokela kwa iye ?
( Ŵelengani 1 Samueli 16 : 7b . )
Kodi kudziŵa kuti Yehova ni amene amatiumba , kuyenela kukhudza bwanji mmene timaonela ( a ) anthu a m’gawo lathu ?
Patapita nthawi , n’nakumana ndi banja lina limene n’nakonda cifukwa ca makhalidwe awo abwino .
Tsiku lina n’nadabwa kwambili n’tadziŵa kuti iwo anali a Mboni za Yehova .
Khalidwe lawo labwino linan’cititsa kuzindikila kuti n’nali kuzonda a Mboni za Yehova cifukwa cosawadziŵa bwino ndiponso cifukwa ca zinthu zabodza zimene ena anali kuniuza zokhudza iwo . ”
( Ŵelengani Aheberi 12 : 5 , 6 , 11 . )
Kodi Yehova amatiphunzitsa bwanji masiku ano ? Nanga maphunzilo amenewa adzapitiliza bwanji mtsogolo ?
( Yohane 13 : 35 ) Ndipo taphunzila kukonda anthu ena .
Kodi Yesu anaonetsa bwanji luso ndi kuleza mtima kwa Woumba Wamkulu ?
( Ŵelengani Salimo 103 : 10 - 14 . )
Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali monga dothi lofewa ? Nanga tingatengele bwanji citsanzo cake ?
Kodi Yehova amatiumba bwanji pogwilitsila nchito mzimu woyela ndi mpingo wacikhiristu ?
Ngakhale kuti Yehova amatiumba , kodi amalemekeza bwanji ufulu wathu wosankha ?
Kodi ophunzila Baibulo amaonetsa bwanji kuti afuna kuumbidwa ndi Yehova ?
( a ) Mumamvela bwanji mukaganizila kuti Yehova amakuumbani ?
( b ) Tidzaphunzila ciani m’nkhani yotsatila ?
Kodi Yehova Mulungu wathu ni “ Yehova mmodzi ” m’njila ya bwanji ?
Tingaonetse bwanji kuti timalambila “ Yehova mmodzi ” ?
Tingacite ciani kuti tikhalebe amtendele ndi ogwilizana ?
( b ) N’cifukwa ciani Mose anakamba mau amenewo ?
4 , 5 . ( a ) Kodi mau akuti “ Yehova mmodzi ” atanthauza ciani ?
( b ) Nanga Yehova amasiyana bwanji ndi milungu ya mitundu ina ?
Kodi mau akuti “ mmodzi , ” amatanthauzanso ciani ? Nanga Yehova anaonetsa bwanji kuti ni “ mmodzi ” ?
8 , 9 . ( a ) Kodi Yehova amafuna kuti amene amamulambila azicita ciani ?
( b ) Kodi Yesu anaonetsa bwanji kuti mau a Mose ni ofunika kwambili ?
( Ŵelengani Maliko 12 : 28 - 31 . )
10 , 11 . ( a ) Tingaonetse bwanji kuti timalambila Yehova yekha ?
( b ) Kodi acicepele aciheberi anaonetsa bwanji kuti anali odzipeleka kwa Yehova yekha ?
Ngati tifuna kudzipeleka kwa Yehova yekha , kodi tiyenela kusamala ndi ciani ?
N’zinthu ziti zimene tingayambe kukonda kwambili kuposa Yehova ?
N’cifukwa ciani Paulo anakumbutsa Akhiristu kuti Mulungu ni “ Yehova mmodzi ” ?
16 , 17 . ( a ) Ni ulosi wa bwanji umene ukukwanilitsika masiku ano ? Nanga ukukwanilitsika bwanji ?
( b ) N’ciani cingawononge mgwilizano wathu ?
18 , 19 . ( a ) Ni malangizo otani amene ali pa Aefeso 4 : 1 - 3 ?
( b ) Tingacite ciani kuti tithandize mpingo kukhala wogwilizana ?
( Ŵelengani Aefeso 4 : 1 - 3 . )
Tingaonetse bwanji kuti timamvetsetsa tanthauzo la mau akuti “ Yehova Mulungu wathu ndi Yehova mmodzi ” ?
M’mbali mwa zilumba za Trinidad ndi Tobago muli midzi yambili imene asodzi amakhalamo .
Mboni za Yehova zimalalikila asodzi amene zimapeza kumeneko
Kodi Baibulo imaonetsa bwanji kuti tonse ndife ocimwa ?
Kodi tiyenela kucita bwanji ndi zolakwa zathu ndi za ena ?
Kodi Baibulo inakambilatu ciani ponena za kuculuka kwa anthu a Yehova ?
( Ŵelengani Mika 4 : 1 , 3 . )
Izi zawathandiza kuti akhale “ oyela pa mlandu wa magazi a anthu onse . ” — Machitidwe 20 : 26 .
N’cifukwa ciani n’zocititsa cidwi kuti gulu la Yehova likukulilakulila ?
N’cifukwa ciani nthawi zina anthu ena amatikhumudwitsa ?
( Ŵelengani Aroma 5 : 12 , 19 . )
Kodi mukanakhala ku Isiraeli m’nthawi ya Eli ndi ana ake , sembe munacita ciani ?
Kodi Eli analephela bwanji kulanga ana ake ?
Ni macimo aakulu ati amene Davide anacita ? Nanga Mulungu anacita ciani ?
( a ) Kodi mtumwi Petulo analephela bwanji kusunga lonjezo lake ?
( b ) N’cifukwa ciani Yehova anapitiliza kugwilitsila nchito Petulo pambuyo pakuti wacimwa ?
Kodi mumakhulupilila kuti Mulungu nthawi zonse amacita zinthu mwacilungamo ? Cifukwa ciani ?
Kodi Yesu anazindikila ciani pa zolakwa za Yudasi Isikariyoti ndi Petulo ?
Kodi Baibulo inakamba ciani ponena za atumiki a Yehova a masiku ano ?
Kodi tiyenela kucita ciani ena akatilakwila ?
13 , 14 . ( a ) N’cifukwa ciani tiyenela kukhala oleza mtima ndi abale athu ?
( b ) Ni lonjezo liti limene tiyenela kumakumbukila ?
Kodi Yesu anakamba kuti tiyenela kucita ciani ena akatilakwila ?
Kodi inu mudzacita ciani ngati ena akulakwilani ?
( Ŵelengani Mateyu 5 : 23 , 24 . )
Mayankho a mafunso amenewa si ovuta .
Tingamvetsetse mfundo imeneyi tikaganizila zimene Baibulo imakamba pankhani yokhala wozindikila ndi wanzelu .
Lemba la Miyambo 3 : 13 - 15 limati : “ Wodala ndi munthu amene wapeza nzelu , ndiponso munthu amene wapeza kuzindikila , cifukwa kupeza nzelu monga phindu n’kwabwino kuposa kupeza siliva monga phindu , ndipo kukhala nazo monga zokolola n’kwabwino kuposa kukhala ndi golide .
N’zamtengo wapatali kuposa miyala ya korali , ndipo zonse zimene umakonda sizingafanane nazo . ”
Yesu anapeleka citsanzo cabwino pankhani yokhala woona mtima .
Popeza n’nali bwana wamkulu pa kampaniyo , n’nali kufunika kunyengelela anthu otenga msonkho mwa kuwapatsa n’cekeleko kuti asaulule cinyengo ca kampaniyo .
Izi zinacititsa kuti ndizidziŵika monga munthu wosaona mtima .
N’taphunzila coonadi , ndinaleka nchitoyo ngakhale kuti n’nali kulandila ndalama zambili .
Napeleka citsanzo cabwino kwa ana anga aŵili aamuna , ndipo tsopano n’naikidwa paudindo mumpingo .
Cifukwa cokhala woona mtima , nili ndi mbili yabwino kwa anthu amene amatenga misonkho ndi ena amene nimacita nawo bizinesi . ”
Kumeneko anayamba kulambila Mulungu woona .