© 2017 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania Zopeleka zaufulu n’zimene zimathandiza kupititsa patsogolo nchito imeneyi . Kuti mupeleke copeleka canu , yendani pa webusaiti ya www.jw.org . Baibo imene taseŵenzetsa ni Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika kusiyapo ngati taonetsa ina . © 2018 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania Yehova ndi dzina la Mulungu monga mmene lalembedwela m’Baibo . Cifunilo canu cicitike , monga kumwamba , cimodzi - modzinso pansi pano , ” silinayankhidwe kothelatu . ( Mat . ( Ŵelengani Luka 21 : 1 - 4 . ) Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 8 m’buku ili Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova ( b ) Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? ( b ) Ndi mafunso ati amene tidzakambitsilana m’nkhani yotsatila ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 10 : 13 . ) Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 3 m’buku ili , Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova ( Ŵelengani 1 Akorinto 6 : 9 - 11 . ) Pamenepo amene ali mu Yudeya adzayambe kuthaŵila kumapili , ndipo amene ali mkati mwa mzindawo adzatulukemo . Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Ineyo Yehova ndidzafulumizitsa zimenezi pa nthawi yake . ” ( b ) Kodi tidzakambitsilana mafunso ati ? ( Ŵelengani Luka 10 : 29 - 37 . ) Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ? Koma usadye zipatso za mtengo wodziŵitsa cabwino ndi coipa . Cifukwa tsiku limene udzadya , udzafa ndithu . ” Ndimupangila womuthandiza , monga mnzake womuyenelela . ” ( b ) Tikambilana mafunso ati ? “ Mau a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu . ” — AHEB . ( Ŵelengani Chivumbulutso 14 : 6 , 7 . ) ( Ŵelengani 1 Atesalonika 2 : 13 . ) Adzaweluza mwacilungamo anthu onyozeka ndipo adzadzudzula anthu moongoka mtima , pothandiza ofatsa pa dziko lapansi . ” “ Cikhulupililo ndico ciyembekezo cotsimikizilika ca zinthu zoyembekezeledwa . ” — AHEB . ( Ŵelengani Aheberi 13 : 7 , 17 . ) ( b ) Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ? Yesu anati : “ Kumene kuli cuma cako , mtima wako umakhalanso komweko . ” ( Ŵelengani Aroma 7 : 21 - 25 . ) Ngati n’conco , tikuyamikilani kwambili . ( Ŵelengani Aheberi 11 : 24 - 27 . ) “ Odala ndi anthu amene Mulungu wao ndi Yehova . ” — SAL . Maakaunti Akubanki : Mukhoza kupeleka zinthu monga maakaunti anu akubanki , zikalata zosungitsila ndalama , kapena maakaunti a ndalama zimene mukusunga kuti mudzagwilitse nchito mukadzapuma pa nchito . Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Kodi mwaŵelenga mosamala magazini aposacedwapa a Nsanja ya Mlonda ? Yesani kuyankha mafunso otsatilawa : Lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova koma tsopano anasiya kulisindikiza . Maina ena asinthidwa . ( Ŵelengani Yakobo 5 : 14 - 16 . ) ( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Iye anati : “ Ine ndine wakuthupi , wogulitsidwa ku ucimo . Kodi tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? ( b ) Tikambilana ciani m’nkhani ino ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 58 . ) Simungathe kutumikila Mulungu ndi Cuma nthawi imodzi . ” ( Ŵelengani Aheberi 10 : 24 , 25 . ) ( Ŵelengani 2 Akorinto 8 : 13 - 15 . ) ( Ŵelengani Mateyu 24 : 37 - 39 . ) Nowa anayenda ndi Mulungu woona . ” — Gen . © 2016 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania MAGAZINI ya Nsanja ya Mlonda , imalemekeza Yehova Mulungu , amene ndi Wolamulila wa cilengedwe conse . Imalimbikitsa anthu ndi uthenga wabwino wakuti Ufumu wa Mulungu posacedwapa udzacotsa zoipa zonse ndi kusintha dziko lapansi kukhala paladaiso . Imalimbikitsa anthu kukhulupilila Yesu Kristu amene anatifela kuti tidzapeze moyo wosatha , ndipo panthawi ino iye akulamulila monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu . Magaziniyi yakhala ikufalitsidwa kuyambila mu 1879 ndipo si yandale . Mfundo zake zonse n’zocokela m’Baibulo . Bebe anali kukonda kwambili atate ake . Bwenzi la banja lao ndilo linakamba mau amene ali pamwambapa , koma mauwo sanamutonthoze . Iye mobwelezabweleza anali kudziuza kuti : “ Atate anafa imfa yoipa . ” Patapita zaka , Bebe analemba za imfa ya atate ake m’buku . Izi zinaonetsa kuti anali akali ndi cisoni . Malinga ndi zimene zinacitikila Bebe , zimatenga nthawi yaitali kuti munthu apilile cisoni makamaka ngati munthu amene anamwalila anali kum’konda kwambili . M’pomveka kuti Baibulo limacha imfa kuti “ mdani womalizila . ” ( 1 Akorinto 15 : 26 ) Imfa imasokoneza kwambili umoyo wathu , ndipo mwadzidzidzi imatenga anthu amene timakonda kwambili . Palibe amene angapewe zotsatilapo za imfa . Conco , n’zosadabwitsa kuti zimativuta kupilila imfa ndi zotsatilapo zake . Mwina mumadzifunsa kuti : ‘ Kodi cisoni cimatenga nthawi yaitali bwanji kuti cithe ? Ndingatonthoze bwanji anthu amene okondedwa ao anamwalila ? Kodi pali ciyembekezo ciliconse kaamba ka okondedwa athu amene anamwalila ? ’ Kodi munadwalapo ? Mwacitsanzo , ganizilani mmene Abulahamu anamvelela pamene mkazi wake anamwalila . Baibulo limati : “ Abulahamu analoŵa muhema kukamulila Sara . ” Mau akuti “ kukamulila ” aonetsa kuti cinamutengela nthawi yaitali kuti apilile imfa ya mkazi wake . Yakobo analila mwana wake kwa “ masiku ambili , ” ndipo anali kukana kutonthozedwa ndi anthu a m’banja lake . Ngakhale panali patapita zaka zambili , iye anali kukumbukilabe imfa ya Yosefe . — Genesis 23 : 2 ; 37 : 34 , 35 ; 42 : 36 ; 45 : 28 . “ Mwamuna wanga Robert anamwalila pa July 9 , 2008 . Ngakhale papita zaka 6 , ndimamvabe cisoni mumtima mwanga . Sindidziŵa ngati imfa ya Rob ndidzaiiŵala . ” — Gail , wazaka 60 . Papita zaka 18 kucokela pamene mkazi wanga anamwalila , koma ndimamuyewabe ndipo ndimamvabe cisoni . Ndikaona cinthu cocititsa cidwi m’cilengedwe , ndimakumbukila mkazi wanga ndipo ndimaganizila mmene iye akanasangalalila kuona zinthu zimene ineyo ndikuona . ” — Etienne , wazaka 84 . Kukamba zoona , n’kwacibadwa kumva ululu ndi cisoni . Aliyense amalila m’njila zosiyanasiyana , ndipo kungakhale kupanda nzelu kuweluza munthu kaamba ka mmene akulilila cifukwa ca mavuto . Komanso panthawi imodzimodzi , tisamadziimbe mlandu tikakhala ndi cisoni cimene sicikutha . Malinga ndi zimene zili m’nkhani yakuti “ Tengelani Cikhulupililo Cao ” imene ili mu Nsanja ya Mlonda ino , Isaki analila amai ake kwa zaka zitatu . — Genesis 24 : 67 . Mwacitsanzo , ena angakuuzeni kuti musalile kapena kuonetsa cisoni . Ena angakuuzeni kuti muonetse cisoni canu conse . Malangizo ake ndi ogwilizana kwambili ndi zimene ofufuza apeza masiku ano . M’zikhalidwe zina , anthu amakamba kuti mwamuna weniweni salila . Koma kodi tifunika kucita manyazi kulila tikakhala pagulu la anthu ? Akatswili oona za matenda a m’maganizo anati , kulila ndi njila yabwino yoonetsela cisoni . M’kupita kwa nthawi , kulila kungakuthandizeni kupilila imfa ya wokondedwa wanu . Koma kubisa cisoni canu kungabweletse mavuto ambili . Baibulo silicilikiza mfundo yakuti mwamuna weniweni salila . Iye analila pamaso pa anthu pamene Lazaro bwenzi lake anamwalila , ngakhale kuti anali ndi mphamvu zoukitsa anthu . — Yohane 11 : 33 - 35 . Kukhala wokwiya ndi njila inanso yoonetsela cisoni , makamaka pa imfa ya mwadzidzidzi . Munthu wofeledwa amakhala wokwiya pa zifukwa zosiyanasiyana . Cifukwa cimodzi cingakhale cakuti , munthu amene amamulemekeza angakambe mau osathandiza kwenikweni . Mwamuna wina dzina lake Mike , amene akhala ku South Africa , anakamba kuti : “ Atate anamwalila ndili ndi zaka 14 . Tili pamalilo , m’busa wa chalichi ca Anglican anakamba kuti Mulungu amafuna anthu abwino ndipo amawatenga . * Zimenezi zinandikhumudwitsa cifukwa atate ndinali kuŵakonda kwambili . Pakacitika imfa ya mwadzidzidzi , wofeledwa angakhale ndi maganizo akuti , ‘ Ndikanacita zakutizakuti , munthuyo sakanamwalila . ’ Ngati mukudziimba mlandu kapena ndinu wokwiya cifukwa ca imfa ya wokondedwa wanu , musabise mmene mukumvelela . Fotokozelani mnzanu wapamtima amene angakumvetseleni ndi kukutsimikizilani kuti maganizo otelo amavutitsa ofeledwa ambili . Baibulo limati : “ Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse , ndipo ilo ndi m’bale amene anabadwila kuti akuthandize pakagwa mavuto . ” — Miyambo 17 : 17 . Bwenzi la pamtima limene anthu ofeledwa angakhale nalo ndi Mlengi wathu , Yehova Mulungu . Muuzeni zakukhosi kwanu m’pemphelo cifukwa iye “ amakudelani nkhawa . ” ( 1 Petulo 5 : 7 ) Kuonjezela apo , iye walonjeza onse amene amatelo kuti adzatsitsimula mtima ndi maganizo ao , cifukwa “ mtendele wa Mulungu umaposa kuganiza mozama kulikonse . ” ( Afilipi 4 : 6 , 7 ) Cinanso , lolani Mulungu kuti akuthandizeni kupilila cisoni kupitila m’Mau ake , Baibulo . Kuganizila malembawa mozama kungakuthandizeni kwambili makamaka usiku mukakhala nokha , ndiponso ngati mukulephela kugona . — Yesaya 57 : 15 . Mwamuna wina wa zaka 40 amene tam’patsa dzina lakuti Jack , mkazi wake anamwalila ndi matenda a kansa . Iye anati : “ Kupemphela kwa Yehova kumandithandiza kuona kuti sindili ndekha . Kaŵilikaŵili , ndimauka pakati pa usiku ndipo ndimalephela kugonanso . Ndikaŵelenga ndi kuganizila mozama Malemba otonthoza , ndimauza Mulungu zakukhosi kwanga m’pemphelo . Ndikatelo , mtima wanga umakhala m’malo ndipo ndimakhala ndi mtendele wa m’maganizo . Izi zimandithandiza kupeza tulo . ” Mai a mtsikana wina dzina lake Vanessa , anamwalila atadwala kwambili . Iyenso waona kuti pemphelo limathandiza kwambili . Iye anati : “ Panthawi yovutayi , ndinali kupemphela kwa Mulungu uku ndikulila . Yehova anamvetsela mapemphelo anga ndipo anandipatsa mphamvu zakuti ndipilile . ” Alangizi ena a anthu ofedwa amauza amene akuvutika ndi cisoni kuti azigwila nchito zothandiza ena . Kugwila nchito zotelo kumabweletsa cimwemwe ndipo kumacepetsa cisoni ca munthu . ( Machitidwe 20 : 35 ) Ofedwa ambili amene ndi Akristu , aona kuti kugwila nchito zimenezi n’kotonthoza kwambili . — 2 Akorinto 1 : 3 , 4 . Mulungu amamvetsa mmene mukumvelela . — Salimo 55 : 22 ; 1 Petulo 5 : 7 . Mulungu amamvela mapemphelo a atumiki ake . — Salimo 86 : 5 ; 1 Atesalonika 5 : 17 . Mulungu amakumbukila anthu amene anamwalila . — Yobu 14 : 13 - 15 . Mulungu analonjeza kuti adzaukitsa akufa . — Yesaya 26 : 19 ; Yohane 5 : 28 , 29 . Kodi munasoŵapo cocita pamene mnzanu anali ndi cisoni cifukwa ca wokondedwa wake amene anamwalila ? Izi zikacitika , nthawi zina timasoŵa cokamba kapena cocita , cakuti timangokhala cete . Komabe , pali zinthu zina zimene tingacite kuti tithandize olila . Cofunika kwambili ndi kupita kunyumba ya malilo ndi kunena mau monga akuti , “ Pepani ndi zimene zacitika . ” M’zikhalidwe zambili , anthu amaona kuti kukumbatila munthu ndi kulila naye ndi njila yabwino yoonetsela kuti mumasamala za ena . Ngati wofeledwa akukuuzani zinazake , mvetselani bwinobwino . Koposa zonse , mungacitile banja limene lili ndi cisoni zinthu zina , makamaka zimene silingakwanitse kucita . Zinthu monga kuphika cakudya , kusamalila ana , kapena kukonza pulogalamu yamalilo ngati n’zotheka . M’kupita kwa nthawi , mungayambe kukamba za womwalilayo . Mwacitsanzo , mungakambe za makhalidwe ake abwino , kapena zocitika zina zosangalatsa zokhudza iye . Makambilano a conco , angathandize munthu wofeledwa kukhala wosangalala . Mwacitsanzo , Pam , amene mwamuna wake anamwalila zaka 6 zapitazo anati : “ Nthawi zina , anthu amandiuza zinthu zabwino zimene mwamuna wanga Ian anali kucita , zimene sindinali kuzidziŵa . Zimenezo zimandipangitsa kumva bwino . ” Ofufuza ena apeza kuti ofeledwa ambili amangolandila thandizo panthawi ya malilo yokha , koma m’kupita kwa nthawi amanyalanyazidwa , cifukwa anzao amakhala otangwanika ndi zocitika zina . Conco , muziyesetsa kukamba ndi wofeledwa nthawi zonse kucokela pamene wokondedwa wao anamwalila . * Ofeledwa ambili amayamikila mocokela pansi pamtima ngati mwakamba nao . Zimenezi zimacepetsa cisoni cao . Ganizilani za Kaori , mtsikana wa Cijapanizi amene anakhumudwa kwambili amai ake atamwalila . Patapita caka ndi miyezi itatu , mkulu wake nayenso anamwalila . Koma zosangalatsa n’zakuti anzake okhulupilika anali kum’thandiza panthawi yovutayo . Mai wina wacikulile dzina lake Ritsuko , anakhala mnzake wa pamtima wa Kaori . Kaori anati : “ Kukamba zoona , sindinali wokondwa ndipo sindinali kufuna aliyense kuti akhale amai anga . Koma cifukwa ca mmene a Ritsuko anali kucitila nane zinthu , ndinayamba kuwakonda kwambili . Mlungu uliwonse , tinali kupitila limodzi mu ulaliki ndi ku misonkhano yacikristu . Nthawi zambili anali kundiitana kuti tidzamwele tiyi pamodzi , kundibweletsela zakudya , ndiponso kundilembela makalata ndi makadi . Cikondi cimene a Ritsuko anandionetsa cinandilimbikitsa kwambili . ” Papita zaka 12 kucokela pamene amake Kaori anamwalila . Tsopano , iye ndi mwamuna wake ndi alaliki a nthawi zonse a Mau Mulungu . Kaori anati : “ A Ritsuko amandikondabe mpaka pano . Ndikabwelela kwathu , nthawi zonse ndimapita kukawaona , ndipo amandilimbikitsa kwambili . ” Citsanzo cina ndi Poli , wa Mboni za Yehova wa m’dziko la Cyprus , amene anapindula ndi thandizo limene anali kulandila . Mwamuna wa Poli dzina lake Sozos anali m’busa wacikristu wacitsanzo cabwino komanso wokoma mtima . Iye anali kuitana ana ndi akazi amasiye kunyumba kwao kuti adzaceze nao ndi kudya nao pamodzi . ( Yakobo 1 : 27 ) Zacisoni n’zakuti Sozos anapezeka ndi cotupa mu ubongo , ndipo anamwalila ali ndi zaka 53 . Kumeneko , iye anapitiliza kusonkhana ndi mpingo wina wa Mboni za Yehova . Poli anati : “ Mabwenzi a mumpingo watsopanowo sanali kudziŵa mavuto amene tinali kukumana nao . Ngakhale n’conco , io sanaleke kutitonthoza ndi mau ao abwino komanso kutithandiza mwakuthupi . Thandizo limenelo linali la mtengo wapatali makamaka pa nthawi imene mwana wanga anali kuyewa atate ake . Anthu amene anali kutsogolela mumpingo anali kum’konda kwambili Daniel . Mkulu wina mumpingowo , anali kuitana Daniel kuti adzaceze naye pamodzi ndi mabwenzi ena kapena kukachaya bola . ” Masiku ano , Poli ndi mwana wake akusangalala . Kukamba zoona , pali njila zambili za mmene tingatonthozele ndi kuthandizila anthu olila . Baibulo nalonso limatitonthoza mwa kutipatsa ciyembekezo cabwino kwambili ca mtsogolo . Ena amalemba pa kalenda tsiku limene munthuyo anamwalila , n’colinga cakuti azikumbukila kutonthoza ofeledwa pamene akufunikila citonthozo . Kumbukilani kuti Gail amene tamuchula m’nkhani zapita zija , anakaikila ngati adzakwanitsa kupilila imfa ya mwamuna wake Rob . Komabe , iye ali ndi ciyembekezo cakuti adzaonananso naye m’dziko latsopano la Mulungu . Ndimacitila cifundo anthu amene okondedwa ao anamwalila , amenenso sadziŵa za ciyembekezo cakuti akufa adzaukitsidwa . ” Posacedwapa , Mulungu adzaukitsa Yobu limodzi ndi ena ambili , dzikoli likadzakhala paladaiso . ( Luka 23 : 42 , 43 ) Lemba la Machitidwe 24 : 15 limatitsimikizila kuti : “ Kudzakhala kuuka . ” Yesu nayenso akutitsimikizila kuti : “ Musadabwe nazo zimenezi , cifukwa idzafika nthawi pamene onse ali m’manda acikumbutso adzamva mau ake ndipo adzatuluka . ” Iye adzakhalanso ndi ‘ mphamvu monga mmene analili pa unyamata wake , ’ ndipo ‘ mnofu wake udzasalala kuposa wa mwana . ’ ( Yobu 33 : 24 , 25 ) Izi n’zimene zidzacitikila anthu amene amayamikila makonzedwe acikondi a Mulungu , akuti akufa adzakhalanso ndi moyo padziko lapansi . Ngati munthu amene mumakonda anamwalila , mwina mukuona kuti mfundo zimene takambilanazi sizingathetseletu cisoni canu . Koma kuganizila mozama malonjezo a Mulungu opezeka m’Baibulo , kudzakuthandizani kukhala ndi ciyembekezo komanso mphamvu zakuti mupilile cisoni . — 1 Atesalonika 4 : 13 . Kodi mufuna kudziŵa zambili zokhudza zimene mungacite kuti mupilile cisoni canu ? Kapena kodi mufuna kupeza mayankho a mafunso monga lakuti “ N’cifukwa ciani Mulungu amalolela kuti anthu azivutika ? ” Pitani pa webusaiti yathu ya jw.org kuti mupeze mayankho otonthoza ndi othandiza a m’Baibulo . ZINA ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA “ Mulungu . . . adzapukuta misozi yonse m’maso mwao , ndipo imfa sidzakhalaponso . ” — Chivumbulutso 21 : 3 , 4 . Nsanja ya Mlonda iyi ifotokoza mmene Mulungu adzakwanilitsila lonjezo limeneli ndi mmene mudzapindulila . NKHANI YA PACIKUTO | N’CIFUKWA CIANI YESU ANAVUTIKA NDI KUTIFELA ? Mu 33 C.E . , Yesu wa ku Nazareti anaphedwa . Iye anapatsidwa mlandu wabodza woukila boma , anamenyedwa mwankhanza , ndipo anakhomeledwa pamtengo . Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa , ndipo patapita masiku 40 Yesu anabwelela kumwamba . Zocitika zapadela zimenezi zinalembedwa m’mabuku anai a Uthenga Wabwino a m’Malemba Acigiliki Acikristu , amene amadziŵika kuti Cipangano Catsopano . ( 1 Akorinto 15 : 14 ) Komabe , ngati zinthuzo zinacitikadi , ndiye kuti anthu ali ndi tsogolo labwino kwambili , limene inu mungauzeko ena . Koma kodi nkhani za m’Mauthenga Abwino zinacitika kapena sizinacitike ? Mosiyana ndi nthano zabodza , nkhani za m’Mauthenga Abwino zinafufuzidwa mosamala ndi kulembedwa molondola . Mwacitsanzo , zimachula maina a malo enieni , ndipo ambili mwa malo amenewa anthu angapite kukawaona masiku ano . Cina , zimafotokoza anthu enieni , ndipo akatswili olemba mbili yakale amacitila umboni kuti anthuwo analikodi . — Luka 3 : 1 , 2 , 23 . Olemba ena a m’nthawi ya atumwi komanso a m’zaka za m’ma 100 C.E . , anachulapo za Yesu . Kuonjezela apo , zocitika zimene analemba ndi zofanana m’njila yakuti zinalembedwa molondola ndiponso mosapita m’mbali . Iwo analembanso ngakhale zolakwa za ophunzila ena a Yesu . ( Mateyu 26 : 56 ; Luka 22 : 24 - 26 ; Yohane 18 : 10 , 11 ) Maumboni onsewa akuonetsa kuti olemba Mauthenga Abwino anali oona mtima , ndipo analemba zinthu zokhudza Yesu molondola kwambili . Ngakhale kuti ambili amakhulupilila kuti Yesu anabweladi padziko lapansi kenako anaphedwa , ena amakaikila zakuti iye anaukitsidwa . Atumwi ake naonso sanakhulupilile pamene anamva lipoti lakuti iye waukitsidwa . ( Luka 24 : 11 ) Komabe , pamene io ndi ophunzila ena anamuona Yesu woukitsidwayo panthawi zosiyanasiyana , m’pamene anakhulupilila . Ndipo panthawi ina , Yesu anaonekela kwa anthu oposa 500 . — 1 Akorinto 15 : 6 . Molimba mtima , ophunzila a Yesu analengeza za kuukitsidwa kwake kwa anthu ambili kuphatikizapo amene anamupha , ngakhale kuti kucita zimenezo kunaika moyo wao pangozi . ( Machitidwe 4 : 1 - 3 , 10 , 19 , 20 ; 5 : 27 - 32 ) Kodi ophunzila ambili akanalimba mtima conco zikanakhala kuti sanali otsimikiza mtima kuti Yesu anaukitsidwadi ? Kukamba zoona , mfundo yakuti Yesu anaukitsidwadi ndi imene inacititsa kuti Cikristu cifalikile kwambili m’nthawi zakale ngakhale masiku ano . Nkhani zokhudza imfa ya Yesu ndi kuukitsidwa kwake zolembedwa m’Mauthenga Abwino , ndi umboni wakuti nkhani zonse zofotokoza mbili yakale n’zoona . Kuŵelenga nkhani zimenezi bwinobwino , kudzakuthandizani kukhulupilila kuti zinacitikadi . Ndipo cikhulupililo canu cidzalimbanso mukamvetsetsa cifukwa cake zinthuzo zinacitika . Ena mwa anthu amenewa ndi Tacitus , amene anabadwa mu 55 C.E . Iye analemba kuti Akristu anatengela dzinali kwa “ Kristu ” amene Pontiyo Pilato , mmodzi mwa olamulila athu , anamulamula kuti azunzidwe ndi kuphedwa mu ulamulilo wa mfumu Tiberiyo . ” Enanso amene analemba za Yesu anali Suetonius , ( wa m’nthawi ya atumwi ) , wolemba mbili yakale waciyuda Josephus ( wa m’nthawi ya atumwi ) , ndi Pliny Wamng’ono amene anali bwanamkubwa wa ku Bituniya ( wa kumayambililo kwa zaka za m’ma 100 C.E ) . ( 1 Petulo 1 : 24 , 25 ) Ndiyeno , anthu ambili amene anali kutsutsa Yesu sakanalemba zinthu zimene zikanapangitsa anthu kukhulupilila Yesu . Pankhani ya kuukitsidwa kwa Yesu , Petulo , amene anali mmodzi wa atumwi ake , anafotokoza kuti : “ Ameneyu Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu ndi kumulola kuonekela , osati kwa anthu onse , koma kwa mboni zoikidwilatu ndi Mulungu , zomwe ndi ife amene tinadya ndi kumwa naye limodzi atauka kwa akufa . ” Uthenga Wabwino wa Mateyu umatiuza kuti pamene atsogoleli acipembedzo amene anali adani a Yesu anamva kuti iye waukitsidwa , io anapeza njila yothetsela kufalitsidwa kwa nkhani yakuti Yesu wauka . — Mateyu 28 : 11 - 15 . Kodi izi zitanthauza kuti Yesu anali kufuna kuti nkhani yakuti iye anaukitsidwa isafalikile ? Iyai . Petulo anapitiliza kufotokoza kuti : “ Anatilamula kuti tilalikile kwa anthu ndi kupeleka umboni wokwanila wakuti iyeyu ndi amene Mulungu anamuika kukhala woweluza anthu amoyo ndi akufa . ” Akristu oona akhala akucita zimenezi kuyambila kale . — Machitidwe 10 : 42 . ‘ Ucimo unaloŵa m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi [ Adamu ] , ndi imfa kudzela mwa ucimo . ’ — Aroma 5 : 12 Mungayankhe bwanji mutafunsidwa kuti , “ Kodi mungakonde kukhala ndi moyo kwamuyaya ? ” Anthu ambili angakambe kuti inde , koma amaona kuti zimenezo sizingacitike . Iwo amakamba kuti anthufe tinalengedwa kuti tizifa . Koma bwanji ngati akufunsani kuti , “ Kodi mwakonzekela kufa ? ” Anthu ambili angakambe kuti iyai . Baibulo limakamba kuti Mulungu analenga anthu ndi cifuno cokhala ndi moyo kwamuyaya . Limakamba kuti “ [ iye ] anapatsa anthu mtima wofuna kukhala ndi moyo mpaka kalekale . ” — Mlaliki 3 : 11 . Koma zoona zake n’zakuti anthu sakhala ndi moyo kwamuyaya . Kodi Mulungu anacitapo ciliconse kuti akonze zinthu ? Mayankho a m’Baibulo ndi okhazika mtima pansi , ndipo amaonetsa cifukwa cake Yesu anavutika ndi kufa . Macaputala atatu oyambilila a buku la Genesis m’Baibulo , amatiuza kuti Mulungu anapatsa anthu oyambilila Adamu ndi Hava mwai wakuti akhale ndi moyo kwamuyaya . Iye anawauza zimene anayenela kucita kuti akhale kwamuyaya . Macaputala amenewa afotokoza kuti iwo sanamvele Mulungu ndipo anataya mwai umenewo . Anthu ambili amaona kuti nkhani imeneyo ndi nthano cabe . Koma mofanana ndi mabuku a Uthenga Wabwino , zimene zinalembedwa m’buku la Genesis ponena za mbili yakale n’zoona . Kodi n’ciani cinacitika pambuyo pakuti Adamu sanamvele Mulungu ? Baibulo limayankha kuti : “ Monga mmene ucimo unaloŵela m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi [ Adamu ] ndi imfa kudzela mwa ucimo , imfayo n’kufalikila kwa anthu onse cifukwa onse anacimwa . ” Zimenezi zinacititsa kuti ataye mwai wokhala ndi moyo kwamuyaya . Patapita nthawi , iye anafa . Popeza ndife mbadwa zake , tinatengela ucimo kwa iye . Kodi Mulungu anacitapo ciliconse kuti akonze zinthu ? Mulungu anapanga makonzedwe akuti abwezeletse mwai wokhala ndi moyo kwamuyaya umene Adamu anataya kwa mbadwa zake . M’Baibulo , pa Aroma 6 : 23 pamati : “ Malipilo a ucimo ndi imfa . ” Zimenezi zitanthauza kuti ucimo umabweletsa imfa . Mofananamo , ifenso ndife ocimwa ndipo timalandila malipilo a ucimo amene ndi imfa . Conco , timabadwa ndi ucimo ngakhale kuti si mwakufuna kwathu . Mwacikondi , Mulungu anatuma Mwana wake , Yesu , kudzatilipilila “ malipilo a ucimo . ” Imfa ya Yesu inatsegula njila yodzakhala ndi moyo wacimwemwe komanso wamuyaya Popeza munthu mmodzi wangwilo , Adamu , anabweletsa ucimo ndi imfa mwa kusamvela Mulungu , panafunikanso munthu wangwilo womvela mpaka imfa n’colinga cakuti atimasule ku ucimo . Baibulo limafotokoza kuti : “ Monga mwa kusamvela kwa munthu mmodziyo , ambili anakhala ocimwa , momwemonso kudzela mwa kumvela kwa munthu mmodziyu , ambili adzakhala olungama . ” Iye anacoka kumwamba , ndi kukhala munthu wangwilo * , kenako anatifela . Pa cifukwa cimeneci , zinakhala zotheka kwa ife kuyesedwa olungama ndi kuima pamaso pa Mulungu , komanso kukhala ndi mwai wodzakhala ndi moyo kwamuyaya . Nanga n’cifukwa ciani Yesu anafunika kufa ? Kodi Mulungu Wamphamvuyonse sakanangopeleka lamulo lakuti mbadwa za Adamu zikhale kwamuyaya ? Ngati kuti Mulungu sanaonetse cilungamo pankhaniyi , anthu akanaganiza kuti Mulungu sangacite zinthu mwacilungamo pankhani zinanso . Mwacitsanzo , kodi cikanakhala cilungamo ngati akanasankha mbadwa zina za Adamu kuti zikhale kwamuyaya ? Kodi anthu akanam’khulupilila kuti amasunga malonjezo ake ? Cilungamo cimene Mulungu anatsatila kuti atipulumutse , cimatitsimikizila kuti iye amacita zinthu mwacilungamo nthawi zonse . Cifukwa ca nsembe ya Yesu , Mulungu anatsegula mwai wodzakhala ndi moyo wosatha m’Paladaiso padziko lapansi . Pa Yohane 3 : 16 Yesu anati : “ Mulungu anakonda kwambili dziko mwakuti anapeleka Mwana wake wobadwa yekha , kuti aliyense wokhulupilila iye asaonongeke , koma akhale ndi moyo wosatha . ” Imfa ya Yesu simangoonetsa cilungamo ca Mulungu , koma imaonetsanso cikondi cacikulu cimene Mulungu ali naco pa anthu . Nanga n’cifukwa ciani Yesu anavutika ndi kufa imfa yoŵaŵa monga mmene zinalembedwela m’Mauthenga Abwino ? Mwa kukhalabe wokhulupilika pokumana ndi mavuto aakulu , Yesu anaonetselatu kuti zimene Mdyelekezi anakamba zakuti anthu sangakhale okhulupilika kwa Mulungu akakumana ndi , n’zabodza . ( Yobu 2 : 4 , 5 ) Zimene Satana anakamba zinaoneka monga n’zoona cifukwa poyamba anacititsa Adamu munthu wangwilo kucimwa . Koma Yesu , amene anali wangwilo monga Adamu , anakhalabe womvela ngakhale kuti anavutika kwambili . ( 1 Akorinto 15 : 45 ) Motelo , iye anaonetsa kuti zinali zotheka kwa Adamu kusankha kumvela Mulungu . Mwa kupilila pamene anali kuvutitsidwa , Yesu anatisiila citsanzo cakuti titsatile . ( 1 Petulo 2 : 21 ) Mulungu anadalitsa Mwana wake cifukwa ca kumvela mwa kumuukitsila kumoyo wosafa , kumwamba . Yesu anafotokoza zimene tifunika kucita pamene anati : “ Pakuti moyo wosatha adzaupeza akamaphunzila ndi kudziŵa za inu , Mulungu yekhayo amene ali woona , ndi za Yesu Kristu , amene inu munamutuma . ” — Yohane 17 : 3 . Amene amafalitsa magazini ino akukupemphani kuti muphunzile zambili za Yehova , Mulungu woona , ndi za Mwana wake Yesu Kristu . A Mboni za Yehova amene ali m’dela lanu ndi okonzeka kukuthandizani . Mudzaphunzilanso zambili mukapita pa webusaiti yathu ya www.jw.org . Onani nkhani yakuti “ The Historical Character of Genesis , ” m’buku lacingelezi la Insight on the Scriptures , pa tsamba 922 , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova . Mulungu anasamutsa moyo wa mwana wake ndi kuuika m’mimba mwa Mariya , ndipo iye anakhala ndi pakati . Mzimu woyela wa Mulungu unateteza Yesu kuti asatengele kupanda ungwilo kwa Mariya . — Luka 1 : 31 , 35 . Usiku wakuti aphedwa maŵa , Yesu anasonkhana pamodzi ndi atumwi ake okhulupilika , kenako anayambitsa Cikumbutso ca imfa yake . Iye anawauza kuti : “ Muzicita zimenezi pondikumbukila . ” ( Luka 22 : 19 ) Pomvela lamulo limeneli , Mboni za Yehova padziko lonse zimasonkhana kamodzi pa caka kuti zikumbukile imfa ya Yesu . Caka cino , Cikumbutso ca imfa ya Yesu cidzakhalako pa Citatu , March 23 , dzuŵa litaloŵa . Simudzalipila ndalama iliyonse , ndipo sipadzayendetsedwa mbale ya ndalama . Funsani a Mboni za Yehova a m’dela lanu kuti akuuzeni nthawi ndi malo kumene kudzakhalila cocitikaco . Kapena pitani pa webusaiti yathu ya www.jw.org . KODI MUMAONA KUTI Mdyelekezi ndi . . . Maganizo oipa a munthu ? Mdyelekezi anakamba ndi Yesu , ndi ‘ kumuyesa . ’ Poyamba , Satana anali mngelo wabwino , koma iye “ sanakhazikike m’coonadi . ” ( Yohane 8 : 44 ) Iye anakhala wabodza ndipo anapandukila Mulungu . Angelo enanso anapanduka ndi kugwilizana ndi Satana . — Chivumbulutso 12 : 9 . Mdyelekezi amacititsa anthu kuganiza kuti iye kulibe . ​ — 2 Akorinto 4 : 4 . ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI zoti Mdyelekezi amalamulila anthu ndi nthano cabe , koma ena amaopa kugwidwa ndi ziŵanda . “ Dziko lonse lili m’manja mwa woipayo . ” ( 1 Yohane 5 : 19 ) Mdyelekezi akusonkhezela anthu ambili kucita zoipa , koma sakulamulila anthu onse . Mdyelekezi amagwilitsila nchito cinyengo kuti asokoneze anthu ambili . ​ — 2 Akorinto 11 : 14 . Nthawi zina ziŵanda zimavutitsa anthu . ​ — Mateyu 12 : 22 . Mothandizidwa ndi Yehova , mungathe ‘ kutsutsa Mdyelekezi . ’ ​ — Yakobo 4 : 7 . Kuti mudziŵe zambili , onani nkhani 10 m’buku ili , Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni - ceni , lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova 1 : 16 . Kodi njila yaikulu koposa imene Yehova waonetsela kukoma mtima kwakukulu kwa anthu ni iti ? Tingaonetse bwanji kuti tsopano tikulamulidwa ndi kukoma mtima kwakukulu osati ucimo ? Ni madalitso a bwanji amene timapeza cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova ? 1 , 2 . ( a ) Fotokozani fanizo la Yesu la mwini munda wa mpesa . ( b ) Kodi fanizoli liwonenetsa bwanji khalidwe la kuwolowa manja ndi kukoma mtima kwakukulu ? Kodi n’kosaloleka kupatsa anchito anga onse malipilo amene nifuna ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 6 : 1 . ) N’cifukwa ciani Yehova anaonetsa anthu onse kukoma mtima kwakukulu ? Nanga anacita bwanji zimenezo ? Kodi Malemba atanthauza ciani pamene akamba kuti Yehova wasonyeza kukoma mtima kwake kwakukulu “ m’njila zosiyanasiyana ? ” Mtumwi Petulo analemba kuti : “ Molingana ndi mphatso imene aliyense walandila , igwilitseni nchito potumikilana monga oyang’anila abwino amene alandila kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu , kumene wakusonyeza m’njila zosiyanasiyana . ” ( 1 Pet . Mtumwi Yohane analemba kuti : “ Tonsefe tinalandila zinthu kucokela pa zoculuka zimene ali nazo . Tinalandila kukoma mtima kwakukulu kosefukila . ” ( Yoh . Timapindula bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova ? Nanga tingaonetse bwanji kuti timayamikila ? ( Ŵelengani 1 Yohane 1 : 8 , 9 . ) Ni mwayi wabwanji umene tili nawo cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? Mmene Mulungu waonetsela kukoma mtima kwake kwakukulu : Mwayi womvela uthenga wabwino ( Onani ndime 11 ) Kodi odzozedwa amathandiza bwanji a “ nkhosa zina ” kukhala olungama ? Mphatso ya pemphelo ( Onani ndime 12 ) Kodi pemphelo ligwilizana bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? Tingapindule bwanji ndi kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu “ pa nthawi imene tikufunika thandizo ” ? Kodi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova kumatithandiza bwanji ? Ni ciyembekezo ca bwanji cimene tili naco cifukwa ca kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? ( Ŵelengani Salimo 49 : 7 , 8 . ) Kodi Akhiristu ena akale ananyoza bwanji kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? Ni udindo wa bwanji umene tili nawo cifukwa ca kukoma mtima kwa Yehova ? Kodi m’nkhani yotsatila tidzakambilana za udindo uti ? [ 1 ] ( ndime 2 ) Onani mau akuti “ Kukoma mtima kwakukulu ” pa cigawo cakuti “ Matanthauzo a Mau Ena ” mu Baibulo la Dziko Latsopano . 20 : 24 . Kodi kukoma mtima kwakukulu kwa Yehova kuyenela kutilimbikitsa kucita ciani ? Kodi “ uthenga wabwino wa Ufumu ” umaonetsa bwanji kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? Kodi Yehova adzaonetsa bwanji kukoma mtima kwake kwakukulu m’dziko latsopano ? Kodi mtumwi Paulo anaonetsa bwanji kuti anali kuyamikila kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? MOONA mtima , mtumwi Paulo anakamba kuti : “ Kukoma mtima kwake kwakukulu kumene [ Mulungu ] anandisonyeza sikunapite pacabe . ” ( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 9 , 10 . ) ( Ŵelengani Aefeso 3 : 5 - 8 . ) N’cifukwa ciani tikamba kuti “ uthenga wabwino wa Ufumu ” n’cimodzi - modzi ndi uthenga wabwino wa “ kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ” ? N’cifukwa ciani tingakambe kuti pamene tifotokozela anthu za dipo , ndiye kuti tilalikila uthenga wabwino wa kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu ? N’cifukwa ciani anthu ocimwa ayenela kugwilizana ndi Mulungu ? Yohane anati : “ Iye wokhulupilila mwa Mwanayo ali nawo moyo wosatha . Wosamvela Mwanayo sadzauona moyowu , koma mkwiyo wa Mulungu ukhalabe pa iye . ” ( Yoh . 9 , 10 . ( a ) Ni udindo wa bwanji umene Khiristu anapatsa abale ake odzozedwa ? Cotelo ndife akazembe m’malo mwa Khristu , ngati kuti Mulungu akucondelela anthu kudzela mwa ife . N’cifukwa ciani anthu amakondwela akadziŵa kuti angapemphele kwa Yehova ? Anthu ambili amapemphela kuti amveleko cabe bwino , koma sakhulupilila kuti Mulungu amayankha mapemphelo awo . Iwo afunika kudziŵa kuti Yehova ni “ Wakumva pemphelo . ” Wamasalimo Davide analemba kuti : “ Inu Wakumva pemphelo , anthu a mitundu yonse adzabwela kwa inu . Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Ngati mutapempha ciliconse m’dzina langa , ine ndidzacicita . ” ( Yoh . 13 , 14 . ( a ) Ni udindo wapadela uti umene odzozedwa adzakhala nawo kutsogolo ? ( b ) Ni zinthu zabwino ziti zimene odzozedwa adzacitila anthu ? Kodi Yehova adzaonetsa bwanji kukoma mtima kwake kwakukulu kwa “ nkhosa zina ” m’dziko latsopano ? Anthu mamiliyoni ambili amene anamwalila akalibe kudziŵa Mulungu nawonso adzaukitsidwa . Yohane analemba kuti : “ Ndinaona akufa , olemekezeka ndi onyozeka , ataimilila pamaso pa mpando wacifumuwo , ndipo mipukutu inafunyululidwa . Koma mpukutu wina unafunyululidwa , ndiwo mpukutu wa moyo . Ndipo akufa anaweluzidwa malinga ndi zolembedwa m’mipukutuyo , mogwilizana ndi nchito zawo . Nyanja inapeleka akufa amene anali mmenemo . Nayonso imfa ndi Manda zinapeleka akufa amene anali mmenemo . Aliyense wa iwo anaweluzidwa malinga ndi nchito zake . ” Kodi tiyenela kukumbukila ciani pamene tilalikila uthenga wabwino ? Baibulo imati : “ Cilengedweco cidzamasulidwa ku ukapolo wa kuvunda n’kukhala ndi ufulu waulemelelo wa ana a Mulungu . ” Anakambanso kuti : “ Lemba , pakuti mawu awa ndi odalilika ndi oona . ” Kukamba zoona , pamene tilalikila uthenga wabwino umenewu kwa ena , timalemekeza Yehova cifukwa ca kukoma mtima kwake kwakukulu . “ Pitilizani kufunafuna ufumu [ wa Mulungu ] , ndipo zinthu zimenezi zidzawonjezedwa kwa inu . ” — LUKA 12 : 31 . Kodi zimene timafunikila mu umoyo zimasiyana bwanji ndi zimene timalakalaka ? N’cifukwa ciani sitiyenela kufuna zinthu zambili zakuthupi ? N’cifukwa ciani mumakhulupilila kuti Yehova adzakupatsani zinthu zofunikila mu umoyo ? Kodi Satana amaseŵenzetsa bwanji “ cilakolako ca maso ” ? Musaiŵale kuti mtumwi Yohane anapeleka cenjezo lakuti : “ Dziko likupita limodzi ndi cilakolako cake . ” Kodi anthu amene amacita khama kuti akhale ndi zinthu zambili amakumana ndi mavuto ya bwanji ? Nanga n’cifukwa ciani ? 8 , 9 . ( a ) N’cifukwa ciani sitiyenela kudela nkhawa kwambili zinthu zofunikila mu umoyo ? ( b ) N’ciani cimene Yesu anali kudziŵa ponena za anthu ndi zinthu zimene amafunikila ? Pophunzitsa ophunzila ake kupemphela , kodi Yesu anakamba kuti n’ciani ciyenela kukhala cofunika kwambili ? Tiphunzila ciani tikaganizila mmene Yehova amasamalila mbalame ? ‘ Tizionetsetsa mbalame zam’mlengalenga . ’ ( Sal . 147 : 9 ) Sikuti amacita kutenga zakudya ndi kuziika mkamwa mwa mbalame iyayi . N’ciani cionetsa kuti ndife ofunika kwambili kuposa mbalame ? ( Yelekezelani ndi Luka 12 : 6 , 7 . ) 15 , 16 . ( a ) Tiphunzilapo ciani tikaganizila mmene Yehova amasamalila maluwa ? ( Onani cithunzi kuciyambi kwa nkhani ino . ) ( b ) Ni funso liti limene tingadzifunse ? Cifukwa ? N’ciani cimene Yehova amadziŵa cokhudza aliyense wa ife ? Nanga adzaticitila ciani ? N’cifukwa ciani sitiyenela kudela nkhawa za kutsogolo ? Mungacite ciani kuti mukhale na umoyo wosafuna zambili kuti muike patsogolo zinthu za Ufumu ? ( a ) Ni zolinga za bwanji zimene mungasankhe potumikila Yehova ? ( b ) Mungacite ciani kuti mucepetseko zocita mu umoyo wanu ? N’ciani cingatithandize kuti Yehova akhale bwenzi lathu ? Fotokozani citsanzo cimene cionetsa kufunika kodziŵa nthawi imene tikukhalamo ndi zimene zikucitika . N’cifukwa ciani Yesu anauza ophunzila ake kuti ‘ akhalebe maso ’ ? ( Mat . 24 : 3 ; ŵelengani Maliko 13 : 32 - 37 . ) ( a ) N’cifukwa ciani tikhulupilila kuti Yesu adziŵa tsiku la Aramagedo ? ( b ) Ngakhale kuti sitidziŵa tsiku limene cisautso cacikulu cidzayamba , kodi tiyenela kutsimikiza za ciani ? Pamene Yesu anali pa dziko lapansi , anati : “ Kunena za tsikulo ndi ola lake , palibe amene akudziŵa , ngakhale angelo akumwamba kapenanso Mwana , koma Atate yekha . ” ( Mat . ( Ŵelengani Habakuku 2 : 1 - 3 . ) Fotokozani citsanzo coonetsa kuti maulosi a Yehova amakwanilitsika panthawi yake . Maulosi a Yehova amakwanilitsika panthawi yake . ( Agal . 3 : 17 , 18 ) Patapita nthawi , Yehova anauza Abulahamu kuti : “ Udziŵe ndithu kuti mbewu yako idzakhala mlendo m’dziko la eni , ndipo idzatumikila eni dzikolo . Iwo adzasautsa mbewu yako kwa zaka 400 . ” ( Gen . Patapita zaka zambili anakumbutsa anthu zimene zinacitika . 7 , 8 . ( a ) Kodi kale alonda anali ndi nchito yanji ? Nanga tiphunzilapo ciani ? ( b ) Fotokozani citsanzo ca zimene zingacitike ngati mlonda wagona pa nchito . Kodi anthu ambili masiku ano sadziŵa ciani ? 10 , 11 . ( a ) N’ciani cimene tiyenela kusamala naco ? Cifukwa ? ( b ) N’ciani cimakucititsani kutsimikiza kuti Mdyelekezi wacititsa anthu kunyalanyaza ulosi wa m’Baibulo ? N’cifukwa ciani sitiyenela kulola kuti Mdyelekezi atinamize ? ( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 1 - 6 . ) Yesu anaticenjezanso kuti : “ Khalani okonzeka , cifukwa pa ola limene simukuliganizila , Mwana wa munthu adzafika . ” Kodi mzimu wa dziko umawakhudza bwanji anthu ? Ni cenjezo ya bwanji imene ili pa Luka 21 : 34 , 35 ? ( Ŵelengani Luka 21 : 34 , 35 . ) N’ciani cinacitikila Petulo , Yakobo , ndi Yohane ? Nanga zimenezo zingaticitikile bwanji ? Mogwilizana ndi lemba la Luka 21 : 36 , kodi Yesu anatilangiza kucitanji ? Tingacite ciani kuti tikhale okonzekela zimene zidzacitika posacedwapa ? [ 1 ] ( ndime 14 ) Onani Nkhani 21 m’buku lakuti Ufumu wa Mulungu Ukulamulila . Ndikulimbitsa . Ndithu ndikuthandiza . Pa msonkhano wadela , m’bale wina ananifunsa ngati ningakonde kulalikila . Titapita m’gawo , ananipatsa tumabuku tokamba za Ufumu wa Mulungu . Pamene n’nayendako , mlongo wina anayamba kuphunzitsa ife ana nkhani za m’Baibulo poseŵezetsa buku lakuti Zeze wa Mulungu . Kucokela nili mwana , napeza cimwemwe cifukwa copatsa mwa kuuzako ena ciyembekezo copezeka m’Mau a Mulungu . N’nauza m’baleyo kuti , “ Mbuzi iyo . ” M’baleyo anaimitsa njinga yake ndi kunipempha kuti tikhale pansi pamalo ena ake . Iye ananifunsa kuti : “ Ndani anakupatsa mphamvu zoweluza anthu kuti ni mbuzi ? Udziŵa , nchito yathu n’kuuza anthu uthenga wabwino koma kuweluza n’kwa Yehova . ” M’bale wina wacikulile ananiphunzitsa kuti nthawi zina kupeza cimwemwe kumafuna kupilila . N’zoonekelatu kuti apa Mulungu anadalitsa m’baleyo cifukwa cokhala woleza mtima . Pambuyo pa nkhondo , n’napita kukacita upainiya kum’mwela kwa dziko la Ireland kwa zaka ziŵili . Iwo anacititsanso kuti ticotsedwe m’nyumba zimene tinali kukhala . Popeza n’nali n’kalibe kukwelapo boti n’nakondwela kwambili . Kwa zaka 5 tinalalikila kwambili pa zisumbu za kutali kumene kunalibe Mboni . Anzanga amene n’nali kucita nawo umishonale titakwela boti ( kucokela kumanzele kupita kulamanja ) Ron Parkin , Dick Ryde , Gust Maki , ndi Stanley Carter Nthawi zambili anali kutipatsa nsomba , makotapela , na nshawa . Zinali zokondweletsa kuona kuti anthuwo abwela kudzamvela nkhani . Zinali zosangalatsa kwambili kuona mmene ena anakwanilitsila bwino udindo wawo . Titafika kumeneko n’nakumana ndi Maxine Boyd , mlongo wokongola amene anali m’mishonale . Motelo , n’naziuza kuti : ‘ Ronald , ngati umufunadi mtsikanayu , ufunika kucitapo kanthu mwamsanga . ’ Pambuyo pa milungu itatu ninam’funa , ndipo patapita milungu 6 tinamanga banja . Ndiyeno anatituma kukacita umishonale ku Puerto Rico . Conco , sin’nabwelele nawo anzangawo ndi boti yatsopano . Mwacitsanzo , m’mudzi wina wa Potela Pastillo munali mabanja aŵili a Mboni amene anali ndi ana ambili ndipo n’nali kukonda kuwalizila citolilo . N’nafunsa kamtsikana kena , dzina lake Hilda , ngati kangakonde kukalalikila nafe . Tinakagulila nsapato ndipo kanapita nafe mu ulaliki . Mlongoyo anali pafupi kupita ku Ecuador kukatumikila monga m’mishonale . Anatifunsa kuti : “ Kodi mwanikumbukila ? Ndine uja mtsikana wa ku mudzi wa Pastillo amene munagulila nsapato . ” Johnson ndi mkazi wake ndiwo anali Mboni zoyamba m’dziko la Dominican Republic . M’bale Nathan Knorr , amene anali kutsogolela gulu la Yehova panthawiyo , anabwela ku Puerto Rico . Ngakhale conco , anakhumudwa ndi kunipatsa uphungu wamphamvu . Anakamba kuti sinicita zinthu mwadongosolo . Pamene ine ndi Amayi tinali kuphunzila coonadi , atate anali kukana . Mu 2011 , wokondedwa wanga Maxine anamwalila . Nikuyembekezela mwacidwi kudzamuonanso akadzaukitsidwa . Zaka 60 zimene n’nakhala pa cisumbu , n’nayamba kudziona kuti ndine wa ku Puerto Rico monga kacule ka kumeneko kamene kamakhala m’mitengo kochedwa coqui . Ena amene amanifikila amafuna kuti niwathandize pamavuto aumwini kapena a m’banja . Koma cofunika ni kuganizila cifukwa cake zimene ucita n’zofunika kwambili . 24 : 45 ) Tili ndi mwayi wotamanda Yehova kulikonse kumene tingakhale . Mbili ya m’bale Leonard Smith ili mu Nsanja ya Olonda ya April 15 , 2012 . N’cifukwa ciani tinganene kuti cikwati ni mphatso yocokela kwa Mulungu ? Kodi vikwati vinali bwanji kucokela pa Adamu kudzafika m’nthawi ya Yesu ? N’ciani cingathandize Mkhiristu kusankha kukwatila kapena kusakwatila ? 1 , 2 . ( a ) Kodi cikwati cinayamba kwanji ? ( b ) N’ciani cimene mwamuna ndi mkazi oyamba anazindikila ponena za cikwati ? ( Ŵelengani Genesis 2 : 20 - 24 . ) 2 : 18 ) Cifuno cina cacikulu ca cikwati cinali kubala ana kuti padziko lapansi pakhale anthu . Malinga ndi mmene Adamu na Hava anayankhila kwa Yehova , kodi tiphunzilapo ciani ? Kodi mungalifotokoze bwanji lemba la Genesis 3 : 15 ? ( a ) Kodi nkhani ya cikwati yakhala ikuyenda bwanji kuyambila pa cipanduko ca Adamu na Hava ? ( b ) Nanga Baibulo imawalangizanji amuna ndi akazi ali pabanja ? Kodi vikwati vinali bwanji kucokela pa Adamu kudzafika pa Cigumula ca Nowa ? Kodi Yehova anacita nawo bwanji anthu oipa m’masiku a Nowa ? Ndipo titengapo punzilo lanji pa zimene zinacitikazo ? ( a ) Ni makhalidwe oipa ati amene anafala kwa anthu ambili ? ( b ) Nanga Abulahamu na Sara anapeleka bwanji citsanzo cabwino m’cikwati cawo ? ( Ŵelengani 1 Petulo 3 : 3 - 6 . ) Kodi Cilamulo ca Mose cinawateteza bwanji Aisiraeli ? ( Ŵelengani Deuteronomo 7 : 3 , 4 . ) 12 , 13 . ( a ) M’masiku a Malaki , kodi azimuna ena anali kuwacitila motani akazi awo ? ( b ) Ngati masiku ano munthu wobatizika athaŵitsana ndi mkazi kapena mwamuna wa mwiniwake , kodi pamakhala zotsatilapo zanji ? ( a ) Kodi lamulo lokhudza cikwati mu mpingo wacikhiristu n’lakuti ciani ? Ndiyeno anawonjezela kuti : “ Koma ngati sangathe kudziletsa , akwatile , pakuti ndi bwino kukwatila kusiyana ndi kuvutika ndi chilakolako . ” 18 , 19 . ( a ) Kodi cikwati cacikhiristu ciyenela kuyamba bwanji ? ( b ) Nanga tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Kodi Mulungu anapeleka maudindo anji kwa mwamuna ndi m’kazi m’banja ? N’cifukwa ninji cikondi komanso tumacitidwe tokopana n’tofunika m’cikwati ? Pakaoneka mavuto m’cikwati , kodi Baibulo ingathandize bwanji ? Ngakale kuti cikwati cimayamba ndi cisangalalo , kodi omanga banja ayenela kuyembekezela ciani ? Baibulo imagogomeza kufunika kwa cikondi . Kodi cikondi m’cikwati ciyenela kukhala camphamvu bwanji ? Paulo analemba kuti : “ Amuna inu , pitilizani kukonda akazi anu monga mmene Khiristu anakondela mpingo n’kudzipeleka yekha cifukwa ca mpingowo . ” ( Aef . Ŵelengani Yohane 13 : 34 , 35 ; 15 : 12 , 13 . ) 4 , 5 . ( a ) Monga mutu , kodi mwamuna afunika kucita mbali yanji m’banja ? ( b ) Nanga mkazi ayenela kukaona bwanji kakonzedwe ka umutu ? ( c ) Kodi a m’cikwati ena anapanga masinthidwe otani ? Koma kukwatiwa kunanisintha , cifukwa n’nafunika kuzoloŵela kudalila mwamuna wanga . Cinali cotivuta poyamba , koma tsopano cikondi cathu catiphunzitsa kucita zinthu m’njila ya Yehova . ” Ndiye kukhala aŵili kunangowonjezela vutolo . Koma kupempha citsogozo kwa Yehova , ndi kumvetsela maganizo a mkazi wanga , kwathandiza kucepetsa vutolo . Nimamva kuti mkazi wanga alidi mcilikizi wanga ! ” Kodi cikondi cimakhala bwanji ‘ cogwilizanitsa camphamvu ’ mukabuka mavuto m’banja ? 7 , 8 . ( a ) Kodi Baibulo imalangiza ciani pa nkhani ya kucipinda ? ( b ) N’cifukwa ninji a m’cikwati afunika kumaonetsana cikondano cawo ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 3 - 5 . ) Ifunika izicitika mwacibadwa . N’zoona kuti kaŵili - kaŵili thupi la mwamuna ndilo limatsogola . N’cifukwa ciani tifunika kupewa kaleya koceza mokopana ndi munthu amene sitili naye pabanja ? 10 , 11 . ( a ) Kodi kusudzulana n’kofala bwanji ? ( b ) Nanga Baibulo imati ciani za kupatukana ? ( c ) N’ciani cingathandize wa m’cikwati kusaganiza msanga zopatukana ? N’ciani cingapangitse wa m’cikwati kuganiza zopatukana ? Kodi Baibulo imati ciani kwa Akhiristu amene anzawo a m’cikwati satumikila Yehova ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 12 - 14 . ) Kapena mwamunawe , udziŵa bwanji , mwina ungapulumutse mkazi wako ? ” 15 , 16 . ( a ) Kodi Baibulo imapeleka uphungu wanji kwa akazi acikhiristu amene amuna awo si Mboni ? ( b ) Nanga Mkhiristu angacite bwanji ‘ ngati wosakhulupililayo asankha kucoka ’ ? Mtumwi Petulo analangiza akazi acikhiristu kugonjela amuna awo . Anati “ ngati ali osamvela mawu akopeke , osati ndi mawu , koma ndi khalidwe lanu , poona okha ndi maso awo khalidwe lanu loyela ndi ulemu wanu waukulu . ” Koma bwanji ngati wosakhulupilila asankha kupatukana ? Baibulo imati : “ Ngati wosakhulupililayo wacoka , acoke . M’bale kapena mlongo sakhala womangika zinthu zikatelo , koma Mulungu anakuitanani kuti mukhale mu mtendele . ” ( 1 Akor . N’ciani cimene Akhiristu ali pabanja ayenela kuika patsogolo ? N’cifukwa ciani n’zotheka Akhiristu kukhala ndi cikwati cacimwemwe ndi copambana ? [ 1 ] ( ndime 5 ) Maina asinthidwa . [ 2 ] ( ndime 13 ) Onani kamutu kakuti “ Zimene Baibo Imanena pa Kulekana ndi Kupatukana , ” m’buku yakuti “ Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu , ” masa . 219 - 221 . Kukamba zoona , kulalikila m’maŵa m’mbali mwa mtsinje wa Danube kumakondweletsa kwambili ! Ofalitsa akulalikila mokondwela uthenga wa Ufumu kwa munthu wacidwi m’tawuni ya Vigadó mu Budapest ku Hungary Mungacite ciani kuti mupite patsogolo kuuzimu ? Mungacite ciani kuti musafooke pamene muyesetsa kupita patsogolo ? Mungacite ciani kuti muzilalikila mwaluso ? 1 , 2 . ( a ) Kodi lemba la Yesaya 60 : 22 lakwanilitsika bwanji masiku ano ? ( b ) Kodi m’gulu la Yehova la padziko lapansi mufunika ciani ? “ WAMNG’ONO adzasanduka anthu 1000 , ndipo ocepa adzasanduka mtundu wamphamvu . ” Kupita patsogolo kuuzimu kumatanthauza ciani ? Ni zinthu ziti zimene acicepele angacite kuti acilikize nchito ya Ufumu ? 6 - 8 . ( a ) Kodi wacicepele wina anacita ciani kuti ayambe kuona zinthu zakuuzimu moyenelela ? ( b ) Tingacite ciani kuti ‘ tilawe ndi kuona kuti Yehova ni wabwino ? Nikayang’ana madalitso amene napeza , nimayamikila kwambili Mulungu cakuti nimapitiliza kucita zambili mu utumiki wake . ( Ŵelengani Salimo 34 : 8 - 10 . ) N’cifukwa ciani mufunika ‘ kuyembekezela moleza mtima ’ ? Ni makhalidwe abwino ati amene tifunika kukhala nawo ? Nanga n’cifukwa ciani ni ofunika ? Kodi anthu mumpingo angaonetse bwanji kuti ni okhulupilika ? Mungatsatile bwanji citsanzo ca Yosefe ngati ena akucitilani zoipa ? Mumacita ciani ngati anthu ena akucitilani zinthu zoipa ? 14 , 15 . ( a ) N’cifukwa ciani tifunika ‘ kusamala nthawi zonse ’ ndi kalalikidwe kathu ? ( b ) N’cifukwa ciani nthawi zina mungafunikile kusintha njila yolalikilila ? ( Onani cithunzi kuciyambi kwa nkhani ino , ndi bokosi yakuti “ Kodi Mumayesako Kulalikila M’njila Zina ? ” ) Kodi tingalalikile bwanji mwaluso mu ulaliki wapoyela ? 17 , 18 . ( a ) N’ciani cingakuthandizeni kukhala ndi cidalilo mu ulaliki wapoyela ? ( b ) N’cifukwa ciani mzimu wa Davide wotamanda Yehova ni wothandiza pamene tili mu ulaliki ? Iye anati : “ Pakulambila kwa pabanja , ndinali kufufuza ndi mkazi wanga m’zofalitsa zathu kuti tipeze mfundo zoyankhila anthu pa zimene amakhulupilila kapena amene amatsutsa . Timapemphanso malingalilo kwa Mboni zinzathu . ” ( Ŵelengani 1 Timoteyo 4 : 15 . ) Iwo adzanena za ulemelelo wa ufumu wanu . Ndi kulankhula za mphamvu zanu , Kuti ana a anthu adziŵe za nchito zanu zamphamvu Ndi kukula kwa ulemelelo wa ufumu wanu . ” ( Sal . Kodi anthu ena angapindule bwanji ngati mwapita patsogolo m’gulu la Yehova ? Lomba Venecia amati : “ Ulaliki wa pa foni ni wothandiza . ” Mkazi wanga anamwalila zaka zitatu zapita , ndipo mwana wanga anafa pangozi caka catha . ” Papita zaka ziŵili tsopano , ndipo nalemba kalata ino kuti nikuuzeni kuti ndine mlongo wanu wakuuzimu . ” N’cifukwa ciani tiyenela kuthandiza anthu amene timaphunzila nawo Baibulo kuti azikonda kucita phunzilo laumwini ? Tingathandize bwanji acatsopano kuti azimasuka kukambilana ndi anthu mu ulaliki ? N’cifukwa ciani tiyenela kuyesetsa kuphunzitsa ena kuti ayenelele kuŵeta gulu la nkhosa za Mulungu ? N’cifukwa ciani tifunika kuphunzitsa ena kuti akwanilitse utumiki wawo ? 3 , 4 . ( a ) Kodi Paulo anagwilizanitsa bwanji kuphunzila Baibulo ndi kubala zipatso mu ulaliki ? ( b ) Tiyenela kucita ciani coyamba tikalibe kulimbikitsa ophunzila Baibulo kuti azicita phunzilo laumwini ? Pelekani malingalilo a mmene mungathandizile acatsopano kukhala na cizoloŵezi cocita phunzilo laumwini . Dzifunseni kuti , ‘ Ningaphunzitse bwanji wophunzila Baibulo kuti azicita phunzilo laumwini nthawi zonse ? ’ Mungamulimbikitse kuti aziŵelenga magazini iliyonse yatsopano ya Nsanja ya Mlonda ndi Galamukani ! ( a ) Mungathandize bwanji wophunzila wanu kuti azikonda kuŵelenga Baibulo ? ( b ) Kodi wophunzila Baibulo adzapindula bwanji ngati wayamba kukonda kuŵelenga Baibulo ? Kodi Yesu anaphunzitsa bwanji atumwi ake kulalikila ? 8 , 9 . ( a ) Kodi Yesu anali kukambilana nawo bwanji anthu mu ulaliki ? ( b ) Tingathandize bwanji acatsopano kuti azikambilana ndi anthu mu ulaliki monga mmene Yesu anacitila ? 10 - 12 . ( a ) Kodi Yesu anakulitsa bwanji cidwi ca anthu mu ulaliki ? ( b ) Tingathandize bwanji ofalitsa atsopano kuwonjezela luso lawo ? 13 , 14 . ( a ) Muphunzilapo ciani mukaganizila zitsanzo za m’Baibulo za anthu amene anadzipeleka kuti athandize ena ? ( b ) Mungathandize bwanji ofalitsa atsopano komanso acicepele kuti adzikonda abale ndi alongo ? ( Mat . 20 : 28 ) Dorika “ anali kucita nchito zabwino zambili , ndi kupeleka mphatso zacifundo zoculuka . ” ( Mac . N’cifukwa ciani akulu ayenela kuyesetsa kuthandiza abale kupita patsogolo mumpingo ? 16 , 17 . ( a ) N’ciani cimene Paulo anacita kuti athandize Timoteyo kupita patsogolo ? ( b ) Kodi akulu angaphunzitse bwanji abale kuti ayenelele kukhala akulu mumpingo ? N’cifukwa ciani kuphunzitsa ena n’kofunika kwambili ? N’cifukwa ciani tingakhale otsimikiza mtima kuti khama lathu pophunzitsa ena mu utumiki wa Yehova silizapita pacabe ? Amandipembedza pacabe , cifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati ziphunzitso za Mulungu . ’ Mumanyalanyaza malamulo a Mulungu , ndi kuumilila mwambo wa anthu . ” — Maliko 7 : 6 - 8 . 3 “ Manja Anu Asakhale Olefuka ” Kodi Mulungu amatiphunzitsa bwanji kulimbana ndi adani athu ? Amatiphunzitsanso mwa zofalitsa zophunzilila Baibulo , misonkhano ya mpingo , ya dela , ndi ya cigawo . Tiyenela kucita ciani kuti tisagonje ku coipa ? ( b ) Tidzakambilana za anthu ati ochulidwa m’Baibulo ? N’ciani cinathandiza Yakobo kucilimika ? ( Ŵelengani Genesis 32 : 24 - 28 . ) N’ciani cinathandiza wacicepele ndi mlongo wina kugonjetsa zilakolako zoipa ? Wacicepeleyo anati : “ Pa cifukwa cimeneci , niona kuti n’zotheka kukhala wokhulupilika tsiku lililonse . Niyamikila Yehova kwambili cifukwa coseŵenzetsa gulu lake kutipatsa malangizo othandiza kuti tikhale osiyana ndi dziko loipali . ” Ganizilani citsanzo cina ca mlongo wa ku America . Iye analemba kuti : “ Nikuyamikilani cifukwa copitiliza kutipatsa malangizo amene tifunikila panthawi yake . Nthawi zambili , nimaona kuti nkhani ngati zimenezi amalembela ine . Kwa zaka zambili , nakhala nikulimbana ndi cizoloŵezi coipa cimene Yehova amadana naco . Nthawi zina , nimangofuna kuleka kumenya nkhondoyo . Nidziŵa kuti Yehova ni wacifundo ndipo amakhululukila . Koma cifukwa cakuti nikulimbanabe na cizoloŵezi coipa cimeneci ndipo sinisintha , nimaona kuti siningalandile thandizo lake . Vuto limeneli lakhudza kwambili umoyo wanga . . . Pambuyo poŵelenga nkhani yakuti ‘ Kodi Muli Ndi “ Mtima Wodziŵa ” Yehova ? ’ mu Nsanja ya Olonda ya March 15 , 2013 , n’naonadi kuti Yehova afuna kunithandiza . ” ( a ) Kodi Paulo anamvela bwanji polimbana ndi zilakolako zoipa ? Tiphunzilapo ciani pa malamulo amene Mulungu anapatsa Aisiraeli pa nkhani ya mavalidwe ? N’ciani cimene cingathandize Akhiristu kusankha bwino zovala ? Ni pa nthawi iti maka - maka pamene tifunika kuvala moyenelela ? ( 1 Tim . 2 : 10 ) Komabe , mavalidwe amene angakhale oyenela kwina angakhale osayenela kumalo ena . ( Ŵelengani 1 Akorinto 10 : 32 , 33 . ) N’ciani cingathandize m’bale kudziŵa ngati n’koyenela kuti azisunga ndevu kapena ayi ? Cilamulo ca Mose cinalamula amuna kusunga ndevu . Komanso , sikulepheletsa anthu kumvela uthenga wa Ufumu . Ndipo abale ena a maudindo amasunga ndevu . Kodi mavalidwe athu na mmene timadzikonzela afunika kupangitsa anthu kutiona bwanji ? M’bale wacicepele ku Germany analemba kuti : “ Matica kusukulu kwathu amaona kuti nkhani za m’Baibulo ni nthano cabe . Ndipo amangoona ngati ana a sukulu onse amakhulupilila za cisanduliko . ” Mlongo wacicepele ku France anati : “ Matica kusukulu kwathu amadabwa ngako akamvela kuti pakali ana a sukulu amene amakhulupilila Baibulo . ” na kakuti The Origin of Life — Five Questions Worth Asking , na buku yakuti Is There a Creator Who Cares About You ? Natuŵelenga nthawi zambili . ” Zimaonetsa kuti , ngakhale kuti akatswili opanga zinthu ali na luso lapatali , safikako olo pang’ono kwa amene anapanga zacilengedwe . ” N’cifukwa ciani Mulungu amafuna kuti acicepele aziseŵenzetsa luso la kuganiza ? ( Ŵelengani Aroma 12 : 1 , 2 ; 1 Timoteyo 2 : 4 . ) Ambili a iwo anakhalako pa nthawi zosiyana - siyana ndipo sanali kudziŵana . ” N’naganizilapo kwambili za cakudya ca Pasika cokambidwa m’maulosi . ” ( 2 Sam . 12 : 1 - 14 ; Maliko 14 : 50 ) M’bale wacicepele ku Britain anati : “ Kuona mtima kwa conco n’kosoŵa kwambili . Ni umboni wakuti Baibulo inacokeladi kwa Yehova . ” ( Ŵelengani Salimo 19 : 7 - 11 . ) Wacicepele wina ku Japan analemba kuti : “ Pamene tinayamba kutsatila mfundo za m’Baibulo m’banja mwathu , timakhala acimwemwe kwambili . Timakhala amtendele , ogwilizana , ndi okondana . ” Palinso amene amaleka kukhulupilila Mulungu cifukwa cokhumudwa na zocitika za cipembedzo . Ngakhale kamoyo kakang’ono - ng’ono , moyo wake ni wocolowana modabwitsa kwambili . ” Iye anati : “ Nyumba iliyonse inamangidwa ndi winawake , koma amene anapanga zinthu zonse ndi Mulungu . ” ( Aheb . N’cifukwa ninji mufunika kuwadziŵa bwino ana anu ? Ana athu afunika kucikulitsa pang’ono - pang’ono . ” Amanifunsa kuti : ‘ Baibulo imati ciani ? ’ ‘ Kodi ukhulupilila zimene ikamba ? ’ Amafuna kuti n’ziyankha m’mau anga - anga , osati kungotengela iwo kapena amayi . Popeza tsopano nikukula , nimayankha mofikapo . ” Anayankha mafunso anga onse kucokela m’Baibulo . ” ( Ŵelengani Deuteronomo 6 : 5 - 8 ; Luka 6 : 45 . ) Conco , ngati amati moyo unasandulika kucokela ku twamoyo tung’ono - ng’ono tosacolowana kufika ku zamoyo zikulu - zikulu zocolowana , n’cifukwa ciani twamoyo twamakedzanato tunali tocolowana kale kwambili ? Mfundoyi inanigwila mtima cakuti n’nauzako mwana wanga . ” Ndiyeno anapempha kuti mwana aliyense am’pangile khofi . “ Aliyense anacita khama kwambili , ” anatelo mayiyo . “ N’tawafunsa kuti n’cifukwa ciani anacita mosamala conco , aliyense anati anafuna kuti anipangile khofi yabwino mmene nimaikondela . Ndiyeno n’nawauza kuti ni mmenenso Mulungu naye anacitila khama posakaniza bwino mipweya yopanga cifungadziko ( atmosphere ) kuti tikhalepo na moyo pa dziko lapansi . ” Ndipo n’ciani cimacita congo pouluka , mbalame kapena ndeke ? Conco , uganiza wanzelu kwambili n’ndani , wopanga ndeke olo amene anapanga mbalame ? ” ( Ŵelengani Salimo 1 : 1 - 3 . ) Tate wina anati : “ Osalema kuyesa njila zatsopano pokambilana nkhani za m’Baibulo . ” Anawonjezela kuti : “ Kuyambila ali ana , n’nali kuphunzila nawo kwa mphindi 15 cabe tsiku lililonse , kupatulapo masiku osonkhana . Koma m’kupita kwa nthawi , mafunso anga ambili anayankhidwa pa misonkhano , pa kulambila kwa pabanja kapena pocita phunzilo laumwini . Ndiye cifukwa cake makolo safunika kuleka kuphunzitsa ana awo . ” Ana anu aziona kuti Yehova ni weni - weni kwa inu . Amalimbikitsanso ana awo kumapemphela pawokha . Anati : “ Timauzanso mtsikana wathu wamkulu kuti ‘ Uzidalila Yehova , osada nkhawa kwambili , uziika patsogolo zinthu za Ufumu . ’ Akaona kuti zimenezi zamuthandiza , amadziŵa kuti Yehova ali nafe . Nkhani yoyamba ionetsa mmene cikhulupililo cingakulile na kukhalabe colimba . Lekani nifotokoze cimene cinayambitsa makambilano amenewa . N’NABADWA pa 10 December mu 1936 , ku Wichita ku Kansas mu America . Ndine woyamba pa ana 4 . Ndiyeno panafika msilikali , ndipo dokota ameneyo anakuwa kuuza msilikali kuti , “ Cigwile ici cimunthu ca mantha ! ” Msilikaliyo anazindikila kuti dokotayo anali woledzela , conco anamuuza kuti “ Yenda kunyumba ukhale bwino coyamba ! ” Iwo anali ndi ma babashopu aŵili m’tauni ya Wichita ndipo dokota ameneyo anali kasitoma wawo . Pamene n’nali na zaka 8 , makolo anga anagulitsa nyumba na mashopu awo , n’kupanga nyumba yamawilo ( kalavani ) imene tinali kuyenda nayo . Ndi dalitso la Yehova pamodzi na khama lawo panchito yolalikila , anakhazikitsa mpingo . M’baleyo ananigulitsilanso motoka ija pamtengo wa madola 25 . Tinatumidwa kukacita upainiya wapadela ku tauni ya Walnut Ridge ku Arkansas . Mu 1962 , tinakondwela kwambili titaitanidwa ku sukulu ya Giliyadi ya namba 37 . Tili mu ulaliki na Mary ndi Chris Kanaiya Ndiyeno , mwana wathu woyamba wamkazi Kimberly anabadwa . Patapita miyezi 17 , Stephany anabadwa . Tinalinso kuyenda nawo kumalo okaceza ndi kukagona m’matenti , tikumaceza pootha moto . Tinapanga makonzedwe akuti atumiki ena a nthawi zonse tiziwalandilako kunyumba kwathu . Anawo anadabwa kwambili ndipo anayamba kulila na kukamba kuti afuna tiphunzile . Kukamba zoona , tinakondwela maningi onse aŵili atayamba upainiya pambuyo potsiliza sukulu . Paulendo wina , Kimberly anakumana ndi mnzake wa Paul dzina lake Brian Llewellyn . Conco , anakhaladi mbeta mpaka atakwanitsa zaka 23 . Panthawi imodzi - modzi , Brian na Kimberly anaitanidwa kukatumikila pa Beteli ya ku London . Tsiku lotsatila , pambuyo popita ku Likulu la Maphunzilo la Watchtower ku Patterson , Linda anatuma foni kutiuza kuti Amayi amwalila . Ndiyeno , tinayenda kuphunzitsa ku Zimbabwe ndi ku Zambia . Ndiyeno mu 2006 , Brian na Kimberly anabwela kuno kudzalela ana awo akazi aŵili , Mackenzie na Elizabeth . Koma Paul na Stephany akali ku Malawi kumene Paul akutumikila mu Komiti ya Nthambi . N’cifukwa ciani tingafunike kusintha mmene timaonela alendo ? N’tacoka ku eyapoti , n’namvela kuzizila kumene sin’nakumvelepo cibadwile cakuti ninayamba kulila . ” 6 : 1 ) Pofuna kuthetsa vuto limeneli , atumwi anasankha amuna 7 okatsimikizila kuti aliyense asanyalanyazidwe . 1 : 22 ) Kaya tidziŵa kapena ayi , kaonedwe kathu ka zinthu kamasonkhezeledwa ndi cikhalidwe ca kwathu . ( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 22 . ) 7 : 12 ) Muzicita zinthu moleza mtima ndi anthu amene akuyesetsa kuzoloŵela dziko lacilendo . Poyamba , sitingamvetsetse mmene amaganizila ndi mmene amacitila zinthu . N’citsanzo citi cimene alendo angatengele poonetsa ulemu ndi kuyamikila ? Coyamba , iye analemekeza miyambo ya m’dziko lacilendo , mwa kupempha cilolezo kuti akunkhe tiligu . [ 1 ] ( ndime 1 ) Dzina talisintha . 14 : 6 ) Kodi ndinu mmodzi wa anthu amene akuphunzila cinenelo cina ? ( Ŵelengani Nehemiya 13 : 23 , 24 . ) ( b ) Zimenezi zingatheke bwanji ? 1 : 9 , 10 ) Kumbukilani kuti nthawi zambili pokonzekela ulaliki , misonkhano kapena nkhani , sitingaganizile mmene mfundozo zikhudzila umoyo wathu . Popeza nimaika maganizo pa kudziŵa cinenelo , zimene nimaŵelenga sizinifika pamtima . Ndiye cifukwa cake nimapatula nthawi yophunzila Baibo ndi zofalitsa zina m’cinenelo ca kwathu . ” “ Sanali kukondwela kulalikila m’cinenelo cina , koma kale anali kukondwela kulalikila m’cinenelo cathu Cifulenci , ” anatelo Muriel . “ Titaona kuti zimenezi zikupangitsa mwana wathu kusapita patsogolo kuuzimu , tinaganiza zobwelela kumpingo wakale , ” anafotokoza conco Serge . Muzionetsetsa kuti coonadi cikufika pamtima pa ana anu ( Onani ndime 14 , 15 ) Koma timakonzekela ulaliki ndi kucita maseŵela ena m’Cilingala kuti ana athu aziphunzila cinenelo uku akusangalala . ” Yesetsani kudziŵa cinenelo ca kumaloko ndi kuyankhapo pamisonkhano ( Onani ndime 16 , 17 ) Tinapanganso zoti tizipezeka pa misonkhano ya Cifulenci kamodzi pa mwezi . Tikakhala pa holide timapezelapo mwayi wopita kumisonkhano yacigawo ya m’cinenelo cathu . ” ( Ŵelengani Aroma 15 : 1 , 2 . ) Tingaonetse bwanji kuti timakonda Mau a Mulungu ? Abale ali m’gawo la malonda , ndipo alalikila makanika pamalo okonzela mamotoka . ( Ŵelengani Chivumbulutso 21 : 3 - 6 . ) N’ciani cinathandiza Abulahamu na banja lake kukhalabe na cikhulupililo colimba ? ( Ŵelengani 1 Yohane 5 : 14 , 15 . ) Ni mayeselo ati amene aneneli ena anapilila cifukwa ca cikhulupililo cawo ? Enanso monga Eliya , “ anayenda uku ndi uku m’zipululu , m’mapili , m’mapanga , ndi m’maenje a dziko lapansi . ” Kodi citsanzo ca Nowa citithandiza bwanji kumvetsa zimene kukhala na cikhulupililo kumatanthauza ? Tingaonetse bwanji kuti tili na cikhulupililo ? Kodi Aheberi 11 : 1 imafotokoza cikhulupililo m’njila ziŵili ziti ? Waonatu kuti cikhulupililo cake cinayendela limodzi ndi nchito zake , ndipo mwa nchito zakezo cikhulupililo cakeco cinakhala cangwilo . ” Mwacitsanzo , Yohane anati : “ Iye wokhulupilila mwa Mwanayo ali nawo moyo wosatha . Wosamvela Mwanayo sadzauona moyowu , koma mkwiyo wa Mulungu ukhalabe pa iye . ” ( Yoh . Cofunika kwambili n’citi pakati pa cikondi na cikhulupililo ? ( 1 Pet . 1 : 8 ) Ngakhale Yakobo anafunsa abale ake odzozedwa kuti : “ Mulungu anasankha anthu amene ali osauka m’dzikoli kuti akhale olemela m’cikhulupililo ndi olandila colowa ca ufumu umene anaulonjeza kwa omukonda , sanatelo kodi ? ” ( Yak . Aroma anali kulanga aliyense amene waphwanya malamulo na kubweletsa msokonezo . Aroma anapatsa mphamvu atsogoleli a ndale kuti aziyang’anila zocitika mumzinda wawo . Tumizani ndalamazo pamodzi na kalata yokamba kuti n’zobweleketsa . N’lonjezo liti limene Yehova anapatsa anthu ake ? Nanga n’cifukwa ciani lonjezoli linali locititsa cidwi ? Conco , zioneka kuti anthu a Yehova sanaloŵe mu ukapolo kwa Babulo Wamkulu mu 1918 . ( Ŵelengani 1 Petulo 2 : 9 , 10 . ) ( Ŵelengani Mateyu 13 : 24 , 25 , 37 - 39 . ) Kodi zinali zotheka kuti Akhiristu oona akamasuke ndi kulambila Mulungu mwaufulu ? Kodi odzozedwa anamasulidwa liti kucoka m’Babulo wamkulu ? Ndiyeno , M’bale Rutherford anatipempha kulinganiza misonkhano m’mizinda ingapo ya kumadzulo kwa America ndi kutumiza alankhuli kuti akalimbikitse abale athu . 13 : 15 . Nimalila nthawi zambili , ndipo nimangoleka kukamba nawo . Pamene n’namuuza mmene n’nali kumvelela anamvetsela mwacifundo . Ndiyeno ananikumbutsa zinthu zabwino zimene n’nali kucita . Ananikumbutsanso mau a Yesu akuti , aliyense wa ife ni wofunika kuposa mbalame zambili zampheta . Nthawi zonse nikakumbukila lembali , nimalimbikitsika kwambili . Tingaphunzilenji tikaona mmene Yehova , Yesu na Paulo anali kulimbikitsila ena ? ( Ŵelengani Mlaliki 4 : 9 , 10 . ) Tiphunzilapo ciani tikaona mmene Yesu anacitila ndi atumwi ake ? Iye anayenda - yenda m’madela akumeneko ndi kulimbikitsa ophunzila ndi mawu ambili , kenako anafika ku Girisi . ’ ( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 12 , 13 . ) Tikafunika cilimbikitso , timawatenga n’kumaŵelenga . 7 : 8 - 11 ) Andreas amene alela ana aŵili anati : “ Kulimbikitsa ana kumawathandiza kukula kuuzimu na m’nzelu . Koma cimene cimawathandiza kucita cabwino nthawi zonse ni cilimbikitso cathu cosalekeza . ” ( Ŵelengani Luka 21 : 1 - 4 ; 2 Akorinto 8 : 12 . ) ( Ŵelengani Chivumbulutso 2 : 18 , 19 . ) Dziŵani kuti pamene munali kukamba mokoma mtima pa pulatifomu , ndi pokamba na ine mwacindunji , n’naona kuti ni mphatso yocokela kwa Yehova . ” [ 1 ] ( palagilafu 1 ) Maina ena tawasintha . ( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani ino ? 15 : 6 ) Amuna a m’bungwe lolamulila ndi owathandiza anali kupeleka uphungu na malangizo kwa Akhiristu kupitila m’makalata ouzilidwa . ( Ŵelengani 3 Yohane 9 , 10 . ) ( Ŵelengani Mateyu 5 : 23 , 24 ; 18 : 15 - 17 . ) 3 : 8 ) Izi zinathandiza abale ndi alongo amenewo kucita zambili m’nchito yolalikila . Baibo imatilangiza kuti tizipezeka ku misonkhano nthawi zonse . Kodi mumaiseŵenzetsa webusaiti yathu mu ulaliki ndi pa kulambila kwanu kwa pabanja ? kapena kukambilana naye bulosha yakuti Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano ? Tili na zifukwa ziti zoyamikilila Yehova ? Ha , tili na zifukwa zambili cotani nanga zoyamikilila Yehova ! Idzaonetsanso mmene tingapindulile na ciyembekezo codzalandila mphoto . Panthawiyo n’nali na zaka 8 cabe . Atate anali kuletsa amayi kuniuzako zimene anali kuphunzila . Koma popeza n’nali na cidwi , n’nali kufunsa mafunso . Conco anali kuphunzila nane atate akacokapo . Pa cifukwa cimeneci , inenso n’nafuna kudzipeleka kwa Yehova . Ndiye amayi ananiuza kuti nikakambe na mtumiki woyendela ( amene lomba timati woyang’anila dela ) . Ananiuza kuti , “ Kulekelanji ! ” Patapita miyezi inayi , n’nasankha m’bale wina kukhala mnzanga wocita naye upainiya . Amayi nawo ndi mlongo wina anakacitila upainiya ku mpingo wina . Mu 1951 , n’nalemba fomu yofunsila Sukulu ya Giliyadi . Nili m’ndendemo , n’nalandila ciitano ca sukulu ya Giliyadi ya namba 22 . Ndiyeno n’nakwela sitima yopita ku South Lansing ku New York , kumene kunali sukuluyo . Nili na Janet pa cisumbu cina ku Philippines Tikali kutumikila pa ofesi ya nthambi ku Quezon City Kodi mungapeze bwanji “ mtendele wa Mulungu ” ? Nanga mpingo ungakuthandizeni bwanji kucepetsa nkhawa zanu ? ( Onani pikica pamwambapa . ) ( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani ino ? 5 : 7 ) Koma kodi tingacite bwanji zimenezi ? Wamasalimo anacondelela Yehova kuti : “ Inu Mulungu , mvetselani pemphelo langa . ” N’cifukwa ciani pemphelo n’lofunika tikakhala na nkhawa ? ( Ŵelengani Mateyu 11 : 28 - 30 . ) Kodi Yesu anatanthauza ciani pamene anati : “ Musamade nkhawa ” ? Tsiku lililonse limakhala kale na mavuto ake . Kodi mufunika kucita ciani na nkhawa zakumbuyo ? 55 : 2 - 5 ) Koma sanalole nkhawa kumutayitsa cidalilo cake mwa Yehova . Baibo imati : “ Nkhawa mumtima mwa munthu ndi imene imauwelamitsa , koma mau abwino ndi amene amausangalatsa . ” 10 : 24 , 25 ) ‘ Kulimbikitsana ’ kumeneku kudzakupatsani mphamvu mwauzimu , ndipo mudzakwanitsa kulimbana na nkhawa iliyonse . — Aroma 1 : 12 . ( a ) Tingam’tulile bwanji nkhawa zathu Mulungu ? Tingatsimikize bwanji kuti Yehova amapeleka mphoto kwa atumiki ake ? Kodi Yehova anadalitsa bwanji atumiki ake kumbuyoku ? 1 , 2 . ( a ) Kodi cikondi na cikhulupililo n’zogwilizana bwanji ? ( Kodi ciyembekezo codzalandila mphoto cimatithandiza bwanji ? Yesu anati ophunzila ake adzafupidwa pa kudzimana kwawo ( Onani palagilafu 5 ) Mtumwi Petulo anafunsa Yesu kuti : “ Ife tasiya zinthu zonse ndi kukutsatilani , kodi tidzapeza ciani ? ” Pa Ulaliki wa pa Phili , Yesu anati : “ Kondwelani , dumphani ndi cimwemwe , cifukwa mphoto yanu ndi yaikulu kumwamba , pakuti umu ndi mmenenso anazunzila aneneli amene analipo inu musanakhaleko . ” Mose anauza mtundu wa Isiraeli kuti : “ Yehova adzakudalitsa ndithu m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa kuti likhale colowa cako . Adzakudalitsa ngati udzamveladi mau a Yehova Mulungu wako ndi kutsatiladi malamulo onsewa amene ndikukupatsa lelo . Yehova Mulungu wako adzakudalitsa ndithu monga mmene anakulonjezela . ” Waciŵiliyo anamucha Efuraimu , cifukwa anati , ‘ Mulungu wandipatsa ana m’dziko la masautso anga . ’ ” Mau a Mulungu amati : “ Cifukwa ca cimwemwe cimene anamuikila patsogolo pake , anapilila mtengo wozunzikilapo . Komanso , Atate wake anamuyanja na kumuonjezela maudindo osililika . Kodi Yehova amamvela bwanji pa zimene timacita kaamba ka iye ? “ Wokomela mtima munthu wonyozeka akukongoza Yehova , ndipo adzam’bwezela zimene anacitazo . ” Kodi timapeza citonthozo canji pa 1 Yohane 3 : 19 , 20 ? ( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 19 , 20 . ) Ni madalitso ena ati amene tili nawo kale ? Kodi atumiki a Yehova amamvela bwanji na madalitso amene amalandila ? Mwacitsanzo , Bianca wa ku Germany anati : “ Nicita kusoŵa mau oyamikilila Yehova ponithandiza pa nkhawa zanga , na kunicilikiza tsiku ndi tsiku . Kunja kuli msokonezeko wokha - wokha m’dziko . Koma potumikila moyandikana na Yehova , nimamva kukhala wotetezeka m’manja mwake . Pamene nidzimana zinthu pom’tumikila , m’pamenenso iye amaniwonjezela madalitso . ” Kuti nizikumbukila mfundo zonilimbikitsa , nimalemba m’kabuku malemba na mfundo za m’zofalitsa zathu kuti niziyang’anamo . Nimakaitana kuti ‘ Cithandizo ca Panthawi Yake . ’ Tikasumika maganizo pa malonjezo a Yehova , mavuto amaoneka kuti ni a kanthawi cabe . Yehova ni wokonzeka kutithandiza nthawi zonse , olo tikumane na mavuto abwanji . ” Komabe , mukhoza kuganizila njila zimene Yehova wakudalitsilani imwe na anthu ena . Kodi Paulo na anthu ena anamasulidwa bwanji ku ucimo ndi imfa ? ( Ŵelengani Aroma 6 : 1 , 2 . ) N’cosankha canji cimene aliyense wa ife afunika kupanga ? ( Ŵelengani Aroma 7 : 21 - 23 . ) ( Ŵelengani Miyambo 14 : 5 ; Aefeso 4 : 25 . ) Iwo amalandila “ mzimu ” monga amene ‘ akudikila . . . kuti atengedwe kukhala ana a Mulungu , . . . kuti atuluke m’matupi [ awo a nyama ] . ’ ( Ŵelengani Aroma 4 : 20 - 22 . ) ( Ŵelengani Machitidwe 18 : 2 - 4 ; 20 : 20 , 21 , 34 , 35 . ) Anthu ambili okaona malo amapita ku mzinda wa Aveiro , kumpoto kwa dziko la Portugal , kukaona maiŵe a mcele . Mboni za kumaloko zimatengela mwayi kulalikila uthenga wabwino kwa anthu ogulitsa mcele kumeneko Mfundo zina zimene Baibo imakamba “ Olungama adzalandila dziko lapansi , ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya . ” — Salimo 37 : 29 . M’nkhani iyi , tidzaona mmene tingagwilitsile nchito mphatso yathu ya ufulu wosankha m’njila yokondweletsa Mulungu . Nkhani yoyamba , idzafotokoza tanthauza la kudzicipetsa ndi zimene sikutanthauza . Kodi Yehova amafuna kuti tiziseŵenzetsa bwanji maluso athu ? 4 : 10 ) N’zoonekelatu kuti Yehova amafuna tizicita zinthu zopindulitsa ife ndi anthu ena . Nowa anali kukhala m’dziko ‘ lodzala ndi ciwawa ’ ndi zaciwelewele . Kuletsa nchito yathu ( Onani palagilafu 6 mpaka 9 ) 6 , 7 . ( a ) N’ciani cimene Nowa sakanakwanitsa kucita ? ( b ) Nanga n’zofanana bwanji kwa ifenso ? Ifenso tikukhala m’dziko lodzala ndi zoipa , ndipo tidziŵa kuti Yehova adzaliwononga . ( 1 Yoh . 2 : 17 ) Sitingakakamize anthu kulandila “ uthenga wabwino wa Ufumu . ” Zimene Nowa anakwanitsa kucita : M’malo molefuka ndi zimene sakanakwanitsa kucita , Nowa anasumika maganizo pa zimene anakwanitsa kucita . ( Maliko 4 : 22 ) Koma pamene linaululika , kodi Davide anacita ciani ? Macimo akale ( Onani palagilafu 11 mpaka 14 ) 11 , 12 . ( a ) Sakanakwanitsa kucita ciani Davide ? Zimene Davide sakanakwanitsa kucita : Kwa Davide , inali nkhani ya madzi akatayika sayoleka , sakanatha kuzibwezela m’mbuyo . 12 : 10 - 12 , 14 ) Conco , anafunika kukhulupilila kuti ngati alapa , Yehova adzam’khululukila , ndi kum’thandiza kupilila zotulukapo zimenezo . 8 : 1 - 3 ) Anafunikila kusiya nkhaniyo m’manja mwa Yehova . Citsanzo ni m’bale Malcolm , amene anakhalabe wokhulupilika mpaka imfa yake mu 2015 . Sumika maganizo pa zimene ungakwanitse , osati zimene sungakwanitse . ” ( b ) Nanga imwe pa canu , lidzakuthandizani bwanji lembali mu umoyo wanu ? Lemba lathu la caka ca 2017 : “ Khulupilila Yehova ndipo cita zabwino . ” Nanga tingalemekeze bwanji ufulu wa ena pa zimene amasankha ? Ndidzawakonda mwa kufuna kwanga . ” 4 , 5 . ( a ) Ndani anali woyamba kupatsidwako mphatso ya ufulu wosankha zocita ? ( b ) Aliyense afunika kudzifunsa funso liti ? Yankho la funso limeneli lingakhudze tsogolo lathu lonse . Mulungu “ anayamba kuzibweletsa kwa munthuyo , kuti ciliconse aciche dzina . ” Tipeweletu kucita ciani ndi mphatso yathu yosankha zocita ? Yelekezani kuti munapatsa mnzanu mphatso yodula kwambili . Monga Akhiristu , tingapewe bwanji kuseŵenzetsa molakwa ufulu wathu ? ( Ŵelengani 1 Petulo 2 : 16 . ) Munthu amene akuyenda alibe ulamulilo wowongolela mapazi ake . ” Tiphunzilanji pa mfundo ya pa Agalatiya 6 : 5 ? Kumbukani mfundo ya pa Agalatiya 6 : 5 . Mudzacita ciani poonetsa kuti mumayamikila mphatso ya ufulu wosankha zocita ? ( a ) Kodi anthu ambili amakuona bwanji kudzicepetsa ? Ndipo kudzicepetsa n’ciani maka - maka ? N’cifukwa ciani tiyenela kupewa kuganizila molakwa zolinga za ena ? Tingaphunzilenji kwa Yesu utumiki wathu ukasintha ? ( Ŵelengani Agalatiya 6 : 4 , 5 . ) ( Ŵelengani Miyambo 3 : 5 , 6 . ) ( Ŵelengani Mlaliki 11 : 4 - 6 . ) N’ciani cidzatithandiza kukhalabe wodzicepetsa kwamuyaya ? N’cifukwa ciani cimakhala covuta kwa ena kugaŵilako ena maudindo ? Anauza Natani kuuza Davide kuti : “ Si iwe amene udzandimangila nyumba yokhalamo . ” ( Ŵelengani Numeri 11 : 24 - 29 . ) Ayi usatelo . Ndikanakonda anthu onse a Yehova akanakhala aneneli , cifukwa Yehova akanaika mzimu wake pa iwo ! ” ( Ŵelengani Afilipi 2 : 20 - 22 . ) Ofesi ya nthambi inatitumizila magazini ogaŵila mu ulaliki okwana 800 . N’nali kuphunzitsa m’mizinda ya Manaus , Belém , Fortaleza , Recife , ndi Salvador . Mu August 1964 , tinafika mumzinda wa Lisbon , ku Portugal . Ndilo gulu lokha limene likugwila nchito imene Yesu analamula ophunzila ake kucita — yolalikila uthenga wabwino wokamba za Ufumu wa Mulungu . ” Pamene nkhani ino inali kulembedwa kuti ifalitsidwe , m’bale Douglas Guest anamwalila pa 25 October , 2015 ali wokhulupilika kwa Yehova . ( Ŵelengani Yesaya 63 : 11 - 14 . ) ( Ower . 6 : 34 ) Ndipo “ mzimu wa Yehova unayamba kugwila nchito pa Davide . ” N’cifukwa ciani Mulungu anafuna kuti anthu ake azilemekeza atsogoleli mu Isiraeli ? ( Ŵelengani Aheberi 1 : 7 , 14 . ) Baibo imachula Cilamulo cimene cinapatsidwa kwa Aisiraeli kuti “ Cilamulo ca Mose . ” 11 , 12 . ( a ) Kodi Yoswa ndi mafumu olamulila anthu a Mulungu anafunika kucita ciani ? “ Mfumuyo itangomva mau a m’buku la cilamulolo , nthawi yomweyo inang’amba zovala zake . ” N’cifukwa ciani Yehova anali kulanga atsogoleli ena a anthu ake ? Nthawi zina , Yehova anali kuwalanga kapena kusankha wina kuti atsogolele . N’ciani cionetsa kuti mzimu woyela unalimbitsa Yesu ? Patangopita nthawi yocepa Yesu atabatizika , “ kunabwela angelo ndi kuyamba kum’tumikila . ” ( Mat . 4 : 11 ) Kutatsala maola ocepa kuti Yesu aphedwe , “ mngelo wocokela kumwamba anaonekela kwa iye ndi kumulimbikitsa . ” Kodi Mau a Mulungu anatsogolela bwanji umoyo wa Yesu ndi ziphunzitso zake ? Amandipembedza pacabe , cifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati ziphunzitso za Mulungu . ” ( Mat . Palibe wabwino , koma Mulungu yekha . ” “ Nthawi yomweyo mngelo wa Yehova anamukantha , cifukwa sanapeleke ulemelelo kwa Mulungu . Ndipo anadyedwa ndi mphutsi n’kumwalila . ” ( Mac . Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? M’nkhani yotsatila tidzakambilana mayankho a mafunso amenewa . Umenewu uyenela kuti unali mpukutu woyambilila wolembedwa ndi Mose . 1 : 15 - 26 ) N’cifukwa ciani cosankha cimeneci cinali cofunika kwambili kwa iwo ndi kwa Yehova ? Pokhala bungwe lolamulila , anali kupeleka malangizo ku mipingo yonse . — Mac . 15 : 2 . 5 , 6 . ( a ) Kodi mzimu woyela unali kugwila bwanji nchito pa bungwe lolamulila ? ( c ) Kodi Mau a Mulungu anatsogolela bwanji bungwe lolamulila ? Cifukwa coyamba n’cakuti mzimu woyela unali kugwila nchito pa bungwe lolamulila . 5 : 19 , 20 ) Cacitatu , Mau a Mulungu anatsogolela bungwe lolamulila . N’cifukwa ciani tingati Yesu anali kutsogolela Akhiristu oyambilila ? ( a ) Ni liti pamene Yesu anasankha “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ” ? Mu 1919 , apo n’kuti papita zaka zitatu pamene m’bale Russell anamwalila , Yesu anasankha “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu . ” 6 : 4 ) Nsanja ya Mlonda ya July 1 , 2013 inafotokoza kuti “ kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ” ni kagulu kocepa ka abale odzozedwa amene amapanga Bungwe Lolamulila . Conco , kodi tingaliyankhe bwanji funso la Yesu lakuti : “ Ndani kweni - kweni amene ali kapolo wokhulupilika ndi wanzelu ? ” ( Mat . Kodi mzimu woyela wathandiza bwanji Bungwe Lolamulila ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 10 . ) Ni njila imodzi iti imene tingakumbukile Bungwe Lolamulila ? N’cifukwa ciani ndimwe ofunitsitsa kutsatila Mtsogoleli wathu , Yesu ? Pamene Yesu anabwelela kumwamba , sanaiŵale otsatila ake . ( Mat . Posacedwa , adzatitsogolela ku moyo wamuyaya . Kuyambila mu 1955 , bungwe limenelo lakhala likuchedwa kuti Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania . Yehova “ amatitonthoza m’masautso athu onse ” “ Ineyo ndalankhula ndipo ndidzazicita . 1 , 2 . ( a ) Kodi Yehova anatidziŵitsa ciani ? MAU oyamba m’Baibo ali ndi mfundo yosavuta kumvetsa koma yofunika yakuti : “ Pa ciyambi , Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi . ” ( c ) Nanga tidzakambilana mafunso ati ? N’cifukwa ciani nsembe ya dipo la Yesu ndiye inatsegula khomo kuti colinga ca Mulungu cikwanilitsike ? Ni mphatso zina ziti zimene Yehova anapatsa Adamu ndi Hava ? Zinali ngati kuti iye akukamba kuti : ‘ Kodi simungacite zimene mufuna ? ’ Koma Yehova ni wokhulupilika ku malamulo ake , ndipo sawaphwanya olo pang’ono . ( Ŵelengani Deuteronomo 32 : 4 , 5 . ) N’cifukwa ciani dipo ni mphatso ya mtengo wapatali ? Yehova anapeleka dipo ya mtengo wapatali . ( 1 Pet . Ni liti pamene Yehova adzakhala “ zinthu zonse kwa aliyense ” ? ( Ŵelengani Salimo 40 : 8 - 10 . ) Nanga ise tingaonetse bwanji kuti timaikonda dzina la Yehova ? ( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 15 , 16 . ) N’cifukwa ciani Yehova angatione olungama ngakhale kuti ndise ocimwa ? Iye amalandila anthu amene adzipeleka kwa iye kukhala alambili ake . Kodi Yesu anatanthauza ciani pamene anapempha kuti : “ Cifunilo canu cicitike ” ? Kodi dipo limapindulitsa bwanji anthu amene anafa ? Kodi Mulungu ali nalo colinga canji “ khamu lalikulu ” ? ( a ) Ni madalitso anji amene timalandila kwa Yehova ? ( Ŵelengani Machitidwe 3 : 19 - 21 . ) ( Mal . 3 : 6 ) Yehova anatipatsa zinthu zambili osati cabe mphatso ya moyo . Baibo imati : “ Tikudziŵa ndipo tikukhulupilila za cikondi cimene Mulungu ali naco kwa ife . ” Kodi m’poyenela nthawi zina kusintha zosankha zimene tinapanga kale ? M’nkhani imeneyi tidzapeza mayankho a mafunso amenewa . Ngakhale n’conco , Yehova anaona kuti mafumuwo anali na mtima wathunthu . Nanga bwanji ife ? Kodi Mulungu adzaona kuti tili na mtima wathunthu ngakhale kuti nthawi zina timalakwa ? Tinali kukhala pa famu yaing’ono kum’maŵa kwa South Dakota . Nchito yaikulu imene tinali kugwila pa banja lathu ni yaulimi , koma sikuti ndiyo inali nchito yofunika kwambili pa umoyo wathu . Makolo anga anabatizika n’kukhala Mboni za Yehova mu 1934 . Atate , dzina lawo a Clarence , ndi akulu awo , a Alfred , onse anatumikilapo monga mtumiki wa mpingo ( tsopano mgwilizanitsi wa bungwe la akulu ) mu mpingo wathu waung’ono ku Conde , m’dela la South Dakota . Ine ndi mlongo wanga , Dorothy , tinakhala ofalitsa uthenga wa Ufumu pamene tinali na zaka 6 . Tinali kukondanso kupezeka pa misonkhano yadela ndi yacigawo . Baibo imati : “ Munthu woyenda ndi anthu anzelu adzakhala wanzelu . ” Nthawi zina akamatumikila mipingo ya pafupi ndi kwathu , anali kunipempha kuti nipite nawo mu ulaliki . Naimilila pa galimoto ya pa famu , nitangofika kumene ku Beteli Pa famu ya ku Staten Island panali nyumba ya wailesi ya Mboni yochedwa WBBR . Pa famuyo panali kuseŵenzela atumiki a pa Beteli okwana cabe 15 mpaka 20 . Ambili amene tinali kumeneko tinali acicepele ndi osadziŵa zambili . M’baleyu anali kugwila mokhulupilika nchito yake pa Beteli , koma sanali kunyalanyaza nchito yolalikila . Nili na Angela mu 1975 , kuyembekezela kuti atifunse mafunso pa TV Patapita zaka zitatu , tinaitanidwa kuti tikatumikile ku Beteli . N’cifukwa ciani Yehova ndi Khristu ayenela kulemekezedwa ? Anthu analengedwa “ m’cifanizilo ca Mulungu . ” 8 , 9 . ( a ) Kodi Mboni za Yehova zimawaona bwanji olamulila a boma ? ( Aef . Komanso musamachule aliyense kuti atate wanu padziko lapansi pano , pakuti Atate wanu ndi mmodzi , wakumwamba Yekhayo . Musamachedwe ‘ atsogoleli , ’ pakuti Mtsogoleli wanu ndi mmodzi , Khristu . Koma wamkulu kwambili pakati panu akhale mtumiki wanu . Aliyense wodzikweza adzatsitsidwa , koma aliyense wodzicepetsa adzakwezedwa . ” ( Mat . N’cifukwa ciani anthu ena safunika kutipangila zosankha ? ( a ) Kuti tipange zosankha mwanzelu , kodi tifunika kukhulupilila ciani ? N’ciani cingatithandize kupanga zosankha mwanzelu ? ( Ŵelengani Yakobo 1 : 5 - 8 . ) ( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 24 ) Masiku ano , akulu ayenela kutsatila citsanzo ca Paulo pamene apeleka uphungu kwa ena pa nkhani zaumwini . Akulu acikondi amathandiza ena kudziŵa mmene angapangile zosankha paokha ( Onani palagilafu 11 ) 21 : 9 - 12 ) Nawonso akulu afunika kupeza nthawi yofufuza asanapange zosankha . Kodi cidzathandiza banja langa kukhala lacimwemwe ndi lamtendele ? Nanga kodi cidzaonetsa kuti ndine woleza mtima ndi wokoma mtima ? ’ N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizidzipangila tokha zosankha ? Kodi kutumikila Yehova ndi mtima wathunthu kumatanthauzanji ? Pa mafumu anayi amenewa , kodi inu mungafune kutengela iti ? ( Ŵelengani 2 Mbiri 14 : 11 . ) Kodi mtima wanu ungakusonkhezeleni kucita ciani ? Yehosafati mwana wa Asa “ anapitiliza kuyenda m’njila za Asa bambo ake . ” ( Ŵelengani 2 Mbiri 20 : 2 - 4 . ) ( Ŵelengani Yesaya 37 : 15 - 20 . ) ( Ŵelengani 2 Mafumu 20 : 1 - 3 . ) ( Ŵelengani 2 Mbiri 34 : 1 - 3 . ) ( Ŵelengani 2 Mbiri 34 : 18 , 19 . ) N’cifukwa ciani tidzakambilana zitsanzo za mafumu anayi aciyuda ? ( Ŵelengani 2 Mbiri 16 : 7 - 9 . ) ( Ŵelengani 2 Mbiri 32 : 31 . ) Ndipo abale ndi alongo ambili angayambe kumutamanda . ( Ŵelengani 2 Mbiri 35 : 20 - 22 . ) Baibo imakamba kuti mau a Neko anali “ ocokela pakamwa pa Mulungu . ” Tiyeni tipitilize kuganizila nkhani za m’Baibo zimenezi , ndipo tiziyamikila kuti Yehova watipatsa zitsanzo zimenezi kuti zitilangize . Kodi munapangapo malonjezo angati kwa Yehova ? Nanga bwanji ponena za lonjezo lanu la kudzipeleka kapena la cikwati ? Tikaona kuti ife kapena munthu wina wacitilidwa zinthu zopanda cilungamo , cikhulupililo , kudzicepetsa , ndi kukhulupilika kwathu zingayesedwe . “ Dziko likupita limodzi ndi cilakolako cake , koma wocita cifunilo ca Mulungu adzakhala kosatha . ” — 1 YOH . Kodi Yehova adzacita ciani kwa anthu oipa ndi mabungwe acinyengo ? Baibo imati : “ Dziko likupita . ” ( 1 Yoh . Kulibe mdima wandiweyani woti amene akucita zopweteka ena abisaleko . ” Vesi ina mu salimo imeneyi imati : “ Olungama adzalandila dziko lapansi , ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya . ” ( Sal . 37 : 11 , 29 ) Kodi “ ofatsa ” ndi “ olungama ” amenewa n’ndani ? Tingatsimikize bwanji kuti anthu okhala m’dziko latsopano azidzacita zinthu mwadongosolo ? Kodi padziko padzakhala dongosolo lililonse pambuyo pa Aramagedo ? 14 : 33 ) Conco , “ dziko lapansi latsopano ” lidzakhala ladongosolo . Ni makhalidwe oipa ati amene ni ofala m’dela lanu ? Nanga inu ndi a m’banja lanu amakukhudzani bwanji ? Tiphunzilapo ciani pa ciŵeluzo cimene Yehova anapeleka ku mizinda ya Sodomu ndi Gomora ? ( Ŵelengani 2 Petulo 2 : 6 - 8 . ) ( Ŵelengani Salimo 46 : 8 , 9 . ) N’zinthu ziti zimene sizidzakhalakonso pambuyo pa Aramagedo ? Fotokozani citsanzo . ( b ) Tifunika kucita ciani kuti tidzapulumuke pamene dziko loipali liwonongedwa ? “ KODI Woweluza wa dziko lonse lapansi sadzacita colungama ? ” Akhristu amadziŵa kuti angacitilidwe zinthu zopanda cilungamo ndi munthu amene sali mumpingo wacikhristu . Mu 1946 , analoŵa kalasi ya namba 8 ya Sukulu ya Giliyadi , ku New York , m’dziko la United States . Atatsiliza maphunzilo , anam’tumiza ku Switzerland kukatumikila monga woyang’anila dela . Kodi tidzakambilana zocitika ziti m’nkhani ino ndi yotsatila ? M’nkhani ino , tidzakambilana za Yosefe mdzukulu wa Abulahamu , ndi zimene abale ake anamucitila . 10 , 11 . ( a ) N’zinthu zopanda cilungamo ziti zimene zinacitikila Yosefe ? ( Ŵelegani Mateyu 5 : 23 , 24 ; 18 : 15 . ) Kukhala wokhulupilika kwa Yehova ndi kwa abale athu kudzatithandiza kupewa mijedo . Cacikulu , iye sanalole kuti kupanda ungwilo ndi zolakwa za ena zisokoneze ubale wake na Yehova . N’cifukwa ciani tifunika kuyandikila kwambili Yehova ngati wina mumpingo watilakwila ? Tingaonetse bwanji kuti timakhulupilila “ Woweluza wa dziko lonse lapansi ” ? Onani nkhani yofotokoza mbili ya moyo wa m’bale Willi Diehl , yamutu wakuti “ Yehova Ndiye Mulungu Wanga , Amene Ndimkhulupirira , ” mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 1991 . ( Onani mapikica pamwambapa . ) ( b ) Ni mafunso ati amene adzayankhidwa m’nkhani ino ? Iwo n’zitsanzo zabwino ngako kwa amuna ndi akazi amakono , amene amacita malonjezo kwa Yehova . N’cifukwa ciani malonjezo amene timapanga kwa Mulungu ni nkhani yaikulu ? Nanga tingaphunzile ciani kwa Yefita ndi Hana pa nkhaniyi ? 2 , 3 . ( a ) Kodi lonjezo n’ciani ? ( b ) Kodi Malemba amati ciani pa nkhani yopanga malonjezo kwa Mulungu ? Acite malinga ndi mau onse otuluka pakamwa pake . ” ( a ) Kodi kupanga lonjezo kwa Mulungu ni nkhani yaikulu bwanji ? ( b ) Tidzaphunzila zotani zokhudza Yefita ndi Hana ? ( a ) Kodi cinali copepuka kwa Yefita na mwana wake kukwanilitsa zimene analonjeza kwa Mulungu ? Iye anati : “ Ndatsegula pakamwa panga pamaso pa Yehova , ndipo sindingathe kubweza mau anga . ” ( b ) Kodi lonjezo la Hana linatanthauza ciani kwa Samueli ? Ndipo Hana anauza Eli kuti : “ Ndinali kupemphela kuti Yehova andipatse mwana uyu , kuti andipatse cimene ndinam’pempha . Lonjezo lina lofunika kwambili limene munthu angapange , ni lonjezo la cikwati . Kodi Baibo imakamba zotani pa pankhani yothetsa cikwati ndi kupatukana ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 7 : 10 , 11 . ) Banja lina linati : “ Kucokela pamene tinayamba kuphunzila kabuku kameneka , banja lathu lakhala lacimwemwe ngako . ” Lomba banja lathu likuyenda bwino . ” 18 , 19 . ( a ) Kodi makolo ambili Acikhristu acita ciani ? ( b ) Fotokozani zokhudza atumiki a nthawi zonse apadela . Lonjezo la utumiki wanthawi zonse wapadela ( Onani palagilafu 19 ) Amavomelezanso kuti adzakhala na umoyo wosalila zambili , ndi kuti sadzaloŵa nchito kwina kulikonse popanda cilolezo . Onani buku lakuti “ Khalanibe M’cikondi ca Mulungu , ” mapeji . 219 - 221 . Kodi Wamphamvuyonse amasangalala kuti ndiwe wolungama ? Kapena amapindula ciliconse cifukwa cakuti sucita colakwa ? ” ( b ) Kodi Aisiraeli anagonjetsa bwanji asilikali a Yabini ? ( Ŵelengani Oweruza 4 : 14 - 16 . ) Mtsinje wa Kisoni unawakokolola . ” Onani nkhani yakuti “ Nkhawa Zokhudza Ndalama , ” mu Nsanja ya Mlonda ya September 1 , 2015 . 1 , 2 . ( a ) Kodi Naboti ndi ana ake anacitilidwa zinthu zopanda cilungamo ziti ? ( b ) Ni makhalidwe aŵili ati amene tidzakambilana m’nkhani ino ? Nanga n’cifukwa ciani anakana kugulitsa munda wake wa mpesa kwa Mfumu Ahabu ? Naboti anakhalabe wokhulupilika kwa Yehova pa nthawi imene Aisiraeli ambili anali kutsatila citsanzo coipa ca Mfumu Ahabu ndi mkazi wake , Yezebeli . Ŵelengani 1 Mafumu 21 : 1 - 3 . Mwaulemu , iye anafotokoza kuti : “ Sindingacite zimenezo pamaso pa Yehova , kupeleka colowa ca makolo anga kwa inuyo . ” Kodi kudzicepetsa kuyenela kuti kunawateteza bwanji acibale a Naboti ndi mabwenzi ake ? ( Ŵelengani Deuteronomo 32 : 3 , 4 . ) ( b ) Kodi kudzicepetsa kumatiteteza bwanji ? Mungacite bwanji ngati akulu apeleka cilengezo cimene inu simunagwilizane naco ? Kodi tidzakambilana ciani tsopano ? Nanga n’cifukwa ciani ? Kodi Petulo anawongoleledwa bwanji ? Nanga pakubuka mafunso otani ? Ndipo pambuyo pa izi , iye anauzilidwa kulemba makalata aŵili amene anakhala mbali ya Baibo . 3 Kuthandiza Alendo Ocokela ku Mayiko Ena “ Kutumikila Yehova Mokondwela ” Nkhani yaciŵili idzafotokoza mmene mfundo za m’Baibo zingathandizile makolo amene akukhala m’dziko lina kupanga zosankha zimene zingapindulitse ana awo . Tinaona anthu akuthaŵa , ndipo ena anali kuombela mfuti anzawo . Makolo anga na ise ana 11 tinathaŵa kuti tipulumutse miyoyo yathu , ndipo tinangothaŵa na zovala za m’thupi . N’cifukwa ciani Yesu ndi ophunzila ake ambili anathaŵa kwawo ? Iye anati : “ Akakuzunzani mumzinda wina , muthaŵile mumzinda wina . ” ( b ) pamene akhala m’kampu ? Mendo yanga yanatupa ngako cakuti n’nauza abale anga kuti anisiye cabe . Koma atate ananinyamula . Sanafune kuti asilikali oukilawo anipeze n’kunipha . Anali kungokhalila kujeda anzawo , kuledzela , kuchova njuga , kuba , ndipo anali kucita ciwelewele . ” ( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 17 , 18 . ) ( b ) N’cifukwa ciani tifunika kuwathandiza moleza mtima ? Iwo afunika kuona kuti timawakonda . ( b ) Nanga angaonetse bwanji kuyamikila ? Kodi tingawathandize bwanji abale na alongo athu othaŵa kwawo ? ( a ) Ni ciyeso citi cimene othaŵa kwawo afunika kupewa ? Ndiyeno , ananyamula cola copanda katundu cija n’kukamba kuti : ‘ Mwaona ka ? Zonse zimene zinali m’colamu sizofunika kweni - kweni pa moyo ! ’ ” — Ŵelengani 1 Timoteyo 6 : 8 . Conco , akafika m’dela lathu afunika kuona kuti Yehova na ise Akhristu anzawo timawakonda . Masiku ano , anthu ambili othaŵa kwawo amacokela m’mayiko amene nchito yolalikila si yovomelezeka mwalamulo . ( b ) Tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Mlongoyu anati : “ Abale kumeneko anatilandila monga acibale awo . Anatipatsa zakudya , zovala , pogona ndi ndalama zoyendela . Ni Mboni za Yehova zokha ! ” — Ŵelengani Yohane 13 : 35 . Abale othaŵa kwawo akangofika , akulu ayenela kutsatila malangizo a m’buku la Gulu Lochita Chifunilo ca Yehova mutu 8 , palagilafu 30 . Poyembekezela , iwo mosamala angafunse abale othaŵa kwawo za mipingo imene anali kusonkhanako , ndi zokhudza utumiki kuti adziŵe umoyo wawo wauzimu . “ Palibe cimene cimandisangalatsa kwambili kuposa kumva kuti ana anga akuyendabe m’coonadi . ” — 3 YOH . 4 . Kodi makolo angapeleke bwanji citsanzo cabwino kwa ana awo ? Pofuna kusankha kuti banja lizisonkhana mpingo wa citundu citi , kodi mutu wa banja angacite ciani ? Kodi ena angathandize bwanji makolo amene anasamukila m’dziko lina pamodzi na ana awo ? 1 , 2 . ( a ) Ni vuto liti limene makolo ambili osamukila m’dziko lina amakumana nalo ? ( b ) Tidzakambilana mafunso ati m’nkhani ino ? Iye anapitiliza kuti : “ Koma n’tayamba kupita kusukulu , n’nayamba kukonda citundu ca m’dziko limene tinasamukila . Patapita zaka zocepa cabe , zinthu zinasinthilatu . Sin’nali kumvetsetsa zimene zinali kukambidwa pa misonkhano , ndipo sin’nali kudziŵa bwino cikhalidwe ca makolo anga . ” 3 , 4 . ( a ) Kodi makolo angapeleke bwanji citsanzo cabwino kwa ana awo ? ( b ) Kodi makolo sayenela kuyembekezela ciani kwa ana awo ? Ana anu akaona kuti ‘ mukufuna - funa ufumu coyamba , ’ amaphunzila kudalila Yehova kuti adzawapatsa zofunika pa umoyo . Musamakhale bize kwambili mpaka kusoŵa nthawi yoceza ndi ana anu . Kodi ana anu angapindule bwanji ngati aphunzila citundu canu ? Mukacita zimenezi , mudzakwanitsa kuphunzitsa ana anu coonadi mosavuta . Kodi mungacite ciani ? Kodi simungaphunzile cinenelo camanja kuti muzikwanitsa kukamba naye ? 3 : 15 ) Ngati m’banja lanu muli vuto laconco , n’zotheka ndithu kuthandiza ana anu kudziŵa Yehova ndi kum’konda . Koma tinali kuwaona akucita phunzilo laumwini , kupemphela , ndi kucititsa kulambila kwa pabanja wiki iliyonse . Zimenezi zinatithandiza kuona kuti kudziŵa Yehova n’kofunika ngako . ” N’cifukwa ciani ana ena amafunika kuphunzila za Yehova m’zitundu ziŵili ? ( a ) N’ndani afunika kusankha mpingo umene banja lizisonkhanako ? Koma ngati citundu sacimvetsetsa , sangapindule mokwanila . ( Ŵelengani 1 Akorinto 14 : 9 , 11 . ) Tinalinso kupempha nzelu kwa Mulungu . Zimene tinapeza sizinali zotikomela . Koma titaona kuti anawo sapindula mokwanila na misonkhano ya m’citundu cathu , tinaganiza zosamukila mumpingo wa citundu ca m’dzikolo . Nthawi zonse , tinali kusonkhana ndi kuyenda muulaliki pamodzi . Tinalinso kuitana abale na alongo a kumaloko , kuti tidzadye nawo cakudya kapena kupita nawo kokaona malo . Zimenezi zinathandiza ana athu kudziŵana ndi abale . Zinawathandizanso kudziŵa Yehova Mulungu ndi kuyamba kumuona monga Tate ndi Bwenzi lawo . Tinaona kuti zimenezi ndizo zinali zofunika ngako kwa anawo kupambana kuti aphunzile citundu cathu . ” M’bale Samuel anakambanso kuti : “ Pofuna kuti tikhalebe olimba mwauzimu , ine na mkazi wanga tinali kusonkhananso na mpingo wa citundu cathu . Umoyo unali wa bize kwambili , ndipo tinali kukhala otopa . Koma Yehova anatidalitsa cifukwa ca khama lathu ndi kudzipeleka kwathu , ndipo timamuyamikila kwambili . Tsopano , ana athu onse atatu akutumikila Yehova mu utumiki wanthawi zonse . ” Kristina anati : “ N’nali kudziŵako ndithu citundu ca makolo anga , koma zimene zinali kukambidwa kumisonkhano sin’nali kuzimvetsetsa . Pamene n’nafika zaka 12 , n’napezeka pa msonkhano wacigawo wa m’citundu cimene n’naphunzila kusukulu . Kwa nthawi yoyamba , n’nadziŵa kuti zimene n’nali kumva ni coonadi . Zinthu zinasinthanso kwambili n’tayamba kupemphela m’citundu cimene n’naphunzila kusukulu . N’nayamba kupemphela kwa Yehova mocokela pansi pa mtima . ” Inu acicepele , kodi muona kuti mufunika kusamukila mumpingo wa citundu ca m’dela limene mukhala ? Nadia , amene lomba atumikila pa Beteli , anati : “ Pamene ine na abale anga tinafika zaka za pakati pa 13 ndi 19 , tinafuna kusamukila mumpingo wacinenelo ca m’dela limene tikhala . ” Nadia anati : “ Tsopano timayamikila kuti makolo athu anayesetsa kutiphunzitsa citundu cawo , ndipo tinapitiliza kukhala mumpingo wa citundu ca m’dziko limene tinacokela . Zimenezi zatithandiza kukhala na umoyo watanthauzo , ndiponso zatipatsa mwayi waukulu wothandiza anthu kudziŵa Yehova . ” ( b ) Nanga makolo angapeze kuti thandizo pophunzitsa ana awo coonadi ? ( Ŵelengani Miyambo 1 : 8 ; 31 : 10 , 27 , 28 . ) Komabe , makolo amene sadziŵa bwino cinenelo ca ana awo , afunika thandizo kuti aphunzitse ana awo mowafika pamtima . Ana ndi makolo awo , onse amapindula akamagwilizana ndi mpingo ( Onani mapalagilafu 18 ndi 19 ) ( b ) Kodi makolo afunika kupitiliza kucita ciani ? Akanithandiza kukonzekela nkhani za m’sukulu , n’nali kuphunzilapo zambili . Komanso n’nali kukondwela na zosangulutsa zimene tinali kucita . ” Makolo , muzipemphela kwa Yehova kuti akuthandizeni , ndipo muzicita zimene mungathe kuti muphunzitse ana anu . ( Ŵelengani 2 Mbiri 15 : 7 . ) Muziona ubwenzi wa anawo ndi Yehova kuti ni wofunika kwambili kuposa zofuna zanu . Koma mu 1946 m’pamene n’namvetsetsa coonadi ca m’Baibo . M’kupita kwa nthawi , n’naphunzila cinenelo camanja , ndipo n’nayamba kusangalala nikamaseŵela na anzanga . Iye analembetsa kuti azilandila magazini , ndipo ananipempha kuti nikalalikilekonso mwamuna wake , Gary . Posapita nthawi , atsikanawo anayamba kuuzako anzawo a m’kilasi zimene anali kuphunzila . Panthawiyo , ananipatsa switi n’kunipempha kuti nikhale mnzake . Atasankha kuti abatizike , makolo ake anamuuza kuti , “ Ukakhala wa Mboni za Yehova , udzacoka pano panyumba . ” Iye anapitilizabe kuphunzila Baibo ndipo anabatizika . Pamene tinakwatilana mu 1960 , makolo ake sanabwele ku cikwati cathu . Mwana wanga , Nicholas na mkazi wake , Deborah , atumikila pa Beteli ku London Faye na James , Jerry na Evelyn , Shannan na Steven Lomba , tisonkhana mumpingo wa cinenelo camanja wa Calgary , ndipo nikali kutumikila monga mkulu . Tingacite ciani kuti tipitilize kum’konda kwambili Yehova ? Tingacite ciani kuti tizikonda kwambili coonadi ca m’Baibo ? N’cifukwa ciani tifunika kukonda abale athu ? N’ciani cimene ciyenela kuti cinacititsa cikondi ca Akhristu ena kuzilala ? Anthu mamiliyoni ambili aleka kudalila Mulungu . Limeneli ndilo lamulo lalikulu kwambili komanso loyamba . ” Muzionetsa kuti mumakonda Yehova ( Onani palagilafu 10 ) ( Ŵelengani Salimo 119 : 97 - 100 . ) Muzionetsa kuti mumakonda coonadi ca m’Baibo ( Onani palagilafu 14 ) Usiku wakuti mawa aphedwa , Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Ndikukupatsani lamulo latsopano , kuti muzikondana . Mmene ine ndakukondelani , inunso muzikondana . Mwakutelo , onse adzadziŵa kuti ndinu ophunzila anga , ngati mukukondana . ” — Yoh . 13 : 34 , 35 . ( 1 Yoh . Muzionetsa kuti mumakonda abale na alongo ( Onani palagilafu 17 ) Ni zinthu ziti zimene tingacite zoonetsa kuti timakonda abale na alongo athu ? Ŵelengani 1 Atesalonika 4 : 9 , 10 . 21 : 15 . Ndiyeno , anati : “ ‘ Ponyani ukonde kumbali ya kudzanja lamanja kwa ngalawayo ndipo mupeza kenakake . ’ Pamenepo anaponyadi ukondewo , koma sanathenso kuukoka cifukwa ca kuculuka kwa nsomba . ” — Yoh . 21 : 1 - 6 . ( b ) Ni mfundo yofunika kwambili iti imene m’bale wina ku Thailand anaphunzila pankhani yokhudza nchito ? Zimenezi zinapangitsa kuti nizisoŵa nthawi yocita zinthu zauzimu . Patapita nthawi , n’nazindikila kuti nifunika kupeza nchito ina kuti nizikwanitsa kuika zinthu za Ufumu patsogolo . ” M’baleyu anati : “ N’takonzekela pafupi - fupi kwa caka cathunthu , n’naleka kugwila nchitoyo n’kuyamba kugulitsa aisikilimu m’misewu . Poyamba , n’nali kusoŵa ndalama , ndipo n’nanganiza zongoleka . Nikakumana na anzanga amene n’nali kugwila nawo nchito yokonza makompyuta , anali kuniseka ndi kunifunsa cifukwa cake n’naleka nchito yokonza makompyuta pa malo abwino n’kuyamba kugulitsa aisikilimu . N’napemphela kwa Yehova kuti anithandize kupilila ndi kukwanilitsa colinga canga cofuna kukhala na nthawi yokwanila yocita zinthu zauzimu . N’nafika podziŵa bwino zimene makasitomala anga anali kukonda , ndipo n’naidziŵa bwino nchito yopanga aisikilimu . N’nayamba kugulitsa aisikilimu yonse imene napanga patsiku . Kunena zoona , n’nali kupeza ndalama zambili kusiyana ndi pamene n’nali kugwila ntchito yokonza makompyuta . Ndine wosangalala kwambili cifukwa nilibenso nkhawa ngati imene n’nali nayo pa nchito yakale ija . Ndipo cokondweletsa ngako n’cakuti lomba nili pa ubale wolimba na Yehova . ” — Ŵelengani Mateyu 5 : 3 , 6 . Atabatizika , anati : “ Nimaona kuti n’nachedwa kuyamba kutumikila Mulungu . Kutumikila Yehova kumabweletsa cimwemwe coculuka kuposa kucita zosangulutsa za m’dzikoli . ” Yesu anakamba kuti “ kapolo sangatumikile ambuye aŵili . ” Anakambanso kuti : “ Simungathe kutumikila Mulungu ndi Cuma nthawi imodzi . ” ( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 14 . ) Onani nkhani yakuti “ Kodi Zimene Mumachita pa Nthawi Yosangalala Zimakhala Zopindulitsa ? ” Komanso , tinali kulalikila mokhazikika . ” Tinali kukwinyilila tikaganizila kuti tidzasiya maphunzilo athu a Baibo . ” Koma patangopita mwezi umodzi , iwo analandila uthenga wokondweletsa . Miriam anati : “ Tinauzidwa kuti tiyambe kutumikila monga apainiya apadela . Tinakondwela ngako kudziŵa kuti tidzapitiliza utumiki wathu . ” Anakhulupilila lonjezo la pa Salimo 37 : 5 , pamene pamati : “ Lola kuti Yehova akutsogolele panjila yako , umudalile ndipo iye adzacitapo kanthu . ” Koma lomba timakwanitsa . Sitisoŵa ciliconse cofunika paumoyo . ” N’cifukwa ciani tingayembekezele kuti munthu akaloŵa m’banja adzakumana ndi mavuto ? Tingakhale otsimikiza kuti iye amatifunila zabwino , monga mmene anacitila na atumiki ake akale . — Ŵelengani Yeremiya 29 : 11 , 12 . ( Ŵelengani 1 Samueli 1 : 4 - 7 . ) Paula anati : “ Ngakhale kuti Ann sanali m’bululu wanga , cikondi cimene ananionetsa cinanithandiza kwambili . Cinanithandiza kuti nipitilize kutumikila Yehova . ” ( Ŵelengani Salimo 145 : 18 , 19 . ) “ Kumene kuli cuma canu , mitima yanunso idzakhala komweko . ” — LUKA 12 : 34 . Pamene tikambilana , ganizilani zimene inu pamwekha mungacite kuti muzikonda kwambili cuma cauzimu cimeneci . Mosakayikila , ngaleyo inalidi yamtengo wapatali kwa iye . ( Ŵelengani Maliko 10 : 28 - 30 . ) ( a ) N’cifukwa ciani mtumwi Paulo anakamba kuti utumiki wathu ni “ cuma m’zonyamulila zoumbidwa ndi dothi ? ” ( Ŵelengani Aroma 1 : 14 , 15 ; 2 Timoteyo 4 : 2 . ) Ena mwa iwo ni atumiki a pa Beteli , ena ni apainiya , ndipo ena ni akulu . Irene anati : “ Niona kuti palibe colinga cina cimene cikananibweletsela cimwemwe coculuka kuposa zimene n’nasankha kucita . ” Kodi “ mosungilamo cuma , ” kapena kuti nkhokwe , imene Yesu anachula pa Mateyu 13 : 52 n’ciani ? ( Welengani Miyambo 2 : 4 - 7 . ) Ganizilani zimene zinacitikila m’bale wina , dzina lake Peter . M’rabiyo pofuna kuyesa Peter anamufunsa kuti : “ Mnyamata iwe , buku la Danieli linalembedwa m’citundu canji ? ” Pamene n’nabwelela kunyumba ndi kufufuza m’magazini a Nsanja ndi Galamukani ! a miyezi yapambuyo , n’napeza nkhani imene inafotokoza kuti buku la Danieli linalembedwa m’Ciaramu . ” Pamene mucita zimenezi , mudzaunjika “ cuma cosatha kumwamba , kumene mbala singafikeko , ndipo njenjete singawononge . Pakuti kumene kuli cuma canu , mitima yanunso idzakhala komweko . ” — Luka 12 : 33 , 34 . “ Ine n’nali na vuto lokonda kukangana ndi m’bale amene nimaseŵenza naye . Tsiku lina pamene tinali kukangana , anthu aŵili anabwela kuti amvele zimene tinali kukangana . ” — CHRIS . “ Mlongo wina amene kaŵili - kaŵili n’nali kugwila naye nchito yolalikila , mwadzidzidzi analeka kulalikila na ine . Ine sin’nadziŵe cifukwa cimene anacitila zimenezo . ” — JANET . “ Tsiku lina n’nalumikizana ndi anzanga aŵili n’kumaceza pafoni . Mmodzi wa iwo anakamba kuti bayi , kuonetsa kuti walaila . Ndipo ine n’naganiza kuti wadula foni . Conco , n’nayamba kukamba mau oipa okhudza mnzangayo , osadziŵa kuti iye sanadule foniyo . ” — MICHAEL . “ Mumpingo mwathu , apaniya aŵili anayamba kukangana . Kukangana kwawo kunali kukhumudwitsa ena mumpingo . ” — GARY . “ Musakanganetu m’njila . ” ( Gen . “ Zolingalila sizikwanilitsidwa ngati anthu sakambilana moona mtima . ” ( Miy . Michael anati : “ M’baleyo ananikhululukila ndi mtima wonse . ” “ Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana ndi mtima wonse , ngati wina ali ndi cifukwa codandaulila za mnzake . ” ( Akol . Tsopano amalalikila uthenga wabwino pamodzi mwamtendele . Kusiyana kumeneku kungaoneke ngati nkhani yaing’ono , koma kungabweletse mavuto aakulu . ” Mkwiyo utakula , n’nayamba kum’citila zinthu mwamwano . Mumtima n’nati : ‘ Iye sanipatsa ulemu , na ine n’dzaleka kum’patsa ulemu . ’ ” Iye anati : “ N’nazindikila kuti zimene n’nali kucita si zabwino , ndipo n’nayamba kudziimba mlandu . N’naona kuti nifunika kusintha . N’tapemphela kwa Yehova za nkhaniyi , n’nagulila mlongoyo kamphatso , kumulembela kakalata , na kupita kukam’pepesa . Tinakumbatilana ndi kugwilizana zoiŵalako nkhaniyo . Apa lomba , ndise ogwilizana . ” ANTHU ambili masiku ano amaona kuti ndalama ndiye nkhani yaikulu . N’cifukwa ciani nkhani yokhudza ulamulilo wa Mulungu iyenela kuthetsedwa ? Kodi kucilikiza ulamulilo wa Yehova n’kofunika bwanji ? Taonani , kucokela tsiku limene makolo athu anamwalila , zinthu zonse zikupitililabe cimodzimodzi ngati mmene zakhalila kuyambila pa ciyambi ca cilengedwe . ” ( Ŵelengani Yesaya 55 : 10 , 11 . ) ( Ŵelengani Yobu 1 : 7 - 12 . ) ( Ŵelengani Yobu 38 : 18 - 21 . ) ( Ŵelengani Aroma 5 : 3 - 5 . ) Cimodzi n’cakuti iye amalamulila mwacikondi . Amatisamalila kuposa mmene ise tingadzisamalile . Kodi akulu na mitu ya mabanja angatengele bwanji citsanzo ca Yehova ? Salimo 147 imalimbikitsa anthu a Mulungu mobweleza - bweleza kuti afunika kutamanda Yehova . N’zinthu ziti zokhudza Yehova zimene zinapangitsa wolemba salimoyi kuona kuti Mulungu ni wofunika kutamandidwa ? Abale na alongo ambili acicepele ayamba utumiki wa nthawi zonse . “ Dzipezeleni mabwenzi ndi cuma cosalungama . ” — LUKA 16 : 9 . Tingapewe bwanji kukhala akapolo kwa anthu amalonda a m’dzikoli masiku ano ? N’cifukwa ciani nthawi zonse m’dziko la Satanali mudzakhala anthu osauka ? Tingaphunzilepo ciani pa malangizo a Yesu amenewa ? Tidziŵa bwanji kuti kucita malonda siinali mbali ya colinga ca Mulungu ? Fotokozani zitsanzo za mmene ena aonetsela kukhulupilika poseŵenzetsa cuma cawo . Nakhala munthu wokonzeka kukhululukila ena , woleza mtima , wopilila , ndi wokonzeka kulandila uphungu . ” Kodi Abulahamu anaonetsa bwanji kuti anali kudalila Mulungu ? ( b ) Nanga tingaonetse bwanji kuti timamvela malangizo a Paulo ? Paulo anachula Timoteyo kuti ndi “ msilikali wabwino wa Khristu Yesu . ” Pambuyo pake anamuuza kuti : “ Msilikali amene ali pa nkhondo sacita nawo zamalonda zimene anthu wamba amacita , pofuna kukondweletsa amene anamulemba usilikali . ” ( 2 Tim . Yehova amadalitsa anthu amene ni “ olemela pa nchito zabwino . ” ( Ŵelengani 1 Timoteyo 6 : 17 - 19 . ) Golide , siliva , ndi miyala ina yamtengo wapatali zidzakhala zinthu zokongoletsela , osati zogulitsa kapena zosunga monga cuma . Kuti mupeleke ndalama kupitila pa intaneti , yendani pa jw.org ndi kutinika pa mau akuti , “ Citani Copeleka ku Nchito Yathu ya Padziko Lonse . ” “ MWANA wathu wamwamuna atamwalila , tinavutika na cisoni pafupi - fupi kwa caka cathunthu , ” anatelo Susi . ( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 3 , 4 . ) Nthawi zonse tikacita zimenezi , mtendele wa Mulungu unali kuteteza mitima yathu na maganizo athu . ” — Ŵelengani Afilipi 4 : 6 , 7 . Pamene Lazaro anafa , kodi Yesu anaonetsa bwanji kuti anali ndi cisoni ? ( Aroma 15 : 4 ) Ngati munafedwa , mungapeze citonthozo pa malemba monga awa : ( Ŵelengani 1 Atesalonika 5 : 11 . ) N’ciani cimene tifunika kukumbukila pankhani ya kumva cisoni ? ( Miy . 14 : 10 ) Ngakhale munthu atafotokoza mmene amvelela , nthawi zina zimakhalabe zovuta kumumvetsetsa . Panthawiyi , nimatonthozedwa poona kuti anzanga nawonso ali na cisoni . ” Junia anati : “ Nikalandila meseji yonilimbikitsa kapena ngati Mkhristu waniitana kuti nikaceze kwawo , nimalimbikitsidwa ngako . Zimenezi zimanicititsa kuona kuti ena amanikonda ndi kuniganizila . ” Dalene anati : “ Nthawi zina alongo akabwela kudzaniona , nimawapempha kuti anipemphelele . Poyamba kupemphela , nthawi zambili amakamba movutikila , koma posakhalitsa mau awo amayamba kumveka amphamvu ndi acidalilo , ndipo pemphelo limene amapeleka limakhala locokela pansi pamtima . Cikhulupililo canga cimalimba kwambili nikaganizila cikondi cawo , nkhawa imene amanionetsa , ndi cikhulupililo cawo . ” Baibo imati : “ Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse , ndipo ilo ndi m’bale amene anabadwila kuti akuthandize pakagwa mavuto . ” M’bale wina anati : “ Mkazi wanga atamwalila , n’nadziŵa kuti tsiku lokumbukila cikwati cathu likadzafika nidzavutika kwambili ndi cisoni , ndipo zinalidi zovuta . Koma abale na alongo ena , amene nanzanga anakonza zakuti tidzakhale na maceza n’colinga cakuti patsikulo nisadzakhale nekha . ” Junia anati : “ Nthawi zambili , kukhala na maceza ndi kupeleka thandizo kwa munthu pamene kulibe zocitika zapadela kumakhala kothandiza kwambili . Kucita zinthu mwanjila imeneyi n’kopindulitsa ndiponso kumatonthoza kwambili . ” Ananicititsa kuona kuti Yehova amanikonda . ” Kodi malonjezo a Yehova amatitonthoza bwanji ? Adzacita zimenezi pamene “ onse ali m’manda acikumbutso adzamva mau ake [ a Yesu ] ndipo adzatuluka . ” ( Yoh . Malemba ena amene amatonthoza anthu ambili ndi Salimo 20 : 1 , 2 ; 31 : 7 ; 38 : 8 , 9 , 15 ; 55 : 22 ; 121 : 1 , 2 ; Yesaya 57 : 15 ; 66 : 13 ; Afilipi 4 : 13 ; na 1 Petulo 5 : 7 . Onani nkhani yakuti “ Muzitonthoza Anthu Amene Aferedwa , Ngati Mmene Yesu Anachitira , ” mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 2010 . “ Sitidziŵa cimene tingakambe , koma timakukondani kwambili . Ife sitingadziŵe bwino - bwino mmene mumvelela , koma Yehova adziŵa ndipo adzapitiliza kukulimbikitsani . Tidzapitiliza kukupemphelelani . ” “ Yehova akulimbitseni panthawi yovuta kwambili imeneyi . ” “ Dziŵani kuti Mulungu akum’kumbukila wokondedwa wanu . Iye sadzamuiŵala ngakhale pang’ono ndipo adzamuukitsa . ” “ Mulungu sanaiŵale nchito za cikhulupililo za wokondedwa wanu , ndipo adzamuukitsa m’Paradaiso . Akadzaukitsidwa , sadzakumananso na mdani wotsiliza , imfa . ” “ Sitingakwanitse kufotokoza mmene cimaŵaŵila ngati munthu amene tinali kum’konda wamwalila . Koma tiyembekezela mwacidwi nthawi pamene Atate wathu wakumwamba adzaukitsa wokondedwa wanu . Pa cisautso cacikulu , Akhristu adzadalila Yehova , osati kudziteteza okha Wofalitsa akulalikila mmodzi mwa oseŵenza m’munda wa maapozi ku Grójec . ( b ) Nanga kuphunzila za lemba limeneli kungatithandize bwanji ? Ndipo cioneka kuti mumlengalenga muli milalang’amba mathililiyoni ambili . Nifuna kuti uzisangalala pa umoyo wako cifukwa ndiwe Mboni yanga . ” ( Ŵelengani Salimo 147 : 8 , 9 . ) Mutsuo anati : “ N’naona kuti Yehova anali pafupi na aliyense wa ife ndi kuti anali kutisamalila . 12 , 13 . ( a ) Kodi tifunika kupewa ciani kuti Mulungu azitithandiza ? Mosiyana ndi ofatsa , “ anthu oipa [ Mulungu ] amawagwetsela pansi . ” Malemba amati : “ Yehova amasangalala ndi anthu amene amamuopa , amene amayembekezela kukoma mtima kwake kosatha . ” 15 - 17 . ( a ) Kodi nthawi zina tingamvele bwanji cifukwa ca mavuto amene timakumana nawo ? Masiku ano , Yehova amatitsogolela kupitila m’Mau ake , Baibo . ( Ŵelengani Salimo 147 : 19 , 20 . ) Kodi wacicepele angaphunzile ciani pamene acita utumiki wa nthawi zonse ? Kodi acicepele afunika kusankha ciani cokhudza tsogolo lawo ? IMWE acicepele mungavomeleze kuti ni cinthu canzelu kudziŵa kumene mufuna kupita mukalibe kuyamba ulendo . Moyo nawonso uli ngati ulendo , ndipo nthawi yabwino yosankha zimene mudzayamba kucita pa umoyo wanu , ndi pamene muli wacicepele . Mudziŵa bwanji kuti Yehova amafuna kuti muzipanga zosankha mwanzelu n’colinga cakuti mudzakhale na tsogolo labwino ? Mlengi wathu ndi “ Mulungu wacikondi ” ndi “ wacimwemwe , ” ndipo analenga anthu “ m’cifanizilo cake . ” ( 2 Akor . 13 : 11 ; 1 Tim . 1 : 11 ; Gen . 1 : 27 ) Ngati mutengela citsanzo ca Mulungu wathu , amene ni wacikondi , mudzakhala na umoyo wacimwemwe . Yesu Khristu anapeleka citsanzo cabwino kwambili kwa inu acicepele . 3 : 4 ) Yesu analinso kuphunzila Malemba kuti alimbitse ubwenzi wake na Yehova . Baibo imati : “ Zolingalila sizikwanilitsidwa ngati anthu sakambilana moona mtima , koma aphungu akaculuka zimakwanilitsidwa . ” Mofanana ndi nchito ina iliyonse , pafunika nthawi kuti mukhale na luso pa nchito imeneyi . Poyamba n’nalibe phunzilo , koma pamene n’nasamukila m’gawo lina , n’napeza maphunzilo ambili m’mwezi umodzi cabe . Mmodzi wa ophunzilawo anayamba kupezeka pamisonkhano . Mwacitsanzo , Jacob wa ku North America , analemba kuti : “ Pamene n’nali na zaka 7 , anzanga ambili m’kilasi anali ocokela ku Vietnam . N’nali kufuna kuwauza za Yehova . Conco , patapita nthawi yocepa n’naganiza zoyamba kuphunzila citundu cawo . Cacikulu cimene cinanithandiza ni kulinganiza nkhani za m’magazini a Nsanja ya Mlonda yacizungu ndi ya Civietinamu . Cinanso , n’napeza anzanga mumpingo wa Civietinamu umene unali pafupi na kwathu . N’takwanitsa zaka 18 , n’nayamba kucita upainiya . Pambuyo pake , n’naloŵa Sukulu Yophunzitsa Baibo ya Abale Osakwatila . Tsopano nitumikila m’kagulu ka Civietinamu , ndipo ndine nekha amene nikutumikila monga mkulu . Anthu ambili ocokela ku Vietnam amadabwa kwambili kuti n’naphunzila citundu cawo . Iwo amanilandila ku nyumba zawo , ndipo ambili amavomela kuti niziphunzila nawo Baibo . Ena apita patsogolo mpaka kufika pa kubatizika . ” — Yelekezelani na Machitidwe 2 : 7 , 8 . Nimakonda kulimbikitsa abale acicepele mumpingo mwathu ndipo nimasangalala kuona mmene akupitila patsogolo mwauzimu . N’tatsiliza maphunzilo a Sukulu Yophunzitsa Baibo ya Abale Osakwatila , ananitumiza ku gawo lina latsopano kumene n’napitiliza kucita upainiya . N’zoona kuti pa anthu amene n’nali kuphunzila nawo Baibo m’gawolo , palibe amene anapita patsogolo kufika pobatizika . Kodi kucita upainiya kungakupatseni bwanji mwayi wocitako mautumiki ena ? M’bale wina dzina lake Kevin anati : “ Kuyambila nili mwana , n’nali na colinga cakuti nikadzakula nidzatumikile Yehova mu utumiki wanthawi zonse . N’takwanitsa zaka 19 , n’nayamba kucita upainiya . Kuti nizipeza zofunika pa umoyo , n’nali kuseŵenza kwa maola ocepa kwa m’bale amene anali kugwila nchito yomanga . N’naphunzila kukhoma mtenje , kuika mawindo ndi zitseko . Pambuyo pake , kwa zaka ziŵili n’natumikila m’gulu la abale amene anali kupeleka thandizo kwa okhudzidwa ndi cimphepo coopsa ca mkuntho . N’tamvela kuti ku South Africa kufunikila anchito omanga , n’nafunsila utumiki umenewu ndipo ananiitana . Kuno ku Africa , timamanga Nyumba ya Ufumu kwa mawiki angapo cabe , ndipo tikatsiliza timapita pa ina . Timakhala pamodzi , kuphunzila Baibo pamodzi , na kuseŵenzela pamodzi . Nimasangalalanso kugwila nchito yolalikila wiki iliyonse pamodzi na abale a pampingo umene tili . Zolinga zimene n’napanga nili mwana zanicititsa kukhala na cimwemwe coculuka kuposa cimene n’nali kuyembekezela . ” Kucita utumiki wa pa Beteli kumabweletsa cimwemwe cifukwa zilizonse zimene munthu ungacite , umacitila Yehova . Kumeneko , n’naphunzila kuseŵenzetsa mashini opulintila , ndipo pambuyo pake n’naphunzila kukonza mapulogilamu a pa kompyuta . Kuno ku Beteli , nimadzionela nekha mmene nchito yopanga ophunzila ikupitila patsogolo padziko lonse . Nimakondwela kutumikila kuno cifukwa zimene timacita zimathandiza anthu kukhala pa ubwenzi na Yehova . ” Yehova amafuna kuti ‘ mugwile mwamphamvu ’ tsogolo lacimwemwe . Ndiyeno , dziikileni zolinga zimene zingam’kondweletse . Iye wakhala akuphunzila zocita za anthu kucokela pamene munthu woyamba analengedwa . Mufunika kucitapo kanthu kuti mucipeze . ” Yesu anati : “ Musamaope amene amapha thupi lokha , amene sangathe kucita zoposa pamenepa . ” Usacite mantha kapena kuopa , pakuti Yehova Mulungu wako ali nawe kulikonse kumene upiteko . ” ( Yos . ( Miy . 26 : 24 , 25 ) Muzimvetsela kwa Yehova na kum’dalila m’zocita zanu zonse . Nkhani yaciŵili idzaonetsa mmene Yehova nthawi zina amacitila zinthu m’njila imene sitinali kuyembekezela . 1 : 7 ) Molingana ndi mlimi , ifenso tifunika kuyembekezela moleza mtima . Tingaphunzile ciani pa citsanzo ca mneneli Mika ? ( Ŵelengani Mika 7 : 1 - 3 . ) Ngati tili na cikhulupililo monga ca Mika , tidzayembekezela Yehova na mtima wonse . Conco , ‘ timapilila zinthu zonse ndi kukhala oleza mtima ndiponso acimwemwe . ’ Abulahamu anafunika kuyembekezela kwa zaka zambili kuti adzukulu ake , Esau na Yakobo abadwe ( Onani palagilafu 9 , 10 ) ( Ŵelengani Aheberi 11 : 8 - 12 . ) Koma ganizilani cabe cimwemwe cimene iye adzakhala naco akadzaukitsidwa m’paradaiso padziko lapansi . Koma Mulungu anali ndi colinga cabwino , kuti apulumutse miyoyo ya anthu ambili ngati mmene akucitila panomu . ” ( Gen . ( b ) Nanga n’ciani cinam’thandiza kuyembekezela moleza mtima ? Mtima wanga ukondwele cifukwa ca cipulumutso canu . ( Ŵelengani 2 Petulo 3 : 9 . ) N’ciani cidzatithandiza kukhala okonzeka kuyembekezela moleza mtima ? Tiphunzilapo ciani pa zimene zinacitikila mtumwi Paulo ku Filipi ? ( Ŵelengani Machitidwe 16 : 8 - 10 . ) Atangofika ku Makedoniya , anaikidwa m’ndende . Mosakayikila , Paulo anadzifunsa kuti : ‘ N’cifukwa ciani Yehova walola zimenezi kunicitikila ? M’malomwake , onse aŵili Paulo na Sila , anayamba “ kupemphela ndi kutamanda Mulungu poimba nyimbo . ” ( Mac . 4 , 5 . ( a ) Kodi zimene zimaticitikila zingalingane bwanji na zimene zinacitikila Paulo ? ( b ) Kodi zinthu zinasintha bwanji pamene Paulo anali m’ndende ? Kodi lomba tidzakambilana ciani ? ( Ŵelengani 1 Petulo 5 : 6 , 7 . ) Timafunika kucita zinthu mogwilizana ndi mapemphelo athu . Anatumiza mngelo amene anapha asilikali 185,000 a Senakeribu pa usiku umodzi cabe . ( a ) Tiphunzilapo ciani pa zimene zinacitikila Yosefe ? 40 : 15 ; 41 : 39 - 43 ; 50 : 20 ) Mosakayikila , Yosefe sanayembekezele kuti Yehova angamuthandize mwanjila imeneyi . Ganizilaninso za Sara , ambuye ake a Yosefe . ( Ŵelengani Yesaya 43 : 10 - 13 . ) Timadziŵa kuti Yehova amatikonda ndipo amafuna kuti zinthu zizitiyendela bwino . N’ciani cingatithandize kuvula umunthu wakale ndi kusauvalanso ? Podzafika mu 1939 , [ m’ndende zozunzilako anthu ] za Nazi munali Mboni za Yehova zokwana 6,000 . ” Ndiponso anthu inu mwayeletsa bwino kwambili sitediyamuyi . Koma koposa zonse , ndinudi gulu locokela m’mitundu yosiyana - siyana . ” Kodi tidzaphunzila ciani m’nkhani ino ? Koma pamene n’napitiliza kucita zaciwelewele , vuto langa lodziona kuti ndine wosafunika linakulila - kulila . ” Sakura anapitiliza khalidwe loipali mpaka pamene anakwanitsa zaka 23 . Iye anati : “ Pang’ono ndi pang’ono , n’nakhala na cizoloŵezi cotamba zamalisece . N’ciani cinathandiza Stephen kuleka kupsa mtima ndi kukamba mau acipongwe ? Iye anati : “ Zinthu zinayamba kuyenda bwino m’banja lathu . Pali pano , Stephen ni mtumiki wothandiza , ndipo mkazi wake wakhala akucita upainiya wa nthawi zonse kwa zaka zambili . Koma malemba amene ananilimbikitsa kusintha ndi Yesaya 55 : 7 , imene imati : ‘ Munthu woipa asiye njila yake , ’ ndi 1 Akorinto 6 : 11 , imene imakamba za anthu amene analeka makhalidwe oipa . Lembali limati : ‘ Ndipo ena mwa inu munali otelo . ’ Kwa zaka zambili , Yehova ananithandiza moleza mtima pogwilitsila nchito mzimu wake woyela kuti nivale umunthu watsopano . ” Tifunikanso kupempha Mulungu kuti atipatse nzelu ndi mphamvu n’colinga cakuti tikwanitse kuseŵenzetsa mfundo za m’Baibo . ( Yos . 1 : 8 ; Sal . 119 : 97 ; 1 Ates . M’nkhani ino , maina ena asinthidwa . Onani mutu 25 m’buku lakuti Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa , Buku Loyamba . ( Ŵelengani Akolose 3 : 10 - 14 . ) Iye anakamba kuti palibe “ Mgiriki kapena Myuda , kudulidwa kapena kusadulidwa , mlendo , Msukuti , kapolo , kapena mfulu . ” ( a ) Kodi atumiki a Yehova afunika kuwaona bwanji anthu ena ? ( Onani pikica kuciyambi . ) ( b ) Nanga pakhala zotulukapo zanji ? Ndiyeno , tsiku lina iye anapezeka pa msonkhano wa Mboni za Yehova . Umadzionela wekha ubale wa padziko lonse ndi mgwilizano wapadela umene tili nawo . ” Tikawaonetsa malemba monga Chivumbulutso 21 : 3 , 4 kapena Salimo 37 : 10 , 11 , 29 m’Baibo yawo ya Cipwitikizi , anali kucita cidwi ndipo nthawi zina anali kucita kugwetsa misozi ya cisangalalo . ” Timamuyamikila ngako Yehova . ” — Ŵelengani Machitidwe 10 : 34 , 35 . Kodi Yesu anapeleka citsanzo canji pankhani yokhala wofatsa ndi woleza mtima ? Monga Yehova anakukhululukilani ndi mtima wonse , inunso teloni . ” Ndiyeno , anawonjezela kuti : “ Mukapitiliza kukhala okondela , mukucita chimo . ” N’cifukwa ciani tifunika kuvala cikondi ? Kuwonjezela apo , cikondi “ n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima ” ndipo “ sicidzikuza . ” Poonetsa kufunika kwa khalidweli , Paulo anakamba kuti popanda cikondi , sembe iye ‘ sali kanthu . ’ Cikondi cimeneci cikutanthauza kuti ife sitinakonde Mulungu , koma iye ndi amene anatikonda ndi kutumiza Mwana wake monga nsembe yophimba macimo athu . ” ( 1 Yoh . Yesu anati : “ Palibe amene ali ndi cikondi cacikulu kuposa ca munthu amene wapeleka moyo wake cifukwa ca mabwenzi ake . ” ( Yoh . Tiyeni tione mmene tingacitile zimenezo . Mtumwi Yohane analemba kuti : “ Ana anga okondedwa , tisamakondane ndi mau okha kapena ndi pakamwa pokha , koma tizisonyezana cikondi ceniceni m’zocita zathu . ” ( 1 Yoh . Koma n’nadzifunsa kuti , ‘ Ningatengele bwanji Yesu pocita zinthu na munthu ameneyu ? ’ Pambuyo poganizila zimene Yesu akanacita , n’nasankha kungoiŵalako nkhaniyo , osalimbana naye . Patapita nthawi , n’namva kuti mnzangayo ali na matenda aakulu , ndipo amavutika kwambili na nkhawa . Conco , n’naona kuti mwina analemba mesejiyo cifukwa covutika maganizo . Kuganizila mmene Yesu anaonetsela cikondi ngakhale pamene anali kunyozedwa , kunanithandiza kunyalanyaza colakwa ca mnzanga wakunchito . ” Pamene iye anacoka kumwamba , “ anasiya zonse zimene anali nazo ” ‘ mpaka kufa ’ cifukwa ca ise . MTENDELE : ‘ Kulolelana m’cikondi ’ kumatithandiza kukhala pa mtendele , umene uli “ monga comangila cotigwilizanitsa . ” ( Aef . Kodi si zoona kuti mtendele umenewu ni wapadela kwambili m’dzikoli , limene ni logaŵikana ? ( Sal . Paulo analemba kuti : “ Cikondi cimamangilila . ” ( 1 Akor . Tsiku lotsatila , anthu anaculuka kwambili pamsonkhanowo cakuti malo anacepa . ” Pa cithunzico panali mau akuti : “ Anakhamukila m’miseu . ” Conco , iwo anali kukwela mahosi kapena kuyenda na mendo masiku angapo kuti akafike kokwelela sitima , imene ikanawanyamula kupita kumene kukucitikila msonkhano . Ku Mexico , anthu amene anapezeka pa Cikumbutso mu 2016 anali 2,262,646 . Buku la Mateyu limafotokoza kwambili zocitika zokhudza Yosefe . 1 , 2 . ( a ) Ni mavuto ati amene amabwela cifukwa ca kusadziletsa ? Tiyenelanso kupempha nzelu kwa Mulungu kuti tikambe na kucita zinthu mwanzelu . Mungakonzekele bwanji kukaniza ziyeso ? N’ciani cinacitikila m’bale wina ? Kodi makolo angathandize bwanji ana awo kukhala odziletsa ? Kodi mungathandize bwanji ana anu kukhala odziletsa ? ( Ŵelengani Ekisodo 34 : 5 - 7 . ) ( b ) N’cifukwa ciani kuphunzila zimene Baibo imakamba ponena za khalidwe la cifundo n’kofunika ? ( a ) N’cifukwa ciani Yehova anatumiza angelo ku Sodomu ? ( Ŵelengani Ekisodo 22 : 26 , 27 . ) Baibo imati : “ Yehova Mulungu wa makolo awo anapitiliza kuwatumizila macenjezo kudzela mwa amithenga ake . Anawatumiza mobwelezabweleza cifukwa ankamvela cisoni anthu akewo ndiponso malo ake okhala . ” “ Anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambili . ” Koma nchito yathu ni kuyesetsa kuthandiza anthu mmene tingathele . 3 : 8 ) Tanthauzo limodzi la liu lakuti cifundo ni “ kuvutikila pamodzi . ” “ Limba mtima , ugwile nchitoyi mwamphamvu . Kodi acicepele na makolo awo angaonetse bwanji kulimba mtima ? 1 , 2 . ( a ) Kodi Solomo anapatsidwa nchito iti yofunika kwambili ? Kuti akwanitse nchitoyo , Solomo anafunika kukhala wolimba mtima ndi kugwila nchito mwamphamvu . Kodi Solomo ayenela kuti anaphunzila ciani kwa atate wake pankhani ya kulimba mtima ? ( Ŵelengani 1 Mbiri 28 : 20 . ) . Kodi kulimba mtima kwa Yesu kunawathandiza bwanji atumwi ? ( Ŵelengani 2 Timoteyo 1 : 7 . ) Tsopano tiyeni tikambilane mmene tingaonetsele kulimba mtima m’banja ndi mumpingo . ( b ) Kodi acicepele angatengele bwanji citsanzo ca Mose ? M’zaka 100 zoyambilila , wacicepele Timoteyo anayesetsa kukwanilitsa zolinga zake zauzimu . Iye analemba kuti : “ Pamene n’nali wamng’ono , n’nali wamanyazi kwambili . Maka - maka kugogoda pa makomo a anthu osawadziŵa mu ulaliki , zinali kunivuta kwambili . ” Mothandizidwa na makolo ake ndi ena mumpingo , mlongo wacicepeleyu anakwanilitsa colinga cake cokhala mpainiya wanthawi zonse . Kodi malemba awa : Salimo 37 : 25 ndi Aheberi 13 : 5 , angathandize bwanji makolo ? ( Ŵelengani Salimo 37 : 25 ; Aheberi 13 : 5 . ) M’bale wina amene ali ndi ana aŵili anati : “ Makolo ambili amacita khama ndi kuwononga cuma cawo pothandiza ana awo kuti akhale akatswili a zamaseŵela ndi zosangalatsa zina , ndiponso kuti akhale ophunzila kwambili . Niona kuti ni cinthu canzelu kwambili kucita khama ndi kugwilitsila nchito cuma cathu pothandiza ana kukwanilitsa zolinga zimene zidzawathandiza kukhalabe pa ubwenzi wabwino na Yehova . Timasangalala kwambili kuona ana athu akukwanilitsa zolinga zawo zauzimu , ndipo zimakhala ngati kuti nafenso tikulandila nawo madalitso . ” Fotokozani njila zina zimene tingaonetsele kulimba mtima mumpingo . ( Ŵelengani Tito 2 : 3 - 5 . ) ( a ) Kodi abale obatizika angaonetse bwanji kulimba mtima ? ( Ŵelengani Afilipi 2 : 13 ; 4 : 13 . ) Tikukulimbikitsani abale nonse obatizika kuti mukhale olimba mtima , ndipo mugwile nchito mwamphamvu pothandiza mpingo . Conco , ‘ limbani mtima , ndipo mugwile nchito mwamphamvu . ’ 1 , 2 . ( a ) Kodi umoyo ukanakhala bwanji kukanakhala kuti kulibe Baibo ? Mtumwi Petulo anagwila mau a pa Yesaya 40 : 8 . ( Ŵelengani 1 Petulo 1 : 24 , 25 . ) ( Ŵelengani Chivumbulutso 14 : 6 . ) M’mabaibo amene anapulintiwa pambuyo pake , dzina lakuti “ AMBUYE , ” lolembedwa m’zilembo zazikulu , limapezekanso m’mavesi ena a Malemba Acigiriki Acikhristu . N’cifukwa ciani timayamikila kuti tili na Baibulo la Dziko Latsopano ? ( b ) Kodi Septuagint ya Cigiriki n’ciani ? ( Ŵelengani Salimo 119 : 162 - 165 . ) ( Ŵelengani Yesaya 48 : 17 , 18 . ) Onani nkhani yakuti “ Kodi Muyenera Kuphunzira Chiheberi ndi Chigiriki ? ” mu Nsanja ya Olonda ya November 1 , 2009 . Pa April 3 , 2017 , nyumba yosungilamo Mabaibo akale na zinthu zina zakale zokhudzana ndi Baibo , inatsegulidwa ku likulu lathu ku Warwick , mumzinda wa New York , m’dziko la United States . M’nyumba imeneyi , muli malo oonetselapo zinthu zakale zacikhalile . Pamalowo m’polemba kuti , “ Baibo na Dzina la Mulungu . ” Tikuitanani kuti mukabwele kukaona nyumba yosungilamo zinthu zakale imeneyi , ndi malo ena osungilako zinthu zakale zokhudzana ndi Baibo , amene ali ku likulu lathu . Pitani pa www.jw.org ndi kutumiza pempho lanu lodzaona malo . Yendani pa ZOKHUDZA IFE > MAOFESI NDI KUONA MALO . ( Ŵelengani Aefeso 5 : 15 , 16 . ) Anaŵelenga 2 Akorinto 1 : 3 , 4 , imene imati : “ Tate wacifundo cacikulu ndi Mulungu amene amatitonthoza m’njila iliyonse , . . . amatitonthoza m’masautso athu onse . ” Kodi abale amene amaphunzitsa papulatifomu ali na udindo wanji ? Ndithudi , timamuyamikila kwambili Yehova cifukwa cotipatsa Mau ake , Baibo ! Onani bokosi yakuti “ Mmene Anasinthila . ” Fotokozani lemba , pelekani fanizo , ndi kumveketsa bwino mmene tingaseŵenzetsele mfundo yake “ Zinthu zinasintha pambuyo pa zaka 15 kucokela pamene n’nabatizika . Tsiku lina , m’bale pokamba nkhani m’Nyumba ya Ufumu . . . , anaŵelenga lemba la Yakobo 1 : 23 , 24 . Mavesi amenewa amayelekezela Mau a Mulungu na gilasi . Mau a Mulungu angatithandize kuti tizidziona monga mmene Yehova amationela . N’nayamba kuzindikila kuti mmene nimadzionela si mmene Yehova amandionela . Koma poyamba sin’nakhutile na mfundo imeneyi . N’nali kuonabe kuti n’zosatheka Yehova kunikonda . “ Patapita masiku ocepa , n’naŵelenga lemba limene linasinthalatu umoyo wanga . Linali lemba la Yesaya 1 : 18 , pamene pali mau a Yehova akuti : ‘ Bwelani tsopano anthu inu . Tiyeni tikambilane . . . Ngakhale macimo anu atakhala ofiila kwambili , adzayela kwambili . ’ N’namvela monga kuti Yehova akamba na ine kuti : ‘ Bwela Victoria , tiye tikambilane . Nimakudziŵa , nimadziŵanso zolakwa zako , na mtima wako , ndipo nimakukonda . ” “ Tsiku limenelo sin’nagone . N’nali kukaikilabe kuti Yehova anganikonde . Kenako , n’nayamba kuganizila za nsembe ya dipo la Yesu . Nthawi imeneyo , n’nazindikila kuti Yehova wakhala akunilezela mtima kwa nthawi yaitali . Anali kunicitila zinthu zambili zoonetsa kuti amanikonda . Koma , zinali monga kuti ine nikumuuza kuti : ‘ Cikondi canu n’cosakwanila kwa ine . Nsembe ya Mwana wanu siingakwanitse kuphimba macimo anga . ’ Zinali ngati kuti nikukana nsembe imene Yehova anapeleka na kuibweza kwa iye . Koma cifukwa cosinkha - sinkha za mphatso ya dipo imeneyi , n’nayamba kuona kuti Yehova amanikondadi . ” Nkhani izi zidzafotokoza masomphenya a Zekariya a namba 6 , 7 , na 8 . Coyamba , lekani n’kuuzeni mmene umoyo wanga unalili poyamba . N’NABADWILA m’tauni ya Hemsworth mu 1923 , ku Yorkshire , m’dziko la England . Caka cotsatila , ine na mlongo Mary Henshall tinaikiwa kukhala apainiya apadela . Tinatumiziwa ku gawo limene kunalibe ofalitsa , m’dela lochedwa Cheshire . M’maŵa , tinali kudya cakudya cogwila pamimba . Mlongosi wanga na mkazi wake , Lottie , anali kale ku Northern Ireland , kumene anali kutumikila monga apainiya apadela . Mu 1952 , tonse anayi tinacitila pamodzi msonkhano wacigawo ku Belfast . Conco , tinafunafuna nyumba yokhalamo koma sitinaipeze cakuti usikuwo tonse tinagona m’motoka . Cokondweletsa n’cakuti alimi anali kutikomela mtima potilola kuika kalavani yathu pafamu pawo . Kukamba zoona , tinali kukondwela maningi m’nchito yadela . Mu 1965 , m’dziko la Ireland munacitika msonkhano woyamba wa maiko . Panapezeka anthu 3,948 , ndipo okwana 65 anabatizika . Arthur akupeleka moni kwa M’bale Nathan Knorr atangofika pamsonkhano wacigawo wa mu 1965 Mu 1983 , Arthur atulutsa buku lakuti Buku Langa la Nkhani za M’baibo la Cigaeliki Mu 2011 , zinthu zinasintha kwambili mu umoyo wathu pamene ofesi ya nthambi ya Britain ndi ya Ireland zinaphatikiziwa pamodzi . M’zaka zapitazi , nakhala nikupsinjika maganizo ndi kuvutika na cisoni . Arthur anali kunilimbikitsa nthawi zonse . Koma mavuto onse amene napitamo , anicititsa kuyandikila kwambili kwa Yehova . “ Tisamakondane ndi mau okha kapena ndi pakamwa pokha , koma tizisonyezana cikondi ceni - ceni m’zocita zathu . ” — 1 YOH . 3 : 18 . Kodi “ cikondi copanda cinyengo ” cimatanthauza ciani ? Kodi Yehova waonetsa bwanji cikondi copanda dyela kwa anthu ? Iye analenga dziko kuti tikhalepo kwamuyaya . ( Yak . 2 : 21 ) Molingana ndi amuna okhulupilika amenewa , na ise tifunika kuonetsa cikondi , ngakhale kuti nthawi zina zingakhale zovuta . 6 , 7 . ( a ) Kodi “ cikondi copanda cinyengo ” cimatanthauza ciani ? ( Ŵelengani Mateyu 6 : 1 - 4 . ) Kodi cikondi ceni - ceni tingacionetse bwanji poceleza ena ? ( Ŵelengani 1 Yohane 3 : 17 . ) ( Ŵelengani Aroma 12 : 17 , 18 . ) Tingaonetse bwanji kuti takhululuka na mtima wonse ? Kodi “ lupanga ” limene Yesu anakamba kuti adzabweletsa n’ciani ? N’ciani cingakuthandizeni kukhalabe wokhulupilika kwa Yehova ngati abululu anu sagwilizana ndi kulambila koona ? 3 , 4 . ( a ) Kodi ziphunzitso za Yesu zimawakhudza bwanji anthu ? Yesu anati : “ Musaganize kuti ndinabweletsa mtendele padziko lapansi , sindinabweletse mtendele koma lupanga . Ndinabwela kudzacititsa munthu kutsutsana ndi bambo ake , mwana wamkazi kutsutsana ndi mayi ake , ndiponso mtsikana wokwatiwa kutsutsana ndi apongozi ake aakazi . Kodi Akhristu angaphunzitse bwanji ana awo kuti azilemekeza kholo losakhulupilila ? M’malomwake , afotokozeleni kuti munthu aliyense ali na ufulu wosankha kutumikila Yehova kapena ayi . Baibo imakamba kuti : “ Nthawi zonse mau anu azikhala acisomo . ” ( Ŵelengani 1 Petulo . Mungacite ciani ngati mumadela nkhawa kuti zocita zanu zidzakhumudwitsa abululu anu ? Amodzi mwa malo ocitilapo ulaliki wapoyela ku Lagos , mzinda wokhala na anthu ambili mu Africa . Kodi zinthu panthawiyo zinali bwanji pakati pa Aisiraeli ? ( Ŵelengani Zekariya 1 : 3 , 4 . ) Caputa 5 ya buku la Zekariya imayamba na masomphenya ocititsa cidwi kwambili . ( Ŵelengani Zekariya 5 : 1 , 2 . ) 8 - 10 . ( a ) Kodi lumbilo n’ciani ? Tiphunzilapo ciani pa masomphenya a namba 6 a Zekariya ? ( Ŵelengani Zekariya 5 : 5 - 8 . ) ( Ŵelengani Zekariya 5 : 9 - 11 . ) Kodi mumamvela bwanji mukaganizila za nchito yaikulu kwambili yomanga imene icitika masiku ano ? ( Ŵelengani Zekariya 6 : 1 - 3 . ) Yehova akali kuseŵenzetsa angelo poteteza na kulimbikitsa anthu ake 7 , 8 . ( a ) Kodi mapili aŵili amkuwa aimila ciani ? ( b ) N’cifukwa ciani ni amkuwa ? M’Baibo , mapili nthawi zina amaimila maufumu , kapena maboma . Kodi okwela pa magaleta n’ndani ? Nanga anapatsiwa nchito yanji ? ( Ŵelengani Zekariya 6 : 5 - 8 . ) ( Ŵelengani Zekariya 6 : 9 - 12 . ) Kodi Yehova anawatsimikizila za ciani Ayuda ? Yehova sadzaiŵala ngakhale pang’ono cikondi cimene timamuonetsa ! ATATE ake John anabatizika n’kukhala Mboni ya Yehova cakumapeto kwa zaka za m’ma 1950 , m’tauni yaing’ono ku Gujarat , m’dziko la India . Mlongoyo anaona kuti John anali atadziceka pacala . Iye anapita kwa wansembe wa ku chechi kwawo kukam’funsa mafunso amodzi - modzi amene anakambilana ndi mlongo uja . Ni pati m’Baibo pamene pamakamba kuti Yesu si Mulungu ? Nanga ni pati pamene pamakamba kuti sitifunika kulambila Mariya ? Tingaphunzilepo zambili pa makonzedwe a mizinda yothaŵilako ya ku Isiraeli wakale . Kodi kuimba n’kofunika bwanji pa kulambila koona ? Koma mau a m’nyimbo zoimba pakamwa amacititsa munthu kumvela bwino . ” ( b ) Kodi tiyenela kuimba bwanji nyimbo zotamanda Yehova ? Ŵelengani mau a m’nyimboyo mokweza ndi mwamphamvu . ( a ) N’ciani cina cimene tingacite kuti tiziimba mwamphamvu na mokweza ? ( a ) Kodi pamsonkhano wa pacaka wa mu 2016 panalengezedwa ciani ? Nyimbo zimenezi muziziphunzila pa kulambila kwanu kwa pabanja ( Onani palagilafu 18 ) ( Ŵelengani Numeri 35 : 24 , 25 . ) Pokumbukila zimene zinacitikazo , iye anati : “ Kukamba zoona , n’nali kucita mantha kuulula chimo langa kwa akulu . Iye analemba kuti : “ Taonani zimene cisoni cogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu cimeneci cakucitilani . Cakucititsani kukhala akhama kwambili , cakucititsani kudziyeletsa , kuipidwa , mantha , kufunitsitsa kulapa , kudzipeleka , ndiponso kukonza colakwaco . ” ( 2 Akor . Nkhani yanga itasamalidwa , n’naleka kudziimba mlandu . Ngati Mulungu wakukhululukila chimo , ndiye kuti latha . Monga mmene Yehova anakambila , amacotsa zolakwa zathu na kuziika kutali kwambili na ise cakuti sitingakwanitse kuzionanso . ” N’cifukwa ciani muyenela kuthaŵila kwa Yehova ? Tingatengele bwanji cifundo ca Yehova ngati ena atilakwila ? 1 , 2 . ( a ) Kodi Yesu anali kuciona bwanji Cilamulo ca Mulungu ? ( b ) Kodi zimenezi zitiphunzitsa ciani za Yehova ? ( Ŵelengani Machitidwe 20 : 26 , 27 . ) ( Ŵelengani Numeri 35 : 20 - 24 . ) Conco pitani mukaphunzile tanthauzo la mau akuti , ‘ Ndikufuna cifundo , osati nsembe . ’ Cifukwa ine sindinabwele kudzaitana anthu olungama , koma ocimwa . ” ( Mat . Iwo sanabwele kunyumba kwa Mateyu kudzadya cakudya cabe . Pa zimene taphunzila zokhudza mizinda yothaŵilako , ni mfundo ziti zimene mufuna kuseŵenzetsa mu umoyo wanu ? Alongo aŵili akulalikila uthenga wa m’Baibo kwa munthu wamalonda m’tauni ya Tipitapa Ni malangizo anji amene mtumwi Paulo anapeleka ponena za maganizo a anthu a m’dzikoli ? Chulani citsanzo ca maganizo a dziko na kufotokoza mmene tingapewele kutengela maganizo aconco . Samalani : mwina wina angakugwileni ngati nyama , mwa nzelu za anthu ndi cinyengo copanda pake , malinga ndi miyambo ya anthu , malinganso ndi mfundo zimene zili maziko a moyo wa m’dzikoli , osati malinga ndi Khristu . ” “ Ningakhalebe munthu wabwino popanda kukhulupilila Mulungu . ” “ Munthu angakhale wacimwemwe olo kuti sali m’cipembedzo . ” Lamulo la Mulungu n’lakuti mwamuna na mkazi okwatilana ndiwo okha ayenela kugonana . Tsopano ngati diso lako lakumanja limakucimwitsa , ulikolowole ndi kulitaya . ” ( Mat . Paja Yesu anati : “ Kapolo sangatumikile ambuye aŵili , pakuti adzadana ndi mmodzi ndi kukonda winayo , kapena adzakhulupilika kwa mmodzi ndi kunyoza winayo . ( Ŵelengani 1 Atesalonika 2 : 13 , 19 , 20 . ) “ Anthu angakwanitse kuthetsa mavuto awo . ” Mungacite ciani kuti nonse m’banja lanu mukapeze mphoto ? ( b ) N’ciani cimatithandiza kuyang’anabe pa mphoto ? Kodi tingadziteteze bwanji pa zocitika zimene zingatiike pa ciyeso ? Kuti tithetse zilakolako zoipa , tifunika kupewa zosangalatsa zoipa . Pitilizani kulolelana ndi kukhululukilana ndi mtima wonse , ngati wina ali ndi cifukwa codandaulila za mnzake . Monga Yehova anakukhululukilani ndi mtima wonse , inunso teloni . ( Ŵelengani Mlaliki 7 : 21 , 22 . ) 10 , 11 . ( a ) N’cifukwa ciani nsanje ni yoopsa ? Mau a Mulungu amati : “ Cikondi n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima . 23 : 16 - 18 ) Na ise tiyenela kukhala okoma mtima ndi acikondi ngati Yonatani . Inu amuna , musaleke kukonda akazi anu ndipo musamawapsele mtima kwambili . Ananu , muzimvela makolo anu pa zinthu zonse , pakuti kucita zimenezi kumakondweletsa Ambuye . Inu abambo , musamakwiyitse ana anu , kuti angakhale okhumudwa . ” ( Akol . Kodi mwamuna wacikhristu ayenela kucita ciani ngati mkazi wake amene si Mboni samulemekeza ? Mau a Mulungu amati : “ Aliyense wosalankhulapo mau ake ndi wodziŵa zinthu , ndipo munthu wozindikila amakhala wofatsa . ” Nkhani zimenezi zidzalimbitsa cikhulupililo canu cakuti akufa adzauka . 11 : 11 . Ni nkhani za m’Baibo ziti zimene zinacititsa Marita kukhulupilila kuti akufa adzauka ? Mofanana na Marita , kodi imwe muyembekezela cocitika cokondweletsa citi cam’tsogolo ? Koma anakamba kuti , “ Ndikudziŵa kuti adzauka . ” 17 : 8 - 16 ) Patapita nthawi , mwana wake anadwala mpaka kufa . Mulungu anamvela pemphelo la Eliya , ndipo mwanayo anakhalanso na moyo . ( Ŵelengani 1 Mafumu 17 : 17 - 24 . ) ( Ŵelengani 2 Mafumu 4 : 32 - 37 ) Mzimayiyo ayenela kuti anakumbukila pemphelo la Hana , mkazi amene poyamba anali wosabeleka . Kodi Petulo anam’thandiza bwanji mlongo wacikhristu amene panthawiyo anali atamwalila ? Tsiku lina , mtumwi Paulo anali pa msonkhano m’cipinda capamwamba ku Torowa , kumene manje ni kumpoto ca kum’madzulo kwa dziko la Turkey . Mnyamata wina dzina lake Utiko anali kumvetsela atakhala pawindo . 13 : 14 - 16 ; 18 : 18 ; Aroma 4 : 17 , 18 ) Komanso , Yehova anakamba kuti mbeuyo ‘ idzacokela mwa Isaki . ’ ( Gen . ( Ŵelengani Aheberi 11 : 17 - 19 . ) 89 : 48 ) Koma izi sizitanthauza kuti Mulungu angalephele kuukitsa munthu wakufa . ( Ŵelengani Yobu 14 : 13 - 15 . ) ( b ) N’cifukwa ciani cikhulupililo cakuti akufa adzauka n’cofunika kwambili ? Koma kodi mungachule ciyembekezo ca kuuka kwa akufa monga cimodzi mwa zikhulupililo zanu zofunika ngako ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 15 : 12 - 19 . ) Komabe , tidziŵa kuti Yesu anaukitsidwa . Kodi ulosi wa mu Salimo 118 unakwanilitsika bwanji pa Yesu ? ‘ Omanga nyumba anam’kana ’ Mesiya ( Onani palagilafu 7 ) Kodi Yesu anakhala bwanji “ mwala wofunika kwambili wapakona ” ? Popeza kuti Yesu anakaniwa ndipo anaphedwa , kodi zikanatheka bwanji kuti iye akhale “ mwala wofunika kwambili wapakona ” ? ( a ) Kodi lemba la Salimo 16 : 10 linalosela ciani ? Simudzalola kuti wokhulupilika wanu aone dzenje . ” ( Ŵelengani Machitidwe 2 : 29 - 32 . ) ( Ŵelengani Machitidwe 2 : 33 - 36 . ) ( Ŵelengani Machitidwe 13 : 32 - 37 , 42 . ) Inde , pali zinthu zina zokhudza “ nthawi kapena nyengo zimene Atate waziika pansi pa ulamulilo wake . ” ( Mac . 1 : 6 , 7 ; Yoh . Paulo analemba kuti , “ Khristu anaukitsidwa kwa akufa , n’kukhala cipatso coyambilila ca amene akugona mu imfa . ” N’ciani cidzacitikila ena mwa odzozedwa pa nthawi ya kukhalapo kwa Khristu ? Pakuti ngati timakhulupilila kuti Yesu anafa ndi kuukanso , ndiye kuti amenenso agona mu imfa . . . Mulungu adzawasonkhanitsa kuti akhale naye limodzi . . . Ife amoyofe amene tidzakhalapo pa nthawi ya kukhalapo kwa Ambuye , sitidzakhala patsogolo pa amene agona mu imfa . Cifukwa Ambuye mwini adzatsika kumwamba , ndi mfuu yolamula . . . Ndipo amene anafa mwa Khristu adzauka coyamba . Odzozedwa amene adzakhala na moyo pa nthawi ya cisautso cacikulu ‘ adzatengedwa m’mitambo . ’ Ukabwelanso , nidzakuthyola miyendo . ” N’nabadwa pa July 29 , 1929 , ndipo n’nakulila m’mudzi wina umene uli m’cigawo ca Bulacan , ku Philippines . N’nali kukonda kuŵelenga Baibo , maka - maka mabuku anayi a Uthenga Wabwino . Kucita izi kunanisonkhezela kutsatila citsanzo ca Yesu . — Yoh . 10 : 27 . Ca panthawi imeneyo , makolo anga ananiuza kuti nibwelele ku nyumba . Wacikulile wina wa Mboni anafika pa nyumba pathu , ndipo anatifotokozela zimene Baibo imakamba ponena za “ masiku otsiliza . ” ( 2 Tim . 3 : 1 - 5 ) Iye anatipempha kuti tikapezekepo pa phunzilo la Baibo m’mudzi wina wapafupi . Madzulo a tsikulo , tinakambilana kwambili nkhani zokhudza Baibo . Ine n’nayankha kuti , “ Inde , nifuna . ” N’nali kufuna ‘ kutumikila Ambuye wathu , Khristu , monga kapolo . ’ ( Akol . 3 : 24 ) Conco , pa February 15 , 1946 , ine na mnzanga wina tinabatizika mu mtsinje wina wapafupi . Ndiyeno , banja la m’bale Cruz linanipempha kuti nikakhale nawo ku Angat . Nkhaniyo anaikamba m’Cizungu . M’mamaŵa , n’nali kuthandizila nchito yophika cakudya . Pamene tinatsiliza maphunzilo a Giliyadi , n’natumiziwa ku Bronx , mu mzinda wa New York , kukatumikila monga mpainiya wapadela wogwilizila . Wiki yotsatila , tinapita kukacezela mpingo wa pa cisumbu ca Rapu Rapu . Tinafika mpaka pogula malo a munthu uja amene anakamba kuti , “ Ise Machainizi sitigulitsa malo . ” Zikakhala conco , dzilalo lingayambe kukulila m’cubu yopita ku cibalilo , ( monga mimba yokhala pa malo olakwika ) , kapena lingayende n’kukaloŵa m’cibalilo . Komabe , akatswili amakamba kuti zaconco sizicitika - citika . Buku lofalitsidwa na bungwe lina la zaumoyo ku Britain linati : “ Ma IUD okhala na kopa yambili ni odalilika ngako cakuti ciŵelengelo ca azimayi amene satenga mimba ngati amaseŵenzetsa njilayi cimapitilila 99 pelesenti . Izi zitanthauza kuti ciŵelengelo ca azimayi amene angatenge mimba pa caka ngati aseŵenzetsa ma IUD aconco sicifika ngakhale 1 pelesenti . Koma ma IUD okhala na kopa yocepa , amakhalanso ocepelako mphamvu . ” — England’s National Health Service . ( a ) Kodi ‘ kukhulupilila pambuyo pokhutila nazo ’ kumatanthauzanji ? ( b ) Tidziŵa bwanji kuti Timoteyo anakhutila na uthenga wabwino wokamba za Yesu ? Kukamba zoona , timakhalako na nkhawa ngati iye avomeleza zilizonse popanda kufunsa mafunso . ” Kodi zimene Baibo imakamba pankhaniyi amazikhulupilila ? N’ciani cina cofunika pophunzitsa ana anu ? Stephanie , amene ni kholo la ana atatu , anati : “ Kucokela pamene ana anga anali aang’ono , nakhala nikudzifunsa kuti , ‘ Kodi nimawauza ana anga cifukwa cake ine nimakhulupilila kuti Yehova aliko , amatikonda komanso kuti mfundo zake n’zabwino ? Kodi ana anga amaona kuti ine nimam’kondadi Yehova ? ’ Siningayembekezele ana anga kukhulupilila zinthu zimene ine sinizikhulupilila . ” Baibo imakamba kuti “ ucitsilu umakhazikika mumtima mwa mwana . ” ( Miy . 2 : 12 ) Kucita zinthu mwanjila imeneyi kumaonetsa kuti ali na nzelu zimene n’zofunika kuti akapulumuke . Kodi makolo angathandize bwanji ana awo kukhala na ‘ nzelu zowathandiza kuti akapulumuke ’ ? Pitani pa peji ya Chichewa ya jw.org , na kuona pa ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > ZOKUTHANDIZANI POPHUNZIRA BAIBULO . Kodi mungakonze bwanji cipulumutso canu ? Ena mwa iwo analeledwa na makolo amene ni Mboni . Koma pambuyo pa zaka zingapo , pamene cilakolako cake cakugonana cikhala camphamvu kwambili , angayambe kukayikila ngati kumvela malamulo a Yehova n’kwabwino nthawi zonse . ” ( b ) Kodi tiphunzilapo ciani pa lemba la Afilipi 4 : 11 - 13 ? Kodi kukonza cipulumutso canu “ mwamantha ndi kunjenjemela ” kutanthauza ciani ? Ni zida ziti zimene zimakuthandizani pa phunzilo lanu laumwini ? Yesu anati : “ Palibe munthu angabwele kwa ine akapanda kukokedwa ndi Atate amene anandituma ine . ” ( Yoh . Nimaona kuti na ine nifunika kukamba momasuka nanzanga . Conco , mkati mokambilana nkhani inayake , nimakambako tumau monga twakuti , ‘ Tsiku lina pamene n’nali kuphunzitsa anthu Baibo , . . . ’ Kenako , nimapitiliza na nkhaniyo . Olo kuti nkhani imene tinali kukambilana siinali yokhudzana na Baibo , nthawi zambili anzanga amacita cidwi ndipo amafuna kudziŵa zimene nimacita pophunzitsa anthu Baibo . Pamene niseŵenzetsa njila imeneyi kaŵili - kaŵili , m’pamenenso zimakhala zosavuta kulalikila . Ndipo nikatelo , nimamvela bwino ngako ! ” M’malomwake , anayamba kuganizila kuti : “ Acicepele ambili sadziŵa zambili zokhudza Mboni za Yehova . Conco , zimene timacita zingapangitse kuti amvetsele uthenga wathu kapena ayi . Bwanji ngati timacita manyazi na mantha , kapena ngati sitimasuka pofotokoza zimene timakhulupilila ? Ndiye kuti iwo angayambe kuona kuti sitinyadila kukhala a Mboni za Yehova . Mwina angafike mpaka potinyoza cifukwa coona kuti timacita zinthu modzikayikila . Koma ngati tikamba momasuka na molimba mtima pofotokozela anzathu zimene timakhulupilila , monga kuti tikuceza nawo cabe , iwo angayambe kutilemekeza . ” Yesu anati : “ Ngati munthu akufuna kunditsatila , adzikane yekha ndi kunyamula mtengo wake wozunzikilapo ndipo anditsatile mosalekeza . ” ( Mat . Ni mfundo yanji imene tingaphunzilepo pa Yesaya 40 : 26 ? Palibe munthu amene angakwanitse kuŵelenga nyenyezi zonse kumwamba . Tidziŵa bwanji kuti Yehova angakwanitse kutipatsa mphamvu zotithandiza kupilila mavuto ? Ndipo anapitiliza kuti : “ Mudzatsitsimulidwa , pakuti goli langa ndi lofewa ndipo katundu wanga ndi wopepuka . ” ( Mat . Koma kodi timamvela bwanji tikabwelako ? Nkhaniyo inakambiwa mogwila mtima na mwaubwenzi cakuti n’nakhudzidwa kwambili mpaka kugwetsa misozi . N’nakumbutsidwa kuti kupezeka pa misonkhano n’kofunika ngako . ” Kodi mtumwi Paulo anatanthauzanji pamene analemba kuti : “ Pamene ndili wofooka , m’pamene ndimakhala wamphamvu ” ? Iye anaimba kuti : “ Ndi thandizo lanu , ndingathamangitse gulu la acifwamba . Ndi thandizo la Mulungu wanga ndingakwele khoma . ” Kapena tidzatsatila malangizo anzelu a m’Baibo akuti tiyenela kuthetsa nkhani mwamsanga ? ” Ngati zokambilana zanu sizinayende bwino kweni - kweni , yesani kusakila mpata wina wabwino wokakamba naye kuti mukhazikitse mtendele . Pakuti dzanja lanu linali kundilemela usana ndi usiku . ” Ndipo inu munandikhululukila zolakwa zanga ndi macimo anga . ” ( Sal . ( 4 ) Kodi kudzakhala Cikumbutso cothela ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 13 : 5 . ) ( Ŵelengani Yohane 3 : 16 ; 17 : 3 . ) ( a ) Kodi Yesu anapemphelela ciani pa tsiku limene anayambitsa Mgonelo wa Ambuye ? ( b ) N’ciani cimaonetsa kuti Yehova anayankha pemphelo la Yesu ? ( Ŵelengani Yohane 17 : 20 , 21 . ) ( Ŵelengani Ezekieli 37 : 15 - 17 . ) Kodi tingalimbitse bwanji mgwilizano pakati pa anthu a Mulungu ? Tingaonetse bwanji kuti ‘ timalolelana m’cikondi ’ ? Tidziŵa bwanji kuti kudzakhala Cikumbutso cothela ? Abale aŵili na azikazi awo akupakila mabuku m’ndeke ku Riberalta , m’cigawo ca Beni . N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizim’patsako cuma cathu olo kuti zonse ni zake ? Kodi gulu la Mulungu limaseŵenzetsa bwanji zopeleka masiku ano ? N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tizim’patsako cuma cathu olo kuti zonse ni zake ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 8 : 18 - 21 . ) Zopeleka zanu zimathandiza pa nchito ya padziko lonse ( Onani palagilafu 14 - 16 ) Mwa ici , nthawi zina timadziona monga tili kwa tekha , ndipo timaiwala zinthu zambili zimene Yehova akucita m’gulu lake . Koma tikaonelela mapulogilamu a JW Broadcasting , timakumbukila kuti tili m’gulu la abale a pa dziko lonse . Abale na alongo athu okondedwa amakondwela ngako na JW Broadcasting . Nthawi zambili amakamba kuti akaonelela mapulogilamu apamwezi , amamvela kuti ali pafupi na abale a m’Bungwe Lolamulila . Tsopano amanyadila kwambili kukhala m’gulu la Mulungu . ” ( Ŵelengani Miyambo 11 : 24 , 25 . ) Yesu anati : “ Uzikonda mnzako mmene umadzikondela wekha . ” Amene amakonda mkazi wake amadzikonda yekha , pakuti palibe munthu anadapo thupi lake , koma amalidyetsa ndi kulikonda . ” ( Aef . Tingapewe bwanji kukhala odzikonda ? Paulo analemba kuti anthu adzakhala “ okonda ndalama . ” Munthuyo anatenga kacikwama kake , na kutulutsamo ndalama . Kodi Aguri analemba ciani ponena za cuma na umphawi ? Iye anafotokoza kuti : “ Kuti ndisakhute kwambili n’kukukanani kuti : ‘ Kodi Yehova ndani ? ’ ” Anali kukonda kukamba kuti : ‘ Ine nimaseŵenzela bwana wabwino ngako ! ’ Koma popeza tonse lomba ndise apainiya , timaseŵenzela Bwana mmodzi , Yehova . ” Tingapewe bwanji kukhala okonda ndalama ? Koma imatanthauza kuti sam’konda ngakhale pang’ono . ” Tingapewe bwanji kukhala okonda zosangalatsa ? ( Ŵelengani 2 Timoteyo 3 : 1 - 5 , 13 . ) 3 : 12 ) Komanso , timadziŵa kuti cikondi “ sicidzitama , sicidzikuza . ” N’nali kuona kuti amanikonda , ndipo zimenezo zinanilimbikitsa kuti nizicita zinthu zowakondweletsa . ” ( Ŵelengani Yohane 13 : 34 , 35 . ) Anali kucilitsa akhungu , olumala , akhate , na ogontha . ( Ŵelengani Yesaya 11 : 6 , 7 . ) Mungaŵelenge za ena mwa anthu amenewa , m’nkhani za pa jw.org , za mutu wakuti “ Baibo Imasintha Anthu . ” Sitiyenela kudzibisa kuti ndise a Mboni za Yehova . 3 Tengelani Cikhulupililo ndi Kumvela kwa Nowa , Danieli , na Yobu 28 Cimwemwe — Khalidwe Locokela kwa Mulungu 9 , 10 . ( a ) Kodi tingatengele bwanji cikhulupililo ndi kumvela kwa Nowa ? ( Ŵelengani Malaki 3 : 17 , 18 . ) ( b ) Kodi Yehova anali kumuona bwanji Danieli ? ( b ) Kodi makolo masiku ano angatengele bwanji citsanzo ca makolo a Danieli ? ( Ŵelengani Yobu 1 : 9 , 10 . ) 19 , 20 . ( a ) Tingatengele bwanji cikhulupililo ndi kumvela kwa Yobu ? 1 - 3 . ( a ) N’ciani cingatithandize kukhalabe okhulupilika kwa Mulungu m’masiku otsiliza ano ? ( Ŵelengani Danieli 6 : 7 - 10 . ) ( Ŵelengani Salimo 11 : 5 ; 26 : 4 . ) ( Sal . 1 : 1 - 3 ) Cotelo , dzifunseni kuti , ‘ Kodi nimam’dziŵa Yehova monga mmene Nowa , Danieli , na Yobu anali kum’dziŵila ? ’ Nayenso Inoki , ambuye awo a atate ake a Nowa , “ anayenda ndi Mulungu woona . ” ( Gen . 22 : 15 - 18 ; Aheb . Siningakwanitse kufotokoza cimwemwe cimene tili naco . ” Pakuti mwa mzimu wake , Mulungu anaululila ifeyo zinthu zimenezi . ” ( 1 Akor . Yesu anati : “ Ndalankhula zinthu izi kwa inu , kuti cimwemwe canga cikhale mwa inu , ndi kuti cimwemwe canu cisefukile . ” ( Yoh . ( 3 ) Kodi kuyetsetsa kukhala na “ maganizo a Khristu ” kungatithandize bwanji kukhala anthu auzimu ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 2 : 14 - 16 mau amunsi . ) Kodi Baibo imakamba ciani ponena za anthu okonda zinthu zauzimu ? Kodi tingaphunzile ciani pa citsanzo ca Yakobo ? Kodi tingaphunzile ciani pa citsanzo ca Mariya ? ( Ŵelengani Luka 1 : 46 - 55 . ) ( Ŵelengani Yesaya 63 : 9 ; Maliko 6 : 34 . ) Koma kuphunzila coonadi kunanilimbikitsa kusintha na kukhala munthu wauzimu . Kusintha sikunali kopepuka , koma n’tasintha n’napeza cimwemwe ndipo lomba nimaona kuti moyo wanga uli na colinga . ” Motelo , kutsatila citsanzo Yesu kumatithandiza kumuyandikila kwambili Yehova . Ophunzilawo anati : “ Ife ndife mboni za zinthu zonse zimene anacita . ” ( Mac . Kodi kukhala na maganizo ofanana ndi a Khristu kungakhudze bwanji umoyo wathu wa tsiku na tsiku ? Iye anati : “ Sin’nacite colakwa ciliconse , koma n’nali kucita zinthu zauzimu mwamwambo cabe . N’nali kupezeka pa misonkhano yonse , ndipo n’nali kucitako upainiya wothandiza kangapo pa caka . Iye anati : “ Zinali monga kuti sin’nali kudziŵa ciliconse . N’nayamba kuganiza kuti , ‘ Monga mutu wa mkazi wanga , nifunika kuwongolela . ’ ” Iye anakamba kuti : “ N’nayamba kuŵelenga kwambili Baibo , ndipo m’kupita kwa nthawi n’namvetsetsa mfundo za coonadi . N’nakhala na cidziŵitso , ndipo koposa zonse , ubwenzi wanga na Yehova unalimba . ” ( 3 ) Kodi kukhala munthu wolimba mwauzimu kungatithandize bwanji mu umoyo wathu wa tsiku na tsiku ? ( b ) Tiyenela kukhala na colinga canji tikamaphunzila na kusinkha - sinkha Mau a Mulungu ? ( b ) Nanga ni citsanzo citi ca m’Baibo cimene tingatengele ? 12 , 13 . ( a ) N’ciani cingatithandize “ kukhala ndi maganizo amene Khristu Yesu anali nawo ” ? ( Ŵelengani 2 Petulo 1 : 5 - 8 . ) Kodi kukhala munthu wauzimu kumakhudza bwanji umoyo wathu ? Kodi ni “ nchito zakufa ” ziti zimene tifunika kupewa ? Kodi zosankha zanga zidzanithandiza kukhala na zolinga zauzimu ? N’cifukwa ciani ndimwe ofunitsitsa kupita patsogolo mwauzimu ? Mtumwi Petulo anauza Akhristu a m’nthawi yake kuti : “ Muzicelezana popanda kudandaula . ” ( 1 Pet . Nyamuka , ubatizidwe . ” — MAC . 22 : 16 . Kodi makolo acikhristu amafuna kutsimikizila ciani ana awo asanabatizike ? POFOTOKOZA zimene zinacitika atapanga cosankha cobatizika , mlongo Blossom Brandt anati : “ Kwa miyezi ingapo n’nali kuuza atate na amayi kuti nifuna kubatizika , ndipo iwo nthawi zambili anali kukamba nane za nkhaniyi . Iwo anali kufuna kutsimikizila ngati n’nali kudziŵadi kuti kubatizika ni nkhani yaikulu . Tsiku la cocitika capadela cimeneci mu umoyo wanga , linafika pa December 31 , 1934 . ” 5 , 6 . ( a ) Kodi zimene Baibo imakamba zokhudza Timoteyo zitiphunzitsa ciani pa nkhani ya ubatizo ? ( Ŵelengani Akolose 1 : 9 , 10 . ) Iwo anauza Yehova kuti akondwela ngako kuti ine mwana wawo wamng’ono nasankha kupeleka moyo wanga kwa iye . ” ( Ŵelengani 1 Petulo 3 : 20 , 21 . ) N’cifukwa ciani sitifunika kukakamiza aliyense kuti abatizike ? Tidzakambilana mafunso ati m’nkhani yotsatila ? Ngati ndimwe kholo , mwina munadzifunsapo kuti : ‘ Kodi mwana wanga ni wokonzekadi kubatizika ? Funso loyamba limakhala lakuti , “ Pamaziko a nsembe ya Yesu Khristu , kodi munalapa macimo anu na kudzipeleka kwa Yehova kuti mucite cifunilo cake ? ” Pa misonkhano yathu , tingaonetse bwanji kuti ndise oceleza ? ( Ŵelengani 3 Yohane 5 - 8 . ) Iye analemba kuti : “ Poyamba n’nali kuyopa kulandila alendo cifukwa tinali titangokwatilana kumene , ndipo tinali kukhala m’nyumba yaing’ono . Koma tinakondwela ngako kukhala na abale na alongo amenewo . Monga okwatilana kumene , tinaona cimwemwe cimene anthu amakhala naco ngati akutumikila Yehova mogwilizana na kuyesetsa kukwanilitsa zolinga zawo zauzimu pamodzi . ” N’cifukwa ciani tifunika kuceleza ofalitsa amene akukila mu mpingo mwathu ? ( Ŵelengani Luka 10 : 41 , 42 . ) Tsiku lina , mkazi wanga anayewa kwambili ku nyumba . N’nayesetsa kumulimbikitsa , koma sizinathandize . Ndiyeno , ca m’ma 19 : 30hrs tinamva kugogoda pakhomo . Iye anabwela kudzationa . Tinamuuza kuti aloŵe , ndipo tinamupatsa madzi akumwa . Ngati mumaopa kuceleza alendo , dziŵani kuti si ndinu nokha . Mkulu wina wa ku Britain anati : “ Nthawi zina , munthu angakhale na nkhawa pamene akukonzekela kulandila alendo . Koma molingana na zinthu zina zimene timacita potumikila Yehova , kuceleza ena kumatibweletsela mapindu na cimwemwe coculuka . Ine nthawi zina nimamwa cabe khofi na alendo , kwinaku tikuceza . ” Mkulu winanso analemba kuti : “ Kuceza na abale a mu mpingo mwathu ku nyumba kwanga kumanipatsa mwayi wowadziŵa bwino , maka - maka kudziŵa mmene anaphunzilila coonadi . ” Koma mkazi wa mmodzi wa alangizi a sukuluzi ananilimbikitsa ngako . Anakamba kuti pamene iye na mwamuna wake akutumikila m’dela , amakondwela kwambili akapita kukaceza kwa munthu wauzimu , olo wosauka , amene ali na umoyo wosalila zambili , ndipo amaika mtima wake wonse pa kutumikila Yehova . Izi zinanikumbutsa zimene amayi anali kutiuza pamene tinali ana . Anali kukamba kuti ‘ Ni bwino kudya zamasamba pamene pali cikondi . ’ ” ( Miy . ( Ŵelengani Miyambo 25 : 21 , 22 . ) Nthawi zambili , anthu amene aitana alendo amakonzekela bwino ( Onani palagilafu 20 ) Wamasalimo Davide anafunsa kuti : “ Inu Yehova , ndani amene angakhale mlendo m’cihema canu ? ” Cinanso , ni bwino kulemekeza cikhalidwe ca kwanuko . Koma m’zikhalidwe zina , kukana ciitano kumaoneka monga n’kusayamikila . Abale aŵili akugaŵila kapepa kauthenga kwa munthu wogwila nchito yopenta , pa ulalo wa pafupi na malo a citetezo camphamvu ochedwa Kaštilac , amene anamangidwa m’zaka za m’ma 1500 C.E . Malowa ali pafupi na mzinda wa Split ( Ŵelengani Tito 2 : 11 - 14 . ) Mkuluyo anati : “ Graham anali na khalidwe lonyada . Anali kupeza zifukwa akulu amene anasamalila mlandu wake umene unam’cotsetsa mu mpingo . Conco , pa maulendo angapo otsatila , tinakambilana malemba ofotokoza za kunyada na zotulukapo za khalidweli . Pamene tinali kukambilana , zinali monga kuti Graham akudziyang’ana pa gilasi ya Mau a Mulungu , ndipo sanakondwele na mmene anali kuonekela . Graham anavomeleza kuti anacititsidwa khungu na mzimu wonyada , umene unali ngati “ mtanda wa denga ” m’diso lake . Anazindikila kuti iye ndiye anali na vuto . Anali kukonda kupeza zifukwa akulu . Conco , mwamsanga anayamba kusintha . Iye anayamba kupezeka pa misonkhano ya mpingo nthawi zonse , kuphunzila Mau a Mulungu mwakhama , na kupemphela tsiku lililonse . Anati , ‘ Nakhala m’coonadi kwa zaka zambili , ndipo natumikilapo monga mpainiya . Mtumwi Petulo anati : “ Wetani gulu la nkhosa za Mulungu lomwe analisiya m’manja mwanu , osati mokakamizika , koma mofunitsitsa . Osatinso cifukwa cofuna kupindulapo kenakake , koma ndi mtima wonse . Osati mocita ufumu pa anthu amene ali coloŵa cocokela kwa Mulungu , koma mukhale zitsanzo kwa gulu la nkhosa . ” ( 1 Pet . Kodi makolo angalele bwanji ana awo m’malangizo a Yehova ? ( Ŵelengani Aheberi 12 : 5 - 11 . ) Kodi mwana angaphunzile bwanji kudzilanga yekha ? 4 , 5 . ( a ) N’cifukwa ciani kudzilanga wekha ni mbali yofunika kwambili ya “ umunthu watsopano ” ? Tingacite ciani kuti tizikonda kuŵelenga Mau a Mulungu ? M’bale wina anati , “ Nimayamikila ngako kuti makolo anga ananilela bwino . ( b ) Kodi banja lina linapindula bwanji pamene makolo a m’banjalo anamvela Yehova ? Patapita zaka , mwanayo anabwezeletsedwa . ( b ) N’ciani cimene tiyenela kucita kuti akulu azikondwela na utumiki wawo ? Conco , n’naona kuti nifunika kuuzako akulu . Iwo sananikalipile kapena kunidzudzula , koma ananilimbikitsa . Ndipo nthawi zonse pambuyo pa misonkhano , akulu anali kunifunsako za umoyo wanga olo pamene anali otangwanika kwambili . Cifukwa ca zimene zinanicitikila m’mbuyomo , n’nali kuona kuti Mulungu sanganikonde . Komabe , nthawi na nthawi , Yehova anali kuseŵenzetsa mpingo na akulu ponitsimikizila kuti amanikonda . Nimapemphela kuti nisakamusiye . ” Ukasintha n’kucita cabwino , sindikuyanja kodi ? Koma ngati susintha kuti ucite cabwino , ucimo wamyata pakhomo kukudikilila , ndipo ukulakalaka kukudya . Kodi iweyo suugonjetsa ? ” ( Gen . 1 : 24 - 31 ) Conco , tifunika ‘ kumvela malangizo kuti tikhale anzelu . ’ Anthu pa dziko lonse amafunitsitsa kukhala na ufulu waukulu . 15 Tengelani Yehova — Mulungu Amene Amapeleka Cilimbikitso 8 : 36 . ( Ŵelengani 1 Mbiri 29 : 11 , 12 . ) Kuti anthu akhale na umoyo ‘ wabwino , ’ afunika kudalila Mulungu na kumumvela . Apo ayi , adzafunika kudziŵa okha cabwino . . . na coipa . ” Angacite ngozi yoopsa kwambili . Anati : “ Mukamasunga mau anga nthawi zonse , ndiye kuti ndinudi ophunzila anga . Mudzadziŵa coonadi , ndipo coonadi cidzakumasulani . ” N’cifukwa ciani tingakambe kuti ufulu umene Yesu anatilonjeza udzakhaladi weni - weni ? ( Ŵelengani Aroma 8 : 1 , 2 , 20 , 21 . ) ( c ) Tidzakambilana mafunso ati ? ( Pitani pa ZOCITIKA NA KUFUNSA MAFUNSO > KUPILILA ZIYESO . ) Zinthu zonse ndi zololeka , koma si zonse zimene zili zolimbikitsa . ” N’citsanzo canji cimene Nowa na banja lake anapeleka ? Iwo anali kukhala m’dziko lokonda ciwawa na ciwelewele . Baibo imati : “ Nowa anacita zonse motsatila zimene Mulungu anamulamula . Nanga Yehova watipatsa nchito yanji masiku yano ? ( Ŵelengani Luka 4 : 18 , 19 . ) Apa m’pamene n’namvetsetsadi tanthauzo la Yakobo 4 : 8 , imene imati : ‘ Yandikilani Mulungu , ndipo iyenso adzakuyandikilani . ’ N’nadziŵa kuti napeza cimene n’nali kufuna , cimene ni umoyo waphindu . ” M’bale na mkazi wake , amene na apainiya apadela akulalikila m’dela linalake lakutali ca kufupi na mzinda wa Balykchy ( b ) Kodi Yehova anamulimbikitsa bwanji Mwana wake ? Ndikugwila mwamphamvu ndi dzanja langa lamanja lacilungamo . ” ( Yes . 41 : 10 ) Nawonso Akhristu oyambilila anali kudziŵa kuti Mulungu amatilimbikitsa . Sangalala limodzi ndi ine mbuye wako . ” Kodi Hezekiya anawalimbikitsa bwanji akulu - akulu a asilikali ndi anthu a mu Yerusalemu ? Kodi Petulo anawalimbikitsa bwanji Akhristu anzake ? Koma ine ndakupemphelela iwe kuti cikhulupililo cako cisathe . Cotelo iwenso , ukabwelela , ukalimbikitse abale ako . ” — Luka 22 : 31 , 32 . Nanga n’cifukwa ciani ? Kodi akulu angapeleke bwanji uphungu m’njila yolimbikitsa ? Makolo , kodi mumaphunzitsa ana anu kuti azilimbikitsa ena ? Mlongoyo ananiuza kuti nayenso anakumanapo na vuto monga limene ine n’nali nalo . Conco , n’nayamba kuona kuti si ine nekha amene n’nali na vutolo . ” Mfumu Solomo inalemba kuti : “ Mawu onenedwa pa nthawi yoyenela ndi abwino kwambili . Maso owala amapangitsa mtima kusangalala . Uthenga wabwino umanenepetsa mafupa . ” Pakuti mwandicititsa kusangalala , inu Yehova , cifukwa ca zocita zanu . Ndimafuula mosangalala cifukwa ca nchito ya manja anu . ” ( Sal . Mtumwi Paulo anati : “ Mulungu si wosalungama woti angaiŵale nchito yanu ndi cikondi cimene munacisonyeza pa dzina lake . ” ( Aheb . 6 : 10 ) Mukhoza kudziikila zolinga olo pamene muli wamng’ono . Miyambo 21 : 5 imati : “ Zolinga za munthu wakhama zimam’pindulila . ” Mukadziikila zolinga zabwino mukali aang’ono , kupanga zosankha kumakhala kosavuta . N’zoona kuti nikanaphunzila ku univesiti na kutenga digili ya za malamulo , sembe nilandila ndalama zambili . Koma sembe nilibe mwayi wokwanila wopeza nchito ya uloya ya maola ocepa . ” 17 , 18 . ( a ) Kodi Yehova amawafunila zotani acicepele masiku ano ? N’nabadwila m’nyumba yamitengo ya cipinda cimodzi m’tauni yaing’ono yochedwa Liberty , ku Indiana , m’dziko la United States . M’kupita kwa nthawi , amayi anabeleka ang’ono anga aŵili na mlongosi wanga mmodzi . PAMENE n’nali pa sukulu , zinthu zambili sizinasinthe . Tauni ya Liberty inali yozungulilidwa na mafamu ang’ono - ang’ono , ndipo alimi ambili anali kulima milisi . Anali kupita nase ku chechi ya Baptist pa Sondo paliponse . Koma ine sin’naikonde nchitoyi . Koma panthawiyi , ananiitanila ku Phunzilo la Buku la Mpingo , kumene anali kukambilana na kuphunzila zokhudza Baibo . Phunziloli linali kucitikila ku nyumba kwawo . N’nawauza kuti nidzaganizilapo . N’nadabwa poona kuculuka kwa zimene anali kudziŵa zokhudza Baibo . Zaka zingapo m’mbuyomo , pamene n’nafunsa amayi za Mboni za Yehova , ananiuza kuti , “ Amalambila munthu winawake wakale wochedwa Yehova . ” Koma n’tayamba kuphunzila , n’naona kuti maso anga ayamba kutseguka . Caka cotsatila ca 1958 , n’nayamba upainiya . Gloria anali ciphadzuwa , ndipo na manje ni ciphadzuwa . Ine na Gloria tinakwatilana mu February , 1959 . M’bale wokondedwa , dzina lake Simon Kraker anatifunsa mafunso kuti aone ngati tinali oyenelela . Iye anatiuza kuti pa nthawiyo ku Beteli sanali kuitana anthu amene ali pabanja . Mkazi wanga anali kugwila nchito pa nyumba zingapo . Ine n’nali kugwila nchito za panja , kutsuka mawindo , na nchito zina . Nikumbukila zimene zinacitika nthawi ina pamene tinaima pa filing’i sitesheni . Mosiyana na zimenezi , tinali kukondwela ngako kukhala na abale , komanso ulaliki tinali kuukonda . Inenso n’nayamba kuphunzila na mwana wawo wamkazi pamodzi na mwamuna wake . Mwanayo na amayi ake , onse anasankha kutumikila Yehova ndipo anabatizika . Tinalinso na anzathu mumpingo wa azungu . Pa nthawiyo , gulu lolimbikitsa tsankho na ciwawa , lochedwa Ku Klux Klan ( KKK ) , linali lamphamvu maningi . Mu 1962 , ananiitana ku Sukulu ya Utumiki wa Ufumu ku South Lansing , mu New York . Ngakhale n’conco , kampani ina ya zamafoni ku Pine Bluff inali itanifunsa mafunso kuti inilembe nchito . Nikanalembedwa nchitoyo , sembe n’nakhala munthu woyamba wakuda pa kampaniyo . N’nalibe ndalama zoyendela ku New York . Iye anati , “ Yendani ku sukulu mukaphunzile zambili , kuti mukadzabwela mudzatiphunzitse ! ” Ndine wokondwa kuti sin’nayambe nchitoyo . Lomba lekani Gloria afotokozeko mmene anali kumvelela pamene tinali kutumikila ku Pine Bluff : “ Gawo la kumeneko n’nalikonda ngako ! Conco , tinali kucita ulaliki wa ku nyumba ndi nyumba m’maŵa , ndipo m’madzulo tinali kucititsa maphunzilo a Baibo . Pamene tinali kucita upainiya ku Pine Bluff , tinafunsila upainiya wapadela ku Beteli . Pa nthawiyo , nayenso M’bale Leon Weaver , amene lomba ni mgwilizanitsi wa Komiti ya Nthambi ya ku United States anaikidwa kukhala woyang’anila dela . N’nali kuyopa kukhala woyang’anila dela . N’taikidwa pa udindowo , M’bale Thompson ndiye anali woyang’anila wacigawo woyamba kutumikila naye . M’masiku amenewo , woyang’anila dela sanali kuphunzitsidwa kwa nthawi itali . Nikumbukila n’nauza mkazi wanga kuti , “ Niona kuti acoka mwamsanga . ” Tsiku lina , gulu la KKK linacita zionetselo m’tauni ya Tennessee , kumene tinali kucezetsa mpingo . M’mwezi wokonkhapo , tinayamba utumiki wathu wa pa Beteli . Mkazi wanga Gloria anali ciphadzuwa , ndipo na manje ni ciphadzuwa Ndiyeno , mu 1999 , n’naikidwa kukhala mmodzi wa mamembala a m’Bungwe Lolamulila . Lemba la Yesaya 32 : 17 limati : “ Nchito ya cilungamo ceniceni idzakhala mtendele , ndipo zocita za cilungamo ceniceni zidzakhala bata ndi mtendele mpaka kalekale . ” Yaciŵili , tifunika kupempha mzimu woyela wa Mulungu . Ngati nyumbayo ili yoyenela , mtendele umene mukuifunila ukhale panyumbayo , koma ngati si yoyenela , mtendele wanu ubwelele kwa inu . ” Conco , n’namupatsa moni m’citundu cakeco . Iye anadabwa , ndipo ananifunsa kuti : ‘ Tikuthandizeni ciani ? ’ Mwaulemu , n’namuuza kuti nifuna kuonana ndi Kazembe . Iye anatumila foni Kazembeyo , ndipo anabwela na kunipatsa moni m’citundu ca kwawo . Pambuyo pake , anamvetsela mwachelu pamene n’nali kumufotokozela za nchito ya mtendele ya Mboni za Yehova . ” ‘ Komano zogwela panthaka yabwino , ndi anthu amene . . . amabeleka zipatso mwa kupilila . ’ — LUKA 8 : 15 . N’ciani cimene cingatithandize kupitiliza kubala zipatso mopilila ? ( Onani pikica pamwambapa . ) ( b ) Kodi Yesu anakamba ciani za kulalikila m’gawo la “ kwawo ” ? Winanso anati : “ Kukhulupilika kwawo kumanilimbikitsa kupitiliza kulalikila mopilila ndi molimba mtima . ” Kodi tidzakambilana mafunso atatu ati ? Cifukwa ciani ? Koma palibe nchito ina imene ningakonde kugwila kuposa imeneyi . ” Ni mmene ise tonse timaonela . Ŵelengani Yohane 15 : 1 - 5 , 8 . Kutanthauza kulalikila uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu . Ŵelengani Luka 8 : 5 - 8 , 11 - 15 . Kodi timabala bwanji zipatso mwa kupilila ? Pakuti ndikuwacitila umboni kuti ndi odzipeleka potumikila Mulungu , koma samudziŵa molondola . ” Tsiku lina titapitanso pa malowo , munthu wina wopita na njila anatifunsa kuti , ‘ N’cifukwa ninji simunali kuoneka ? Kodi mwatsimikiza mtima ‘ kubala zipatso mwa kupilila ’ ? 15 : 8 ( Ŵelengani Yohane 15 : 1 , 8 . ) Kumbukilani kuti Yesu anauza atumwi kuti : “ Atate amalemekezeka mukapitiliza kubala zipatso zambili . ” ( b ) Kodi mumamvela bwanji mukaganizila mwayi umene muli nawo woyeletsa dzina la Mulungu ? Zimenezi zimanilimbikitsa kupitiliza kulalikila . ” ( a ) Kodi lemba la Yohane 15 : 9 , 10 limachula cifukwa cina citi cogwilila nchito yolalikila ? Kodi timaonetsa bwanji kuti tifuna kukhalabe m’cikondi ca Khristu ? Baibo imakamba kuti Nowa anali “ mlaliki . ” ( Ŵelengani 2 Petulo 2 : 5 . ) ( a ) Kodi pa Mateyu 22 : 39 pali cifukwa canji cimene tiyenela kugwilila nchito yolalikila ? Iwo amafunikila kumva uthenga wabwino . ” 13 , 14 . ( a ) Ni mphatso yanji imene imachulidwa pa Yohane 15 : 11 ? ( a ) Ni mphatso yanji imene imachulidwa pa Yohane 14 : 27 ? ( a ) Ni mphatso iti imene yachulidwa pa Yohane 15 : 15 ? ( b ) Kodi atumwi anafunika kucita ciani kuti akhalebe mabwenzi a Yesu ? ( Ŵelengani Yohane 15 : 14 - 16 . ) Timakhulupilila kuti Yehova amayankha mapemphelo athu opempha thandizo ( Onani palagilafu 18 ) Mtumwi Petulo anachula Satana Mdyelekezi kuti “ mkango wobangula , ” ndipo Yohane anamuchula kuti “ njoka , ” komanso “ cinjoka . ” ( 1 Pet . 5 : 8 ; Chiv . Mwa thandizo lawo , tingakwanitse kumutsutsa Satana . 18 : 11 ) Anthu amene amakhulupilila bodza limeneli amaseŵenzetsa moyo wawo wonse kutumikila “ Cuma ” m’malo motumikila Mulungu . ( Mat . Tifunika kum’dziŵa bwino mdani wathu , koma sitifunika kumuyopa . 2 : 14 ) Ngati timutsutsa , iye adzatithaŵa . ( Yak . Kodi zida zankhondo yathu yauzimu ni ziti ? Ndipo makolo anga na anzanga amanidalila . ” Kumatithandiza kukhala wolimba mtima na kuyandikila kwambili Yehova , ndipo anthu amene amatikonda amayamba kutilemekeza . ” Lamba wa coonadi ( Onani palagilafu 3 - 5 ) Cifukwa ca zimenezi , n’nayamba kudzikayikila na kuvutika maganizo . ” Anzanga ena anayamba kuseŵenzetsa amkolabongo , ndipo ena analeka sukulu . Cinali comvetsa cisoni kuona mavuto amene anakumana nawo . Iye anati : “ Nimayesetsa kukumbukila kuti ndine Mboni ya Yehova na kuti ciyeso ni njila imene Satana amaseŵenzetsa pofuna kunigonjetsa . Nikapambana ciyeso , nimamvela bwino ngako . ” Codzitetezela pacifuwa cacilungamo ( Onani palagilafu 6 - 8 ) Lomba , nimakondwela kulalikila anzanga . ” Mwa ici , nimakwanitsa kudziŵa zimene zingawathandize . Nikakhala wokonzeka , nimakwanitsa kukamba nawo mfundo zimene zingawapindulitse . ” Ine nimaonetsetsa kuti naŵelenga nkhani na zofalitsa zonse zokhudza acicepele . Mwa ici , nimatha kuwaonetsa mfundo za m’Baibo kapena zofalitsa za pa jw.org zimene zingawathandize . ” Mapazi ovekedwa nsapato zokonzekela uthenga wabwino ( Onani palagilafu 9 - 11 ) Kodi ina mwa “ mivi yoyaka moto ” ya Satana ni iti ? Koma lomba nimakonzekela misonkhano na kuyesetsa kuyankhapo , kaŵili kapena katatu . Zimanivuta , koma nimamvela bwino kwambili nikayankhapo . Komanso , abale na alongo amanilimbikitsa maningi . Conco , nthawi zonse pamene nicoka ku misonkhano , nimakhala wotsimikiza kuti Yehova amanikonda . ” Cishango cacikulu cacikhulupililo ( Onani palagilafu 12 - 14 ) Cisoti colimba cacipulumutso ( Onani palagilafu 15 - 18 ) Naona kuti anthu amamvetsela kwambili akazindikila kuti umaikonda Baibo komanso umayesetsa kuwathandiza . ” Lupanga la mzimu ( Onani palagilafu 19 - 20 ) 20 : 1 - 3 , 7 - 10 ) Mdani wathu timam’dziŵa bwino . Lemba la Miyambo 14 : 15 limati : “ Munthu amene sadziŵa zinthu amakhulupilila mau alionse , koma wocenjela amaganizila za mmene akuyendela . ” N’cifukwa ciani kukonda abale n’kofunika kwambili ? N’cifukwa ciani Paulo analembela kalata Akristu aciheberi ? ( Ŵelengani Aheberi 10 : 36 - 39 ) Ndiye cifukwa cake , mouzilidwa ndi Yehova , Paulo anawalembela kalata abale ndi alongo okondedwa amenewo . N’cifukwa ciani buku la Aheberi n’lothandiza kwa ife ? Kodi lemba la caka ca 2016 ndi liti ? Vesi limeneli ndi limene lasankhidwa kukhala lemba la caka ca 2016 . Lemba la caka ca 2016 : “ Mupitilize kukonda abale . ” ​ — Aheberi 13 : 1 Kodi Akristu oona amaona kuti ‘ m’bale ’ wao ndani ? ( a ) Kodi cifukwa cacikulu cimene tiyenela kuonetsela cikondi kwa abale athu n’citi ? ( b ) Ndi cifukwa cina citi cimene tiyenela kulimbitsila cikondi pakati pathu ? Yesu anali atafotokozelatu kuti nthawi imeneyo idzakhala yovuta kwambili . N’ciani cimene tiyenela kucita tsopano cisautso cacikulu cisanayambe ? ( a ) Ndi mipata iti imene tingaonetsele kuti timakonda abale athu ? ( b ) Fotokozani zitsanzo za mmene anthu a Yehova anaonetsela cikondi kwa abale ao . Kodi tingawakumbukile bwanji “ amene ali m’ndende ” ? “ Kumbukilani amene ali m’ndende . ” “ Ukwati ukhale wolemekezeka kwa onse . ” Kodi kukhala okhutila kumatithandiza bwanji kukonda abale athu ? “ Mukhale okhutila ndi zimene muli nazo pa nthawiyo . ” Kodi kukhala “ olimba mtima ” kumatithandiza bwanji kukonda abale athu ? N’ciani cingatilimbikitse kukonda kwambili akulu ? “ Kumbukilani amene akutsogolela . ” Tingacite ciani kuti tiziwakonda kwambili abale ? Kodi cikondi ca Kristu cimatilimbikitsa kucita ciani ? Kodi cikondi ca Mulungu cimatilimbikitsa bwanji kukonda abale athu ? Kodi kudziŵa kuti Mulungu ndi wokhululukila kungatilimbikitse bwanji kukhululukila abale athu ? 1 , 2 . ( a ) Kodi mphatso ya Mulungu ‘ imene sitingathe kuifotokoza ’ imaphatikizapo ciani ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 20 . ) 3 , 4 . ( a ) Mumamva bwanji munthu wina akakupatsani mphatso ? ( b ) Kodi mphatso yapadela ingasinthe bwanji umoyo wanu ? Kodi mphatso ya dipo imaposa bwanji mphatso zina zonse ? ( a ) Ndi madalitso ati amene tidzalandila cifukwa ca mphatso imene Yehova anapeleka ? ( b ) Chulani zinthu zitatu zimene cikondi ca Mulungu cimatilimbikitsa kucita . Kodi tiyenela kumva bwanji tikaganizila cikondi cimene Kristu anatisonyeza ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 5 : 14 , 15 . ) Komanso wondikonda ine , Atate wanga adzamukondanso . Inenso ndidzamukonda ndipo ndidzadzionetsela bwinobwino kwa iye . ” — Yohane 14 : 21 ; 1 Yohane 5 : 3 . Pa nyengo ino ya Cikumbutso , ndi mafunso ati amene tiyenela kudzifunsa ? Nanga mayankho ake angatilimbikitse kucita ciani ? ( Ŵelengani 1 Timoteyo 2 : 9 , 10 . ) ( a ) Kodi kukonda Yehova ndi Yesu kumatilimbikitsa kucita ciani pa nchito yathu yolalikila ? ( b ) Kodi kukonda Mulungu kudzatilimbikitsa kucitila ciani abale athu mumpingo ? Kodi cikondi ca Mulungu cidzatilimbikitsanso kucita ciani ? Kodi Yesu anapeleka citsanzo cotani pa nkhani yokonda anthu ena ? Kodi mungathandizeko m’bale kapena mlongo wokalamba kulalikila ? Tingaonetse bwanji kuti timakonda abale athu ? ( Ŵelengani Luka 14 : 12 - 14 . ) 16 , 17 . ( a ) Tingaphunzile ciani pa fanizo la Yesu la mfumu ndi akapolo ? ( b ) Pambuyo poganizila fanizo la Yesu , kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ? Kodi cikondi ca Mulungu cinalimbikitsa mlongo wina kucita ciani ? Ndifuna kuti ndikam’dziwe bwino ali wangwilo . ” Kodi mphatso yaulele ya Mulungu ‘ imene sitingathe kuifotokoza ’ imakulimbikitsani kucita ciani ? [ 1 ] ( ndime 18 ) Maina ena m’nkhani ino asinthidwa . Ndi zinthu ziti zimene zinapangitsa tsiku la Pentekosite mu 33 C.E . kukhala lapadela ? Nanga zimenezo zinakwanilitsa bwanji ulosi wa m’Malemba ? ( a ) Kodi zimene zinacitika pa Pentekosite zimatikhudza bwanji ? ( b ) Ndi cocitika citi cimene ciyenela kuti cinacitika zaka zambili m’mbuyomo pa tsiku lofanana ndi la Pentekosite ? Timadziŵa bwanji kuti Akristu sadzozedwa m’njila yofanana ndendende ? Kodi Akristu onse odzozedwa amalandila ciani ? Kodi Mkristu aliyense wodzozedwa ayenela kucita ciani kuti adzalandile colowa cake ? Petulo anafotokoza kuti : “ Pa cifukwa cimeneci abale , citani ciliconse cotheka kuti mukhalebe okhulupilika , n’colinga coti mupitilizebe kukhala pakati pa anthu amene Mulungu wawaitana ndi kuwasankha , pakuti mukapitiliza kucita zinthu zimenezi simudzalephela ngakhale pang’ono . Ndipo mukatelo , adzakutsegulilani khomo kuti mulowe mwaulemelelo mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Kristu . ” 8 , 9 . ( a ) N’cifukwa ciani ambili amalephela kumvetsa zimene zimacitika munthu akadzozedwa ? ( b ) Kodi munthu amadziŵa bwanji kuti wasankhidwa kuti adzapita kumwamba ? Iye anati : “ Simunalandile mzimu wa ukapolo woyambitsanso mantha , koma munalandila mzimu wakuti mukhale ana , umene timafuula nao kuti : ‘ Abba , Atate ! ’ Pakuti mzimuwo umacitila umboni limodzi ndi mzimu wathu kuti ndife ana a Mulungu . ” Kodi lemba la 1 Yohane 2 : 27 limatanthauza ciani pamene limati Mkristu wodzozedwa sakufunikila wina aliyense kuti azimuphunzitsa ? Kodi Mkristu wodzozedwa angakhale ndi maganizo otani ? Nanga n’ciani cimene sakaikila ? Kodi kaganizidwe ka odzozedwa kamasintha bwanji akadzozedwa ? Nanga n’ciani cimacititsa zimenezi ? Kodi odzozedwa amamva bwanji pamene ali ndi moyo pano padziko lapansi ? Ndi zinthu ziti zimene sizipeleka umboni wakuti munthu anadzozedwa ndi mzimu woyela ? Timadziŵa bwanji kuti ena amene analandila mzimu wa Mulungu sanapite kumwamba ? 17 , 18 . ( a ) Ndi ciyembekezo cotani cimene atumiki ambili a Mulungu ali naco ? Kodi lemba la Zekariya 8 : 23 likukwanilitsidwa bwanji masiku ano ? 1 , 2 . ( a ) Kodi Yehova anakamba kuti n’ciani cidzacitika masiku ano ? ( b ) Ndi mafunso ati amene adzayankhidwa m’nkhani ino ? N’cifukwa ciani n’zosatheka kwa ife kudziŵa amene adzakhaladi mbali ya a 144,000 ? Ndi cenjezo liti limene odzozedwa ayenela kukumbukila ? Nanga n’cifukwa ciani ? Kodi Akristu odzozedwa sayembekezela ciani ? N’cifukwa ciani tiyenela kusamala ndi mmene timaonela Akristu amene amadya mkate ndi kumwa vinyo pa Cikumbutso ? ( Onani bokosi lakuti “ Cikondi ‘ Sicicita Zosayenela . ’ ” ) Yesu anauza ophunzila ake kuti : “ Nonsenu ndinu abale . ” Mungaonetse bwanji kuti mumalemekeza Akristu odzozedwa ? Kodi timadziteteza bwanji ngati tipewa ‘ kutamanda anthu ena ’ ? N’cifukwa ciani sitiyenela kuda nkhawa ndi ciŵelengelo ca amene amadya mkate ndi kumwa vinyo pa Cikumbutso ? “ Yehova amadziŵa anthu ake . ” Kodi Baibulo limakamba ciani za ciŵelengelo ca odzozedwa amene adzakhala padziko lapansi pamene cisautso cacikulu cidzayamba ? N’ciani cimene tiyenela kudziŵa pa nkhani ya a 144,000 osankhidwa ndi Yehova ? M’nthawi ya atumwi , Mulungu anagwilitsila nchito Akristu odzozedwa ocepa kuti alembe Malemba Acigiliki Acikristu . imalimbitsa ubwenzi wathu ndi Mulungu ndiponso anzathu ? Ngakhale kuti Yehova ndi Mulungu Wamkulu Koposa , kodi wapatsa ena mwai wotani ? Kodi Yehova anapatsa Yesu mwai wogwila naye nchito yotani ? Nanga n’cifukwa ciani ? Mwacitsanzo , anapatsa Adamu nchito yakuti ache nyama maina . Kodi anthu ena anagwila nchito bwanji ndi Mulungu pokwanilitsa cifunilo cake ? Kodi tili ndi mwai wogwila nao nchito iti ? Kodi Yehova amafunikadi thandizo lathu kuti akwanitse kugwila nchitoyi ? ( 1 Akorinto 3 : 9 ) Mtumwi Paulo analemba kuti : “ Pamene tikugwila naye nchito limodzi , tikukudandaulilaninso kuti musalandile kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu n’kuphonya colinga ca kukoma mtimako . ” Kodi Mwana woyamba kubadwa wa Mulungu anali kumva bwanji pamene anali kugwila nchito ndi Atate wake ? N’cifukwa ciani nchito yolalikila imatipatsa cimwemwe ? Kodi anthu ena anakamba ciani za cimwemwe cimene amapeza cifukwa cogwila nchito ndi Yehova ? Nayenso Franco amene akutumikila ku Italy anati : “ Kudzela m’Mau ake ndi zogaŵila zakuuzimu , nthawi zonse Yehova amatikumbutsa kuti amatikonda ndi kuti amayamikila zimene timacita pom’tumikila , ngakhale kuti nthawi zina tingaone ngati palibe zimene tikucita . Kumandipangitsanso kuona moyo wanga kukhala wofunika . ” Kodi Yehova ndi Yesu anali pa ubwenzi wotani ? Nanga n’cifukwa ciani ? Kodi nchito yolalikila imalimbitsa bwanji ubwenzi wathu ndi Mulungu ndiponso anzathu ? Iye anati : “ Kuti akhale amodzi mmene ife tilili . ” Timadziŵa cifukwa cake tiyenela kum’dalila ndi kumvela malangizo ake . N’ciani cidzalimbitsa kwambili ubwenzi wathu ndi Yehova ndiponso ndi anzathu m’dziko latsopano ? Kodi m’bale wina wa ku Australia amaiona bwanji nchito yolalikila ? Joel , amene amakhala ku Australia , anati : “ Kulalikila kumandithandiza kuti ndiziona zinthu moyenela . Kumandikumbutsa za mavuto amene anthu akukumana nao ndiponso mapindu amene ndapeza cifukwa cotsatila mfundo za m’Baibulo pa umoyo wanga . Nchito yolalikila imandithandiza kukhala wodzicepetsa . Imandipatsanso mwai wodalila Yehova ndi abale ndi alongo anga . ” Kodi kupilila kwathu pa nchito yolalikila kumaonetsa bwanji kuti mzimu wa Mulungu ukutitsogolela ? Kodi mungapitilize kugwila nchito yotelo ? Kodi nchito yolalikila uthenga wabwino imagwilizana bwanji ndi colinga ca Mulungu cokhudza anthu ? Kodi kulalikila kumagwilizana bwanji ndi malamulo aakulu a Mulungu ? Laciŵili lofanana nalo ndi ili , ‘ Uzikonda mnzako mmene umadzikondela wekha . ’ ” Kodi mumamva bwanji cifukwa ca mwai wolalikila uthenga wabwino ? Ndakupatsa mphamvu , Mau anga Baibulo , thandizo la angelo , anzako padziko , maphunzilo , ndi malangizo a panthawi yake . ’ Ndithudi , ndi mwai waukulu kwambili kucita zimene Yehova watilamula ndi kugwila naye nchito . ” Ndinauza wapolisi kuti ndinakhalapo kale m’ndende cifukwa cokana kumenya nkhondo . NDINABADWA mu 1926 , mumzinda wa Crooksville ku Ohio , m’dziko la United States . Amai ndi Atate sanali kupemphela , koma anali kulimbikitsa anafe kupita ku chalichi . Margaret Walker ( mlongo waciŵili kucokela kumanzele ) anandithandiza kuphunzila coonadi Panthawi imeneyo , mai wina wa Mboni za Yehova , amene tinali kukhala naye pafupi dzina lake Margaret Walker , anayamba kucezela amai ndi kuwauza uthenga wa m’Baibulo . Koma ndinayesetsa kuti ndizimvetselako zimene anali kukambilana . Atawacezela kwa maulendo angapo , a Margaret anandifunsa kuti , “ Kodi dzina la Mulungu umalidziŵa ? ” Ndinayankha kuti , “ Aliyense amalidziŵa , ndi Mulungu . ” Iwo anati , “ Tenga Baibulo lako ndipo uŵelenge Salimo 83 : 18 . ” Nditaŵelenga lembalo , ndinadziŵa kuti dzina la Mulungu ndi Yehova . Ndinathamangila panja ndi kuuza anzanga kuti , “ Mukafika ku nyumba , muŵelenge Salimo 83 : 18 m’Baibulo lanu , kuti mudziŵe dzina la Mulungu . ” Mwina tinganene kuti apa m’pamene ndinayambila kulalikila . Ndinayamba kuphunzila Baibulo , ndipo mu 1941 ndinabatizidwa . Pambuyo pake , ndinapatsidwa udindo wocititsa phunzilo la buku la mpingo . Ndinalimbikitsa amai ndi azilongosi anga onse kuti azipezekapo pa phunzilo limenelo , ndipo anayambadi kupezekapo . Nthawi zina , amai akamapita kumisonkhano , io anali kuwathamangila ndi kuwakokela ku nyumba . Koma amai anali kutulukila khomo lina ndi kupita kumisonkhano . Koma ndinauza akuluakulu a boma kuti sindingakhale msilikali . Woweluza wina anati : “ Nditapatsidwa mwai wokuweluza , ndikhoza kulamula kuti ukhale m’ndende kwa umoyo wako wonse . Ndinayankha kuti : “ Wolemekezeka , ine ndine minisitala . Nchito yanga ndi kulalikila Uthenga wabwino wa Ufumu khomo ndi khomo , ndipo ndalalikila anthu ambili . ” Ndiyeno woweluzayo anauza oweluza anzake kuti : “ Simunabwele kuno kudzakambilana ngati mnyamatayu ndi minisitala kapena ai . Mwabwela kudzakambilana ngati iye anavomela kuloŵa usilikali kapena ai . ” Ndili mmenemo , ndinapemphela kwa Yehova kuti : “ Yehova sindingakwanitse kukhala muno zaka 5 . Tsiku lotsatila , asilikali olondela ananditulutsa m’cipindaco . Nditatuluka ndinapita pamene panali mkaidi wina wamtali ndi wojincha . Tinaimilila pa windo ndi kumayang’ana panja . Iye anandifunsa kuti , “ Unalakwa ciani iwe ? ” Ndinayankha kuti , “ Ndine Mboni ya Yehova . ” Ndinati , “ Mboni za Yehova sizipita kunkhondo ndi kupha anthu . ” Ndinati , “ Iyai , si cilungamo . ” Kenako iye anati , “ Kwa zaka 15 ndinali m’ndende ina ndipo ndinali kuŵelengako mabuku anu . ” Ndinali pakati pa Mboni zimene zinaikidwa m’ndende ku Ashland ku Kentucky cifukwa cokana kumenya nkhondo Izi n’zimene tinali kucita kuti tizilalikila mwadongosolo . Ndinali kudela nkhawa a m’banja langa cifukwa atate anandiuzapo kuti , “ Ndikathana ndi iwe , enawa sangandivute . ” Pamenepo ndinati , “ Cabwino , ngakhale n’telo sindingaloŵe usilikali . ” Ndinagwila mau lemba la 2 Timoteyo 2 : 3 ndi kukamba kuti , “ Ndine kale msilikali wa Kristu . ” Iye anakhala cete kwa kanthawi , kenako anati , “ Ungapite kunyumba . ” Patapita nthawi yocepa , ndinapezeka pa kukumana kwa ofuna kutumikila pa Beteli pa msonkhano umene unacitikila ku Cincinnati ku Ohio . Ndinalinso kukonza makina oonongeka ndi maloko . Ndapeza mabwenzi ambili pa Beteli ndiponso mumpingo . Ndinaphunzilako Cicainizi Cacimandarini , ndipo ndimakonda kulalikila m’miseu kwa anthu okamba Cicainizi . Nthawi zina m’maŵa ndimagaŵila magazini 30 kapena 40 kwa anthu a cidwi . Kulalikila anthu a Cicainizi ku Brooklyn , New York Panthawi ina , ndinacita ulendo wobweleza kwa munthu amene anali ku China . Analandila ndipo anandiuza kuti dzina lake ndi Katie . Kuyambila pamenepo , Katie akandiona , anali kubwela kudzandilankhula . Ndinam’phunzitsa maina a Cingelezi a zipatso ndiponso a ndiwo za masamba , ndipo iye anali kubweleza zimene ndinali kukamba . Ndinamuuzanso uthenga wa m’Baibulo ndi kum’gawila buku la Zimene Baibo Imaphunzitsa . Koma patapita milungu yocepa , ndinaleka kumuona . Mlungu wotsatila , mtsikanayo anandipatsa foni ndi kukamba kuti , “ Pali munthu wina wa ku China amene afuna kukamba nanu . ” Ndinamuuza kuti , “ Sindidziŵa munthu aliyense ku China . ” Koma mtsikanayo analimbikila , conco ndinatenga foni ndi kukamba kuti , “ Halo , ndine Robison . ” Kenako ndinamva mau pa foniyo akuti , “ A Robby , ndine Katie . Conde nayenso m’phunzitseni zimene munandiphunzitsa . ” Ndinati , “ Ndidzacita zimene ndingathe Katie . Zikomo kwambili pondidziŵitsa kumene uli . ” Ndinapitiliza kukambilana ndi mkulu wakeyo kwa kanthawi , koma nayenso anasiya kuoneka . Ndikhulupilila kuti anthu a m’banja langa ndi anzanga amene anamwalila adzakhalanso ndi moyo m’dziko latsopano . Pamene nkhaniyi inali kukonzedwa , m’bale Corwin Robison anamwalila ali wokhulupilika kwa Yehova . Kodi zimene Abulahamu anali kudziŵa zokhudza Mulungu , ndiponso zocitika pa umoyo wake zinalimbitsa bwanji cikhulupililo cake ? Kodi Abulahamu anacita ciani kuti alimbitse ubwenzi wake ndi Mulungu ? Kodi mungatengele bwanji citsanzo ca Abulahamu kuti mulimbitse ubwenzi wanu ndi Yehova ? 1 , 2 . ( a ) Timadziŵa bwanji kuti anthu angakhale mabwenzi a Mulungu ? 3 , 4 . ( a ) Ndi nthawi iti pamene cikhulupililo ca Abulahamu cinayesedwa kwambili ? ( b ) N’cifukwa ciani Abulahamu anali wokonzeka kupeleka Isaki nsembe ? Kodi zioneka kuti Abulahamu anaphunzila bwanji za Yehova ? Nanga zimene anaphunzila zinam’thandiza bwanji ? Kodi tiyenela kucita ciani kuti tim’dziŵe bwino Yehova ndi kum’mvela ? 9 , 10 . ( a ) Kodi cofunika n’ciani kuti ubwenzi ukhale wolimba ? ( b ) N’ciani cionetsa kuti Abulahamu analimbitsa ubwenzi wake ndi Yehova ndi kuuona kukhala wamtengo wapatali ? Abulahamu anaona ubwenzi wake ndi Yehova kukhala cinthu camtengo wapatali ndipo anali kuuteteza . N’cifukwa ciani Abulahamu anada nkhawa atamva kuti Sodomu ndi Gomora adzaonongedwa ? 12 , 13 . ( a ) Kodi zimene Abulahamu anaphunzila ndi zocitika pa umoyo wake zinamuthandiza bwanji panthawi ina ? ( b ) N’ciani cimene cionetsa kuti Abulahamu anali kukhulupilila Yehova ? Ndi mavuto otani amene mumakumana nao potumikila Yehova ? Nanga citsanzo ca Abulahamu cingakuthandizeni bwanji ? Abulahamu ndi Sara anadziŵa Yehova ndi kuyamba kumulambila Abulahamu anamwalila “ ali wokalamba , atakhala ndi moyo wabwino , wautali ndi wokhutila ” N’cifukwa ciani ndife otsimikiza kuti Abulahamu sanadziimbepo mlandu cifukwa cokhala wokhulupilika kwa Yehova ? Kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ? Nanga tidzakambilana ciani m’nkhani yotsatila ? Motelo , tiyeni tonse tiziyesetsa kutengela cikhulupililo ca Abulahamu . ( Ŵelengani Aheberi 6 : 10 - 12 . ) M’nkhani yotsatila , tidzakambilana zitsanzo zitatu za anthu okhulupilika amene anakhala mabwenzi a Mulungu . Kodi tingaphunzile ciani pa ubwenzi wa Rute ndi Mulungu ? N’cifukwa ciani Mfumu Hezekiya anali bwenzi lapamtima la Yehova ? Ndi makhalidwe otani amene Mariya , mai wa Yesu , anali nao omwe anam’pangitsa kukhala bwenzi la Yehova Mulungu ? 1 - 3 . ( a ) N’cifukwa ciani sitiyenela kukaikila zoti tingakhale mabwenzi a Mulungu ? ( b ) Tikambilana za ndani m’nkhani ino ? Kodi Rute anafunika kupanga cosankha cotani ? Nanga n’cifukwa ciani kusankha zimenezo kunali kovuta ? ( a ) Ndi cosankha ca nzelu citi cimene Rute anapanga ? ( b ) N’cifukwa ciani Boazi anakamba kuti Rute anathaŵila m’mapiko mwa Yehova ndi kupezamo citetezo ? N’ciani cingathandize anthu amene amawayawaya kudzipeleka kwa Yehova ? 9 , 10 . ( a ) N’cifukwa ciani cinali capafupi kuti Hezekiya akwiile Mulungu ? ( b ) N’cifukwa ciani sitiyenela kukwiila Mulungu ? ( c ) Nanga n’cifukwa ciani sitiyenela kuganiza kuti banja limene tinakulilamo likhoza kuticititsa kukhala munthu woipa kapena wabwino ? Acicepele ambili aphunzila coonadi ngakhale kuti anakulila m’banja la citsanzo coipa ( Onani ndime 9 ndi 10 ) N’ciani cinacititsa kuti Hezekiya akhale mfumu yabwino ya Yuda ? ( Ŵelengani 2 Mafumu 18 : 5 , 6 . ) Mofanana ndi Hezekiya , kodi anthu ambili masiku ano aonetsa bwanji kuti ndi mabwenzi a Yehova ? N’cifukwa ciani udindo umene Mariya anapatsidwa unaoneka wovuta kwambili ? Koma kodi Mariya anayankha ciani kwa Gabirieli ? N’ciani cionetsa kuti Mariya anali mmvetseli wabwino ? Pa zocitika zonsezi , Mariya anamvetsela ndi kusunga zimene anamva , kenako anayamba kuzisinkhasinkha . — Ŵelengani Luka 2 : 16 - 19 , 49 , 51 . Tiphunzila ciani zokhudza Mariya tikaona zimene anali kukamba ? Tingatengele bwanji cikhulupililo ca Mariya ? Kodi tingayembekezele ciani ngati titengela zitsanzo za m’Baibulo za anthu a cikhulupililo ? KUMBUKILANI tsiku limene munasangalala kwambili pa umoyo wanu . Kodi ndi tsiku limene mwana wanu woyamba anabadwa ? Mosakaikila , kucokela pamene munabatizidwa , mwapeza cimwemwe cacikulu potumikila Yehova . Kodi ndi zinthu ziti zimene zimatilimbikitsa kupitiliza kutumikila Yehova mwacimwemwe ? ( 1 Yohane 5 : 3 ) Kumbukilani mau a Yesu akuti : “ Bwelani kwa ine nonsenu ogwila nchito yolemetsa ndi olemedwa , ndipo ndidzakutsitsimutsani . Timatumikila Mulungu wacimwemwe , amene anatipatsa moyo . Ganizilani za Héctor , amene anatumikila Yehova kwa zaka 40 monga woyang’anila dela . Iye anati : “ Cimandiŵaŵa kuona mkazi wanga akudwaladwala , ndipo ndimavutika pom’samalila . Koma sindilola kuti zimenezi zindilande cimwemwe canga potumikila Mulungu woona . Kudziŵa kuti ndili ndi moyo cifukwa ca Yehova , amene analenga munthu n’colinga , kumandicititsa kum’konda kwambili ndi kum’tumikila ndi mtima wonse . Ndimayesetsa kukhala wacangu pa nchito yolalikila , ndiponso ndimaganizila za madalitso amene Ufumu wa Mulungu udzabweletsa . Timatha kukhala acimwemwe cifukwa cakuti Yehova watipatsa nsembe ya dipo . Zoonadi , “ Mulungu anakonda kwambili dziko mwakuti anapeleka Mwana wake wobadwa yekha , kuti aliyense wokhulupilila iye asaonongeke , koma akhale ndi moyo wosatha . ” Jesús anasintha umoyo wake ndipo anatumikila Yehova mwacimwemwe kwa zaka zambili Ndinali kucita zimenezi kuti ndipeze ndalama zambili . Kenako , ndinaphunzila za Yehova ndi kuti anapeleka Mwana wake wokondedwa cifukwa ca anthu , ndipo ndinayamba kufuna kum’tumikila . Conco , ndinadzipeleka kwa Yehova . Pambuyo poseŵenza kwa zaka 28 pa kampani , ndinasankha zosiya nchito ndi kuyamba utumiki wa nthawi zonse . ” Kodi mukumbukila mmene umoyo wanu unalili musanadziŵe Yehova ? Mtumwi Paulo anakumbutsa Akristu a ku Roma kuti poyamba anali “ akapolo a ucimo , ” koma anakhala “ akapolo a cilungamo . ” “ Ngati pali zaka zosangalatsa kwambili pa umoyo wanga , ndi zaka zimene ndakhala ndikutumikila Yehova . ” ​ — Jaime Kuti asinthe umoyo wake wakale , Jaime anapempha Yehova kuti am’thandize kukhala ndi cikhulupililo mwa Iye . Jaime anati : “ Pang’ono ndi pang’ono , ndinadziŵa kuti kuli Tate wacikondi ndiponso Mulungu wacifundo . Zikanakhala kuti sindinasinthe umoyo wanga , ndikanaphedwa monga anzanga ena amene anali ankhonya . Ngati pali zaka zosangalatsa kwambili pa umoyo wanga , ndi zaka zimene ndakhala ndikutumikila Yehova . ” Kodi Yonatani mwana wa Mfumu Sauli anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Yehova ? Tingaonetse bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Mulungu ngati munthu winawake waudindo sacita zinthu mwacilungamo ? Tingaonetse bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Yehova ngati anthu ena sakutimvetsetsa kapena akuticitila zinthu mopanda cilungamo ? N’cifukwa ciani ubwenzi wa Davide ndi Yonatani ndi citsanzo cabwino ca kukhulupilika ? N’ciani cinali cofunika kwambili kwa Yonatani kuposa kukhala wokhulupilika kwa Davide ? ( a ) N’ciani cingatithandize kukhaladi osangalala komanso okhutila ? N’cifukwa ciani cinali covuta kwa Aisiraeli kukhala okhulupilika kwa Mulungu pamene Sauli anali mfumu ? N’ciani cionetsa kuti Yonatani anakhalabe wokhulupilika kwa Yehova ? Kodi kulemekeza amene amatitsogolela kumaonetsa bwanji kuti ndife okhulupilika kwa Mulungu ? ( Ŵelengani Aroma 13 : 1 , 2 . ) N’cifukwa ciani Yonatani anasankha kukhala wokhulupilika kwa Davide ? Kodi kukonda Mulungu kumatithandiza bwanji kusankha kukhala wokhulupilika kwa iye ? Kodi kukhala wokhulupilika kwa Mulungu kungatithandize bwanji kulimbana ndi mavuto m’banja ? N’ciani cimene tiyenela kucita ngati m’bale waticitila zinthu mopanda cilungamo ? Ndi pa zocitika ziti pamene tiyenela kukhala okhulupilika kwa Yehova ndi kupewa kudzikonda ? [ 1 ] ( ndime 9 ) Maina ena asinthidwa . N’cifukwa ciani Yonatani ndi Abineri anali kuona Davide mosiyana kwambili ? Ndi makhalidwe ati amene angatithandize kukhala okhulupilika kwa Mulungu ? Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ? ( a ) Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ? ( b ) Tikambilana zitsanzo zina ziti ? Ndi mfundo yofunika iti imene tikuphunzila pa maganizo olakwika amene Abisai anali nao ? Ngakhale kuti timafuna kukhala okhulupilika kwa acibale athu ndi anzathu , n’cifukwa ciani tiyenela kusamala ? Kodi mlongo wina anaonetsa bwanji kukhulupilika kwa Mulungu ngakhale panthawi zovuta ? Ndi makhalidwe ati amene angatithandize kukhala okhulupilika kwa Yehova ? Kodi zitsanzo za m’Baibulo za Abineri , Abisalomu , ndi Baruki zingatipindulitse bwanji ? Koma iwe , ukufunafunabe zinthu zazikulu . Fotokozani citsanzo coonetsa kuti sitingakhale okhulupilika kwa Mulungu ngati ndife odzikonda ? Pambuyo popeleka mapemphelo ambili uku ndikulila , ndinaleka kum’tumila mameseji . Davide atacimwa , kodi Natani anaonetsa bwanji kuti anali wokhulupilika kwa Mulungu ndiponso kwa Davide ? Mungaonetse bwanji kuti ndinu wokhulupilika kwa Yehova ndi kwa mnzanu kapena wacibale ? N’cifukwa ciani Husai anafunika kulimba mtima kuti akhalebe wokhulupilika kwa Mulungu ? N’cifukwa ciani tifunika kulimba mtima kuti tikhale okhulupilika ? Ndinapempha Yehova kuti andithandize kukhala wolimba mtima kuti ndisasinthe maganizo anga . Tsopano , io anasintha ndipo ndimapita kukawacezela nthawi zambili . ” — Ŵelengani Miyambo 29 : 25 . [ 1 ] ( ndime 7 ) maina ena asinthidwa . “ Ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja sayamba wakhala pansi ndi kuŵelengela ndalama zimene adzaononge , kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanila kumalizila nsanjayo ? ” — LUKA 14 : 28 . Kodi kukhala wokhwima mwakuuzimu kumatanthauza ciani ? Kodi mungadziŵe bwanji kuti mwasankha kucokela pansi pamtima kuti mubatizidwe ? Kodi kudzipeleka n’kutani ? Nanga kumagwilizana bwanji ndi kubatizidwa ? 1 , 2 . ( a ) N’ciani cimasangalatsa anthu a Mulungu masiku ano ? ( b ) Kodi makolo acikristu ndi akulu angathandize bwanji acinyamata kumvetsa tanthauzo la ubatizo ? Kenako anati : “ Koma n’cifukwa ciani ufuna kubatizidwa ? ” ( Ŵelengani Luka 14 : 27 - 30 . ) ( a ) Kodi zimene Yesu ndi Petulo anakamba zimaonetsa bwanji kuti ubatizo ndi wofunika ? ( Mateyu 28 : 19 , 20 ; 1 Petulo 3 : 21 ) ( b ) Tikambilana mafunso ati ? ( 2 ) Kodi ndikufuna kubatizidwa mwa kufuna kwanga ? ( 3 ) Kodi ndimamvetsetsa tanthauzo la kudzipeleka kwa Yehova ? 4 , 5 . ( a ) N’cifukwa ciani ubatizo si wa anthu acikulile okha ? ( b ) Kodi kukhala Mkristu wokhwima kumatanthauza ciani ? Pa Miyambo 20 : 11 timaŵelenga kuti : “ Ngakhale mnyamata amadziŵika ndi nchito zake , ngati zocita zake zili zoyela ndiponso zoongoka . ” 6 , 7 . ( a ) Fotokozani mavuto amene Danieli anakumana nao ku Babulo . ( b ) Kodi Danieli anaonetsa bwanji kuti anali wofikapo mwakuuzimu ? Wacinyamata wofikapo mwakuuzimu sakhala bwenzi la Mulungu ku Nyumba ya Ufumu koma akapita kusukulu n’kukhala bwenzi la dziko ( Onani ndime 8 ) Wacinyamata wotelo sacita zinthu monga bwenzi la Mulungu ku Nyumba ya Ufumu koma akapita kusukulu n’kukhala bwenzi la dziko . 9 , 10 . ( a ) Kodi wacinyamata angapindule bwanji akaganizila zimene anacita atayesedwa ? 11 , 12 . ( a ) Kodi munthu amene afuna kubatizidwa ayenela kuonetsetsa kuti wacita ciani ? ( b ) N’ciani cidzakuthandizani kuona moyenelela makonzedwe a Yehova a ubatizo ? Mungadziŵe bwanji ngati cosankha canu cofuna kubatizidwa ndi cocokeladi pansi pa mtima ? Iye wakupatsani mapepala oonetsa kuti galimotoyo ndi yanu , ndipo akukuuzani kuti : “ Galimotoyi ndi yanu . ” 18 , 19 . ( a ) Kodi mau amene Rose ndi Christopher anakamba akuonetsa bwanji kuti ubatizo umabweletsa madalitso ? ( b ) Kodi mumamva bwanji mukaganizila za ubatizo ? Ndimakhala ndi zocita zambili zosangalatsa potumikila Yehova ndi gulu lake . ” Kodi ‘ kukhulupilila pambuyo pokhutila ’ kumatanthauza ciani ? Kodi ‘ makhalidwe oyela ’ ndiponso ‘ nchito zosonyeza kudzipeleka kwa Mulungu ’ n’ciani ? Kodi kusinkhasinkha za dipo kungakuthandizeni bwanji kuyamikila kwambili Yehova ? 1 , 2 . ( a ) N’cifukwa ciani ubatizo ndi cosankha cacikulu ? Kodi acinyamata angaphunzile ciani pa citsanzo ca Timoteyo ? Fotokozani mmene nkhani zakuti “ Kodi Baibulo Limaphunzitsa Ciani ? ” za pa webusaiti yathu zingakuthandizileni kulimbitsa cikhulupililo . Mlongo wina wacitsikana anati : “ Ndikalibe kuganiza zobatizidwa , ndinaphunzila Baibulo ndipo ndinakhulupilila kuti ici ndiye cipembedzo coona . Ndipo tsiku ndi tsiku , cikhulupililo canga cinali kulimbilalimbila . ” N’cifukwa ciani Mkristu wobatizidwa ayenela kukhala ndi makhalidwe oonetsa kuti ali ndi cikhulupililo ? Baibulo limati : “ Cikhulupililo pacokha , ngati cilibe nchito zake , ndi cakufa . ” Kodi ‘ makhalidwe oyela ’ n’ciani ? Mwacitsanzo , ganizilani za miyezi 6 yapitayi . Kodi “ nchito zosonyeza kuti ndinu odzipeleka kwa Mulungu ” zimaphatikizapo ciani ? Ndipo inuyo mumaziona bwanji ? N’ciani cingakuthandizeni kucita “ nchito zosonyeza kuti ndinu odzipeleka kwa Mulungu ” ? Nanga acinyamata ena apindula bwanji ndi mbali imeneyi ? Nanga mapemphelo anuwo amasonyeza kuti mumakondadi Yehova ? ” “ Kodi mumaloŵa mu utumiki ngakhale ngati makolo anu sanaloŵe ? ” Mlongo wina wacitsikana , dzina lake Tilda anati : “ Ndinalemba zolinga zanga pa masamba amenewo . Ndinayamba kukwanilitsa zolinga zimenezo cimodzi ndi cimodzi , ndipo patapita caka cimodzi ndinakhala woyenelela kubatizidwa . ” Kodi mungapitilize kutumikila Yehova ngakhale makolo anu atasiya kum’tumikila ? N’cifukwa ciani muyenela kudzipeleka mwa kufuna kwanu ? 16 , 17 . ( a ) N’ciani ciyenela kulimbikitsa munthu kukhala Mkristu ? ( b ) Ndi fanizo liti limene lionetsa kuti tifunika kuyamikila dipo ? Yesu anamuyankha kuti : “ Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse , moyo wako wonse , ndi maganizo ako onse . ” ( Ŵelengani 2 Akorinto 5 : ​ 14 , 15 ; 1 Yohane 4 : ​ 9 , 19 . ) 18 , 19 . ( a ) N’cifukwa ciani simuyenela kuopa kudzipeleka kwa Yehova ? ( b ) Kodi kutumikila Yehova kungakupindulitseni bwanji ? Kodi wacinyamata angacite ciani kuti akhale wokonzeka kudzipeleka ndi kubatizidwa ? “ Kodi Ndingatani Kuti Mapemphelo Anga Azikhala Abwino ? ” — November 2008 “ Kodi Ndingatani Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzindisangalatsa ? ” — April 2009 “ Kodi Ndimadziwa Mfundo Zimene Ndimayendera ? ” — October 2011 “ Kodi Ndingatani Kuti Ndizisangalala Ndikamawerenga Baibulo ? ” — February 2012 “ N’chifukwa Chiyani Ndiyenera Kumapita ku Misonkhano ya Mpingo ? ” — April 2012 Kodi kugwila nchito yolalikila kumatithandiza bwanji kukhala ogwilizana ? Ndi zinthu zina ziti zimene tingacite kuti tilimbitse mgwilizano mumpingo ? N’ciani cingathandize mwamuna ndi mkazi kukhala ogwilizana ? Kuyambila paciyambi , kodi Mulungu wakhala akugwila bwanji nchito ndi ena ? ( a ) Kodi Akristu oyambilila anali kudziŵika ndi mzimu wotani ? ( b ) Kodi tikambilana mafunso ati ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 12 : 4 - 6 , 12 . ) N’ciani cimene timakwanitsa kucita tikamagwila nchito yolalikila mogwilizana ? 8 , 9 . ( a ) Ndi fanizo lotani limene Paulo anapeleka kuti athandize Akristu kukhala ogwilizana ? ( b ) Tingatani kuti tikhale ogwilizana mumpingo ? ( Welengani Aefeso 4 : 15 , 16 . ) N’ciani cingathandize kuti onse m’banja azigwilizana ? Ngati mwamuna kapena mkazi wanu satumikila Yehova , kodi mungacite ciani kuti banja likhalebe lolimba ? Kodi Akristu amene akhala m’banja kwa zaka zambili angathandize bwanji acinyamata amene ali pabanja ? Ndi ciyembekezo cotani cimene atumiki a Mulungu ali naco ? Kodi Yehova anapeleka malangizo otani m’nthawi ya Nowa ndi ya Mose ? Ndi malangizo ena ati amene Mulungu anapeleka kwa Akristu ? Tingaonetse bwanji kuti timafuna kutsogoleledwa ndi Mulungu ? 1 , 2 . ( a ) Ndi cenjezo lotani limene lateteza anthu ambili ? N’ciani cinacititsa kuti anthu akhale pa njila yopita ku imfa ? ( a ) N’cifukwa ciani Mulungu anapeleka malangizo ena pambuyo pa Cigumula ? ( b ) Pamene zinthu zinasintha , kodi Mulungu anaonetsa bwanji maganizo ake ? Nanga n’cifukwa ciani ? N’cifukwa ciani anthu a Mulungu anafunika kumvela malamulo amene Mulungu anawapatsa kudzela mwa Mose ? Nanga anafunika kuwaona bwanji malamulowo ? ( a ) N’cifukwa ciani Yehova anapatsa malangizo anthu ake ? ( b ) Kodi Cilamulo cinakhala bwanji mtsogoleli kwa Aisiraeli ? N’cifukwa ciani tiyenela kutsatila mfundo za m’Cilamulo ca Mose ? Ndi kusintha kotani kumene kunacititsa kuti Mulungu apelekenso malangizo atsopano ? N’cifukwa ciani mpingo wacikristu unapatsidwa malamulo atsopano ? Ndithudi , “ Mulungu alibe tsankho . Kodi “ cilamulo ca Kristu ” cinali kukhudza mbali ziŵili ziti za umoyo wa Mkristu ? Zimenezi zinatanthauza kuti Akristu anayenela kulalikila munthu aliyense padziko lapansi . 13 , 14 . ( b ) Tikuphunzila ciani pa citsanzo cimene Yesu anapeleka ? Kodi zinthu zasintha bwanji masiku ano ? Nanga Mulungu amatitsogolela bwanji ? Kodi tiyenela kucita ciani ndi malangizo amene timalandila ? Kodi mumaona kuti malangizo amenewa ndi ocokeladi kwa Mulungu ? Ndi mipukutu yotani imene idzafunyululidwa mtsogolo ? Ifotokozanso nchito imene khalidwe la kupilila liyenela kumaliza mwa aliyense wa ife . Kodi citsanzo ca Yefita ndi mwana wake cingatithandize bwanji kupewa maganizo a dziko ? Ndi mfundo za m’Baibulo ziti zimene zimakuthandizani kuthetsa mikangano ? Kodi nkhani ino yakulimbikitsani bwanji kudzipeleka pocilikiza Ufumu wa Mulungu ? Kodi Yefita ndi mwana wake anakumana ndi zocitika zotani ? Kodi citsanzo ca Yefita ndi mwana wake cingatithandize bwanji masiku ano ? 4 , 5 . ( a ) Kodi Yehova anapeleka lamulo lotani kwa Aisiraeli pamene analoŵa m’Dziko Lolonjezedwa ? ( b ) Malinga ndi Masalimo 106 , kodi mtundu wa Aisiraeli unakumana ndi mavuto otani cifukwa ca kusamvela ? Ndi zinthu ziti zimene anthu m’dzikoli amakonda ? ( a ) Ndi zinthu ziti zimene anthu a mtundu wa Yefita anam’citila ? 8 , 9 . ( a ) Ndi mfundo ziti za m’Cilamulo ca Mose zimene zinathandiza Yefita ? ( b ) N’ciani cimene cinali cofunika kwambili kwa Yefita ? Kodi tingacite ciani kuti mfundo za m’Baibulo zitithandize kucita zinthu monga Mkristu ? Kodi Yefita analonjeza ciani ? Nanga lonjezolo linali kutanthauza ciani ? Kodi mau a Yefita a pa Oweruza 11 : 35 amaonetsa bwanji cikhulupililo cake ? Kodi ndi lonjezo lotani limene ambili a ife tinapanga ? Kodi mwana wa Yefita anacita ciani atamva za lonjezo la atate ake ? ( a ) Kodi tingatsanzile bwanji cikhulupililo ca Yefita ndi mwana wake ? ( b ) Kodi mau a pa Aheberi 6 : 10 - 12 amakulimbikitsani bwanji kukhala odzipeleka ? Kodi taphunzila ciani pa nkhani ya Yefita ndi mwana wake ? Nanga tingawatsanzile bwanji ? Kodi ‘ kulola kuti kupilila kumalize kugwila nchito yake ’ kumatanthauza ciani ? 1 , 2 . ( a ) Tingaphunzilepo ciani pa citsanzo ca kupilila kwa Gidiyoni ndi asilikali ake 300 ? ( Onani cithunzi pamwambapa . ) ( b ) Malinga ndi Luka 21 : 19 , n’cifukwa ciani kupilila n’kofunika ? Adani athu ndi Satana , dziko lake , ndi kupanda ungwilo kwathu . Kodi tingaphunzilepo ciani pa zitsanzo za anthu amene anapilila m’mbuyomu ? N’cifukwa ciani tingakambe kuti cikondi n’cimene cimatilimbikitsa kupilila ? ( Ŵelengani 1 Akorinto 13 : 4 , 7 . ) ( Luka 22 : 41 , 42 ) Kukonda abale athu kumatilimbikitsa kunyalanyaza zolakwa zao . N’cifukwa ciani Yehova ndiye yekha amene angatithandize kwambili kupilila ? Yehova ndi “ Mulungu amene amatipatsa mphamvu kuti tithe kupilila ndiponso amene amatitonthoza . ” Mogwilizana ndi zimene Baibulo linalonjeza , kodi Yehova amapeleka bwanji “ njila yopulumukila ” ciyeso ? Fotokozani citsanzo coonetsa kuti timafunika cakudya cakuuzimu kuti tithe kupilila . 8 , 9 . ( a ) Malinga ndi Yobu 2 : 4 , 5 , ndi nkhani iti imene imaloŵetsedwamo tikakumana ndi ziyeso ? ( b ) Mukakumana ndi mavuto , ndi zocitika zosaoneka ziti zimene muyenela kuganizila ? ( Yobu 2 : 4 , 5 ) Kodi tsopano Satana analeka kuneneza anthu a Mulungu ? N’cifukwa ciani tiyenela kukambilana za “ anthu amene anapilila ” ? Tikuphunzilapo ciani pa citsanzo ca akerubi amene anaikidwa mu Edeni ? Akerubi . N’ciani cinathandiza Yobu kupilila ziyeso ? Yobu anakhala ndi moyo wautali ndiponso wokhutilitsa . — Yobu 42 : 10 , 17 . Malinga ndi 2 Akorinto 1 : 6 , kodi ena anapindula bwanji cifukwa ca kupilila kwa Paulo ? ( Ŵelengani 2 Akorinto 1 : 6 . ) 15 , 16 . ( a ) Ndi “ nchito ” yotani imene kupilila kuyenela kumaliza ? ( b ) Pelekani zitsanzo zoonetsa zimene tingacite kuti ‘ tilole kupilila kumaliza kugwila nchito yake . ’ Kupilila mayeselo kumatithandiza kukonza umunthu wathu ( Onani ndime 15 ndi 16 ) 17 , 18 . ( a ) Pelekani citsanzo coonetsa kuti tifunika kupilila mpaka mapeto . ( b ) Kodi sitiyenela kukaikila za ciani pamene mapeto akuyandikila ? Pakuti ndatsimikiza mtima kuti imfa , moyo , angelo , maboma , zinthu zimene zilipo , zinthu zimene zikubwela m’tsogolo , mphamvu , msinkhu , kuzama , kapena colengedwa cina ciliconse , sicidzatha kutilekanitsa ndi cikondi ca Mulungu cimene cili mwa Kristu Yesu Ambuye wathu . ” [ 1 ] ( ndime 11 ) Mungalimbikitsidwenso kwambili mukaŵelenga za kupilila kwa anthu a Mulungu amakono . [ 2 ] ( ndime 12 ) Baibulo silikamba ciŵelengelo ca akerubi amene anapatsidwa udindo umenewu . NWT ] — MACHITIDWE 2 : 42 . mmene timalimbikitsila ena tikapezeka pa misonkhano . 1 - 3 . ( a ) Kodi Akristu amaonetsa bwanji kuti amafunitsitsa kupezeka pamisonkhano ? ( Onani cithunzi pamwambapa . ) ( b ) Tikambilana ciani m’nkhani ino ? Panthawi imeneyi , tinalimbikitsidwa ndipo cikhulupililo cathu cinalimba kwambili . ” Kodi misonkhano imatithandiza bwanji kuphunzila za Yehova ? Nanga yakuthandizani bwanji kunola luso lanu mu ulaliki ? Kodi misonkhano yathu imatithandiza bwanji kuti tikhalebe olimba ? ( Ŵelengani Machitidwe 15 : 30 - 32 . ) N’cifukwa ciani kupezeka pamisonkhano yathu n’kofunika ? Kodi kupezeka pamisonkhano , kupeleka mayankho , ndi kuimba nyimbo zimathandiza bwanji Akristu anzathu ? ( Onaninso Bokosi lakuti “ Amamvelako Bwino Akapezeka Pamisonkhano . ” ) 9 , 10 . ( a ) Fotokozani mmene mau a Yesu a pa Yohane 10 : 16 amatithandizila kumvetsa cifukwa cake kupezeka pamisonkhano n’kofunika kwambili . ( b ) Kodi kupezekapo kwathu pamisonkhano kungathandize bwanji anthu amene anakanidwa ndi mabanja ao ? “ POSACEDWAPA , ndinayamba kudwala matenda amene amacititsa kuti ndizivutika kufika pamisonkhano . Koma ndikakhala ndi mwai wopezekapo , ndimasangalala ndi cakudya cakuuzimu cimene Yehova amakonza . Popita kumisonkhano ndimakhala kuti sindikumvela bwino cifukwa ca matenda a shuga , vuto la mtima , ndi kuŵaŵa kwa nkhongono . Koma pambuyo pamisonkhano , ndimamvelako bwino . “ Tsiku loyamba kumva nyimbo nambala 68 , ya mutu wakuti ‘ Pemphero la Munthu Wovutika , ’ ikuimbidwa pamisonkhano , ndinakhudzika kwambili cakuti ndinagwetsa misozi . Makina amene amandithandiza kuti ndizimvetsela bwino , anandithandiza kumva mau a anthu onse amene anali kuimba ndipo ndinaimba nao pamodzi . Kodi pamisonkhano timakhala ndi mipata iti yolambila Yehova ? Kodi Yehova amamva bwanji tikamvela lamulo lakuti tizipezeka pamisonkhano ? Kodi kupezeka pamisonkhano kumatithandiza bwanji kuyandikila Yehova ndi Yesu ? Ngati tipezeka pamisonkhano , kodi timaonetsa bwanji kuti tifuna kumvela Mulungu ? 16 , 17 . ( a ) Tidziŵa bwanji kuti Akristu oyambilila anali kuona misonkhano kukhala yofunika kwambili ? ( b ) Kodi m’bale George Gangas anali kuiona bwanji misonkhano yacikristu ? Ndimakonda kufika mwamsanga pa Nyumba ya Ufumu , ndipo ndimakhala mmodzi wa anthu othela kucoka . Ndimasangalala kuceza ndi anthu a Mulungu . Ndikakhala pamodzi ndi abale ndi alongo , ndimamva ngati ndikuceza ndi banja langa , m’paladaiso wauzimu . Kodi misonkhano mumaiona bwanji ? Nanga ndinu ofunitsitsa kucita ciani ? [ 2 ] ( ndime 3 ) Onani bokosi lakuti “ Cifukwa Cake Tiyenela Kupezeka Pamisonkhano . ” Kumeneko amamva uthenga wabwino kwa Mboni zimene zimacita ulaliki wa poyela Malo okhala masisitele ku Zaragoza , ku Spain ( kumanzele ) Baibulo la Cináka - kolunga ( kulamanja ) Koma sindinali kudziŵa ngati ndinali kucita zinthu zoyenela . Ndikumbukila tsiku lina ndinapemphela kuti , “ Yehova , ndiyamikila kwambili cifukwa simunandisiye , ndipo nthawi zambili munali kundipatsa mwai wopeza cidziŵitso colondola ca m’Baibulo cimene ndinali kufuna . ” Nanga anthu a m’banja langa ndi mamembala a chalichi canga adzandiona bwanji ? ” Ndinam’yankha kuti : “ Nanga muganiza kuti Mulungu adzamvela bwanji ? ” Iwo anamwalila kutatsala miyezi iŵili kuti abatizidwe . Kodi tiyenela kucita ciani ngati zavuta kuti tipewe kutenga mbali m’ndale ? Tingaphunzile ciani kwa atumiki okhulupilika a Yehova amene sanatengemo mbali m’ndale ? Tingacite ciani kuti tizimvela Mulungu ndi maboma a anthu ? Kodi timaonetsa bwanji kuti sititenga mbali m’ndale za dzikoli ? ( a ) Tidziŵa bwanji kuti mtsogolomu zidzakhala zovuta kupewa kutenga mbali m’ndale ? ( b ) N’cifukwa ciani tifunika kukonzekela tsopano kuti tisadzatenge mbali m’ndale ? Kodi akuluakulu a boma tiyenela kuwaona bwanji ? Tingacite ciani kuti tikhale “ ocenjela ” koma “ oona mtima ” ngati tayesedwa kuti titenge mbali m’ndale ? ( Ŵelengani Mateyu 10 : 16 , 17 . ) Ndi zinthu ziti zimene tiyenela kusamala nazo pamene tikukambilana ndi anthu ? Tingacite ciani kuti maganizo athu asasokonezeke ndi zimene ofalitsa nkhani amakamba ? 12 , 13 . ( a ) Kodi Yehova amawaona bwanji anthu ? ( b ) Tingadziŵe bwanji kuti tayamba kukonda kwambili dziko lathu ? Nanga m’Baibulo muli citsanzo cotani coonetsa kuti zimenezi n’zoona ? Kodi Baibulo lingatithandize bwanji kupewa kutenga mbali m’ndale ? ( Onaninso bokosi lakuti “ Mau a Mulungu Anawathandiza Kuti Asatenge Mbali m’Ndale . ” ) Tingaphunzile ciani kwa atumiki a Mulungu okhulupilika amene sanatenge mbali m’ndale ? ( Ŵelengani Danieli 3 : 16 - 18 . ) 18 , 19 . ( a ) Kodi abale ndi alongo mumpingo wanu angakuthandizeni bwanji kuti musatenge mbali m’ndale ? ( b ) Kodi mwatsimikiza mtima kucita ciani ? “ Kuganizila kwambili lemba la Miyambo 27 : 11 , Mateyu 26 : 52 , ndi la Yohane 13 : 35 kunandilimbikitsa kukana kuloŵa usilikali . Malemba amenewa anandithandizanso kukhala wodekha pamene anali kundiimba mlandu . ” — Andriy , wa ku Ukraine . “ Lemba la Yesaya 2 : 4 linandithandiza kusatenga mbali m’ndale pamene ndinali kuyesedwa . Ndinali kuganizila za umoyo wamtendele umene tidzakhala nao m’paladaiso , pamene anthu sadzanyamulanso zida kuti aphe anzao . ” — Wilmer , wa ku Colombia . “ Sungani mtendele pakati panu . ” — MALIKO 9 : 50 . Kodi Yesu anapeleka malangizo otani otithandiza kuthetsa mikangano mwamtendele ? Ndi mafunso ati amene Mkristu ayenela kudzifunsa akamasankha mmene ayenela kuthetsela mikangano ? Kodi tingagwilitsile nchito bwanji malangizo a pa Mateyu 18 : 15 - 17 kuti tithetse mikangano ? Ndi mikangano yotani imene inalembedwa m’buku la Genesis ? Ndi mzimu wotani umene wafala padziko lonse ? Nanga pakhala zotsatilapo zotani ? Kodi Yesu anauza ophunzila ake kuti ayenela kucita ciani pakabuka mikangano ? 6 , 7 . ( a ) N’cifukwa ciani kuthetsa mikangano mwamsanga n’kofunika ? ( b ) Ndi mafunso otani amene anthu onse a Yehova ayenela kudzifunsa ? Atate wathu wakumwamba adzayankha mapemphelo ocokela pansi pamtima amenewo . — 1 Yohane 5 : 14 , 15 . Tiyenela kucita ciani munthu wina akatikhumudwitsa ? ( Ŵelengani Miyambo 10 : 12 ; 1 Petulo 4 : 8 . ) ( a ) Kodi mlongo wina anacita ciani anthu ena atamunena ? ( b ) Ndi lemba liti limene linathandiza mlongoyo kukhalabe wosangalala ? 11 , 12 . ( a ) Kodi Mkristu ayenela kucita ciani akaona kuti Mkristu mnzake ‘ ali naye cifukwa ’ ? Kodi woyang’anila wina anacita ciani atauzidwa mau oipa ? Nanga mwaphunzilapo ciani pa citsanzo cake ? 14 , 15 . ( a ) Ndi pa zocitika ziti pamene tingagwilitsile nchito malangizo amene ali pa Mateyu 18 : 15 - 17 ? ( b ) Ndi masitepe atatu ati amene Yesu anakamba ? N’ciani cionetsa kuti kutsatila malangizo a Yesu ndi njila yacikondi yothetsela mikangano ndiponso yothandiza ? Kodi tidzalandila madalitso otani tikamayesetsa kukhala mwamtendele ndi ena ? uthenga umene timalalikila ndiponso cifukwa cimene timalalikilila ? Kodi mau a Yesu a pa Mateyu 24 : 14 amayambitsa mafunso otani ? Mogwilizana ndi lemba la Mateyu 28 : 19 , 20 , kodi otsatila a Yesu ayenela kucita zinthu zinai ziti ? Kodi kukhala “ asodzi a anthu ” kumafuna ciani ? ( Ŵelengani Mateyu 4 : 18 - 22 . ) Ndi mafunso anai ati amene tifunika kuyankha ? Nanga n’cifukwa ciani ? N’cifukwa ciani tingakambe kuti Mboni za Yehova zimalalikila uthenga woyenela ? Tidziŵa bwanji kuti atsogoleli a machalichi acikristu salalikila uthenga woyenela ? Ndi colinga coipa citi cimene anthu ena amakhala naco pogwila nchito yolalikila ? ( Ŵelengani Machitidwe 20 : 33 - 35 . ) Kodi Mboni za Yehova zaonetsa bwanji kuti zimagwila nchito yolalikila ndi colinga cabwino ? Kodi Yesu ndi ophunzila ake anali kulalikila bwanji ? Kodi Mboni za Yehova zimasiyana bwanji ndi Machalichi Acikhristu pankhani yolalikila uthenga wabwino ? Ndiwo okha amene amalalikila kuti Yesu wakhala akulamulila monga Mfumu kuyambila mu 1914 . Kodi nchito yolalikila iyenela kugwilidwa pa mlingo wotani ? N’ciani cikuonetsa kuti Mboni za Yehova zikukwanilitsa ulosi wa Yesu malinga ndi mmene zimagwilila nchito yao ? Komanso webusaiti yathu ikupezeka m’zinenelo zoposa 750 . Tidziŵa bwanji kuti Mboni za Yehova zili ndi mzimu woyela wa Mulungu ? 17 , 18 . ( a ) N’cifukwa ciani tingakambe kuti ndi Mboni za Yehova zokha zimene zikulalikila uthenga wabwino wa Ufumu masiku ano ? ( b ) N’ciani cimatithandiza kupitiliza kugwila nchito imeneyi ? N’ciani cingatilepheletse kupindula ndi zinthu zina zakuuzimu ? Ndi malangizo ati amene angatithandize kupindula ndi mbali zonse za m’Baibulo ? Mungapindule bwanji mwa kuŵelenga zofalitsa zogaŵila ndiponso zimene amalembela acinyamata ? 1 , 2 . ( a ) Kodi Mboni za Yehova zimaliona bwanji Baibulo ? ( b ) Ndi mbali iti ya m’Baibulo imene mumakonda kwambili ? 3 , 4 . ( a ) Kodi zofalitsa zathu timaziona bwanji ? ( b ) Chulani zofalitsa zimene zimalembedwela anthu osiyanasiyana . Kodi Yehova amakondwela ndi ciani ? N’cifukwa ciani tiyenela kuŵelenga Baibulo tili ndi maganizo oyenela ? 8 , 9 . ( a ) Ndi mafunso ati amene tiyenela kudzifunsa tikamaŵelenga Baibulo ? ( b ) Kodi ziyeneletso zimene akulu Acikristu ayenela kukwanilitsa zimatiuza ciani ponena za Yehova ? Nanga ndingazigwilitsile nchito bwanji pothandiza anthu ena ? ’ ( Ŵelengani 1 Timoteyo 3 : 2 - 7 . ) 10 , 11 . ( a ) Pamene tiŵelenga ziyeneletso za akulu , kodi tingazigwilitsile nchito bwanji pa umoyo wathu ? ( b ) Nanga ndingazigwilitsile nchito bwanji pothandiza anthu ena ? 12 , 13 . ( a ) Ndi kufufuza kotani kumene tingacite pogwilitsila nchito zofufuzila zimene tili nazo ? ( b ) Kambani citsanzo coonetsa mmene kufufuza kungatithandizile kudziŵa mfundo zobisika . Kodi zofalitsa zimene zimalembedwela acinyamata zingawathandize bwanji ? Nanga ena zingawathandize bwanji ? N’cifukwa ciani Akristu acikulile ayenela kuŵelenga zofalitsa zimene zimalembedwela acinyamata ? Kodi zofalitsa zathu zimawathandiza bwanji acinyamata ? ( Ŵelengani Mlaliki 12 : 1 , 13 . ) Kodi Ndingatani Kuti Kuŵelenga Baibulo Kuzindisangalatsa ? ” Tingapindule bwanji ndi zofalitsa zogaŵila ? Tingaonetse bwanji kuti timayamikila Yehova cifukwa ca zofalitsa zimene amatipatsa ? Kodi zosankha zathu zingakhudze bwanji ifeyo ndiponso anthu ena ? Ngati Baibulo silinapeleke lamulo pankhani ina yake , kodi tingadziŵe bwanji zimene zingakondweletse Yehova ? Tingacite ciani kuti tiziona zinthu mmene Yehova amazionela ? Ndi malamulo ena ati amene amapezeka m’Baibulo ? Nanga kuwamvela kumatipindulitsa bwanji ? 2 , 3 . ( a ) N’cifukwa ciani Baibulo silipeleka malamulo pankhani zina ? ( b ) Tikambilana mafunso ati m’nkhani ino ? Nanga zingakhudze bwanji anthu ena ? Ngati m’Baibulo mulibe lamulo lacindunji pankhani ina yake , kodi tingadziŵe bwanji zimene Yehova afuna kuti ticite ? Kodi Yesu anazindikila bwanji zimene Yehova anali kufuna kuti iye acite ? ( Ŵelengani Mateyu 4 : 2 - 4 . ) Uzim’kumbukila m’njila zako zonse , ndipo iye adzawongola njila zako . Ndi mafunso ati amene tingadzifunse pamene tiŵelenga Baibulo kapena kucita phunzilo laumwini ? Kodi zofalitsa zathu ndi misonkhano zingatithandize bwanji kudziŵa mmene Yehova amaonela zinthu ? Pelekani citsanzo coonetsa kuti kudziŵa mmene Yehova amaonela zinthu kungatithandize kupanga zosankha mwanzelu . ( Ŵelengani Luka 18 : 29 , 30 . ) Kodi mungadziŵe bwanji ngati sitayilo inayake ya zovala ndi yovomelezeka kwa Yehova ? ( c ) Kodi tiyenela kucita bwanji tikafuna kupanga zosankha zazikulu ? Kodi timapindula bwanji tikapanga zosankha zimene zimakondweletsa Yehova ? N’zoona kuti sitingadziŵe zonse zokhudza Yehova . N’cifukwa ciani tiyenela kupitiliza kusintha zinthu zina pambuyo pobatizidwa ? N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tiziyesetsa kulimbana ndi zizoloŵezi zoipa ? Tingacite ciani kuti Mau a Mulungu apitilize kutisintha ? 1 - 3 . ( a ) Ndi zinthu ziti zimene zingativute kusintha pambuyo pa ubatizo ? ( b ) Ndi mafunso ati amene tingadzifunse ngati tikulephela kusintha zinthu zina zimene siticita bwino ? N’cifukwa ciani nthawi zina timalephela kukondweletsa Yehova ? Ndi zinthu ziti zimene tinasintha tikalibe kubatizika ? Nanga ndi zofooka ziti zimene tingakhale tikulimbana nazo mpaka pano ? 6 , 7 . ( a ) N’ciani cimacititsa kuti tikhale paubwenzi wabwino ndi Yehova ngakhale kuti ndife opanda ungwilo ? ( b ) N’cifukwa ciani sitiyenela kuopa kupempha Yehova kuti atikhululukile ? Tidziŵa bwanji kuti kuvala umunthu watsopano ndi cinthu cimene tifunika kucita nthawi zonse ? Kodi tifunika kucita ciani kuti Baibulo litithandize kusintha umunthu wathu ? Nanga tingadzifunse mafunso ati ? N’cifukwa ciani Yehova amafuna kuti tiziyesetsa kulimbana ndi zofooka zathu ? Kodi tingacite ciani kuti tikhale ndi makhalidwe amene Mulungu amakondwela nawo ? ( Onani bokosi lakuti “ Baibulo ndi Pemphelo Zinasintha Umoyo Wao . ” ) N’cifukwa ciani sitiyenela kutaya mtima ngati sitikusintha mwamsanga ? Kodi tidzapeza madalitso otani ngati tikhalabe okhulupilika kwa Yehova ? Tidziŵa bwanji kuti Baibulo lili ndi mphamvu zotithandiza kusintha umunthu wathu ? [ 1 ] ( ndime 1 ) Dzina lasinthidwa . Russell : “ Kupeleka mapemphelo opembedzela kwa Yehova ndi kuŵelenga Baibulo tsiku lililonse kwandithandiza . Cinanso cimene candithandiza ndi kuganizila lemba la 2 Petulo 2 : 11 ndiponso uphungu umene akulu anandipatsa . ” Maria Victoria : “ Ndinacondelela Yehova m’pemphelo kuti andithandize kulamulila lilime langa . Ndinaona kuti ndifunika kuleka kuceza ndi anthu amene amakonda kunena anzao . Pamene ndinaŵelenga lemba la Salimo 64 : 1 - 4 , ndinaona kuti ndifunika kusintha kuti anthu ena asamandiope . Ndinadziŵanso kuti ndikapitiliza kunena anthu ena ndidzakhala citsanzo coipa ndipo ndidzanyozetsa dzina la Yehova . ” Linda : “ Ndinayesetsa kutudziŵa bwino tumapepala tonse twa uthenga n’colinga cakuti ndizikhala okonzeka kugaŵila anthu ena . Kulalikila ndi anthu amene amagwilitsila njila zosiyanasiyana mu utumiki , kwandithandiza kwambili . Komanso ndimadalila Yehova kudzela m’pemphelo . ” Ife tonse timacita zinthu zimene zingakhumudwitse anthu ena . mmene Yehova amasankhila anthu amene afuna kuwaumba ? mmene Mulungu amaumbila anthu amene amamumvela ? Kodi tingatengele bwanji citsanzo ca Aisiraeli olapa ? Kodi Yehova amasankha bwanji anthu amene amawakokela kwa iye ? ( Ŵelengani 1 Samueli 16 : 7b . ) Kodi kudziŵa kuti Yehova ni amene amatiumba , kuyenela kukhudza bwanji mmene timaonela ( a ) anthu a m’gawo lathu ? Patapita nthawi , n’nakumana ndi banja lina limene n’nakonda cifukwa ca makhalidwe awo abwino . Tsiku lina n’nadabwa kwambili n’tadziŵa kuti iwo anali a Mboni za Yehova . Khalidwe lawo labwino linan’cititsa kuzindikila kuti n’nali kuzonda a Mboni za Yehova cifukwa cosawadziŵa bwino ndiponso cifukwa ca zinthu zabodza zimene ena anali kuniuza zokhudza iwo . ” ( Ŵelengani Aheberi 12 : 5 , 6 , 11 . ) Kodi Yehova amatiphunzitsa bwanji masiku ano ? Nanga maphunzilo amenewa adzapitiliza bwanji mtsogolo ? ( Yohane 13 : 35 ) Ndipo taphunzila kukonda anthu ena . Kodi Yesu anaonetsa bwanji luso ndi kuleza mtima kwa Woumba Wamkulu ? ( Ŵelengani Salimo 103 : 10 - 14 . ) Kodi Davide anaonetsa bwanji kuti anali monga dothi lofewa ? Nanga tingatengele bwanji citsanzo cake ? Kodi Yehova amatiumba bwanji pogwilitsila nchito mzimu woyela ndi mpingo wacikhiristu ? Ngakhale kuti Yehova amatiumba , kodi amalemekeza bwanji ufulu wathu wosankha ? Kodi ophunzila Baibulo amaonetsa bwanji kuti afuna kuumbidwa ndi Yehova ? ( a ) Mumamvela bwanji mukaganizila kuti Yehova amakuumbani ? ( b ) Tidzaphunzila ciani m’nkhani yotsatila ? Kodi Yehova Mulungu wathu ni “ Yehova mmodzi ” m’njila ya bwanji ? Tingaonetse bwanji kuti timalambila “ Yehova mmodzi ” ? Tingacite ciani kuti tikhalebe amtendele ndi ogwilizana ? ( b ) N’cifukwa ciani Mose anakamba mau amenewo ? 4 , 5 . ( a ) Kodi mau akuti “ Yehova mmodzi ” atanthauza ciani ? ( b ) Nanga Yehova amasiyana bwanji ndi milungu ya mitundu ina ? Kodi mau akuti “ mmodzi , ” amatanthauzanso ciani ? Nanga Yehova anaonetsa bwanji kuti ni “ mmodzi ” ? 8 , 9 . ( a ) Kodi Yehova amafuna kuti amene amamulambila azicita ciani ? ( b ) Kodi Yesu anaonetsa bwanji kuti mau a Mose ni ofunika kwambili ? ( Ŵelengani Maliko 12 : 28 - 31 . ) 10 , 11 . ( a ) Tingaonetse bwanji kuti timalambila Yehova yekha ? ( b ) Kodi acicepele aciheberi anaonetsa bwanji kuti anali odzipeleka kwa Yehova yekha ? Ngati tifuna kudzipeleka kwa Yehova yekha , kodi tiyenela kusamala ndi ciani ? N’zinthu ziti zimene tingayambe kukonda kwambili kuposa Yehova ? N’cifukwa ciani Paulo anakumbutsa Akhiristu kuti Mulungu ni “ Yehova mmodzi ” ? 16 , 17 . ( a ) Ni ulosi wa bwanji umene ukukwanilitsika masiku ano ? Nanga ukukwanilitsika bwanji ? ( b ) N’ciani cingawononge mgwilizano wathu ? 18 , 19 . ( a ) Ni malangizo otani amene ali pa Aefeso 4 : 1 - 3 ? ( b ) Tingacite ciani kuti tithandize mpingo kukhala wogwilizana ? ( Ŵelengani Aefeso 4 : 1 - 3 . ) Tingaonetse bwanji kuti timamvetsetsa tanthauzo la mau akuti “ Yehova Mulungu wathu ndi Yehova mmodzi ” ? M’mbali mwa zilumba za Trinidad ndi Tobago muli midzi yambili imene asodzi amakhalamo . Mboni za Yehova zimalalikila asodzi amene zimapeza kumeneko Kodi Baibulo imaonetsa bwanji kuti tonse ndife ocimwa ? Kodi tiyenela kucita bwanji ndi zolakwa zathu ndi za ena ? Kodi Baibulo inakambilatu ciani ponena za kuculuka kwa anthu a Yehova ? ( Ŵelengani Mika 4 : 1 , 3 . ) Izi zawathandiza kuti akhale “ oyela pa mlandu wa magazi a anthu onse . ” — Machitidwe 20 : 26 . N’cifukwa ciani n’zocititsa cidwi kuti gulu la Yehova likukulilakulila ? N’cifukwa ciani nthawi zina anthu ena amatikhumudwitsa ? ( Ŵelengani Aroma 5 : 12 , 19 . ) Kodi mukanakhala ku Isiraeli m’nthawi ya Eli ndi ana ake , sembe munacita ciani ? Kodi Eli analephela bwanji kulanga ana ake ? Ni macimo aakulu ati amene Davide anacita ? Nanga Mulungu anacita ciani ? ( a ) Kodi mtumwi Petulo analephela bwanji kusunga lonjezo lake ? ( b ) N’cifukwa ciani Yehova anapitiliza kugwilitsila nchito Petulo pambuyo pakuti wacimwa ? Kodi mumakhulupilila kuti Mulungu nthawi zonse amacita zinthu mwacilungamo ? Cifukwa ciani ? Kodi Yesu anazindikila ciani pa zolakwa za Yudasi Isikariyoti ndi Petulo ? Kodi Baibulo inakamba ciani ponena za atumiki a Yehova a masiku ano ? Kodi tiyenela kucita ciani ena akatilakwila ? 13 , 14 . ( a ) N’cifukwa ciani tiyenela kukhala oleza mtima ndi abale athu ? ( b ) Ni lonjezo liti limene tiyenela kumakumbukila ? Kodi Yesu anakamba kuti tiyenela kucita ciani ena akatilakwila ? Kodi inu mudzacita ciani ngati ena akulakwilani ? ( Ŵelengani Mateyu 5 : 23 , 24 . ) Mayankho a mafunso amenewa si ovuta . Tingamvetsetse mfundo imeneyi tikaganizila zimene Baibulo imakamba pankhani yokhala wozindikila ndi wanzelu . Lemba la Miyambo 3 : 13 - 15 limati : “ Wodala ndi munthu amene wapeza nzelu , ndiponso munthu amene wapeza kuzindikila , cifukwa kupeza nzelu monga phindu n’kwabwino kuposa kupeza siliva monga phindu , ndipo kukhala nazo monga zokolola n’kwabwino kuposa kukhala ndi golide . N’zamtengo wapatali kuposa miyala ya korali , ndipo zonse zimene umakonda sizingafanane nazo . ” Yesu anapeleka citsanzo cabwino pankhani yokhala woona mtima . Popeza n’nali bwana wamkulu pa kampaniyo , n’nali kufunika kunyengelela anthu otenga msonkho mwa kuwapatsa n’cekeleko kuti asaulule cinyengo ca kampaniyo . Izi zinacititsa kuti ndizidziŵika monga munthu wosaona mtima . N’taphunzila coonadi , ndinaleka nchitoyo ngakhale kuti n’nali kulandila ndalama zambili . Napeleka citsanzo cabwino kwa ana anga aŵili aamuna , ndipo tsopano n’naikidwa paudindo mumpingo . Cifukwa cokhala woona mtima , nili ndi mbili yabwino kwa anthu amene amatenga misonkho ndi ena amene nimacita nawo bizinesi . ” Kumeneko anayamba kulambila Mulungu woona .